< Oweruza 14 >
1 Samsoni anapita ku Timna ndipo kumeneko anaonako mtsikana wa Chifilisiti.
Samson je odšel dol v Timno in v Timni zagledal žensko izmed filistejskih hčera.
2 Atabwerera kwawo, anawuza abambo ndi amayi ake kuti, “Ine ndaona mtsikana wa Chifilisiti ku Timna, tsono mukanditengere ameneyo kuti akhale mkazi wanga.”
Prišel je gor in svojemu očetu in svoji materi povedal ter rekel: »V Timni sem videl žensko izmed filistejskih hčera. Sedaj mi jo torej vzemita za ženo.«
3 Koma abambo ndi amayi ake anayankha kuti, “Kodi palibe mkazi pakati pa abale akowa kapena pakati pa anthu a mtundu wako, kuti iwe upite kukapeza mkazi kwa Afilisti anthu osachita mdulidwe?” Koma Samsoni anawuza abambo ake kuti, “Kanditengereni ameneyu basi, pakuti ndamukonda.”
Potem sta mu njegov oče in njegova mati rekla: » Ali tam ni nobene ženske med hčerami tvojih bratov ali med vsem mojim ljudstvom, da greš, da si vzameš ženo izmed neobrezanih Filistejcev?« Samson je rekel svojemu očetu: »Njo mi vzemi, kajti ta mi ugaja.«
4 (Abambo ndi amayi ake sankadziwa kuti zimenezi zinali zochokera kwa Yehova, pakuti Yehova amafuna powapezera chifukwa Afilistiwo. Nthawi imeneyo nʼkuti Afilisti akulamulira Aisraeli).
Toda njegov oče in njegova mati nista vedela, da je bilo to od Gospoda, da je iskal priložnost zoper Filistejce, kajti ob tistem času so imeli Filistejci gospostvo nad Izraelom.
5 Choncho Samsoni pamodzi ndi abambo ake anapita ku Timna. Akuyandikira minda ya mpesa ya ku Timna, mwadzidzidzi anamva kubuma kwa mkango waungʼono ukubwera kumene kunali iye.
Potem so Samson, njegov oče in njegova mati odšli dol v Timno in prišli do timnatskih vinogradov in glej, proti njemu je zarjovel mlad lev.
6 Tsono Mzimu wa Yehova unafika ndi mphamvu pa Samsoni ndipo ngakhale analibe chida mʼmanja mwake, iye anakadzula mkangowo ngati akukadzula mwana wambuzi. Koma sanawuze abambo kapena amayi ake zimene anachitazo.
Gospodov Duh je mogočno prišel nadenj in raztrgal ga je, kakor bi raztrgal kozliča in ničesar ni imel v svoji roki, toda svojemu očetu ali svoji materi ni povedal, kaj je storil.
7 Kenaka Samsoni anapita kukakambirana ndi mkaziyo, ndipo anamukonda mtsikanayo.
Odšel je dol in govoril z žensko in Samsonu je ugajala.
8 Patapita nthawi, Samsoni anabwerera kukatenga mtsikana uja. Panjira anapatuka kukaona mkango unawupha uja, ndipo anangoona njuchi zili mu mkangowo pamodzi ndi uchi wake.
Čez nekaj časa se je vrnil, da jo vzame in zavil je stran, da pogleda levje truplo in glej, tam je bil roj čebel in med v levjem truplu.
9 Tsono anakomberako uchi uja mʼmanja mwake ndi kumapita akudya. Atabwereranso kwa abambo ndi amayi ake, anawapatsako uchiwo ndipo anadya. Koma sanawawuze kuti uchi umenewo anawufula mu mkango wakufa.
Od tega je vzel v svoje roke in jedoč šel naprej in prišel k svojemu očetu in materi ter jima dal in onadva sta jedla. Toda ni jima povedal, da je med vzel iz levjega trupla.
10 Tsopano Samsoni anapita ku nyumba kwa mtsikanayo. Ndipo kumeneko Samsoni anakonza phwando monga ankachitira anyamata.
Tako je njegov oče odšel dol k ženski in Samson je tam priredil zabavo, kajti tako so imeli mladeniči navado delati.
11 Makolo a mkwatibwiyo atamuona, anasankha anyamata makumi atatu kuti akhale naye.
Pripetilo se je, ko so ga zagledali, da so privedli trideset družabnikov, da bi bili z njim.
12 Samsoni anawawuza kuti, “Bwanji ndikuphereni mwambi. Mukandiwuza tanthauzo lake asanathe masiku asanu ndi awiri aphwandowa, ndidzakupatsani zovala makumi atatu za bafuta ndi zina makumi atatu za tsiku la chikondwerero.
