< Oweruza 13 >
1 Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova, kotero Yehova anawapereka mʼmanja mwa Afilisti kwa zaka makumi anayi.
Tedy opět synové Izraelští činili to, což jest zlého před očima Hospodinovýma, i vydal je Hospodin v ruce Filistinských za čtyřidceti let.
2 Ku Zora kunali munthu wina dzina lake Manowa, wochokera ku fuko la Dani. Mkazi wake analibe ana popeza anali wosabereka.
Byl pak muž jeden z Zaraha, z čeledi Dan, jménem Manue, jehož manželka byla neplodná a nerodila.
3 Mngelo wa Yehova anaonekera mkaziyo ndipo anati, “Ndinu wosabereka ndipo mulibedi mwana, komabe mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna.
I ukázal se anděl Hospodinův ženě té a řekl jí: Aj, nyní jsi neplodná, aniž jsi rodila; počneš pak a porodíš syna.
4 Tsono mudzisamale bwino, osamwa vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa ndiponso musamadye chakudya chilichonse chodetsedwa,
Protož nyní vystříhej se, abys vína nepila aneb nápoje opojného, a abys nejedla nic nečistého.
5 chifukwa mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna. Mwanayo akadzabadwa lumo lisadzapite pa mutu chifukwa mnyamatayo adzakhala Mnaziri, ndiye kuti wopatulika kwa Mulungu kuyambira pa nthawi imene adzakhale ali mʼchiberekero. Ndipo adzayamba ntchito yopulumutsa Israeli mʼmanja mwa Afilisti.”
Nebo aj, počneš a porodíš syna, a břitva ať nevchází na hlavu jeho, nebo bude to dítě od života Nazarejský Boží, a tenť počne vysvobozovati Izraele z ruky Filistinských.
6 Kenaka mayiyo anapita kukawuza mwamuna wake kuti, “Munthu wa Mulungu anabwera kwa ine, ndipo maonekedwe ake anali ngati mngelo wa Mulungu, maonekedwe woopsa kwambiri. Ine sindinamufunse kumene amachokera, ndipo iyeyo sanandiwuzenso dzina lake.
I přišla žena a pověděla to muži svému, řkuci: Muž Boží přišel ke mně, jehož oblíčej byl jako oblíčej anděla Božího, hrozný velmi, a neotázala jsem se jeho, odkud by byl, ani mi svého jména neoznámil.
7 Koma anandiwuza kuti, ‘Mudzakhala ndi pakati ndipo mudzabereka mwana wamwamuna. Choncho musamamwe vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa, musamadye chakudya chilichonse choyipitsidwa chifukwa mwanayo adzakhala Mnaziri, wopatulika kwa Mulungu kuyambira pa nthawi imene adzakhale ali mʼchiberekero mpaka tsiku la kufa kwake.’”
Ale řekl mi: Aj, počneš a porodíš syna, protož nyní nepí vína aneb nápoje opojného, aniž jez co nečistého, nebo to dítě od života bude Nazarejský Boží až do dne smrti své.
8 Kenaka Manowa anapemphera kwa Yehova kuti, “Chonde Ambuye, lolani munthu wa Mulungu amene munamutuma abwerenso kwa ife kuti adzatiphunzitse zochita ndi mwanayo akadzabadwa.”
Tedy Manue modlil se Hospodinu a řekl: Vyslyš mne, můj Pane, prosím, nechť muž Boží, kteréhož jsi byl poslal, zase přijde k nám, a naučí nás, co máme dělati s dítětem, kteréž se má naroditi.
9 Mulungu anamva pemphero la Manowa, ndipo mngelo wa Mulungu anabweranso kwa mkaziyo nthawi imene anali ku munda, koma Manowa mwamuna wake sanali naye.
I vyslyšel Bůh hlas Manue; nebo přišel anděl Boží opět k ženě té, když seděla na poli. Manue pak muž její nebyl s ní.
10 Tsono mkaziyo anathamanga kukawuza mwamuna wake kuti, “Wandionekeranso munthu uja amene anabwera kwa ine tsiku lija.”
A protož s chvátáním běžela žena ta, a oznámila muži svému, řkuci jemu: Hle, ukázal se mi muž ten, kterýž byl ke mně prvé přišel.
11 Choncho Manowa ananyamuka namutsatira mkazi wake. Atafika kwa munthuyo anamufunsa kuti, “Kodi ndinu munayankhula ndi mkazi wanga?” Iye anayankha kuti, “Ndine.”
Vstav pak Manue, šel za manželkou svou, a přišed k muži tomu, řekl jemu: Ty-li jsi ten muž, kterýž jsi mluvil k manželce mé? Odpověděl: Jsem.
12 Kenaka Manowa anafunsa kuti, “Tiyerekeze kuti mawu anuwa akwaniritsidwadi, ndiye mwanayu azidzakhala bwanji ndipo azidzachita chiyani?”
