< Oweruza 15 >

1 Patapita nthawi, mu nyengo yodula tirigu, Samsoni anatenga kamwana kambuzi ndipo anapita kukacheza kwa mkazi wake. Iye anati, “Ndikufuna kukalowa ku chipinda cha mkazi wanga.” Koma abambo a mkaziyo anamuletsa kutero.
Stalo se pak po několika dnech, v čas žně pšeničné, že chtěje navštíviti Samson ženu svou, a přinésti s sebou kozlíka, řekl: Vejdu k ženě své do pokoje. A nedopustil mu otec její vjíti.
2 Abambo a mkaziyo anati, “Ine ndimaganiza kuti umamuda kwambiri nʼchifukwa chake ndinamupereka kwa mnzako. Kodi mngʼono wake uja sindiye wokongola kupambana iye? Ingotengani ameneyo mʼmalo mwake.”
I řekl otec její: Domníval jsem se zajisté, že ji máš v nenávisti, protož dal jsem ji tovaryši tvému. Zdaliž není sestra její mladší pěknější než ona? Nechať jest tedy tvá místo oné.
3 Samsoni anawawuza kuti, “Pano sindikhala wochimwa ndikawachita choyipa chachikulu Afilistiwa.”
I řekl jim Samson: Nebuduť já potom vinen Filistinským, když jim zle učiním.
4 Choncho Samsoni anapita nakagwira nkhandwe 300 nazimangirira michira ziwiriziwiri ndipo pa fundo iliyonse ya michirayo anamangirira nsakali.
Odšed tedy Samson, nalapal tři sta lišek, a vzav pochodně, obrátil jeden ocas k druhému, a dal vše jednu pochodni mezi dva ocasy do prostředka.
5 Anayatsa nsakalizo kenaka ndi kuzitayira nkhandwe zija mʼminda ya tirigu ya Afilisti, ndipo zinatentha milu ya tirigu, ndi wosadula yemwe pamodzi ndi mitengo ya mpesa ndi ya olivi.
Potom zapálil ty pochodně, a pustil do obilí Filistinských, a popálil, jakž sžaté tak nesžaté, i vinice i olivoví.
6 Tsono Afilisti anayamba kufunsana kuti, “Ndani wachita izi?” Ena anati, “Ndi Samsoni mkamwini wa munthu wa ku Timna uja chifukwa Mtimunayo anatenga mkazi wake ndi kumupereka kwa mnzake.” Choncho Afilisti anapita kukatentha mtsikanayo pamodzi ndi abambo ake.
I řekli Filistinští: Kdo je to učinil? Jimž odpovědíno: Samson zeť Tamnejského, proto že vzal ženu jeho a dal ji tovaryši jeho. Tedy přišedše Filistinští, spálili ji ohněm i otce jejího.
7 Samsoni anawawuza kuti, “Ngati mumachita zangati zimenezi, ndiye ine sindileka mpaka nditakulipsirani.”
Tedy řekl jim Samson: Ač jste učinili tak, však až se lépe vymstím nad vámi, teprv přestanu.
8 Choncho Samsoni anamenyana nawo koopsa ndipo anapha ambiri a iwo. Kenaka anakalowa mʼphanga la Etamu, nakhala momwemo.
I zbil je na hnátích i na bedrách porážkou velikou, a odšed, usadil se na vrchu skály Etam.
9 Pambuyo pake Afilisti anakamanga misasa ya nkhondo mʼdziko la Yuda, ndi kuthira nkhondo mʼdera la Lehi.
Pročež vytáhli Filistinští, a rozbivše stany proti Judovi, rozložili se až do Lechi.
10 Anthu a fuko la Yuda anafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mwabwera kudzamenyana nafe?” Iwo anayankha kuti, “Tabwera kudzamanga Samsoni ndi kuti timuchite zofanana ndi zimene anatichita.”
Muži pak Juda řekli: Proč jste vytáhli proti nám? I odpověděli: Vytáhli jsme, abychom svázali Samsona, a učinili jemu tak, jako on nám učinil.
