< Oweruza 14 >

1 Samsoni anapita ku Timna ndipo kumeneko anaonako mtsikana wa Chifilisiti.
Самсон с-а коборыт ла Тимна ши а вэзут аколо о фемее дин фетеле филистенилор.
2 Atabwerera kwawo, anawuza abambo ndi amayi ake kuti, “Ine ndaona mtsikana wa Chifilisiti ku Timna, tsono mukanditengere ameneyo kuti akhale mkazi wanga.”
Кынд с-а суит ынапой, а спус лукрул ачеста татэлуй сэу ши мамей сале ши а зис: „Ам вэзут ла Тимна о фемее дин фетеле филистенилор; луаци-мь-о акум де невастэ.”
3 Koma abambo ndi amayi ake anayankha kuti, “Kodi palibe mkazi pakati pa abale akowa kapena pakati pa anthu a mtundu wako, kuti iwe upite kukapeza mkazi kwa Afilisti anthu osachita mdulidwe?” Koma Samsoni anawuza abambo ake kuti, “Kanditengereni ameneyu basi, pakuti ndamukonda.”
Татэл сэу ши мама са й-ау зис: „Ну есте ничо фемее ынтре фетеле фрацилор тэй ши ын тот попорул ностру, де те дучь сэ-ць ей невастэ де ла филистень, каре сунт нетэяць ымпрежур?” Ши Самсон а зис татэлуй сэу: „Я-мь-о, кэч ымь плаче.”
4 (Abambo ndi amayi ake sankadziwa kuti zimenezi zinali zochokera kwa Yehova, pakuti Yehova amafuna powapezera chifukwa Afilistiwo. Nthawi imeneyo nʼkuti Afilisti akulamulira Aisraeli).
Татэл сэу ши мама са ну штияу кэ лукрул ачеста веня де ла Домнул, кэч Самсон кэута ун прилеж де чартэ дин партя филистенилор. Ын время ачея, филистений стэпыняу песте Исраел.
5 Choncho Samsoni pamodzi ndi abambo ake anapita ku Timna. Akuyandikira minda ya mpesa ya ku Timna, mwadzidzidzi anamva kubuma kwa mkango waungʼono ukubwera kumene kunali iye.
Самсон с-а коборыт ымпреунэ ку татэл сэу ши ку мама са ла Тимна. Кынд ау ажунс ла вииле дин Тимна, ятэ кэ й-а ешит ынаинте ун леу тынэр муӂинд.
6 Tsono Mzimu wa Yehova unafika ndi mphamvu pa Samsoni ndipo ngakhale analibe chida mʼmanja mwake, iye anakadzula mkangowo ngati akukadzula mwana wambuzi. Koma sanawuze abambo kapena amayi ake zimene anachitazo.
Духул Домнулуй а венит песте Самсон ши, фэрэ сэ айбэ чева ын мынэ, Самсон а сфышият пе леу кум се сфышие ун ед. Н-а спус татэлуй сэу ши мамей сале че фэкусе.
7 Kenaka Samsoni anapita kukakambirana ndi mkaziyo, ndipo anamukonda mtsikanayo.
С-а коборыт ши а ворбит ку фемея ачея ши еа й-а плэкут.
8 Patapita nthawi, Samsoni anabwerera kukatenga mtsikana uja. Panjira anapatuka kukaona mkango unawupha uja, ndipo anangoona njuchi zili mu mkangowo pamodzi ndi uchi wake.
Дупэ кытва тимп, с-а дус ярэшь ла Тимна ка с-о я ши с-а абэтут сэ вадэ хойтул леулуй. Ши ятэ кэ ын трупул леулуй ера ун рой де албине ши мьере.
9 Tsono anakomberako uchi uja mʼmanja mwake ndi kumapita akudya. Atabwereranso kwa abambo ndi amayi ake, anawapatsako uchiwo ndipo anadya. Koma sanawawuze kuti uchi umenewo anawufula mu mkango wakufa.
А луат мьеря ын мынэ ши а мынкат-о пе друм ши, кынд а ажунс ла татэл сэу ши ла мама са, ле-а дат ши ау мынкат ши ей дин еа. Дар ну ле-а спус кэ луасе мьеря ачаста дин трупул леулуй.
10 Tsopano Samsoni anapita ku nyumba kwa mtsikanayo. Ndipo kumeneko Samsoni anakonza phwando monga ankachitira anyamata.
Татэл луй Самсон с-а коборыт ла фемея ачея. Ши аколо Самсон а фэкут ун оспэц, кэч аша фэчяу тинерий.
11 Makolo a mkwatibwiyo atamuona, anasankha anyamata makumi atatu kuti akhale naye.
Кум л-ау вэзут, ау пофтит трейзечь де товарэшь, каре ау стат ымпреунэ ку ел.
12 Samsoni anawawuza kuti, “Bwanji ndikuphereni mwambi. Mukandiwuza tanthauzo lake asanathe masiku asanu ndi awiri aphwandowa, ndidzakupatsani zovala makumi atatu za bafuta ndi zina makumi atatu za tsiku la chikondwerero.
