< Oweruza 14 >
1 Samsoni anapita ku Timna ndipo kumeneko anaonako mtsikana wa Chifilisiti.
Ensuite Samson descendit à Thamnatha; et voyant là une femme d’entre les filles des Philistins,
2 Atabwerera kwawo, anawuza abambo ndi amayi ake kuti, “Ine ndaona mtsikana wa Chifilisiti ku Timna, tsono mukanditengere ameneyo kuti akhale mkazi wanga.”
Il monta, et il l’annonça à son père et à sa mère, disant: J’ai vu à Thamnatha une femme d’entre les filles des Philistins, que je vous prie d’accepter pour mon épouse.
3 Koma abambo ndi amayi ake anayankha kuti, “Kodi palibe mkazi pakati pa abale akowa kapena pakati pa anthu a mtundu wako, kuti iwe upite kukapeza mkazi kwa Afilisti anthu osachita mdulidwe?” Koma Samsoni anawuza abambo ake kuti, “Kanditengereni ameneyu basi, pakuti ndamukonda.”
Son père et sa mère lui répondirent: Est-ce qu’il n’y a point de femme parmi les filles de tes frères, et dans tout mon peuple, puisque tu veux prendre une femme d’entre les Philistins qui sont incirconcis? Et Samson dit à son père: Acceptez-la pour moi, parce qu’elle a plu à mes yeux.
4 (Abambo ndi amayi ake sankadziwa kuti zimenezi zinali zochokera kwa Yehova, pakuti Yehova amafuna powapezera chifukwa Afilistiwo. Nthawi imeneyo nʼkuti Afilisti akulamulira Aisraeli).
Mais ses parents ne savaient pas que la chose se faisait par le Seigneur, et qu’il cherchait une occasion contre les Philistins; car en ce temps-là les Philistins dominaient sur Israël.
5 Choncho Samsoni pamodzi ndi abambo ake anapita ku Timna. Akuyandikira minda ya mpesa ya ku Timna, mwadzidzidzi anamva kubuma kwa mkango waungʼono ukubwera kumene kunali iye.
C’est pourquoi Samson descendit avec son père et sa mère à Thamnatha. Et, lorsqu’ils furent arrivés aux vignes de la ville, parut le petit d’un lion furieux et rugissant, et il vint à la rencontre de Samson.
6 Tsono Mzimu wa Yehova unafika ndi mphamvu pa Samsoni ndipo ngakhale analibe chida mʼmanja mwake, iye anakadzula mkangowo ngati akukadzula mwana wambuzi. Koma sanawuze abambo kapena amayi ake zimene anachitazo.
Mais l’Esprit du Seigneur s’empara de Samson, qui déchira le lion comme il aurait mis un chevreau en pièces, n’ayant absolument rien dans la main; et il ne voulut pas le déclarer à son père et à sa mère.
7 Kenaka Samsoni anapita kukakambirana ndi mkaziyo, ndipo anamukonda mtsikanayo.
Et il descendit, et il parla à la femme qui avait plu à ses yeux.
8 Patapita nthawi, Samsoni anabwerera kukatenga mtsikana uja. Panjira anapatuka kukaona mkango unawupha uja, ndipo anangoona njuchi zili mu mkangowo pamodzi ndi uchi wake.
Et, après quelques jours, revenant pour l’épouser, il se détourna pour voir le corps du lion, et voilà qu’un essaim d’abeilles était dans la gueule du lion, et un rayon de miel.
9 Tsono anakomberako uchi uja mʼmanja mwake ndi kumapita akudya. Atabwereranso kwa abambo ndi amayi ake, anawapatsako uchiwo ndipo anadya. Koma sanawawuze kuti uchi umenewo anawufula mu mkango wakufa.
Ayant pris ce rayon dans ses mains, il le mangeait en chemin; et étant arrivé chez son père et sa mère, il leur en donna une partie, qu’eux-mêmes aussi mangèrent; mais cependant il ne voulut pas leur déclarer qu’il avait pris le miel dans la gueule du lion.
10 Tsopano Samsoni anapita ku nyumba kwa mtsikanayo. Ndipo kumeneko Samsoni anakonza phwando monga ankachitira anyamata.
Son père descendit donc chez cette femme, et il fit pour son fils Samson un festin; car c’est ainsi que les jeunes gens avaient coutume de faire.
11 Makolo a mkwatibwiyo atamuona, anasankha anyamata makumi atatu kuti akhale naye.
Or, lorsque les habitants de ce lieu l’eurent vu, ils lui donnèrent trente jeunes hommes pour être avec lui.