Samson jim je rekel: »Sedaj vam bom zastavil uganko. Če mi jo lahko v sedmih dneh praznovanja zagotovo razodenete in jo odkrijete, potem vam bom dal trideset rjuh in trideset zamenjav oblek,
13 Koma ngati simutha kundiwuza tanthauzo lake, inuyo mudzandipatsa zovala makumi atatu zabafuta ndi zina za tsiku la chikondwerero.” Iwo anamuyankha kuti, “Tiwuze mwambi wakowo tiwumve.”
toda če mi je ne morete oznaniti, potem mi boste vi dali trideset rjuh in trideset zamenjav oblek.« Rekli so mu: »Zastavi svojo uganko, da jo bomo lahko slišali.«
14 Iye anati, “Chakudya chinatuluka mu chinthu chodya chinzake; ndipo chozuna chinatuluka mu chinthu champhamvu.” Panapita masiku atatu anthuwo akulephera kumasulira mwambiwo.
Rekel jim je: »Iz jedca je prišla hrana in iz močnega je izšla sladkost.« In v treh dneh niso mogli pojasniti uganke.
15 Tsiku lachinayi anthuwo anawuza mkazi wa Samsoni kuti, “Umunyengerere mwamuna wako kuti akuwuze tanthauzo la mwambiwu. Ngati sutero tikutentha iweyo pamodzi ndi nyumba ya abambo ako. Kodi unatiyitana kuti mudzatilande zinthu zathu?”
Pripetilo se je na sedmi dan, da so Samsonovi ženi rekli: »Premami svojega soproga, da nam lahko oznani uganko, sicer bomo tebe in hišo tvojega očeta zažgali z ognjem. Ali ste nas poklicali, da vzamete kar imamo? Mar ni tako?«
16 Kenaka mkazi wa Samsoni anayamba kulira pamaso pake namuwuza kuti, “Inu mumandida ndipo simundikonda. Mwaphera anyamata a mtundu wathu mwambi, koma ine wosandiwuza tanthauzo lake.” Samsoni anamuyankha kuti, “Taona sindinawuze abambo kapena amayi anga, ndiye ndiwuze iweyo?”
Samsonova žena je jokala pred njim ter rekla: »Ti me le sovražiš in me ne ljubiš. Otrokom mojega ljudstva si zastavil uganko, meni pa je nisi povedal.« Rekel ji je: »Glej, nisem je povedal svojemu očetu niti svoji materi in jo bom povedal tebi?«
17 Mkaziyo anamulirira masiku onse asanu ndi awiri aphwandowo. Choncho pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anamuwuza tanthauzo lake popeza amamukakamiza. Ndipo mkaziyo anakawuza abale ake aja tanthauzo la mwambiwo.
Pred njim je jokala sedem dni, dokler je trajala njihova zabava in pripetilo se je na sedmi dan, da ji je povedal, ker je boleče pritiskala nanj in uganko je povedala otrokom svojega ljudstva.
18 Pambuyo pake anthu a mu mzinda aja anamuwuza Samsoni pa tsiku lachisanu ndi chiwiri dzuwa lisanalowe kuti, “Chozuna nʼchiyani choposa uchi? Champhamvu nʼchiyani choposa mkango?” Samsoni anawawuza kuti, “Mukanapanda kutipula ndi ngʼombe yanga yayingʼono, simukanatha kumasulira mwambi wangawu.”
Možje iz mesta so mu sedmi dan, preden je sonce zašlo, rekli: »Kaj je slajše od meda? In kaj je močnejše kakor lev?« Rekel jim je: »Če ne bi orali z mojo telico, ne bi odkrili moje uganke.«
19 Ndipo Mzimu wa Yehova unafika pa iye mwamphamvu. Choncho anatsikira ku Asikeloni naphako anthu makumi atatu, natenga zovala zawo za tsiku la chikondwerero napereka kwa anthu amene anamasulira mwambi wake. Kenaka anabwerera ku nyumba ya abambo ake ndi mkwiyo waukulu.
In Gospodov Duh je prišel nadenj in odšel je dol v Aškelón in izmed njih usmrtil trideset mož, vzel njihov plen in dal zamenjavo oblačil tistim, ki so pojasnili uganko. Njegova jeza je bila vžgana in odšel je gor do hiše svojega očeta.
20 Ndipo mkazi wa Samsoniyo anamukwatitsa kwa amene anali mnzake womuperekeza pa ukwati paja.
Toda Samsonova žena je bila dana njegovemu družabniku, ki ga je uporabil kakor svojega prijatelja.