< Oweruza 13 >

1 Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova, kotero Yehova anawapereka mʼmanja mwa Afilisti kwa zaka makumi anayi.
Et de nouveau les enfants d’Israël tirent le mal en la présence du Seigneur, qui les livra aux mains des Philistins pendant quarante ans.
2 Ku Zora kunali munthu wina dzina lake Manowa, wochokera ku fuko la Dani. Mkazi wake analibe ana popeza anali wosabereka.
Or, il y avait un certain homme de Saraa, et de la race de Dan, du nom de Manué, ayant une femme stérile,
3 Mngelo wa Yehova anaonekera mkaziyo ndipo anati, “Ndinu wosabereka ndipo mulibedi mwana, komabe mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna.
À qui l’ange du Seigneur apparut, et dit: Tu es stérile et sans enfants; mais tu concevras et tu enfanteras un fils.
4 Tsono mudzisamale bwino, osamwa vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa ndiponso musamadye chakudya chilichonse chodetsedwa,
Prends donc bien garde de ne point boire de vin, et de cervoise, et de ne manger rien d’impur,
5 chifukwa mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna. Mwanayo akadzabadwa lumo lisadzapite pa mutu chifukwa mnyamatayo adzakhala Mnaziri, ndiye kuti wopatulika kwa Mulungu kuyambira pa nthawi imene adzakhale ali mʼchiberekero. Ndipo adzayamba ntchito yopulumutsa Israeli mʼmanja mwa Afilisti.”
Parce que tu concevras et tu enfanteras un fils dont le rasoir ne touchera pas la tête; car il sera nazaréen de Dieu, depuis son enfance et dès le sein de sa mère; et c’est lui qui commencera à délivrer Israël de la main des Philistins.
6 Kenaka mayiyo anapita kukawuza mwamuna wake kuti, “Munthu wa Mulungu anabwera kwa ine, ndipo maonekedwe ake anali ngati mngelo wa Mulungu, maonekedwe woopsa kwambiri. Ine sindinamufunse kumene amachokera, ndipo iyeyo sanandiwuzenso dzina lake.
Et étant venue vers son mari, elle lui dit: L’homme de Dieu est venu vers moi, ayant le visage d’un ange, et inspirant la plus grande terreur. Lorsque je lui ai demandé qui il était, d’où il venait, et de quel nom il s’appelait, il n’a pas voulu me le dire.
7 Koma anandiwuza kuti, ‘Mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna. Choncho musamamwe vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa, musamadye chakudya chilichonse choyipitsidwa chifukwa mwanayo adzakhala Mnaziri, wopatulika kwa Mulungu kuyambira pa nthawi imene adzakhale ali mʼchiberekero mpaka tsiku la kufa kwake.’”
Mais il m’a répondu ceci: Voilà que tu concevras et enfanteras un fils: prends garde de ne point boire de vin ni de cervoise, et de ne rien manger d’impur; car l’enfant sera nazaréen de Dieu depuis son enfance, du sein de sa mère jusqu’au jour de sa mort.
8 Kenaka Manowa anapemphera kwa Yehova kuti, “Chonde Ambuye, lolani munthu wa Mulungu amene munamutuma abwerenso kwa ife kuti adzatiphunzitse zochita ndi mwanayo akadzabadwa.”
C’est pourquoi Manué pria le Seigneur et dit: Je vous conjure. Seigneur, que l’homme de Dieu, que vous avez envoyé, vienne de nouveau, et qu’il nous enseigne ce que nous devons faire de l’enfant qui doit naître.
9 Mulungu anamva pemphero la Manowa, ndipo mngelo wa Mulungu anabweranso kwa mkaziyo nthawi imene anali ku munda, koma Manowa mwamuna wake sanali naye.
Et le Seigneur exauça Manué priant, et de nouveau apparut l’ange de Dieu à sa femme, assise dans la campagne. Or, Manué son mari n’était pas avec elle. Et lorsqu’elle eut vu l’ange,
10 Tsono mkaziyo anathamanga kukawuza mwamuna wake kuti, “Wandionekeranso munthu uja amene anabwera kwa ine tsiku lija.”
Elle se hâta, courut à son mari, et le lui annonça, disant: Voilà que m’a apparu l’homme que j’avais vu auparavant.
11 Choncho Manowa ananyamuka namutsatira mkazi wake. Atafika kwa munthuyo anamufunsa kuti, “Kodi ndinu munayankhula ndi mkazi wanga?” Iye anayankha kuti, “Ndine.”
Manué se leva et suivit sa femme; puis, venant vers l’homme, il lui dit: Vous êtes celui qui avez parlé à cette femme? Et il répondit: Je le suis.
12 Kenaka Manowa anafunsa kuti, “Tiyerekeze kuti mawu anuwa akwaniritsidwadi, ndiye mwanayu azidzakhala bwanji ndipo azidzachita chiyani?”
