< Oweruza 14 >
1 Samsoni anapita ku Timna ndipo kumeneko anaonako mtsikana wa Chifilisiti.
И Самсон слезе в Тамнат и видя в Тамнат една жена от филистимските дъщери.
2 Atabwerera kwawo, anawuza abambo ndi amayi ake kuti, “Ine ndaona mtsikana wa Chifilisiti ku Timna, tsono mukanditengere ameneyo kuti akhale mkazi wanga.”
И отиде да извести на баща си и на майка си, казвайки: Видях в Тамнат една жена от филистимските дъщери; сега, прочее, вземете ми я за жена.
3 Koma abambo ndi amayi ake anayankha kuti, “Kodi palibe mkazi pakati pa abale akowa kapena pakati pa anthu a mtundu wako, kuti iwe upite kukapeza mkazi kwa Afilisti anthu osachita mdulidwe?” Koma Samsoni anawuza abambo ake kuti, “Kanditengereni ameneyu basi, pakuti ndamukonda.”
А баща му и майка му му рекоха: Няма ли някоя жена между дъщерите на братята ти, или между всичките ми люде, та отиваш да вземеш жена от необрязаните филистимци? А Самсон рече на баща си: Нея ми вземи; защото тя ми е угодна.
4 (Abambo ndi amayi ake sankadziwa kuti zimenezi zinali zochokera kwa Yehova, pakuti Yehova amafuna powapezera chifukwa Afilistiwo. Nthawi imeneyo nʼkuti Afilisti akulamulira Aisraeli).
Но баща му и майка му не знаеха, че това беше от Господа, и че той търсеше причина против филистимците; защото по онова време филистимците владееха над Израиля.
5 Choncho Samsoni pamodzi ndi abambo ake anapita ku Timna. Akuyandikira minda ya mpesa ya ku Timna, mwadzidzidzi anamva kubuma kwa mkango waungʼono ukubwera kumene kunali iye.
Тогава Самсон слезе с баща си в Тамнат; а като стигнаха до тамнатските лозя, ето, едно лъвче ревеше против него.
6 Tsono Mzimu wa Yehova unafika ndi mphamvu pa Samsoni ndipo ngakhale analibe chida mʼmanja mwake, iye anakadzula mkangowo ngati akukadzula mwana wambuzi. Koma sanawuze abambo kapena amayi ake zimene anachitazo.
И Господният Дух дойде със сила на него; и той го разкъса както би разкъсал яре, и то без да има нищо в ръката си; но не каза на баща си и на майка си що бе сторил.
7 Kenaka Samsoni anapita kukakambirana ndi mkaziyo, ndipo anamukonda mtsikanayo.
И слезе та говори с жената: и тя бе угодна на Самсона.
8 Patapita nthawi, Samsoni anabwerera kukatenga mtsikana uja. Panjira anapatuka kukaona mkango unawupha uja, ndipo anangoona njuchi zili mu mkangowo pamodzi ndi uchi wake.
И след няколко дни, като се върна да я вземе, той се отби от пътя, за да види трупа на лъва; и ето рой пчели в лъвовия труп, и мед.
9 Tsono anakomberako uchi uja mʼmanja mwake ndi kumapita akudya. Atabwereranso kwa abambo ndi amayi ake, anawapatsako uchiwo ndipo anadya. Koma sanawawuze kuti uchi umenewo anawufula mu mkango wakufa.
И взе от него в ръцете си, па вървеше и ядеше, и като застигна баща си и майка си даде и на тях, та ядоха; но не им каза, че беше взел мед от лъвовия труп.
10 Tsopano Samsoni anapita ku nyumba kwa mtsikanayo. Ndipo kumeneko Samsoni anakonza phwando monga ankachitira anyamata.
И баща му слезе при жената; и там Самсон направи угощение, защото така правеха момците.
11 Makolo a mkwatibwiyo atamuona, anasankha anyamata makumi atatu kuti akhale naye.
И като го видяха филистимците доведоха тридесет другари, за да бъдат с него.
12 Samsoni anawawuza kuti, “Bwanji ndikuphereni mwambi. Mukandiwuza tanthauzo lake asanathe masiku asanu ndi awiri aphwandowa, ndidzakupatsani zovala makumi atatu za bafuta ndi zina makumi atatu za tsiku la chikondwerero.
