< Oweruza 12 >
1 Gulu la nkhondo la fuko la Efereimu linayitanidwa ndipo anawolokera ku Zafoni nakafunsa Yefita kuti, “Nʼchifukwa chiyani unawoloka kukachita nkhondo ndi Aamoni osatiyitana kuti tipite nawe? Ife tikutenthera mʼnyumba mwakomu.”
Možje iz Efrájima so se zbrali skupaj in odšli proti severu in rekli Jefteju: »Zakaj prehajaš preko, da se boriš zoper Amónove otroke, nas pa nisi poklical, da gremo s teboj? Nad teboj bomo tvojo hišo požgali z ognjem.«
2 Yefita anayankha kuti, “Ine ndi anthu anga tinakangana kwambiri ndi Aamoni. Ndinakuyitanani koma inu simunandipulumutse mʼmanja mwawo.
Jefte jim je rekel: »Jaz in moje ljudstvo smo bili v velikem boju z Amónovimi otroki in ko sem vas poklical, me niste osvobodili iz njihovih rok.
3 Nditaona kuti simundithandiza, ndinayika moyo wanga pa chiswe ndipo ndinawoloka kukachita nkhondo ndi a Aamoni. Yehova anandithandiza ndipo ndinawagonjetsa. Nanga nʼchifukwa chiyani mwabwera kwa ine lero kuti muchite nane nkhondo?”
Ko sem videl, da me niste osvobodili, sem svoje življenje vzel v svoje roke in šel preko, proti Amónovim otrokom in Gospod jih je izročil v mojo roko. Zakaj ste torej vi ta dan prišli gor do mene, da se borite zoper mene?«
4 Choncho Yefita anasonkhanitsa anthu a ku Giliyadi ndi kuchita nkhondo ndi Aefereimu. Ndipo Agiliyadi anagonjetsa Aefereimu chifukwa Aefereimuwo amati, “Inu a Giliyadi ndinu othawa kuchokera ku Efereimu ndi pakati pa Amanase.”
Potem je Jefte zbral skupaj vse gileádske može in se bojeval z Efrájimom in gileádski možje so udarili Efrájim, ker so rekli: »Vi Gileádčani ste ubežniki iz Efrájima med Efrájimci in Manásejci.«
5 Choncho Agiliyadi analanda Aefereimu madooko a mtsinje wa Yorodani. Munthu aliyense wothawa ku Efereimu amati akanena kuti, “Ndiloleni ndiwoloke,” Agaliyadi ankafunsa kuti, “Kodi ndiwe mu Efurati?” Ngati iye ayankha kuti, “Ayi”
Gileádčani so pred Efrájimci zavzeli jordanske prehode. In bilo je tako, da ko so tisti Efrájimci, ki so pobegnili, rekli: »Naj grem preko, « da so mu gileádski možje rekli: » Ali si Efrájimec?« Če je rekel: »Ne, «
6 Ndiye amamuwuza kuti, “Nena kuti ‘Shiboleti.’” Tsono munthuyo akanena kuti Siboleti popeza samatha kutchula bwino mawuwa, ankamugwira ndi kumupha pomwepo pa madooko a mtsinje wa Yorodani. Nthawi imeneyo anaphedwa Aefereimu 42,000.
potem so mu rekli: »Reci sedaj Šibólet« in je rekel »Sibólet, « kajti tega ni mogel pravilno naglasiti. Potem so ga prijeli in usmrtil pri jordanskih prehodih in tam jih je ob tistem času izmed Efrájimcev padlo dvainštirideset tisoč.
7 Yefita anatsogolera Israeli zaka zisanu ndi chimodzi. Kenaka Yefita wa ku Giliyadi anamwalira, ndipo anayikidwa mu mzinda wake ku Giliyadi.
Jefte je Izraelu sodil šest let. Potem je Gileádčan Jefte umrl in bil pokopan v enem izmed mest Gileáda.
8 Atamwalira Yefita, Ibizani wa ku Betelehemu anatsogolera Israeli.
Za njim je Izraelu sodil Ibcán iz Betlehema.
9 Iye anali ndi ana aamuna makumi atatu ndi ana aakazi makumi atatu. Anakwatitsa ana ake akaziwo kwa anthu a fuko lina, ndipo ana ake aamuna aja anawabweretsera atsikana makumi atatu kuti awakwatire amenenso anali a fuko lina. Ibizani anatsogolera Israeli kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
Ta je imel trideset sinov in trideset hčera, ki jih je poslal naokrog in za svoje sinove je vzel trideset hčera od drugod. Izraelu je sodil sedem let.
10 Kenaka Ibizani anamwalira, ndipo anayikidwa mu Betelehemu.
Potem je Ibcán umrl in je bil pokopan pri Betlehemu.
11 Iye atamwalira, Eloni wa fuko la Zebuloni anakhala mtsogoleri wa Aisraeli, ndipo anatsogolera Aisraeli kwa zaka khumi.
Za njim je Izraelu sodil Zábulonec Elón. Izraelu je sodil deset let.
12 Kenaka Eloni anamwalira ndipo anayikidwa ku Ayaloni mʼdziko la Zebuloni.
Zábulonec Elón je umrl in je bil pokopan v Ajalónu, v deželi Zábulon.
13 Iye atamwalira, Abidoni mwana wa Hilelo wochokera ku Piratoni, anatsogolera Israeli.
Za njim je Izraelu sodil Abdón, sin Piratónca Hiléla.
14 Iye anali ndi ana aamuna makumi anayi ndi zidzukulu makumi atatu, amene ankakwera pa abulu 70. Iye anatsogolera Israeli kwa zaka zisanu ndi zitatu.
Ta je imel štirideset sinov in trideset nečakov, ki so jahali na sedemdesetih osličjih žrebetih. Izraelu je sodil osem let.
15 Ndipo Abidoni mwana wa Hilelo Mpiratoni uja anamwalira, nayikidwa ku Piratoni, mʼdziko la Efereimu, dziko lamapiri la Aamaleki.
Abdón, sin Piratónca Hiléla, je umrl in je bil pokopan v Piratónu, v deželi Efrájim, na gori Amalečanov.