< Oweruza 14 >

1 Samsoni anapita ku Timna ndipo kumeneko anaonako mtsikana wa Chifilisiti.
И сиђе Самсон у Тамнат, и виде онде једну девојку између кћери филистејских.
2 Atabwerera kwawo, anawuza abambo ndi amayi ake kuti, “Ine ndaona mtsikana wa Chifilisiti ku Timna, tsono mukanditengere ameneyo kuti akhale mkazi wanga.”
И вративши се каза оцу свом и матери својој говорећи: Видех девојку у Тамнату између кћери филистејских; ожените ме њом.
3 Koma abambo ndi amayi ake anayankha kuti, “Kodi palibe mkazi pakati pa abale akowa kapena pakati pa anthu a mtundu wako, kuti iwe upite kukapeza mkazi kwa Afilisti anthu osachita mdulidwe?” Koma Samsoni anawuza abambo ake kuti, “Kanditengereni ameneyu basi, pakuti ndamukonda.”
А отац и мати рекоше му: Зар нема девојке међу кћерима твоје браће у свем народу мом, да идеш да се ожениш између Филистеја необрезаних? А Самсон одговори оцу свом: Њом ме ожени, јер ми је она омилела.
4 (Abambo ndi amayi ake sankadziwa kuti zimenezi zinali zochokera kwa Yehova, pakuti Yehova amafuna powapezera chifukwa Afilistiwo. Nthawi imeneyo nʼkuti Afilisti akulamulira Aisraeli).
А отац и мати његова не знаху да је то од Господа, и да тражи задевицу с Филистејима; јер у оно време Филистеји владаху синовима Израиљевим.
5 Choncho Samsoni pamodzi ndi abambo ake anapita ku Timna. Akuyandikira minda ya mpesa ya ku Timna, mwadzidzidzi anamva kubuma kwa mkango waungʼono ukubwera kumene kunali iye.
И тако сиђе Самсон с оцем својим и с матером својом у Тамнат, и кад дођоше до винограда тамнатских, гле, млад лав ричући сукоби га.
6 Tsono Mzimu wa Yehova unafika ndi mphamvu pa Samsoni ndipo ngakhale analibe chida mʼmanja mwake, iye anakadzula mkangowo ngati akukadzula mwana wambuzi. Koma sanawuze abambo kapena amayi ake zimene anachitazo.
И дух Господњи сиђе на њ, те растрже лава као јаре немајући ништа у руци: и не каза оцу ни матери шта је учинио.
7 Kenaka Samsoni anapita kukakambirana ndi mkaziyo, ndipo anamukonda mtsikanayo.
И тако дошавши говори с девојком, и она омиле Самсону.
8 Patapita nthawi, Samsoni anabwerera kukatenga mtsikana uja. Panjira anapatuka kukaona mkango unawupha uja, ndipo anangoona njuchi zili mu mkangowo pamodzi ndi uchi wake.
А после неколико дана идући опет да је одведе, сврне да види мртвог лава; а гле, у мртвом лаву рој пчела и мед.
9 Tsono anakomberako uchi uja mʼmanja mwake ndi kumapita akudya. Atabwereranso kwa abambo ndi amayi ake, anawapatsako uchiwo ndipo anadya. Koma sanawawuze kuti uchi umenewo anawufula mu mkango wakufa.
И извади га у руку, и пође путем једући; и кад дође к оцу и матери, даде им те једоше; али им не рече да је из мртвог лава извадио мед.
10 Tsopano Samsoni anapita ku nyumba kwa mtsikanayo. Ndipo kumeneko Samsoni anakonza phwando monga ankachitira anyamata.
И тако дође отац његов к оној девојци, и Самсон учини онде весеље, јер тако чињаху момци.
11 Makolo a mkwatibwiyo atamuona, anasankha anyamata makumi atatu kuti akhale naye.
И кад га видеше Филистеји, изабраше тридесет другова да буду с њим.
12 Samsoni anawawuza kuti, “Bwanji ndikuphereni mwambi. Mukandiwuza tanthauzo lake asanathe masiku asanu ndi awiri aphwandowa, ndidzakupatsani zovala makumi atatu za bafuta ndi zina makumi atatu za tsiku la chikondwerero.