Самсон ле-а зис: „Ам сэ вэ спун о гичитоаре. Дакэ мь-о вець гичи ын челе шапте зиле але оспэцулуй ши дакэ о вець дезлега, вэ вой да трейзечь де кэмэшь ши трейзечь де хайне де скимб.
13 Koma ngati simutha kundiwuza tanthauzo lake, inuyo mudzandipatsa zovala makumi atatu zabafuta ndi zina za tsiku la chikondwerero.” Iwo anamuyankha kuti, “Tiwuze mwambi wakowo tiwumve.”
Дар, дакэ н-о вець гичи, сэ-мь даць вой трейзечь де кэмэшь ши трейзечь де хайне де скимб.” Ей й-ау зис: „Спуне-не гичитоаря та с-о аузим.”
14 Iye anati, “Chakudya chinatuluka mu chinthu chodya chinzake; ndipo chozuna chinatuluka mu chinthu champhamvu.” Panapita masiku atatu anthuwo akulephera kumasulira mwambiwo.
Ши ел ле-а зис: „Дин чел че мэнынкэ а ешит че се мэнынкэ, Ши дин чел таре а ешит дулчацэ.”
15 Tsiku lachinayi anthuwo anawuza mkazi wa Samsoni kuti, “Umunyengerere mwamuna wako kuti akuwuze tanthauzo la mwambiwu. Ngati sutero tikutentha iweyo pamodzi ndi nyumba ya abambo ako. Kodi unatiyitana kuti mudzatilande zinthu zathu?”
Трей зиле, н-ау путут дезлега гичитоаря. Ын зиуа а шаптя, ау зис невестей луй Самсон: „Ындуплекэ пе бэрбатул тэу сэ не дезлеӂе гичитоаря, алтфел те вом арде, пе тине ши каса татэлуй тэу. Не-аць адунат аич ка сэ не жефуиць, ну-й аша?”
16 Kenaka mkazi wa Samsoni anayamba kulira pamaso pake namuwuza kuti, “Inu mumandida ndipo simundikonda. Mwaphera anyamata a mtundu wathu mwambi, koma ine wosandiwuza tanthauzo lake.” Samsoni anamuyankha kuti, “Taona sindinawuze abambo kapena amayi anga, ndiye ndiwuze iweyo?”
Неваста луй Самсон плынӂя лынгэ ел ши зичя: „Ту н-ай декыт урэ пентру мине ши ну мэ юбешть; ай спус о гичитоаре копиилор попорулуй меу ши ну мь-ай дезлегат-о!” Ши ел й-а рэспунс: „Н-ам дезлегат-о нич татэлуй меу, нич мамей меле, сэ ць-о дезлег цие?”
17 Mkaziyo anamulirira masiku onse asanu ndi awiri aphwandowo. Choncho pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anamuwuza tanthauzo lake popeza amamukakamiza. Ndipo mkaziyo anakawuza abale ake aja tanthauzo la mwambiwo.
Еа а плынс лынгэ ел тот тимпул челор шапте зиле кыт а цинут оспэцул ши, ын зиуа а шаптя, й-а дезлегат-о, кэч ыл некэжя. Ши еа а дат копиилор попорулуй ей дезлегаря гичиторий.
18 Pambuyo pake anthu a mu mzinda aja anamuwuza Samsoni pa tsiku lachisanu ndi chiwiri dzuwa lisanalowe kuti, “Chozuna nʼchiyani choposa uchi? Champhamvu nʼchiyani choposa mkango?” Samsoni anawawuza kuti, “Mukanapanda kutipula ndi ngʼombe yanga yayingʼono, simukanatha kumasulira mwambi wangawu.”
Оамений дин четате ау зис луй Самсон ын зиуа а шаптя, ынаинте де апусул соарелуй: „Че есте май дулче декыт мьеря ши че есте май таре декыт леул?” Ши ел ле-а зис: „Дакэ н-аць фи арат ку жункана мя, Ну мь-аць фи дезлегат гичитоаря.”
19 Ndipo Mzimu wa Yehova unafika pa iye mwamphamvu. Choncho anatsikira ku Asikeloni naphako anthu makumi atatu, natenga zovala zawo za tsiku la chikondwerero napereka kwa anthu amene anamasulira mwambi wake. Kenaka anabwerera ku nyumba ya abambo ake ndi mkwiyo waukulu.
Духул Домнулуй а венит песте ел ши с-а коборыт ла Аскалон. Аколо а учис трейзечь де оамень, ле-а луат хайнеле ши а дат хайнеле де скимб челор че дезлегасерэ гичитоаря. Ера апринс де мыние ши с-а суит ла каса татэлуй сэу.
20 Ndipo mkazi wa Samsoniyo anamukwatitsa kwa amene anali mnzake womuperekeza pa ukwati paja.
Невастэ-са а фост датэ унуя дин товарэший луй, ку каре ера приетен ел.

< Oweruza 14 >