< Oweruza 14 >

1 Samsoni anapita ku Timna ndipo kumeneko anaonako mtsikana wa Chifilisiti.
USamsoni wasesehlela eThiminathi, wabona owesifazana eThiminathi wamadodakazi amaFilisti.
2 Atabwerera kwawo, anawuza abambo ndi amayi ake kuti, “Ine ndaona mtsikana wa Chifilisiti ku Timna, tsono mukanditengere ameneyo kuti akhale mkazi wanga.”
Wenyuka wabatshela oyise lonina wathi: Ngibone owesifazana eThiminathi wamadodakazi amaFilisti. Ngakho-ke ngithatheleni yena abe ngumkami.
3 Koma abambo ndi amayi ake anayankha kuti, “Kodi palibe mkazi pakati pa abale akowa kapena pakati pa anthu a mtundu wako, kuti iwe upite kukapeza mkazi kwa Afilisti anthu osachita mdulidwe?” Koma Samsoni anawuza abambo ake kuti, “Kanditengereni ameneyu basi, pakuti ndamukonda.”
Kodwa uyise lonina bathi kuye: Kakula owesifazana yini phakathi kwamadodakazi abafowenu loba phakathi kwabo bonke abantu bakithi ukuthi uyethatha umfazi kumaFilisti angasokanga? USamsoni wasesithi kuyise: Ngithathele yena ngoba yena uyathandeka emehlweni ami.
4 (Abambo ndi amayi ake sankadziwa kuti zimenezi zinali zochokera kwa Yehova, pakuti Yehova amafuna powapezera chifukwa Afilistiwo. Nthawi imeneyo nʼkuti Afilisti akulamulira Aisraeli).
Kodwa uyise lonina babengazi ukuthi lokho kuvela eNkosini, ukuthi wayedinga ithuba lokumelana lamaFilisti; ngoba ngalesosikhathi amaFilisti ayebusa phezu kukaIsrayeli.
5 Choncho Samsoni pamodzi ndi abambo ake anapita ku Timna. Akuyandikira minda ya mpesa ya ku Timna, mwadzidzidzi anamva kubuma kwa mkango waungʼono ukubwera kumene kunali iye.
USamsoni wasesehla loyise lonina esiya eThiminathi, bafika ezivinini eThiminathi, khangela-ke, ibhongo lesilwane lambhongela.
6 Tsono Mzimu wa Yehova unafika ndi mphamvu pa Samsoni ndipo ngakhale analibe chida mʼmanja mwake, iye anakadzula mkangowo ngati akukadzula mwana wambuzi. Koma sanawuze abambo kapena amayi ake zimene anachitazo.
UMoya weNkosi wasefika ngamandla phezu kwakhe; walidabula njengodabula izinyane; njalo kwakungelalutho esandleni sakhe; kodwa kabatshelanga oyise lonina lokho akwenzileyo.
7 Kenaka Samsoni anapita kukakambirana ndi mkaziyo, ndipo anamukonda mtsikanayo.
Wasesehla, wakhuluma lowesifazana, njalo wayethandeka emehlweni kaSamsoni.
8 Patapita nthawi, Samsoni anabwerera kukatenga mtsikana uja. Panjira anapatuka kukaona mkango unawupha uja, ndipo anangoona njuchi zili mu mkangowo pamodzi ndi uchi wake.
Lemva kwezinsuku wabuyela ukuyamthatha; waphambuka ukuthi abone isidumbu sesilwane, khangela-ke, kwakulomtshitshi wenyosi loluju esidunjini sesilwane.
9 Tsono anakomberako uchi uja mʼmanja mwake ndi kumapita akudya. Atabwereranso kwa abambo ndi amayi ake, anawapatsako uchiwo ndipo anadya. Koma sanawawuze kuti uchi umenewo anawufula mu mkango wakufa.
Wazithapha ngezandla zakhe, wahamba, ehamba esidla, wafika kuyise lakunina, wabanika, badla. Kodwa kabatshelanga ukuthi wayethaphe uluju esidunjini sesilwane.
10 Tsopano Samsoni anapita ku nyumba kwa mtsikanayo. Ndipo kumeneko Samsoni anakonza phwando monga ankachitira anyamata.
Uyise wasesehla waya kowesifazana, loSamsoni wenza idili khona, ngoba ayesenza njalo amajaha.
11 Makolo a mkwatibwiyo atamuona, anasankha anyamata makumi atatu kuti akhale naye.
Kwasekusithi lapho bembona bathatha abanakwabo abangamatshumi amathathu ukuze babe laye.
12 Samsoni anawawuza kuti, “Bwanji ndikuphereni mwambi. Mukandiwuza tanthauzo lake asanathe masiku asanu ndi awiri aphwandowa, ndidzakupatsani zovala makumi atatu za bafuta ndi zina makumi atatu za tsiku la chikondwerero.
