< Oweruza 15 >

1 Patapita nthawi, mu nyengo yodula tirigu, Samsoni anatenga kamwana kambuzi ndipo anapita kukacheza kwa mkazi wake. Iye anati, “Ndikufuna kukalowa ku chipinda cha mkazi wanga.” Koma abambo a mkaziyo anamuletsa kutero.
But it came to pass after a while, in the time of wheat harvest, that Samson visited his wife with a kid. And he said, I will go in to my wife into the chamber, but her father would not allow him to go in.
2 Abambo a mkaziyo anati, “Ine ndimaganiza kuti umamuda kwambiri nʼchifukwa chake ndinamupereka kwa mnzako. Kodi mngʼono wake uja sindiye wokongola kupambana iye? Ingotengani ameneyo mʼmalo mwake.”
And her father said, I truly thought that thou had utterly hated her, therefore I gave her to thy companion. Is not her younger sister fairer than she? Take her, I pray thee, instead of her.
3 Samsoni anawawuza kuti, “Pano sindikhala wochimwa ndikawachita choyipa chachikulu Afilistiwa.”
And Samson said to them, This time I shall be blameless in regard of the Philistines when I do them a mischief.
4 Choncho Samsoni anapita nakagwira nkhandwe 300 nazimangirira michira ziwiriziwiri ndipo pa fundo iliyonse ya michirayo anamangirira nsakali.
And Samson went and caught three hundred foxes, and took firebrands, and turned tail to tail, and put a firebrand in the midst between every two tails.
5 Anayatsa nsakalizo kenaka ndi kuzitayira nkhandwe zija mʼminda ya tirigu ya Afilisti, ndipo zinatentha milu ya tirigu, ndi wosadula yemwe pamodzi ndi mitengo ya mpesa ndi ya olivi.
And when he had set the brands on fire, he let them go into the standing grain of the Philistines, and burnt up both the shocks and the standing grain, and also the oliveyards.
6 Tsono Afilisti anayamba kufunsana kuti, “Ndani wachita izi?” Ena anati, “Ndi Samsoni mkamwini wa munthu wa ku Timna uja chifukwa Mtimunayo anatenga mkazi wake ndi kumupereka kwa mnzake.” Choncho Afilisti anapita kukatentha mtsikanayo pamodzi ndi abambo ake.
Then the Philistines said, Who has done this? And they said, Samson, the son-in-law of the Timnite, because he has taken his wife, and given her to his companion. And the Philistines came up, and burnt her and her father with fire.
7 Samsoni anawawuza kuti, “Ngati mumachita zangati zimenezi, ndiye ine sindileka mpaka nditakulipsirani.”
And Samson said to them, If ye do after this manner, surely I will be avenged of you, and after that I will cease.
8 Choncho Samsoni anamenyana nawo koopsa ndipo anapha ambiri a iwo. Kenaka anakalowa mʼphanga la Etamu, nakhala momwemo.
And he smote them hip and thigh with a great slaughter. And he went down and dwelt in the cleft of the rock of Etam.
9 Pambuyo pake Afilisti anakamanga misasa ya nkhondo mʼdziko la Yuda, ndi kuthira nkhondo mʼdera la Lehi.
Then the Philistines went up, and encamped in Judah, and spread themselves in Lehi.
10 Anthu a fuko la Yuda anafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mwabwera kudzamenyana nafe?” Iwo anayankha kuti, “Tabwera kudzamanga Samsoni ndi kuti timuchite zofanana ndi zimene anatichita.”
And the men of Judah said, Why have ye come up against us? And they said, We come up to bind Samson, to do to him as he has done to us.
11 Ndipo anthu 3,000 a ku Yuda anapita ku phanga la Etamu, ndi kukamufunsa Samsoni kuti, “Kodi iwe sudziwa kuti ife amatilamulira ndi Afilisti? Tsono ndi chiyani chimene watichitachi?” Iye anayankha kuti, “Ine ndinachita zomwe iwo anandichita.”
Then three thousand men of Judah went down to the cleft of the rock of Etam, and said to Samson, Know thou not that the Philistines are rulers over us? What then is this that thou have done to us? And he said to them, As they did to me, so have I done to them.
12 Iwo anati kwa iye, “Ife tabwera kuti tikumange ndi kukupereka kwa Afilisti.” Ndipo Samsoni anati, “Lonjezani mwa lumbiro kuti simundipha ndinu.”
And they said to him, We have come down to bind thee, that we may deliver thee into the hand of the Philistines. And Samson said to them, Swear to me, that ye will not fall upon me yourselves.
13 Iwo anamuyankha kuti, “Ayi, ife sitikupha. Koma tingokumanga ndi kukupereka mʼmanja mwa Afilisti.” Choncho anamumanga ndi zingwe ziwiri zatsopano namutulutsa mʼphanga muja.
And they spoke to him, saying, No, but we will bind thee fast, and deliver thee into their hand, but truly we will not kill thee. And they bound him with two new ropes, and brought him up from the rock.
14 Samsoni anafika ku Lehi, ndipo Afilisti anamuchingamira akufuwula. Nthawi yomweyo Mzimu wa Yehova unatsika pa iye mwamphamvu ndipo zingwe zimene anamumanga nazo zinasanduka ngati thonje lopsa mʼmoto, zinachita ngati zasungunuka nʼkuchoka mʼmanja mwake.
When he came to Lehi, the Philistines shouted as they met him. And the Spirit of Jehovah came mightily upon him, and the ropes that were upon his arms became as flax that was burnt with fire, and his bands dropped from off his hands.
15 Anapeza chibwano cha bulu amene anali atangofa kumene. Anachitola ndi kuphera nacho anthu 1,000.
And he found a fresh jawbone of a donkey, and put forth his hand, and took it, and smote a thousand men with it.
16 Ndipo Samsoni anati, “Ndi chibwano cha bulu, milu ndi milu ya anthu. Ndi chibwano cha bulu, ndapha anthu 1,000.”
And Samson said, With the jawbone of a donkey, heaps upon heaps, with the jawbone of a donkey I have smitten a thousand men.
17 Atatsiriza kuyankhula, anataya chibwanocho, ndipo malowo anawatcha Ramati-Lehi.
And it came to pass, when he had made an end of speaking, that he cast away the jawbone out of his hand. And that place was called Ramath-lehi.
18 Pambuyo pake anamva ludzu kwambiri ndipo anayitana Yehova mopempha kuti, “Inu mwapatsa mtumiki wanu chipulumutso chachikulu chotere. Kodi tsopano ndife ndi ludzu ndi kugwidwa ndi anthu osachita mdulidwewa?”
And he was very thirsty, and called on Jehovah, and said, Thou have given this great deliverance by the hand of thy servant, and now shall I die for thirst, and fall into the hand of the uncircumcised?
19 Pamenepo Mulungu anangʼamba nthaka ku Lehi, ndipo madzi anatuluka mʼdzenjemo. Samsoni anamwa madziwo, ndipo mphamvu zake zinabwerera nakhalanso monga analili. Choncho chitsimecho chinatchedwa Eni-Hakore, ndipo chilipobe ku Lehiko mpaka lero.
But God split the hollow place that is in Lehi, and water came out there. And when he had drunk his spirit came again, and he revived. Therefore the name of it was called En-hakkore, which is in Lehi to this day.
20 Samsoni anatsogolera Israeli pa nthawi ya Afilisti kwa zaka makumi awiri.
And he judged Israel in the days of the Philistines twenty years.

< Oweruza 15 >