< Oweruza 13 >

1 Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova, kotero Yehova anawapereka mʼmanja mwa Afilisti kwa zaka makumi anayi.
Abantwana bakoIsrayeli babuya-ke benza okubi emehlweni eNkosi. INkosi yasibanikela esandleni samaFilisti iminyaka engamatshumi amane.
2 Ku Zora kunali munthu wina dzina lake Manowa, wochokera ku fuko la Dani. Mkazi wake analibe ana popeza anali wosabereka.
Kwakukhona-ke umuntu othile weZora, owosendo lwakoDani, obizo lakhe lalinguManowa; lomkakhe wayeyinyumba engazali.
3 Mngelo wa Yehova anaonekera mkaziyo ndipo anati, “Ndinu wosabereka ndipo mulibedi mwana, komabe mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna.
Ingilosi yeNkosi yasibonakala kowesifazana yathi kuye: Khangela-ke, uyinyumba, kawuzali, kodwa uzathatha isisu uzale indodana.
4 Tsono mudzisamale bwino, osamwa vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa ndiponso musamadye chakudya chilichonse chodetsedwa,
Ngakho-ke ake uqaphelise, unganathi wayini lokunathwayo okulamandla, ungadli lalutho olungcolileyo,
5 chifukwa mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna. Mwanayo akadzabadwa lumo lisadzapite pa mutu chifukwa mnyamatayo adzakhala Mnaziri, ndiye kuti wopatulika kwa Mulungu kuyambira pa nthawi imene adzakhale ali mʼchiberekero. Ndipo adzayamba ntchito yopulumutsa Israeli mʼmanja mwa Afilisti.”
ngoba khangela, uzathatha isisu uzale indodana. Impuco kayiyikudlula ekhanda layo, ngoba umfana uzakuba ngumNaziri kaNkulunkulu kusukela esizalweni; yena uzaqala ukusindisa uIsrayeli esandleni samaFilisti.
6 Kenaka mayiyo anapita kukawuza mwamuna wake kuti, “Munthu wa Mulungu anabwera kwa ine, ndipo maonekedwe ake anali ngati mngelo wa Mulungu, maonekedwe woopsa kwambiri. Ine sindinamufunse kumene amachokera, ndipo iyeyo sanandiwuzenso dzina lake.
Owesifazana wasesiza wabikela indoda yakhe esithi: Kufikile kimi umuntu kaNkulunkulu, ukubonakala kwakhe kwakunjengokubonakala kwengilosi kaNkulunkulu, kusesabeka kakhulu; kodwa kangimbuzanga ukuthi uvela ngaphi, futhi kangitshelanga ibizo lakhe.
7 Koma anandiwuza kuti, ‘Mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna. Choncho musamamwe vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa, musamadye chakudya chilichonse choyipitsidwa chifukwa mwanayo adzakhala Mnaziri, wopatulika kwa Mulungu kuyambira pa nthawi imene adzakhale ali mʼchiberekero mpaka tsiku la kufa kwake.’”
Kodwa uthe kimi: Khangela, uzathatha isisu, uzale indodana; khathesi-ke unganathi wayini lokunathwayo okulamandla, ungadli lalutho olungcolileyo, ngoba umfana uzakuba ngumNaziri kaNkulunkulu kusukela esizalweni kuze kube sosukwini lokufa kwakhe.
8 Kenaka Manowa anapemphera kwa Yehova kuti, “Chonde Ambuye, lolani munthu wa Mulungu amene munamutuma abwerenso kwa ife kuti adzatiphunzitse zochita ndi mwanayo akadzabadwa.”
UManowa waseyincenga iNkosi wathi: Hawu Nkosi yami, umuntu kaNkulunkulu omthumileyo ake abuye futhi kithi, asifundise ukuthi sizakwenza njani emfaneni ozazalwa.
9 Mulungu anamva pemphero la Manowa, ndipo mngelo wa Mulungu anabweranso kwa mkaziyo nthawi imene anali ku munda, koma Manowa mwamuna wake sanali naye.
UNkulunkulu waselizwa ilizwi likaManowa, lengilosi kaNkulunkulu yafika futhi kowesifazana ehlezi egangeni; kodwa uManowa umkakhe wayengelaye.
10 Tsono mkaziyo anathamanga kukawuza mwamuna wake kuti, “Wandionekeranso munthu uja amene anabwera kwa ine tsiku lija.”
Owesifazana wasehaluzela wagijima wabikela umkakhe wathi: Khangela, lowomuntu ubonakele kimi owafika kimi mhlalokhuyana.
11 Choncho Manowa ananyamuka namutsatira mkazi wake. Atafika kwa munthuyo anamufunsa kuti, “Kodi ndinu munayankhula ndi mkazi wanga?” Iye anayankha kuti, “Ndine.”
UManowa wasesukuma walandela umkakhe, wafika kulowomuntu wathi kuye: Unguye yini lowomuntu owakhuluma kulowesifazana? Wasesithi: Nginguye.
12 Kenaka Manowa anafunsa kuti, “Tiyerekeze kuti mawu anuwa akwaniritsidwadi, ndiye mwanayu azidzakhala bwanji ndipo azidzachita chiyani?”