Et Manué à l’homme: Quand, dit-il, votre parole sera accomplie, que voulez-vous que fasse l’enfant? ou de quoi devra-t-il s’abstenir?
13 Ndipo mngelo wa Yehova uja anamuyankha kuti, “Zonse zimene ndinawawuza akazi anuwa asamale ndipo adzazichitedi.
Et l’ange du Seigneur répondit à Manué: Que ta femme s’abstienne de toutes les choses que je lui ai indiquées;
14 Asadzadye chilichonse chochokera ku mphesa. Asadzamwe vinyo kapena choledzeretsa chilichonse, ngakhale kudya chakudya chilichonse chodetsedwa. Zonse zimene ndinawalamula azisunge bwino.”
Qu’elle ne mange rien de ce qui naît de la vigne; qu’elle ne boive point de vin ni de cervoise; qu’elle ne mange rien d’impur; et que ce que je lui ai ordonné, elle l’accomplisse et le garde.
15 Manowa anamuwuza mngelo wa Yehova uja kuti, “Chonde dikirani pangʼono, timati tikukonzereni mwana wambuzi.”
Alors Manué dit à l’ange du Seigneur: Je vous conjure d’acquiescer à mes prières; et, puissions-nous vous préparer un chevreau.
16 Mngelo wa Yehova anayankha kuti, “Ngakhale mukundidikiritsa, ine sindidya chakudya chanu. Koma ngati mukonze nsembe yopsereza iperekeni kwa Yehova.” (Manowa nʼkuti asakudziwa kuti munthuyo anali mngelo wa Mulungu).
L’ange lui répondit: Quand tu me presserais, je ne mangerais pas de tes pains; mais si tu veux faire un holocauste, offre-le au Seigneur, Et Manué ne savait pas que ce fût l’ange du Seigneur.
17 Tsono Manowa anapempha mngelo wa Yehova kuti, “Chonde tidziwitseni dzina lanu kuti zikadzachitika zimene mwanenazi ife tidzakulemekezeni?”
Il lui dit encore: Quel est votre nom, afin que, si vos paroles s’accomplissent, nous vous honorions?
18 Iye anayankha kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukufunsa dzina langa? Dzina laketu ndi lodabwitsa.”
L’ange lui répondit: Pourquoi demandes-tu mon nom, qui est admirable?
19 Ndipo Manowa anatenga mwana wambuzi pamodzi ndi chopereka cha chakudya nakapereka nsembe pa thanthwe kwa Yehova ndipo Yehova anachita zodabwitsa kwa Manowa ndi mkazi wake akuona.
Manué prit donc le chevreau et les libations, et les plaça sur le rocher, les offrant au Seigneur qui fait les merveilles: or, lui-même et sa femme regardaient.
20 Pamene malawi a moto amakwera kumwamba kuchoka pa guwa, mngelo wa Yehova uja anakwera kumwamba mʼmalawi a motowo Manowa ndi mkazi wake akuona. Tsono anadzigwetsa pansi naweramitsa mitu yawo pansi.
Et lorsque la flamme de l’autel montait vers le ciel, l’ange du Seigneur monta pareillement dans la flamme. Ce qu’ayant vu Manué et sa femme, ils tombèrent inclinés vers la terre.
21 Mngelo wa Yehova uja sanaonekerenso kwa Manowa ndi mkazi wake. Choncho Manowa anazindikira kuti anali mngelo wa Yehova.
Et l’ange du Seigneur n’apparut plus à leurs yeux. Et aussitôt Manué comprit que c’était l’ange du Seigneur.
22 Iye anawuza mkazi wake kuti, “Ife tifa basi pakuti taona Mulungu!”
Et il dit à sa femme: Nous mourrons de mort, parce que nous avons vu le Seigneur.
23 Koma mkazi wake anamuyankha kuti, “Yehova akanafuna kutipha sakanayilandira nsembe yathu yopsereza ndi chopereka chathu chachakudya chija, ndipo sakanationetsanso zinthu zonsezi kapena kutiwuza zinthu ngati zimenezi nthawi ino.”
Sa femme lui répondit: Si le Seigneur voulait nous faire mourir, il n’aurait pas reçu de nos mains d’holocaustes et de libations, il ne nous aurait pas montré toutes ces choses, et il n’aurait pas dit ce qui doit arriver.
24 Motero mkaziyo anabereka mwana wa mwamuna, namutcha dzina lake Samsoni. Iye anakula ndipo Yehova anamudalitsa.
Elle enfanta donc un fils, et elle l’appela du nom de Samson. Et l’enfant grandit, et le Seigneur le bénit.
25 Mzimu wa Yehova unayamba kumulimbikitsa pamene ankakhala ku misasa ya anthu a fuko la Dani, malo amene anali pakati pa Zora ndi Esitaoli.
Et l’esprit du Seigneur commença à être avec lui, dans le camp de Dan, entre Saraa et Esthaol.

< Oweruza 13 >