I řekl Manue: Nechť se nyní stane slovo tvé, ale jaká péče o to dítě a správa při něm býti má?
13 Ndipo mngelo wa Yehova uja anamuyankha kuti, “Zonse zimene ndinawawuza akazi anuwa asamale ndipo adzazichitedi.
Odpověděl anděl Hospodinův Manue: Ode všeho toho, o čemž jsem oznámil ženě, ať se ona vystříhá.
14 Asadzadye chilichonse chochokera ku mphesa. Asadzamwe vinyo kapena choledzeretsa chilichonse, ngakhale kudya chakudya chilichonse chodetsedwa. Zonse zimene ndinawalamula azisunge bwino.”
Ničeho, což pochází z vinného kmene, ať neužívá, to jest, vína aneb nápoje opojného ať nepije, a nic nečistého ať nejí; cožkoli jsem jí přikázal, ať ostříhá.
15 Manowa anamuwuza mngelo wa Yehova uja kuti, “Chonde dikirani pangʼono, timati tikukonzereni mwana wambuzi.”
Tedy řekl Manue andělu Hospodinovu: Medle, nechť tě pozdržíme, a připravímeť kozlíka.
16 Mngelo wa Yehova anayankha kuti, “Ngakhale mukundidikiritsa, ine sindidya chakudya chanu. Koma ngati mukonze nsembe yopsereza iperekeni kwa Yehova.” (Manowa nʼkuti asakudziwa kuti munthuyo anali mngelo wa Mulungu).
I odpověděl anděl Hospodinův Manue: Bys mne i pozdržel, nebuduť jísti pokrmu tvého, ale jestliže připravíš obět zápalnou, Hospodinu ji obětuj. Nebo nevěděl Manue, že byl anděl Hospodinův.
17 Tsono Manowa anapempha mngelo wa Yehova kuti, “Chonde tidziwitseni dzina lanu kuti zikadzachitika zimene mwanenazi ife tidzakulemekezeni?”
Řekl opět Manue andělu Hospodinovu: Jaké jest jméno tvé, abychom, když se naplní řeč tvá, poctili tebe?
18 Iye anayankha kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukufunsa dzina langa? Dzina laketu ndi lodabwitsa.”
Jemuž odpověděl anděl Hospodinův: Proč se ptáš na jméno mé, kteréž jest divné?
19 Ndipo Manowa anatenga mwana wambuzi pamodzi ndi chopereka cha chakudya nakapereka nsembe pa thanthwe kwa Yehova ndipo Yehova anachita zodabwitsa kwa Manowa ndi mkazi wake akuona.
Vzav tedy Manue kozlíka a obět suchou, obětoval to na skále Hospodinu, a on divnou věc učinil, an na to hledí Manue a manželka jeho.
20 Pamene malawi a moto amakwera kumwamba kuchoka pa guwa, mngelo wa Yehova uja anakwera kumwamba mʼmalawi a motowo Manowa ndi mkazi wake akuona. Tsono anadzigwetsa pansi naweramitsa mitu yawo pansi.
Nebo když vstupoval plamen s oltáře k nebi, vznesl se anděl Hospodinův v plameni s oltáře, Manue pak a manželka jeho vidouce to, padli na tvář svou na zemi.
21 Mngelo wa Yehova uja sanaonekerenso kwa Manowa ndi mkazi wake. Choncho Manowa anazindikira kuti anali mngelo wa Yehova.
A již se více neukázal anděl Hospodinův Manue ani manželce jeho. Tedy porozuměl Manue, že byl anděl Hospodinův.
22 Iye anawuza mkazi wake kuti, “Ife tifa basi pakuti taona Mulungu!”
I řekl Manue manželce své: Jistě my zemřeme, nebo jsme Boha viděli.
23 Koma mkazi wake anamuyankha kuti, “Yehova akanafuna kutipha sakanayilandira nsembe yathu yopsereza ndi chopereka chathu chachakudya chija, ndipo sakanationetsanso zinthu zonsezi kapena kutiwuza zinthu ngati zimenezi nthawi ino.”
Jemuž odpověděla manželka jeho: Kdyby nás chtěl Hospodin usmrtiti, nebyl by přijal z rukou našich oběti zápalné a suché, aniž by nám byl ukázal čeho toho, aniž by na tento čas byl nám ohlásil věcí takových.
24 Motero mkaziyo anabereka mwana wa mwamuna, namutcha dzina lake Samsoni. Iye anakula ndipo Yehova anamudalitsa.
A tak žena ta porodila syna a nazvala jméno jeho Samson. I rostlo dítě, a žehnal jemu Hospodin.
25 Mzimu wa Yehova unayamba kumulimbikitsa pamene ankakhala ku misasa ya anthu a fuko la Dani, malo amene anali pakati pa Zora ndi Esitaoli.
I počal ho Duch Hospodinův ponoukati v Mahane Dan, mezi Zaraha a Estaol.