< Oweruza 13 >

1 Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova, kotero Yehova anawapereka mʼmanja mwa Afilisti kwa zaka makumi anayi.
Mwet Israel elos sifilpa oru ma koluk ye mutun LEUM GOD, ke ma inge LEUM GOD El lela tuh mwet Philistia in leum faclos yac angngaul.
2 Ku Zora kunali munthu wina dzina lake Manowa, wochokera ku fuko la Dani. Mkazi wake analibe ana popeza anali wosabereka.
In pacl sac oasr sie mwet in siti Zorah su pangpang Manoah, sin sruf lal Dan, ac mutan kial ah el sie mutan talap.
3 Mngelo wa Yehova anaonekera mkaziyo ndipo anati, “Ndinu wosabereka ndipo mulibedi mwana, komabe mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna.
Na lipufan lun LEUM GOD sikyang nu sin mutan sac ac fahk, “Soenna oasr tulik nutum mweyen kom talap, tusruktu ac tia paht kom ac pitutu, ac oswela sie wen.
4 Tsono mudzisamale bwino, osamwa vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa ndiponso musamadye chakudya chilichonse chodetsedwa,
Karinganang tuh kom in tia nim wain ku kutena mwe nim ku, ac nik kom kang kutena mongo ma oal.
5 chifukwa mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna. Mwanayo akadzabadwa lumo lisadzapite pa mutu chifukwa mnyamatayo adzakhala Mnaziri, ndiye kuti wopatulika kwa Mulungu kuyambira pa nthawi imene adzakhale ali mʼchiberekero. Ndipo adzayamba ntchito yopulumutsa Israeli mʼmanja mwa Afilisti.”
Na tukun wen se nutum an el isusla, kom in tia kal aunsifal, mweyen len se na ma el isusla ah fahla el fah sriyukla nu sin God oana sie mwet Nazirite. El pa ac molela mwet Israel liki inpoun mwet Philistia.”
6 Kenaka mayiyo anapita kukawuza mwamuna wake kuti, “Munthu wa Mulungu anabwera kwa ine, ndipo maonekedwe ake anali ngati mngelo wa Mulungu, maonekedwe woopsa kwambiri. Ine sindinamufunse kumene amachokera, ndipo iyeyo sanandiwuzenso dzina lake.
Na mutan sac som ac fahk nu sin mukul tumal, “Sie mwet lun God tuku nu yuruk. Arulana aksangeng lumahl, oana elan sie lipufan lun God. Nga tiana siyuk lah el tuku ya me, ac el tia pacna fahk inel nu sik.
7 Koma anandiwuza kuti, ‘Mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna. Choncho musamamwe vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa, musamadye chakudya chilichonse choyipitsidwa chifukwa mwanayo adzakhala Mnaziri, wopatulika kwa Mulungu kuyambira pa nthawi imene adzakhale ali mʼchiberekero mpaka tsiku la kufa kwake.’”
Tusruktu el fahk nu sik lah nga ac fah pitutu ac oswela sie wen. Ac el fahk pac mu nga in tiana nim wain ku kutena mwe nim ku, ku kang kutena mongo oal, mweyen tulik sac ac fah sie mwet Nazirite nu sin God ke lusen moul lal nufon.”
8 Kenaka Manowa anapemphera kwa Yehova kuti, “Chonde Ambuye, lolani munthu wa Mulungu amene munamutuma abwerenso kwa ife kuti adzatiphunzitse zochita ndi mwanayo akadzabadwa.”
Na Manoah el pre nu sin LEUM GOD ac fahk, “O LEUM GOD, nunak munas, lela tuh mwet lun God se su kom supwama meet ah in sifil foloko nu yorosr ac fahk nu sesr lah mea kut ac oru nu sin tulik se inge ke el ac isusla uh.”
9 Mulungu anamva pemphero la Manowa, ndipo mngelo wa Mulungu anabweranso kwa mkaziyo nthawi imene anali ku munda, koma Manowa mwamuna wake sanali naye.
God El oru oana ma Manoah el siyuk ah. Lipufan lun God sifilpa foloko nu yurin mutan sac ke el muta in ima ah, tusruktu mukul tumal el wangin in pacl sac.
10 Tsono mkaziyo anathamanga kukawuza mwamuna wake kuti, “Wandionekeranso munthu uja amene anabwera kwa ine tsiku lija.”
Na mutan sac sulaklak som ac fahk nu sin mukul tumal, “Liye, mwet se ma tuh tuku nu yuruk ah el sifilpa sikyak nu sik!”
11 Choncho Manowa ananyamuka namutsatira mkazi wake. Atafika kwa munthuyo anamufunsa kuti, “Kodi ndinu munayankhula ndi mkazi wanga?” Iye anayankha kuti, “Ndine.”
Manoah el tuyak ac fahsr tukun mutan kial ah, ac ke el sun mwet sac, el siyuk sel, “Ku kom pa mwet se ma sramsram nu sin mutan kiuk ah?” Na lipufan sac fahk, “Aok.”
12 Kenaka Manowa anafunsa kuti, “Tiyerekeze kuti mawu anuwa akwaniritsidwadi, ndiye mwanayu azidzakhala bwanji ndipo azidzachita chiyani?”
