< Oweruza 13 >

1 Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova, kotero Yehova anawapereka mʼmanja mwa Afilisti kwa zaka makumi anayi.
Un Israēla bērni darīja joprojām, kas Tam Kungam nepatika; tad Tas Kungs tos nodeva Fīlistu rokā četrdesmit gadus.
2 Ku Zora kunali munthu wina dzina lake Manowa, wochokera ku fuko la Dani. Mkazi wake analibe ana popeza anali wosabereka.
Un tur bija viens vīrs no Careas, no Dana cilts, un viņa vārds bija Manoūs, un viņa sieva bija neauglīga un nedzemdēja.
3 Mngelo wa Yehova anaonekera mkaziyo ndipo anati, “Ndinu wosabereka ndipo mulibedi mwana, komabe mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna.
Un Tā Kunga eņģelis parādījās tai sievai un uz to sacīja: redzi, tu esi neauglīga un neesi dzemdējusi, bet tu tapsi grūta un dzemdēsi dēlu.
4 Tsono mudzisamale bwino, osamwa vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa ndiponso musamadye chakudya chilichonse chodetsedwa,
Tad nu sargies un nedzer vīna nedz stipra dzēriena un neēd nekā, kas nešķīsts.
5 chifukwa mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna. Mwanayo akadzabadwa lumo lisadzapite pa mutu chifukwa mnyamatayo adzakhala Mnaziri, ndiye kuti wopatulika kwa Mulungu kuyambira pa nthawi imene adzakhale ali mʼchiberekero. Ndipo adzayamba ntchito yopulumutsa Israeli mʼmanja mwa Afilisti.”
Jo redzi, tu tapsi grūta un dzemdēsi dēlu, kam uz galvu nebūs nākt nekādam dzenamam nazim, jo tas puisis būs Dievam svētīts (nazīrs) no mātes miesām, un viņš sāks Israēli izpestīt no Fīlistu rokas.
6 Kenaka mayiyo anapita kukawuza mwamuna wake kuti, “Munthu wa Mulungu anabwera kwa ine, ndipo maonekedwe ake anali ngati mngelo wa Mulungu, maonekedwe woopsa kwambiri. Ine sindinamufunse kumene amachokera, ndipo iyeyo sanandiwuzenso dzina lake.
Tad tā sieva nāca un runāja uz savu vīru un sacīja: viens Dieva vīrs pie manis atnāca; viņa ģīmis bija kā Dieva eņģeļa ģīmis, ļoti bijājams, un es viņu nevaicāju, no kurienes tas esot, un viņš man arī savu vārdu neteica.
7 Koma anandiwuza kuti, ‘Mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna. Choncho musamamwe vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa, musamadye chakudya chilichonse choyipitsidwa chifukwa mwanayo adzakhala Mnaziri, wopatulika kwa Mulungu kuyambira pa nthawi imene adzakhale ali mʼchiberekero mpaka tsiku la kufa kwake.’”
Bet viņš uz mani sacīja: redzi, tu tapsi grūta un dzemdēsi dēlu, un nu nedzer vīna nedz stipra dzēriena, nedz ēd ko, kas nešķīsts, jo tas puisis būs Dievam svētīts no mātes miesām līdz pat savai nāves dienai.
8 Kenaka Manowa anapemphera kwa Yehova kuti, “Chonde Ambuye, lolani munthu wa Mulungu amene munamutuma abwerenso kwa ife kuti adzatiphunzitse zochita ndi mwanayo akadzabadwa.”
Tad Manoūs pielūdza To Kungu un sacīja: Ak Kungs, lai jel tas Dieva vīrs, ko Tu esi sūtījis, atkal pie mums atnāk un mums māca, ko lai ar to bērnu darām, kas piedzims.
9 Mulungu anamva pemphero la Manowa, ndipo mngelo wa Mulungu anabweranso kwa mkaziyo nthawi imene anali ku munda, koma Manowa mwamuna wake sanali naye.
Un Dievs paklausīja Manoūs balsi, un tas Dieva eņģelis nāca atkal pie tās sievas; un viņa sēdēja tīrumā, bet Manoūs, viņas vīrs, nebija pie viņas.
10 Tsono mkaziyo anathamanga kukawuza mwamuna wake kuti, “Wandionekeranso munthu uja amene anabwera kwa ine tsiku lija.”
Tad tā sieva steidzās un skrēja un to pasacīja savam vīram, un uz to sacīja: redzi, tas vīrs man parādījies, kas tai dienā pie manis nāca.
11 Choncho Manowa ananyamuka namutsatira mkazi wake. Atafika kwa munthuyo anamufunsa kuti, “Kodi ndinu munayankhula ndi mkazi wanga?” Iye anayankha kuti, “Ndine.”
Tad Manoūs cēlās un gāja savai sievai pakaļ un nāca pie tā vīra un uz to sacīja: vai tu esi tas vīrs, kas uz to sievu runājis? Un tas sacīja: es tas esmu.
12 Kenaka Manowa anafunsa kuti, “Tiyerekeze kuti mawu anuwa akwaniritsidwadi, ndiye mwanayu azidzakhala bwanji ndipo azidzachita chiyani?”
Tad Manoūs sacīja: kad nu tas notiks, ko tu sacījis, kāds tikums tad būs tam zēnam un kāds būs viņa darbs?