11 Ndipo anthu 3,000 a ku Yuda anapita ku phanga la Etamu, ndi kukamufunsa Samsoni kuti, “Kodi iwe sudziwa kuti ife amatilamulira ndi Afilisti? Tsono ndi chiyani chimene watichitachi?” Iye anayankha kuti, “Ine ndinachita zomwe iwo anandichita.”
Tedy vyšlo tři tisíce mužů Juda k vrchu skály Etam, a řekli Samsonovi: Nevíš-liž, že panují nad námi Filistinští? Pročež jsi tedy nám to učinil? I odpověděl jim: Jakž mi učinili, tak jsem jim učinil.
12 Iwo anati kwa iye, “Ife tabwera kuti tikumange ndi kukupereka kwa Afilisti.” Ndipo Samsoni anati, “Lonjezani mwa lumbiro kuti simundipha ndinu.”
Řekli také jemu: Přišli jsme, abychom tě svázali a vydali v ruku Filistinským. Tedy odpověděl jim Samson: Přisáhněte mi, že vy se na mne neoboříte.
13 Iwo anamuyankha kuti, “Ayi, ife sitikupha. Koma tingokumanga ndi kukupereka mʼmanja mwa Afilisti.” Choncho anamumanga ndi zingwe ziwiri zatsopano namutulutsa mʼphanga muja.
Tedy mluvili jemu, řkouce: Nikoli, jediné tuze svížíce, vydáme tě v ruku jejich, ale nezabijeme tě. I svázali ho dvěma provazy novými, a svedli jej s skály.
14 Samsoni anafika ku Lehi, ndipo Afilisti anamuchingamira akufuwula. Nthawi yomweyo Mzimu wa Yehova unatsika pa iye mwamphamvu ndipo zingwe zimene anamumanga nazo zinasanduka ngati thonje lopsa mʼmoto, zinachita ngati zasungunuka nʼkuchoka mʼmanja mwake.
Kterýž když přišel až do Lechi, Filistinští radostí křičeli proti němu. Přišel pak na něj Duch Hospodinův, a učiněni jsou provazové, kteříž byli na rukou jeho, jako niti lněné, když v ohni hoří, i spadli svazové s rukou jeho.
15 Anapeza chibwano cha bulu amene anali atangofa kumene. Anachitola ndi kuphera nacho anthu 1,000.
Tedy našel čelist osličí ještě vlhkou, a vztáh ruku svou, vzal ji a pobil ní tisíc mužů.
16 Ndipo Samsoni anati, “Ndi chibwano cha bulu, milu ndi milu ya anthu. Ndi chibwano cha bulu, ndapha anthu 1,000.”
Protož řekl Samson: Čelistí osličí hromadu jednu, nýbrž dvě hromady, čelistí osličí zbil jsem tisíc mužů.
17 Atatsiriza kuyankhula, anataya chibwanocho, ndipo malowo anawatcha Ramati-Lehi.
A když přestal mluviti, povrhl čelist z ruky své, a nazval to místo Ramat Lechi.
18 Pambuyo pake anamva ludzu kwambiri ndipo anayitana Yehova mopempha kuti, “Inu mwapatsa mtumiki wanu chipulumutso chachikulu chotere. Kodi tsopano ndife ndi ludzu ndi kugwidwa ndi anthu osachita mdulidwewa?”
Žíznil pak velice, i volal k Hospodinu a řekl: Ty jsi učinil skrze ruce služebníka svého vysvobození toto veliké, nyní pak již žízní umru, aneb upadnu v ruku těch neobřezaných.
19 Pamenepo Mulungu anangʼamba nthaka ku Lehi, ndipo madzi anatuluka mʼdzenjemo. Samsoni anamwa madziwo, ndipo mphamvu zake zinabwerera nakhalanso monga analili. Choncho chitsimecho chinatchedwa Eni-Hakore, ndipo chilipobe ku Lehiko mpaka lero.
Tedy otevřel Bůh skálu v Lechi, i vyšly z ní vody, a napil se; i okřál, a jako ožil. Protož nazval jméno její studnice vzývajícího, kteráž jest v Lechi až do dnešního dne.
20 Samsoni anatsogolera Israeli pa nthawi ya Afilisti kwa zaka makumi awiri.
Soudil pak Izraele za času Filistinských dvadceti let.

< Oweruza 15 >