И рече им Самсон: Ја ћу вам загонетнути загонетку, па ако ми је одгонетнете за седам дана док је весеље и погодите, даћу вам тридесет кошуља и тридесет свечаних хаљина.
13 Koma ngati simutha kundiwuza tanthauzo lake, inuyo mudzandipatsa zovala makumi atatu zabafuta ndi zina za tsiku la chikondwerero.” Iwo anamuyankha kuti, “Tiwuze mwambi wakowo tiwumve.”
Ако ли не одгонетнете, ви ћете дати мени тридесет кошуља и тридесеторе свечане хаљине. А они му рекоше: Загонетни загонетку своју, да чујемо.
14 Iye anati, “Chakudya chinatuluka mu chinthu chodya chinzake; ndipo chozuna chinatuluka mu chinthu champhamvu.” Panapita masiku atatu anthuwo akulephera kumasulira mwambiwo.
Тада им рече; од оног који једе изиђе јело, и од љутог изиђе слатко. И не могаше одгонетнути загонетке три дана.
15 Tsiku lachinayi anthuwo anawuza mkazi wa Samsoni kuti, “Umunyengerere mwamuna wako kuti akuwuze tanthauzo la mwambiwu. Ngati sutero tikutentha iweyo pamodzi ndi nyumba ya abambo ako. Kodi unatiyitana kuti mudzatilande zinthu zathu?”
И седми дан рекоше жени Самсоновој: Наговори мужа свог да нам каже загонетку, или ћемо спалити огњем тебе и дом оца твог. Јесте ли нас зато позвали да нам узмете имање? Је ли тако?
16 Kenaka mkazi wa Samsoni anayamba kulira pamaso pake namuwuza kuti, “Inu mumandida ndipo simundikonda. Mwaphera anyamata a mtundu wathu mwambi, koma ine wosandiwuza tanthauzo lake.” Samsoni anamuyankha kuti, “Taona sindinawuze abambo kapena amayi anga, ndiye ndiwuze iweyo?”
И стаде плакати жена Самсонова пред њим говорећи: Ти мрзиш на ме, и ти ме не љубиш; загонетнуо си загонетку синовима народа мог, а нећеш мени да кажеш. А он јој рече: Гле, ни оцу свом ни матери својој нисам је казао, а теби да је кажем?
17 Mkaziyo anamulirira masiku onse asanu ndi awiri aphwandowo. Choncho pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anamuwuza tanthauzo lake popeza amamukakamiza. Ndipo mkaziyo anakawuza abale ake aja tanthauzo la mwambiwo.
И она плака пред њим за седам дана докле трајаше весеље. А седми дан каза јој, јер беше навалила на њ: а она каза загонетку синовима народа свог.
18 Pambuyo pake anthu a mu mzinda aja anamuwuza Samsoni pa tsiku lachisanu ndi chiwiri dzuwa lisanalowe kuti, “Chozuna nʼchiyani choposa uchi? Champhamvu nʼchiyani choposa mkango?” Samsoni anawawuza kuti, “Mukanapanda kutipula ndi ngʼombe yanga yayingʼono, simukanatha kumasulira mwambi wangawu.”
Тада му рекоше људи града оног седми дан док сунце не зађе: Шта је слађе од меда, и шта је љуће од лава? А он им рече: Да нисте орали на мојој јуници, не бисте погодили моје загонетке.
19 Ndipo Mzimu wa Yehova unafika pa iye mwamphamvu. Choncho anatsikira ku Asikeloni naphako anthu makumi atatu, natenga zovala zawo za tsiku la chikondwerero napereka kwa anthu amene anamasulira mwambi wake. Kenaka anabwerera ku nyumba ya abambo ake ndi mkwiyo waukulu.
И дође на њ дух Господњи, те сиђе у Аскалон, и поби онде тридесет људи, и узе одело с њих и даде свечане хаљине онима који одгонетнуше загонетку; и расрди се врло и отиде кући оца свог.
20 Ndipo mkazi wa Samsoniyo anamukwatitsa kwa amene anali mnzake womuperekeza pa ukwati paja.
А жена Самсонова удаде се за друга његовог, с којим се беше удружио.

< Oweruza 14 >