< Oweruza 13 >

1 Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova, kotero Yehova anawapereka mʼmanja mwa Afilisti kwa zaka makumi anayi.
And they repeated [the] people of Israel to do the evil in [the] eyes of Yahweh and he gave them Yahweh in [the] hand of [the] Philistines forty year[s].
2 Ku Zora kunali munthu wina dzina lake Manowa, wochokera ku fuko la Dani. Mkazi wake analibe ana popeza anali wosabereka.
And he was a man one from Zorah from [the] clan of the Danite[s] and name his [was] Manoah and wife his [was] barren and not she had borne children.
3 Mngelo wa Yehova anaonekera mkaziyo ndipo anati, “Ndinu wosabereka ndipo mulibedi mwana, komabe mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna.
And he appeared [the] angel of Yahweh to the woman and he said to her here! please you [are] barren and not you have borne children and you will conceive and you will bear a son.
4 Tsono mudzisamale bwino, osamwa vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa ndiponso musamadye chakudya chilichonse chodetsedwa,
And therefore take care please and may not you drink wine and strong drink and may not you eat any unclean [thing].
5 chifukwa mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna. Mwanayo akadzabadwa lumo lisadzapite pa mutu chifukwa mnyamatayo adzakhala Mnaziri, ndiye kuti wopatulika kwa Mulungu kuyambira pa nthawi imene adzakhale ali mʼchiberekero. Ndipo adzayamba ntchito yopulumutsa Israeli mʼmanja mwa Afilisti.”
For here you [will be] pregnant and you will bear a son and a razor not it will go up on head his for a Nazirite of God he will be the lad from the womb and he he will begin to deliver Israel from [the] hand of [the] Philistines.
6 Kenaka mayiyo anapita kukawuza mwamuna wake kuti, “Munthu wa Mulungu anabwera kwa ine, ndipo maonekedwe ake anali ngati mngelo wa Mulungu, maonekedwe woopsa kwambiri. Ine sindinamufunse kumene amachokera, ndipo iyeyo sanandiwuzenso dzina lake.
And she went the woman and she said to husband her saying man of God he came to me and appearance his [was] like [the] appearance of angel of God awesome very and not I asked him where? from this [was] he and name his not he told to me.
7 Koma anandiwuza kuti, ‘Mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna. Choncho musamamwe vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa, musamadye chakudya chilichonse choyipitsidwa chifukwa mwanayo adzakhala Mnaziri, wopatulika kwa Mulungu kuyambira pa nthawi imene adzakhale ali mʼchiberekero mpaka tsiku la kufa kwake.’”
And he said to me here you [will be] pregnant and you will bear a son and therefore may not you drink - wine and strong drink and may not you eat any uncleanness for a Nazirite of God he will be the lad from the womb until [the] day of death his.
8 Kenaka Manowa anapemphera kwa Yehova kuti, “Chonde Ambuye, lolani munthu wa Mulungu amene munamutuma abwerenso kwa ife kuti adzatiphunzitse zochita ndi mwanayo akadzabadwa.”
And he prayed Manoah to Yahweh and he said pardon me O Lord [the] man of God whom you sent let him come please again to us so he may teach us what? will we do for the lad who is about to be born.
9 Mulungu anamva pemphero la Manowa, ndipo mngelo wa Mulungu anabweranso kwa mkaziyo nthawi imene anali ku munda, koma Manowa mwamuna wake sanali naye.
And he listened God to [the] voice of Manoah and he came [the] angel of God again to the woman and she [was] sitting in the field and Manoah husband her not [was] with her.
10 Tsono mkaziyo anathamanga kukawuza mwamuna wake kuti, “Wandionekeranso munthu uja amene anabwera kwa ine tsiku lija.”
And she made haste the woman and she ran and she told to husband her and she said to him here! he has presented himself to me the man who he came on the day to me.
11 Choncho Manowa ananyamuka namutsatira mkazi wake. Atafika kwa munthuyo anamufunsa kuti, “Kodi ndinu munayankhula ndi mkazi wanga?” Iye anayankha kuti, “Ndine.”
And he arose and he went Manoah after wife his and he came to the man and he said to him ¿ [are] you the man who you spoke to the woman and he said I.
12 Kenaka Manowa anafunsa kuti, “Tiyerekeze kuti mawu anuwa akwaniritsidwadi, ndiye mwanayu azidzakhala bwanji ndipo azidzachita chiyani?”
And he said Manoah now it will come words your what? will it be [the] manner of the lad and work his.