12 Samsoni anawawuza kuti, “Bwanji ndikuphereni mwambi. Mukandiwuza tanthauzo lake asanathe masiku asanu ndi awiri aphwandowa, ndidzakupatsani zovala makumi atatu za bafuta ndi zina makumi atatu za tsiku la chikondwerero.
Samson leur dit: Je vous proposerai une énigme; si vous me l’expliquez pendant les sept jours du festin, je vous donnerai trente vêtements de dessous et autant de tuniques;
13 Koma ngati simutha kundiwuza tanthauzo lake, inuyo mudzandipatsa zovala makumi atatu zabafuta ndi zina za tsiku la chikondwerero.” Iwo anamuyankha kuti, “Tiwuze mwambi wakowo tiwumve.”
Mais si vous ne pouvez pas l’expliquer, c’est vous qui me donnerez trente vêtements de dessous et des tuniques en même nombre. Ils lui répondirent: Propose l’énigme afin que nous l’entendions.
14 Iye anati, “Chakudya chinatuluka mu chinthu chodya chinzake; ndipo chozuna chinatuluka mu chinthu champhamvu.” Panapita masiku atatu anthuwo akulephera kumasulira mwambiwo.
Alors Samson leur dit: De celui qui mangeait est sortie une nourriture, et du fort est sorti de la douceur; et ils ne purent point pendant trois jours expliquer l’énigme.
15 Tsiku lachinayi anthuwo anawuza mkazi wa Samsoni kuti, “Umunyengerere mwamuna wako kuti akuwuze tanthauzo la mwambiwu. Ngati sutero tikutentha iweyo pamodzi ndi nyumba ya abambo ako. Kodi unatiyitana kuti mudzatilande zinthu zathu?”
Mais, lorsqu’approchait le septième jour, ils dirent à la femme de Samson: Gagne ton mari par tes caresses, et persuade-lui de te donner la signification de l’énigme; que si tu ne veux pas le faire, nous te brûlerons, toi et la maison de ton père; est-ce que tu ne nous as appelés aux noces que pour nous dépouiller?
16 Kenaka mkazi wa Samsoni anayamba kulira pamaso pake namuwuza kuti, “Inu mumandida ndipo simundikonda. Mwaphera anyamata a mtundu wathu mwambi, koma ine wosandiwuza tanthauzo lake.” Samsoni anamuyankha kuti, “Taona sindinawuze abambo kapena amayi anga, ndiye ndiwuze iweyo?”
Elle répandait des larmes auprès de Samson, et se plaignait, disant: Tu me hais et tu ne m’aimes point; c’est pour cela que tu ne veux pas m’expliquer l’énigme que tu as proposée aux fils de mon peuple. Mais Samson répondit: Je ne l’ai point voulu dire à mon père et à ma mère; et je pourrai te l’expliquer?
17 Mkaziyo anamulirira masiku onse asanu ndi awiri aphwandowo. Choncho pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anamuwuza tanthauzo lake popeza amamukakamiza. Ndipo mkaziyo anakawuza abale ake aja tanthauzo la mwambiwo.
Ainsi, pendant les sept jours du festin elle pleurait devant lui; et enfin le septième jour, comme elle lui était importune, il lui expliqua. Elle aussitôt la fit connaître à ses concitoyens.
18 Pambuyo pake anthu a mu mzinda aja anamuwuza Samsoni pa tsiku lachisanu ndi chiwiri dzuwa lisanalowe kuti, “Chozuna nʼchiyani choposa uchi? Champhamvu nʼchiyani choposa mkango?” Samsoni anawawuza kuti, “Mukanapanda kutipula ndi ngʼombe yanga yayingʼono, simukanatha kumasulira mwambi wangawu.”
Et eux dirent à Samson le septième jour avant le coucher du soleil: Quoi de plus doux que du miel, et de plus fort que le lion? Et Samson leur répondit: Si vous n’aviez pas labouré avec ma génisse, vous n’auriez pas découvert mon énigme.
19 Ndipo Mzimu wa Yehova unafika pa iye mwamphamvu. Choncho anatsikira ku Asikeloni naphako anthu makumi atatu, natenga zovala zawo za tsiku la chikondwerero napereka kwa anthu amene anamasulira mwambi wake. Kenaka anabwerera ku nyumba ya abambo ake ndi mkwiyo waukulu.
C’est pourquoi l’esprit du Seigneur s’empara de Samson, et il descendit à Ascalon: et là il tua trente hommes dont il donna les vêtements qu’il leur avait pris à ceux qui avaient expliqué l’énigme. Et étant très irrité il monta à la maison de son père.
20 Ndipo mkazi wa Samsoniyo anamukwatitsa kwa amene anali mnzake womuperekeza pa ukwati paja.
Or, sa femme prit pour mari un de ses amis, un de ceux qui l’avaient accompagné à ses noces.