UManowa wasesithi: Kaweze-ke amazwi akho; izakuba yini indlela yomfana, lomsebenzi wakhe?
13 Ndipo mngelo wa Yehova uja anamuyankha kuti, “Zonse zimene ndinawawuza akazi anuwa asamale ndipo adzazichitedi.
Ingilosi yeNkosi yasisithi kuManowa: Kukho konke engakutshoyo kowesifazana akuqaphelise;
14 Asadzadye chilichonse chochokera ku mphesa. Asadzamwe vinyo kapena choledzeretsa chilichonse, ngakhale kudya chakudya chilichonse chodetsedwa. Zonse zimene ndinawalamula azisunge bwino.”
angadli okolutho oluphuma evinini lewayini, anganathi wayini lokunathwayo okulamandla, angadli lutho olungcolileyo; konke engamlaya khona akugcine.
15 Manowa anamuwuza mngelo wa Yehova uja kuti, “Chonde dikirani pangʼono, timati tikukonzereni mwana wambuzi.”
UManowa wasesithi engilosini yeNkosi: Ake sikubambelele, silungise phambi kwakho izinyane lembuzi.
16 Mngelo wa Yehova anayankha kuti, “Ngakhale mukundidikiritsa, ine sindidya chakudya chanu. Koma ngati mukonze nsembe yopsereza iperekeni kwa Yehova.” (Manowa nʼkuti asakudziwa kuti munthuyo anali mngelo wa Mulungu).
Ingilosi yeNkosi yasisithi kuManowa: Uba ungibambelela, kangiyikudla okwesinkwa sakho; njalo uba ulungisa umnikelo wokutshiswa, unikele eNkosini. Ngoba uManowa wayengazi ukuthi yayiyingilosi yeNkosi.
17 Tsono Manowa anapempha mngelo wa Yehova kuti, “Chonde tidziwitseni dzina lanu kuti zikadzachitika zimene mwanenazi ife tidzakulemekezeni?”
UManowa wasesithi kuyo ingilosi yeNkosi: Ungubani ibizo lakho, ukuze kuthi lapho amazwi akho esiza sikuhloniphe.
18 Iye anayankha kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukufunsa dzina langa? Dzina laketu ndi lodabwitsa.”
Ingilosi yeNkosi yasisithi kuye: Ubuzelani kanje ngebizo lami lokhu liyamangalisa?
19 Ndipo Manowa anatenga mwana wambuzi pamodzi ndi chopereka cha chakudya nakapereka nsembe pa thanthwe kwa Yehova ndipo Yehova anachita zodabwitsa kwa Manowa ndi mkazi wake akuona.
UManowa wasethatha izinyane lembuzi lomnikelo wokudla, wakunikela eNkosini phezu kwedwala, yasisenza ngokumangalisayo, njalo uManowa lomkakhe bekhangele.
20 Pamene malawi a moto amakwera kumwamba kuchoka pa guwa, mngelo wa Yehova uja anakwera kumwamba mʼmalawi a motowo Manowa ndi mkazi wake akuona. Tsono anadzigwetsa pansi naweramitsa mitu yawo pansi.
Kwasekusithi lapho ilangabi lisenyuka elathini liqonde emazulwini, ingilosi yeNkosi yenyuka ngelangabi lelathi, uManowa lomkakhe bekhangele, bathi mbo ngobuso babo emhlabathini.
21 Mngelo wa Yehova uja sanaonekerenso kwa Manowa ndi mkazi wake. Choncho Manowa anazindikira kuti anali mngelo wa Yehova.
Kodwa ingilosi yeNkosi kayiphindanga isabonakala kuManowa lomkakhe. Khona uManowa wazi ukuthi kwakuyingilosi yeNkosi.
22 Iye anawuza mkazi wake kuti, “Ife tifa basi pakuti taona Mulungu!”
UManowa wasesithi kumkakhe: Sizakufa lokufa ngoba sibone uNkulunkulu.
23 Koma mkazi wake anamuyankha kuti, “Yehova akanafuna kutipha sakanayilandira nsembe yathu yopsereza ndi chopereka chathu chachakudya chija, ndipo sakanationetsanso zinthu zonsezi kapena kutiwuza zinthu ngati zimenezi nthawi ino.”
Kodwa umkakhe wathi kuye: Uba iNkosi ibithanda ukusibulala, ibingayikwemukela esandleni sethu umnikelo wokutshiswa lomnikelo wokudla, njalo ibingayikusitshengisa zonke lezizinto, njalo ibingayikusizwisa ngalesisikhathi izinto ezinjengalezi.
24 Motero mkaziyo anabereka mwana wa mwamuna, namutcha dzina lake Samsoni. Iye anakula ndipo Yehova anamudalitsa.
Owesifazana wasebeletha indodana, wayitha ibizo layo wathi nguSamsoni; umfana wasekhula, leNkosi yambusisa.
25 Mzimu wa Yehova unayamba kumulimbikitsa pamene ankakhala ku misasa ya anthu a fuko la Dani, malo amene anali pakati pa Zora ndi Esitaoli.
UMoya weNkosi waseqala ukumvusa enkambeni kaDani phakathi kweZora leEshitawoli.

< Oweruza 13 >