< Oweruza 13 >

1 Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova, kotero Yehova anawapereka mʼmanja mwa Afilisti kwa zaka makumi anayi.
А синови Израиљеви опет чинише што је зло пред Господом, и Господ их даде у руке Филистејима за четрдесет година.
2 Ku Zora kunali munthu wina dzina lake Manowa, wochokera ku fuko la Dani. Mkazi wake analibe ana popeza anali wosabereka.
А беше један човек од Сараје од племена синова Данових, по имену Маноје, и жена му беше нероткиња, и не рађаше.
3 Mngelo wa Yehova anaonekera mkaziyo ndipo anati, “Ndinu wosabereka ndipo mulibedi mwana, komabe mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna.
Тој жени јави се анђео Господњи и рече јој: Гле, ти си сад нероткиња, и ниси рађала; али ћеш затруднети и родићеш сина.
4 Tsono mudzisamale bwino, osamwa vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa ndiponso musamadye chakudya chilichonse chodetsedwa,
Него сада чувај се да не пијеш вино ни силовито пиће, и да не једеш ништа нечисто.
5 chifukwa mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna. Mwanayo akadzabadwa lumo lisadzapite pa mutu chifukwa mnyamatayo adzakhala Mnaziri, ndiye kuti wopatulika kwa Mulungu kuyambira pa nthawi imene adzakhale ali mʼchiberekero. Ndipo adzayamba ntchito yopulumutsa Israeli mʼmanja mwa Afilisti.”
Јер гле, затруднећеш, и родићеш сина, и бритва да не пређе по његовој глави, јер ће дете бити назиреј Божји од утробе материне, и он ће почети избављати Израиља из руку филистејских.
6 Kenaka mayiyo anapita kukawuza mwamuna wake kuti, “Munthu wa Mulungu anabwera kwa ine, ndipo maonekedwe ake anali ngati mngelo wa Mulungu, maonekedwe woopsa kwambiri. Ine sindinamufunse kumene amachokera, ndipo iyeyo sanandiwuzenso dzina lake.
И жена дође и рече мужу свом говорећи: Човек Божји дође к мени, и лице му беше као лице анђела Божјег, врло страшно; али га не запитах одакле је, нити ми он каза своје име.
7 Koma anandiwuza kuti, ‘Mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna. Choncho musamamwe vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa, musamadye chakudya chilichonse choyipitsidwa chifukwa mwanayo adzakhala Mnaziri, wopatulika kwa Mulungu kuyambira pa nthawi imene adzakhale ali mʼchiberekero mpaka tsiku la kufa kwake.’”
Него ми рече: Гле, ти ћеш затруднети, и родићеш сина; зато сада не пиј вино ни силовито пиће и не једи ништа нечисто; јер ће дете бити назиреј Божји од утробе материне па до смрти.
8 Kenaka Manowa anapemphera kwa Yehova kuti, “Chonde Ambuye, lolani munthu wa Mulungu amene munamutuma abwerenso kwa ife kuti adzatiphunzitse zochita ndi mwanayo akadzabadwa.”
Тада се Маноје помоли Господу и рече: О Господе! Нека опет дође к нама човек Божји, ког си слао, да нас научи шта ћемо чинити са дететом, кад се роди.
9 Mulungu anamva pemphero la Manowa, ndipo mngelo wa Mulungu anabweranso kwa mkaziyo nthawi imene anali ku munda, koma Manowa mwamuna wake sanali naye.
И услиши Господ глас Манојев; и дође опет анђео Господњи к жени кад сеђаше у пољу; а Маноје муж њен не беше код ње.
10 Tsono mkaziyo anathamanga kukawuza mwamuna wake kuti, “Wandionekeranso munthu uja amene anabwera kwa ine tsiku lija.”
Тада жена брже отрча и јави мужу свом говорећи му: Ево, јави ми се онај човек, који ми је пре долазио.
11 Choncho Manowa ananyamuka namutsatira mkazi wake. Atafika kwa munthuyo anamufunsa kuti, “Kodi ndinu munayankhula ndi mkazi wanga?” Iye anayankha kuti, “Ndine.”
А Маноје уставши пође са женом својом; и кад дође к човеку, рече му: Јеси ли ти онај човек што је говорио овој жени? Он одговори: Јесам.
12 Kenaka Manowa anafunsa kuti, “Tiyerekeze kuti mawu anuwa akwaniritsidwadi, ndiye mwanayu azidzakhala bwanji ndipo azidzachita chiyani?”
