< Oweruza 14 >

1 Samsoni anapita ku Timna ndipo kumeneko anaonako mtsikana wa Chifilisiti.
Et Samson descendit à Thimna; et il vit à Thimna une femme d’entre les filles des Philistins.
2 Atabwerera kwawo, anawuza abambo ndi amayi ake kuti, “Ine ndaona mtsikana wa Chifilisiti ku Timna, tsono mukanditengere ameneyo kuti akhale mkazi wanga.”
Et il remonta et le raconta à son père et à sa mère, et dit: J’ai vu à Thimna une femme d’entre les filles des Philistins; et maintenant, prenez-la-moi pour femme.
3 Koma abambo ndi amayi ake anayankha kuti, “Kodi palibe mkazi pakati pa abale akowa kapena pakati pa anthu a mtundu wako, kuti iwe upite kukapeza mkazi kwa Afilisti anthu osachita mdulidwe?” Koma Samsoni anawuza abambo ake kuti, “Kanditengereni ameneyu basi, pakuti ndamukonda.”
Et son père et sa mère lui dirent: N’y a-t-il pas de femme parmi les filles de tes frères, et dans tout mon peuple, que tu ailles prendre une femme d’entre les Philistins, les incirconcis? Et Samson dit à son père: Prends celle-là pour moi, car elle plaît à mes yeux.
4 (Abambo ndi amayi ake sankadziwa kuti zimenezi zinali zochokera kwa Yehova, pakuti Yehova amafuna powapezera chifukwa Afilistiwo. Nthawi imeneyo nʼkuti Afilisti akulamulira Aisraeli).
Et son père et sa mère ne savaient pas que cela venait de l’Éternel; car [Samson] cherchait une occasion de la part des Philistins. Or en ce temps-là les Philistins dominaient sur Israël.
5 Choncho Samsoni pamodzi ndi abambo ake anapita ku Timna. Akuyandikira minda ya mpesa ya ku Timna, mwadzidzidzi anamva kubuma kwa mkango waungʼono ukubwera kumene kunali iye.
Et Samson descendit à Thimna avec son père et sa mère; et ils arrivèrent jusqu’aux vignes de Thimna. Et voici, un jeune lion rugissant [vint] à sa rencontre.
6 Tsono Mzimu wa Yehova unafika ndi mphamvu pa Samsoni ndipo ngakhale analibe chida mʼmanja mwake, iye anakadzula mkangowo ngati akukadzula mwana wambuzi. Koma sanawuze abambo kapena amayi ake zimene anachitazo.
Et l’Esprit de l’Éternel le saisit: et il le déchira, comme on déchire un chevreau, quoiqu’il n’ait rien en sa main; et il ne déclara point à son père ni à sa mère ce qu’il avait fait.
7 Kenaka Samsoni anapita kukakambirana ndi mkaziyo, ndipo anamukonda mtsikanayo.
Et il descendit, et parla à la femme, et elle plut aux yeux de Samson.
8 Patapita nthawi, Samsoni anabwerera kukatenga mtsikana uja. Panjira anapatuka kukaona mkango unawupha uja, ndipo anangoona njuchi zili mu mkangowo pamodzi ndi uchi wake.
Et il retourna quelque temps après pour la prendre, et se détourna pour voir le cadavre du lion; et voici, il y avait dans le corps du lion un essaim d’abeilles, et du miel;
9 Tsono anakomberako uchi uja mʼmanja mwake ndi kumapita akudya. Atabwereranso kwa abambo ndi amayi ake, anawapatsako uchiwo ndipo anadya. Koma sanawawuze kuti uchi umenewo anawufula mu mkango wakufa.
et il en prit dans ses mains, et s’en alla, mangeant en chemin; et il alla vers son père et vers sa mère, et leur en donna, et ils en mangèrent; mais il ne leur raconta pas qu’il avait tiré le miel du corps du lion.
10 Tsopano Samsoni anapita ku nyumba kwa mtsikanayo. Ndipo kumeneko Samsoni anakonza phwando monga ankachitira anyamata.
Et son père descendit vers la femme, et Samson fit là un festin; car c’est ainsi que les jeunes gens avaient l’habitude de faire.
11 Makolo a mkwatibwiyo atamuona, anasankha anyamata makumi atatu kuti akhale naye.
Et il arriva que, quand ils le virent, ils prirent 30 compagnons, et ils furent avec lui.
12 Samsoni anawawuza kuti, “Bwanji ndikuphereni mwambi. Mukandiwuza tanthauzo lake asanathe masiku asanu ndi awiri aphwandowa, ndidzakupatsani zovala makumi atatu za bafuta ndi zina makumi atatu za tsiku la chikondwerero.
