< Oweruza 14 >
1 Samsoni anapita ku Timna ndipo kumeneko anaonako mtsikana wa Chifilisiti.
I HO aku la o Samesona i Timenata, a ike aku la i kekahi wahine ma Timenata, no na kaikamahine a ko Pilisetia.
2 Atabwerera kwawo, anawuza abambo ndi amayi ake kuti, “Ine ndaona mtsikana wa Chifilisiti ku Timna, tsono mukanditengere ameneyo kuti akhale mkazi wanga.”
Pii mai la ia, a hai mai la i kona makuakane, a me kona makuwahine, i mai la, Ua ike au i kekahi wahine ma Timenata, no na kaikamahine a ko Pilisetia; nolaila ea, e kii aku ia ia, i wahine na'u.
3 Koma abambo ndi amayi ake anayankha kuti, “Kodi palibe mkazi pakati pa abale akowa kapena pakati pa anthu a mtundu wako, kuti iwe upite kukapeza mkazi kwa Afilisti anthu osachita mdulidwe?” Koma Samsoni anawuza abambo ake kuti, “Kanditengereni ameneyu basi, pakuti ndamukonda.”
I aku la kona makuakane, a me kona makuwahine ia ia, Aole anei he wahine iwaena o na kaikamahine o kou poe hoahanau, a me kou poe kanaka a pau, i hele aku ai oe, e lawe i wahine no ka poe okipoepoe ole ia o ko Pilisetia? I mai la o Samesona i kona makuakane, E kii aku ia ia na'u, no ka mea, ua pono ia i ko'u mau maka.
4 (Abambo ndi amayi ake sankadziwa kuti zimenezi zinali zochokera kwa Yehova, pakuti Yehova amafuna powapezera chifukwa Afilistiwo. Nthawi imeneyo nʼkuti Afilisti akulamulira Aisraeli).
Aole i ike kona makuakane a me kona makuwahine, na Iehova mai ia mea, no kona imi hala ana no i ko Pilisetia. Ia manawa e noho lanakila ana ko Pilisetia maluna o ka Iseraela.
5 Choncho Samsoni pamodzi ndi abambo ake anapita ku Timna. Akuyandikira minda ya mpesa ya ku Timna, mwadzidzidzi anamva kubuma kwa mkango waungʼono ukubwera kumene kunali iye.
Alaila, iho aku la o Samesona, a me kona makuakane a me kona makuwahine i Timenata, a hiki i na pawaina o Timenata; uwo mai la kekahi liona opiopio, i kona halawai ana me ia.
6 Tsono Mzimu wa Yehova unafika ndi mphamvu pa Samsoni ndipo ngakhale analibe chida mʼmanja mwake, iye anakadzula mkangowo ngati akukadzula mwana wambuzi. Koma sanawuze abambo kapena amayi ake zimene anachitazo.
Kau mai la ka Uhane o Iehova maluna ona, a haehae iho la oia ia ia, e like me ka haehae ana o ke kaokeiki, aohe mea ma kona lima; aole hoi ia i hai aku i kona makuakane, a me kona makuwahine, i ka mea ana i hana'i.
7 Kenaka Samsoni anapita kukakambirana ndi mkaziyo, ndipo anamukonda mtsikanayo.
Iho aku la ia, a kamailio pu iho la me ua wahine la; a ua pono ia i na maka o Samesona.
8 Patapita nthawi, Samsoni anabwerera kukatenga mtsikana uja. Panjira anapatuka kukaona mkango unawupha uja, ndipo anangoona njuchi zili mu mkangowo pamodzi ndi uchi wake.
A mahope iho hoi mai la ia e lawe ia ia, kipa ae la ia e nana i ke kino o ka liona; aia hoi, he poe nalomeli, a me ka meli pu maloko o ke kino o ua liona la.
9 Tsono anakomberako uchi uja mʼmanja mwake ndi kumapita akudya. Atabwereranso kwa abambo ndi amayi ake, anawapatsako uchiwo ndipo anadya. Koma sanawawuze kuti uchi umenewo anawufula mu mkango wakufa.
Lalau aku la kona mau lima ia mea, a i ka hele ana, hele no ia e ai ana, a hiki i kona makuakane, a me kona makuwahine, a haawi aku la ia laua, a ai iho la laua; aole nae ia i hai aku ia laua, i kona lawe ana i ka meli, mailoko aku o ke kino o ka liona.
10 Tsopano Samsoni anapita ku nyumba kwa mtsikanayo. Ndipo kumeneko Samsoni anakonza phwando monga ankachitira anyamata.
Iho aku la kona makuakane i ua wahine la, a malaila i hana'i o Samesona i ahaaina palala; no ka mea, pela i hana'i na kanaka ui.
11 Makolo a mkwatibwiyo atamuona, anasankha anyamata makumi atatu kuti akhale naye.
A ike lakou ia ia, lawe lakou i kanakolu hoa, e noho pu ai me ia.
12 Samsoni anawawuza kuti, “Bwanji ndikuphereni mwambi. Mukandiwuza tanthauzo lake asanathe masiku asanu ndi awiri aphwandowa, ndidzakupatsani zovala makumi atatu za bafuta ndi zina makumi atatu za tsiku la chikondwerero.