А Маноје рече: Кад буде шта си казао, како ће бити правило за дете и шта ће чинити с њим?
13 Ndipo mngelo wa Yehova uja anamuyankha kuti, “Zonse zimene ndinawawuza akazi anuwa asamale ndipo adzazichitedi.
А анђео Господњи рече Маноју: Жена нека се чува од свега што сам јој казао.
14 Asadzadye chilichonse chochokera ku mphesa. Asadzamwe vinyo kapena choledzeretsa chilichonse, ngakhale kudya chakudya chilichonse chodetsedwa. Zonse zimene ndinawalamula azisunge bwino.”
Нека не једе ништа што долази с винове лозе, и вино ни силовито пиће нека не пије, и ништа нечисто нека не једе. Шта сам јој заповедио све нека држи.
15 Manowa anamuwuza mngelo wa Yehova uja kuti, “Chonde dikirani pangʼono, timati tikukonzereni mwana wambuzi.”
Тада рече Маноје анђелу Господњем: Ради бисмо те уставити да ти зготовимо јаре,
16 Mngelo wa Yehova anayankha kuti, “Ngakhale mukundidikiritsa, ine sindidya chakudya chanu. Koma ngati mukonze nsembe yopsereza iperekeni kwa Yehova.” (Manowa nʼkuti asakudziwa kuti munthuyo anali mngelo wa Mulungu).
А анђео Господњи одговори Маноју: Да ме и уставиш, нећу јести твоје јело; него ако хоћеш зготови жртву паљеницу, принеси је Господу. Јер Маноје није знао да је анђео Господњи.
17 Tsono Manowa anapempha mngelo wa Yehova kuti, “Chonde tidziwitseni dzina lanu kuti zikadzachitika zimene mwanenazi ife tidzakulemekezeni?”
Опет рече Маноје анђелу Господњем: Како ти је име? Да ти захвалимо кад се збуде шта си рекао.
18 Iye anayankha kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukufunsa dzina langa? Dzina laketu ndi lodabwitsa.”
А анђео Господњи одговори му: Што питаш за име моје? Чудно је.
19 Ndipo Manowa anatenga mwana wambuzi pamodzi ndi chopereka cha chakudya nakapereka nsembe pa thanthwe kwa Yehova ndipo Yehova anachita zodabwitsa kwa Manowa ndi mkazi wake akuona.
Тада Маноје узе јаре и дар, и принесе Господу на стени; а анђео учини чудо пред Маном и женом његовом;
20 Pamene malawi a moto amakwera kumwamba kuchoka pa guwa, mngelo wa Yehova uja anakwera kumwamba mʼmalawi a motowo Manowa ndi mkazi wake akuona. Tsono anadzigwetsa pansi naweramitsa mitu yawo pansi.
Јер кад се подиже пламен с олтара к небу, анђео Господњи подиже се у пламену с олтара; а Маноје и жена његова видећи то падоше ничице на земљу;
21 Mngelo wa Yehova uja sanaonekerenso kwa Manowa ndi mkazi wake. Choncho Manowa anazindikira kuti anali mngelo wa Yehova.
А анђео се Господњи не јави више Маноју ни жени његовој. Тада Маноје разуме да је анђео Господњи.
22 Iye anawuza mkazi wake kuti, “Ife tifa basi pakuti taona Mulungu!”
И рече Маноје жени својој: Зацело ћемо умрети, јер видесмо Бога.
23 Koma mkazi wake anamuyankha kuti, “Yehova akanafuna kutipha sakanayilandira nsembe yathu yopsereza ndi chopereka chathu chachakudya chija, ndipo sakanationetsanso zinthu zonsezi kapena kutiwuza zinthu ngati zimenezi nthawi ino.”
А жена му рече: Кад би хтео Бог да нас убије, не би примио из наших руку жртву паљеницу ни дар, нити би нам показао све ово, нити би нам сад објавио такве ствари.
24 Motero mkaziyo anabereka mwana wa mwamuna, namutcha dzina lake Samsoni. Iye anakula ndipo Yehova anamudalitsa.
И тако та жена роди сина, и наде му име Самсон; и дете одрасте, и Господ га благослови.
25 Mzimu wa Yehova unayamba kumulimbikitsa pamene ankakhala ku misasa ya anthu a fuko la Dani, malo amene anali pakati pa Zora ndi Esitaoli.
И дух Господњи поче ходити с њим по логору Дановом, између Сараје и Естаола.

< Oweruza 13 >