13 Ndipo mngelo wa Yehova uja anamuyankha kuti, “Zonse zimene ndinawawuza akazi anuwa asamale ndipo adzazichitedi.
And he said [the] angel of Yahweh to Manoah from all that I said to the woman she will take care.
14 Asadzadye chilichonse chochokera ku mphesa. Asadzamwe vinyo kapena choledzeretsa chilichonse, ngakhale kudya chakudya chilichonse chodetsedwa. Zonse zimene ndinawalamula azisunge bwino.”
Any of all that it comes forth from [the] vine of the wine not she will eat and wine and strong drink may not she drink and any uncleanness may not she eat all that I commanded her she will keep.
15 Manowa anamuwuza mngelo wa Yehova uja kuti, “Chonde dikirani pangʼono, timati tikukonzereni mwana wambuzi.”
And he said Manoah to [the] angel of Yahweh let us detain please you so we may prepare before you a kid of goats.
16 Mngelo wa Yehova anayankha kuti, “Ngakhale mukundidikiritsa, ine sindidya chakudya chanu. Koma ngati mukonze nsembe yopsereza iperekeni kwa Yehova.” (Manowa nʼkuti asakudziwa kuti munthuyo anali mngelo wa Mulungu).
And he said [the] angel of Yahweh to Manoah if you will detain me not I will eat in food your and if you will make a burnt offering to Yahweh you will offer up it for not he knew Manoah that [was] [the] angel Yahweh it.
17 Tsono Manowa anapempha mngelo wa Yehova kuti, “Chonde tidziwitseni dzina lanu kuti zikadzachitika zimene mwanenazi ife tidzakulemekezeni?”
And he said Manoah to [the] angel of Yahweh who? [is] name your if it will come (word your *Q(K)*) and we will honor you.
18 Iye anayankha kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukufunsa dzina langa? Dzina laketu ndi lodabwitsa.”
And he said (to him *L(abh)*) [the] angel of Yahweh why? this are you asking to name my and it [is] incomprehensible.
19 Ndipo Manowa anatenga mwana wambuzi pamodzi ndi chopereka cha chakudya nakapereka nsembe pa thanthwe kwa Yehova ndipo Yehova anachita zodabwitsa kwa Manowa ndi mkazi wake akuona.
And he took Manoah [the] kid of the goats and the grain offering and he offered [it] up on the rock to Yahweh and an extraordinary thing to do and Manoah and wife his [were] looking.
20 Pamene malawi a moto amakwera kumwamba kuchoka pa guwa, mngelo wa Yehova uja anakwera kumwamba mʼmalawi a motowo Manowa ndi mkazi wake akuona. Tsono anadzigwetsa pansi naweramitsa mitu yawo pansi.
And it was when went up the flame from on the altar the heavens towards and he went up [the] angel of Yahweh in [the] flame of the altar and Manoah and wife his [were] looking and they fell on faces their [the] ground towards.
21 Mngelo wa Yehova uja sanaonekerenso kwa Manowa ndi mkazi wake. Choncho Manowa anazindikira kuti anali mngelo wa Yehova.
And not he repeated again [the] angel of Yahweh to appear to Manoah and to wife his then he knew Manoah that [was] [the] angel of Yahweh it.
22 Iye anawuza mkazi wake kuti, “Ife tifa basi pakuti taona Mulungu!”
And he said Manoah to wife his certainly we will die for God we have seen.
23 Koma mkazi wake anamuyankha kuti, “Yehova akanafuna kutipha sakanayilandira nsembe yathu yopsereza ndi chopereka chathu chachakudya chija, ndipo sakanationetsanso zinthu zonsezi kapena kutiwuza zinthu ngati zimenezi nthawi ino.”
And she said to him wife his if he had desired Yahweh to kill us not he accepted from hand our a burnt offering and a grain offering and not he showed us all these [things] and about this time not he caused to hear us like this.
24 Motero mkaziyo anabereka mwana wa mwamuna, namutcha dzina lake Samsoni. Iye anakula ndipo Yehova anamudalitsa.
And she bore the woman a son and she called name his Samson and he grew up the lad and he blessed him Yahweh.
25 Mzimu wa Yehova unayamba kumulimbikitsa pamene ankakhala ku misasa ya anthu a fuko la Dani, malo amene anali pakati pa Zora ndi Esitaoli.
And it began [the] spirit of Yahweh to stir him in Mahaneh Dan between Zorah and between Eshtaol.

< Oweruza 13 >