И рече им Самсон: Сега ще ви предложа една гатанка. Ако можете да ми я отгатнете през седемте дена на угощението, и да я намерите, тогава аз ще ви дам тридесет ленени ризи и тридесет дрехи за премяна;
13 Koma ngati simutha kundiwuza tanthauzo lake, inuyo mudzandipatsa zovala makumi atatu zabafuta ndi zina za tsiku la chikondwerero.” Iwo anamuyankha kuti, “Tiwuze mwambi wakowo tiwumve.”
но ако не можете да ми я отгатнете, тогава вие ще ми дадете тридесет ленени ризи и тридесет дрехи за премяна. И те му казаха: Предложи гатанката си, за да я чуем.
14 Iye anati, “Chakudya chinatuluka mu chinthu chodya chinzake; ndipo chozuna chinatuluka mu chinthu champhamvu.” Panapita masiku atatu anthuwo akulephera kumasulira mwambiwo.
И той им рече: - От ядящия излезе ястие, И от силния излезе сладост. А до третия ден те не можаха да отгатнат гатанката.
15 Tsiku lachinayi anthuwo anawuza mkazi wa Samsoni kuti, “Umunyengerere mwamuna wako kuti akuwuze tanthauzo la mwambiwu. Ngati sutero tikutentha iweyo pamodzi ndi nyumba ya abambo ako. Kodi unatiyitana kuti mudzatilande zinthu zathu?”
Тогава на седмия ден казаха на Самсоновата жена: Предумай мъжа си да ни каже гатанката, за да не би да изгорим тебе и бащиния ти дом с огън. За това ли ни поканихте, да ни оберете? не е ли така?
16 Kenaka mkazi wa Samsoni anayamba kulira pamaso pake namuwuza kuti, “Inu mumandida ndipo simundikonda. Mwaphera anyamata a mtundu wathu mwambi, koma ine wosandiwuza tanthauzo lake.” Samsoni anamuyankha kuti, “Taona sindinawuze abambo kapena amayi anga, ndiye ndiwuze iweyo?”
И тъй, жената на Самсона заплака пред него, като каза: Ти само ме мразиш, и не ме обичаш; предложил си гатанка на ония, които са от людете, ми, а на мене не си я казал. А той й рече: Ето, нито на баща си и на майка си не съм я казал, та на тебе ли ща я кажа?
17 Mkaziyo anamulirira masiku onse asanu ndi awiri aphwandowo. Choncho pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anamuwuza tanthauzo lake popeza amamukakamiza. Ndipo mkaziyo anakawuza abale ake aja tanthauzo la mwambiwo.
Но тя плачеше пред него през седемте дена, в които ставаше угощението им; а на седмия ден й я откри, защото му бе много досадила и тя каза гатанката на мъжете от людете си.
18 Pambuyo pake anthu a mu mzinda aja anamuwuza Samsoni pa tsiku lachisanu ndi chiwiri dzuwa lisanalowe kuti, “Chozuna nʼchiyani choposa uchi? Champhamvu nʼchiyani choposa mkango?” Samsoni anawawuza kuti, “Mukanapanda kutipula ndi ngʼombe yanga yayingʼono, simukanatha kumasulira mwambi wangawu.”
Тогава на седмия ден, преди да зайде слънцето, градските мъже му рекоха: - Що е по-сладко от мед? И що е по-яко от лъв? А той им рече: Ако не бяхте орали с моята юница, не бихте отгатнали гатанката ми.
19 Ndipo Mzimu wa Yehova unafika pa iye mwamphamvu. Choncho anatsikira ku Asikeloni naphako anthu makumi atatu, natenga zovala zawo za tsiku la chikondwerero napereka kwa anthu amene anamasulira mwambi wake. Kenaka anabwerera ku nyumba ya abambo ake ndi mkwiyo waukulu.
И Господният Дух дойде със сила на него; и той слезе в Аскалон та изби тридесет мъже от тях, и като взе облеклата им, даде премените на ония, които отгатнаха гатанката. И гневът му пламна, и отиде в бащиния си дом.
20 Ndipo mkazi wa Samsoniyo anamukwatitsa kwa amene anali mnzake womuperekeza pa ukwati paja.
А Самсоновата жена се омъжи за другаря му, който му беше приятел.