USamsoni wasesithi kibo: Ake ngililibhe ngelibho; uba lingangitshela lona kuhle ensukwini eziyisikhombisa zedili, lilithole, ngizalinika izembatho zelembu elihle ezingamatshumi amathathu lezembatho zokuntshintsha ezingamatshumi amathathu.
13 Koma ngati simutha kundiwuza tanthauzo lake, inuyo mudzandipatsa zovala makumi atatu zabafuta ndi zina za tsiku la chikondwerero.” Iwo anamuyankha kuti, “Tiwuze mwambi wakowo tiwumve.”
Kodwa uba lingelakho ukungitshela, khona lina lizanginika izembatho zelembu elihle ezingamatshumi amathathu lezembatho zokuntshintsha ezingamatshumi amathathu. Basebesithi kuye: Libha ilibho lakho ukuze silizwe.
14 Iye anati, “Chakudya chinatuluka mu chinthu chodya chinzake; ndipo chozuna chinatuluka mu chinthu champhamvu.” Panapita masiku atatu anthuwo akulephera kumasulira mwambiwo.
Wasesithi kubo: Kodlayo kwaphuma ukudla, lakolamandla kwaphuma okumnandi. Kodwa babengelakulichasisa ilibho ensukwini ezintathu.
15 Tsiku lachinayi anthuwo anawuza mkazi wa Samsoni kuti, “Umunyengerere mwamuna wako kuti akuwuze tanthauzo la mwambiwu. Ngati sutero tikutentha iweyo pamodzi ndi nyumba ya abambo ako. Kodi unatiyitana kuti mudzatilande zinthu zathu?”
Kwasekusithi ngosuku lwesikhombisa bathi kumkaSamsoni: Huga umkakho ukuthi asichasisele ilibho, hlezi sikutshise lendlu kayihlo ngomlilo. Lisinxusele ukuthi lisithathele esilakho yini? Akunjalo yini?
16 Kenaka mkazi wa Samsoni anayamba kulira pamaso pake namuwuza kuti, “Inu mumandida ndipo simundikonda. Mwaphera anyamata a mtundu wathu mwambi, koma ine wosandiwuza tanthauzo lake.” Samsoni anamuyankha kuti, “Taona sindinawuze abambo kapena amayi anga, ndiye ndiwuze iweyo?”
UmkaSamsoni wasekhala inyembezi phambi kwakhe wathi: Uyangizonda nje, kawungithandi; uwalibhile ilibho amadodana abantu bakithi, kodwa mina kawungitshelanga. Wasesithi kuye: Khangela ubaba lomama kangibatshelanga, wena-ke ngizakutshela yini?
17 Mkaziyo anamulirira masiku onse asanu ndi awiri aphwandowo. Choncho pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anamuwuza tanthauzo lake popeza amamukakamiza. Ndipo mkaziyo anakawuza abale ake aja tanthauzo la mwambiwo.
Wakhala inyembezi phambi kwakhe insuku eziyisikhombisa beseledili. Kwasekusithi ngosuku lwesikhombisa wamtshela ngoba wamcindezela kakhulu. Wasewatshela amadodana abantu bakibo.
18 Pambuyo pake anthu a mu mzinda aja anamuwuza Samsoni pa tsiku lachisanu ndi chiwiri dzuwa lisanalowe kuti, “Chozuna nʼchiyani choposa uchi? Champhamvu nʼchiyani choposa mkango?” Samsoni anawawuza kuti, “Mukanapanda kutipula ndi ngʼombe yanga yayingʼono, simukanatha kumasulira mwambi wangawu.”
Amadoda omuzi asesithi kuye ngosuku lwesikhombisa ilanga lingakatshoni: Kuyini okumnandi okwedlula uluju? Njalo kuyini okulamandla kulesilwane? Wasesithi kiwo: Uba belingalimanga ngethokazi lami, belingayikulithola ilibho lami.
19 Ndipo Mzimu wa Yehova unafika pa iye mwamphamvu. Choncho anatsikira ku Asikeloni naphako anthu makumi atatu, natenga zovala zawo za tsiku la chikondwerero napereka kwa anthu amene anamasulira mwambi wake. Kenaka anabwerera ku nyumba ya abambo ake ndi mkwiyo waukulu.
UMoya weNkosi wasefika ngamandla phezu kwakhe, wehlela eAshikeloni, watshaya kuwo amadoda angamatshumi amathathu, wathatha izembatho zawo, wanika izembatho zokuntshintsha labo ababechasise ilibho. Intukuthelo yakhe yasivutha wasesenyukela endlini kayise.
20 Ndipo mkazi wa Samsoniyo anamukwatitsa kwa amene anali mnzake womuperekeza pa ukwati paja.
Kodwa umkaSamsoni waba ngowomnakwabo, owayengumngane wakhe.

< Oweruza 14 >