Na Manoah el fahk, “Na inge, ke pacl se ma kas lom inge akpwayeyeyuk, mea tulik se inge ac oru? Moul fuka el ac moulkin?”
13 Ndipo mngelo wa Yehova uja anamuyankha kuti, “Zonse zimene ndinawawuza akazi anuwa asamale ndipo adzazichitedi.
Na lipufan lun LEUM GOD el fahk, “Mutan kiom an el enenu in liyaung ma nukewa nga fahk nu sel ah.
14 Asadzadye chilichonse chochokera ku mphesa. Asadzamwe vinyo kapena choledzeretsa chilichonse, ngakhale kudya chakudya chilichonse chodetsedwa. Zonse zimene ndinawalamula azisunge bwino.”
El tia enenu in kang kutena ma su tuku ke fokin grape, ku nim kutena wain, ku mwe nim ku, ku kang kutena mongo oal. El enenu in oru ma nukewa ma nga sapkin nu sel ah.”
15 Manowa anamuwuza mngelo wa Yehova uja kuti, “Chonde dikirani pangʼono, timati tikukonzereni mwana wambuzi.”
Manoah el fahk nu sin lipufan lun LEUM GOD, “Nunak munas, nimet kom sa som. Soano kut in akmolyela soko nani fusr kom in mongo.”
16 Mngelo wa Yehova anayankha kuti, “Ngakhale mukundidikiritsa, ine sindidya chakudya chanu. Koma ngati mukonze nsembe yopsereza iperekeni kwa Yehova.” (Manowa nʼkuti asakudziwa kuti munthuyo anali mngelo wa Mulungu).
Na lipufan lun LEUM GOD el fahk nu sel Manoah, “Kom finne ikolyuwi, nga ac tia kang mongo kom oru an. Tusruktu kom fin lungse oru, kom kisakin nu sin LEUM GOD.”
17 Tsono Manowa anapempha mngelo wa Yehova kuti, “Chonde tidziwitseni dzina lanu kuti zikadzachitika zimene mwanenazi ife tidzakulemekezeni?”
Na Manoah el fahk, “Su inem an, tuh kut fah ku in akfulatye kom ke pacl se kas lom inge ac akpwayeyuk.”
18 Iye anayankha kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukufunsa dzina langa? Dzina laketu ndi lodabwitsa.”
Na lipufan sac el siyuk, “Efu ku kom ke etu inek? Inek sie ine lukma.”
19 Ndipo Manowa anatenga mwana wambuzi pamodzi ndi chopereka cha chakudya nakapereka nsembe pa thanthwe kwa Yehova ndipo Yehova anachita zodabwitsa kwa Manowa ndi mkazi wake akuona.
Na Manoah el eis soko nani fusr ac kutu wheat, ac el kisakin ma inge fin sie eot nu sin LEUM GOD su oru ma usrnguk.
20 Pamene malawi a moto amakwera kumwamba kuchoka pa guwa, mngelo wa Yehova uja anakwera kumwamba mʼmalawi a motowo Manowa ndi mkazi wake akuona. Tsono anadzigwetsa pansi naweramitsa mitu yawo pansi.
Ke pacl se e sac firiryak liki loang sac, na lipufan lun LEUM GOD el weak firir sac nu inkusrao. Ke Manoah ac mutan kial ah ngetang liye ma inge, eltal putati ac faksufi nu infohk uh.
21 Mngelo wa Yehova uja sanaonekerenso kwa Manowa ndi mkazi wake. Choncho Manowa anazindikira kuti anali mngelo wa Yehova.
Lipufan lun LEUM GOD el tia sifil sikyak nu sel Manoah ac mutan kial ah, na Manoah el tufah akilenak lah lipufan lun LEUM GOD pa mwet sac.
22 Iye anawuza mkazi wake kuti, “Ife tifa basi pakuti taona Mulungu!”
Manoah el fahk nu sin mutan kial ah, “Pwayena lah kut ac misa, mweyen kut liyalak God!”
23 Koma mkazi wake anamuyankha kuti, “Yehova akanafuna kutipha sakanayilandira nsembe yathu yopsereza ndi chopereka chathu chachakudya chija, ndipo sakanationetsanso zinthu zonsezi kapena kutiwuza zinthu ngati zimenezi nthawi ino.”
Na mutan kial ah topuk ac fahk, “LEUM GOD El funu lungse unikuti, El lukun tia insewowo ke mwe kisa kut orala, ac El lukun tia pac akkalemye ma inge nu sesr, ku fahkak kas ouinge nu sesr ke pacl se inge.”
24 Motero mkaziyo anabereka mwana wa mwamuna, namutcha dzina lake Samsoni. Iye anakula ndipo Yehova anamudalitsa.
Na mutan sac oswela wen se, ac sang inel Samson. Ac tulik sac el kapak, ac LEUM GOD El akinsewowoyal.
25 Mzimu wa Yehova unayamba kumulimbikitsa pamene ankakhala ku misasa ya anthu a fuko la Dani, malo amene anali pakati pa Zora ndi Esitaoli.
Ac ku lun LEUM GOD mutawauk in akkeyal ke el muta ke iwen aktuktuk lun mwet Dan in masrlon acn Zorah ac acn Eshtaol.

< Oweruza 13 >