13 Ndipo mngelo wa Yehova uja anamuyankha kuti, “Zonse zimene ndinawawuza akazi anuwa asamale ndipo adzazichitedi.
Un Tā Kunga eņģelis sacīja uz Manoū: no visa, ko es uz to sievu esmu runājis, viņai būs sargāties.
14 Asadzadye chilichonse chochokera ku mphesa. Asadzamwe vinyo kapena choledzeretsa chilichonse, ngakhale kudya chakudya chilichonse chodetsedwa. Zonse zimene ndinawalamula azisunge bwino.”
Viņai nebūs ēst nekā, kas no vīna koka izaug, un viņai nebūs dzert ne vīna, ne stipra dzēriena, nedz ēst, kas nešķīsts, visu, ko es viņai esmu pavēlējis, viņai būs turēt.
15 Manowa anamuwuza mngelo wa Yehova uja kuti, “Chonde dikirani pangʼono, timati tikukonzereni mwana wambuzi.”
Tad Manoūs sacīja uz Tā Kunga eņģeli: lūdzams, pakavējies un mēs sataisīsim priekš tevis kazlēnu.
16 Mngelo wa Yehova anayankha kuti, “Ngakhale mukundidikiritsa, ine sindidya chakudya chanu. Koma ngati mukonze nsembe yopsereza iperekeni kwa Yehova.” (Manowa nʼkuti asakudziwa kuti munthuyo anali mngelo wa Mulungu).
Tad Tā Kunga eņģelis sacīja uz Manoū; jebšu tu mani uzkavētu, tomēr es no tavas maizes neēdīšu, bet ja tu gribi dedzināmo upuri pienest, to tu Tam Kungam vari upurēt. Jo Manoūs nezināja, viņu esam Tā Kunga eņģeli.
17 Tsono Manowa anapempha mngelo wa Yehova kuti, “Chonde tidziwitseni dzina lanu kuti zikadzachitika zimene mwanenazi ife tidzakulemekezeni?”
Un Manoūs sacīja uz Tā Kunga eņģeli: kā tavs vārds? Ka tevi varam godāt, kad notiks pēc tava vārda.
18 Iye anayankha kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukufunsa dzina langa? Dzina laketu ndi lodabwitsa.”
Tad Tā Kunga eņģelis uz viņu sacīja: kāpēc tu tā vaicā pēc Mana Vārda, kas taču ir brīnišķīgs?
19 Ndipo Manowa anatenga mwana wambuzi pamodzi ndi chopereka cha chakudya nakapereka nsembe pa thanthwe kwa Yehova ndipo Yehova anachita zodabwitsa kwa Manowa ndi mkazi wake akuona.
Tad Manoūs ņēma kazlēnu un to ēdamo upuri, un to upurēja Tam Kungam uz tās klints; un viņš darīja brīnumu un Manoūs un viņa sieva skatījās.
20 Pamene malawi a moto amakwera kumwamba kuchoka pa guwa, mngelo wa Yehova uja anakwera kumwamba mʼmalawi a motowo Manowa ndi mkazi wake akuona. Tsono anadzigwetsa pansi naweramitsa mitu yawo pansi.
Jo kad liesma no altāra virsas šāvās pret debesi, tad Tā Kunga eņģelis uzkāpa altāra liesmā. Un Manoūs un viņa sieva to redzēja un metās pie zemes uz saviem vaigiem.
21 Mngelo wa Yehova uja sanaonekerenso kwa Manowa ndi mkazi wake. Choncho Manowa anazindikira kuti anali mngelo wa Yehova.
Un Tā Kunga eņģelis neparādījās vairs ne Manoūm, nedz viņa sievai. Tad Manoūs atzina, ka tas bija Tā Kunga eņģelis.
22 Iye anawuza mkazi wake kuti, “Ife tifa basi pakuti taona Mulungu!”
Un Manoūs sacīja uz savu sievu: mēs tiešām mirsim, jo mēs esam Dievu redzējuši.
23 Koma mkazi wake anamuyankha kuti, “Yehova akanafuna kutipha sakanayilandira nsembe yathu yopsereza ndi chopereka chathu chachakudya chija, ndipo sakanationetsanso zinthu zonsezi kapena kutiwuza zinthu ngati zimenezi nthawi ino.”
Bet viņa sieva uz viņu sacīja: kad Tas Kungs mūs gribētu nokaut, tad Viņš to dedzināmo upuri un ēdamo upuri nebūtu pieņēmis no mūsu rokām; Viņš arī visas šīs lietas mums nebūtu parādījis, nedz mums to licis dzirdēt šai laikā.
24 Motero mkaziyo anabereka mwana wa mwamuna, namutcha dzina lake Samsoni. Iye anakula ndipo Yehova anamudalitsa.
Un tā sieva dzemdēja dēlu un nosauca viņa vārdu Simsons, un tas zēns uzauga, un Tas Kungs to svētīja.
25 Mzimu wa Yehova unayamba kumulimbikitsa pamene ankakhala ku misasa ya anthu a fuko la Dani, malo amene anali pakati pa Zora ndi Esitaoli.
Un Tā Kunga Gars viņu sāka skubināt Dana lēģerī starp Careu un Estaoli.

< Oweruza 13 >