Et Samson leur dit: Je vous proposerai, s’il vous plaît, une énigme; si vous me l’ expliquez dans les sept jours du festin et si vous la trouvez, je vous donnerai 30 chemises, et 30 vêtements de rechange.
13 Koma ngati simutha kundiwuza tanthauzo lake, inuyo mudzandipatsa zovala makumi atatu zabafuta ndi zina za tsiku la chikondwerero.” Iwo anamuyankha kuti, “Tiwuze mwambi wakowo tiwumve.”
Mais si vous ne pouvez pas me l’expliquer, c’est vous qui me donnerez 30 chemises, et 30 vêtements de rechange. Et ils lui dirent: Propose ton énigme, et nous l’entendrons.
14 Iye anati, “Chakudya chinatuluka mu chinthu chodya chinzake; ndipo chozuna chinatuluka mu chinthu champhamvu.” Panapita masiku atatu anthuwo akulephera kumasulira mwambiwo.
Et il leur dit: De celui qui mange est sorti le manger, et du fort est sortie la douceur. Et pendant trois jours ils ne purent expliquer l’énigme.
15 Tsiku lachinayi anthuwo anawuza mkazi wa Samsoni kuti, “Umunyengerere mwamuna wako kuti akuwuze tanthauzo la mwambiwu. Ngati sutero tikutentha iweyo pamodzi ndi nyumba ya abambo ako. Kodi unatiyitana kuti mudzatilande zinthu zathu?”
Et il arriva, le septième jour, qu’ils dirent à la femme de Samson: Persuade ton mari, et il nous expliquera l’énigme, de peur que nous ne te brûlions au feu, toi et la maison de ton père. C’est pour nous dépouiller que vous nous avez appelés, n’est-ce pas?
16 Kenaka mkazi wa Samsoni anayamba kulira pamaso pake namuwuza kuti, “Inu mumandida ndipo simundikonda. Mwaphera anyamata a mtundu wathu mwambi, koma ine wosandiwuza tanthauzo lake.” Samsoni anamuyankha kuti, “Taona sindinawuze abambo kapena amayi anga, ndiye ndiwuze iweyo?”
Et la femme de Samson pleura auprès de lui, et dit: Tu n’as pour moi que de la haine, et tu ne m’aimes pas; tu as proposé une énigme aux fils de mon peuple, et tu ne me l’as pas expliquée. Et il lui dit: Voici, je ne l’ai pas expliquée à mon père et à ma mère, et je te l’expliquerais à toi?
17 Mkaziyo anamulirira masiku onse asanu ndi awiri aphwandowo. Choncho pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anamuwuza tanthauzo lake popeza amamukakamiza. Ndipo mkaziyo anakawuza abale ake aja tanthauzo la mwambiwo.
Et elle pleura auprès de lui pendant les sept jours qu’ils eurent le festin; et il arriva, le septième jour, qu’il la lui expliqua, parce qu’elle le tourmentait; et elle expliqua l’énigme aux fils de son peuple.
18 Pambuyo pake anthu a mu mzinda aja anamuwuza Samsoni pa tsiku lachisanu ndi chiwiri dzuwa lisanalowe kuti, “Chozuna nʼchiyani choposa uchi? Champhamvu nʼchiyani choposa mkango?” Samsoni anawawuza kuti, “Mukanapanda kutipula ndi ngʼombe yanga yayingʼono, simukanatha kumasulira mwambi wangawu.”
Et le septième jour, avant que le soleil se couche, les hommes de la ville lui dirent: Qu’y a-t-il de plus doux que le miel, et qu’y a-t-il de plus fort que le lion? Et il leur dit: Si vous n’aviez pas labouré avec ma génisse, vous n’auriez pas trouvé mon énigme.
19 Ndipo Mzimu wa Yehova unafika pa iye mwamphamvu. Choncho anatsikira ku Asikeloni naphako anthu makumi atatu, natenga zovala zawo za tsiku la chikondwerero napereka kwa anthu amene anamasulira mwambi wake. Kenaka anabwerera ku nyumba ya abambo ake ndi mkwiyo waukulu.
Et l’Esprit de l’Éternel le saisit; et il descendit à Askalon, et en tua 30 hommes, et prit leurs dépouilles, et donna les vêtements de rechange à ceux qui avaient expliqué l’énigme. Et sa colère s’embrasa, et il monta à la maison de son père.
20 Ndipo mkazi wa Samsoniyo anamukwatitsa kwa amene anali mnzake womuperekeza pa ukwati paja.
Et la femme de Samson fut [donnée] à son compagnon, dont il avait fait son ami.

< Oweruza 14 >