I aku la o Samesona ia lakou, E nanenane aku au ia oukou, a ina e koho mai oukou ia ia'u, i keia mau la ehiku o ka ahaaina ana, a loaa pono, alaila, e haawi aku au ia oukou i kanakolu palule, a me na paa kapa he kanakolu.
13 Koma ngati simutha kundiwuza tanthauzo lake, inuyo mudzandipatsa zovala makumi atatu zabafuta ndi zina za tsiku la chikondwerero.” Iwo anamuyankha kuti, “Tiwuze mwambi wakowo tiwumve.”
Aka, ina aole hiki ia oukou ke hai mai ia'u, alaila, na oukou e haawi mai ia'u, i kanakolu palule, a me na paa kapa he kanakolu. I mai la lakou ia ia, E nane mai oe, i lohe makou.
14 Iye anati, “Chakudya chinatuluka mu chinthu chodya chinzake; ndipo chozuna chinatuluka mu chinthu champhamvu.” Panapita masiku atatu anthuwo akulephera kumasulira mwambiwo.
I aku la oia ia lakou, Mailoko mai o ka mea e ai ana i puka mai ai ka ai, a mailoko mai hoi o ka mea ikaika, i loaa mai ai ka ono. A i na la ekolu, aole hiki ia lakou, ke koho mai ia ia i ua nane la.
15 Tsiku lachinayi anthuwo anawuza mkazi wa Samsoni kuti, “Umunyengerere mwamuna wako kuti akuwuze tanthauzo la mwambiwu. Ngati sutero tikutentha iweyo pamodzi ndi nyumba ya abambo ako. Kodi unatiyitana kuti mudzatilande zinthu zathu?”
A i ka hiku o ka la, i ae la lakou i ka wahine a Samesona, E hoowalewale oe i kau kane, i hai mai ai oia ia kakou i ka nane, o puhi auanei makou ia oe, a me ka hale o kou makuakane i ke ahi. Ua kii mai anei oukou ia makou e hoohune ia makou, aole anei?
16 Kenaka mkazi wa Samsoni anayamba kulira pamaso pake namuwuza kuti, “Inu mumandida ndipo simundikonda. Mwaphera anyamata a mtundu wathu mwambi, koma ine wosandiwuza tanthauzo lake.” Samsoni anamuyankha kuti, “Taona sindinawuze abambo kapena amayi anga, ndiye ndiwuze iweyo?”
Uwe iho la ka wahine a Samesona imua ona, i aku la ia ia, Ke hoowahawaha wale mai nei oe ia'u, aole aloha mai ia'u. Ua nanenane mai oe i na keiki a ko'u poe kanaka, aole hoi i hai mai ia'u. I mai la kela ia ia, Aia hoi, aole au i hai aku i ko'u makuakane, a me ko'u makuwahine, a e hai anei au ia oe?
17 Mkaziyo anamulirira masiku onse asanu ndi awiri aphwandowo. Choncho pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anamuwuza tanthauzo lake popeza amamukakamiza. Ndipo mkaziyo anakawuza abale ake aja tanthauzo la mwambiwo.
A ia mau la ehiku o ka lakou ahaaina ana, uwe iho la oia imua ona; a i ka hiku o ka la, hai mai la kela ia ia, no ka mea, koi ikaika loa mai la ia ia; a hai ae la ka wahine i ua nane la i na keiki a kona poe kanaka.
18 Pambuyo pake anthu a mu mzinda aja anamuwuza Samsoni pa tsiku lachisanu ndi chiwiri dzuwa lisanalowe kuti, “Chozuna nʼchiyani choposa uchi? Champhamvu nʼchiyani choposa mkango?” Samsoni anawawuza kuti, “Mukanapanda kutipula ndi ngʼombe yanga yayingʼono, simukanatha kumasulira mwambi wangawu.”
A i ka hiku o ka la, aole i komo ka la, i mai la na kanaka o ke kulanakauhale ia ia, Heaha ka mea i oi aku ka ono mamua o ka meli? a heaha hoi ka mea i oi aku ka ikaika mamua o ka liona? I aku la keia ia lakou, Ina aole oukou i oopalau me ka'u bipi wahine opiopio, ina ua loaa ole ia oukou ka'u nane.
19 Ndipo Mzimu wa Yehova unafika pa iye mwamphamvu. Choncho anatsikira ku Asikeloni naphako anthu makumi atatu, natenga zovala zawo za tsiku la chikondwerero napereka kwa anthu amene anamasulira mwambi wake. Kenaka anabwerera ku nyumba ya abambo ake ndi mkwiyo waukulu.
Kau mai la ka Uhane o Iehova maluna ona, a iho aku la ia i Asekelona, a pepehi iho la i kanakolu kanaka o lakou, a lawe i ko lakou lole, a haawi ae la i paa kapa no ka poe i hai mai i ka nane. Wela iho la kona huhu, a pii aku la ia i ka hale o kona makuakane.
20 Ndipo mkazi wa Samsoniyo anamukwatitsa kwa amene anali mnzake womuperekeza pa ukwati paja.
Lilo ae la ka wahine a Samesona i kona hoa, ana i hoolauna aku ai.