< Oweruza 12 >

1 Gulu la nkhondo la fuko la Efereimu linayitanidwa ndipo anawolokera ku Zafoni nakafunsa Yefita kuti, “Nʼchifukwa chiyani unawoloka kukachita nkhondo ndi Aamoni osatiyitana kuti tipite nawe? Ife tikutenthera mʼnyumba mwakomu.”
و مردان افرایم جمع شده، به طرف شمال گذشتند، و به یفتاح گفتند: «چرابرای جنگ کردنت با بنی عمون رفتی و ما رانطلبیدی تا همراه تو بیاییم؟ پس خانه تو را بر سرتو خواهیم سوزانید.»۱
2 Yefita anayankha kuti, “Ine ndi anthu anga tinakangana kwambiri ndi Aamoni. Ndinakuyitanani koma inu simunandipulumutse mʼmanja mwawo.
و یفتاح به ایشان گفت: «مرا و قوم مرا با بنی عمون جنگ سخت می‌بود، وچون شما را خواندم مرا از دست ایشان رهایی ندادید.۲
3 Nditaona kuti simundithandiza, ndinayika moyo wanga pa chiswe ndipo ndinawoloka kukachita nkhondo ndi a Aamoni. Yehova anandithandiza ndipo ndinawagonjetsa. Nanga nʼchifukwa chiyani mwabwera kwa ine lero kuti muchite nane nkhondo?”
پس چون دیدم که شما مرا رهایی نمی دهید جان خود را به‌دست خود گرفته، به سوی بنی عمون رفتم و خداوند ایشان را به‌دست من تسلیم نمود، پس چرا امروز نزد من برآمدید تابا من جنگ نمایید؟»۳
4 Choncho Yefita anasonkhanitsa anthu a ku Giliyadi ndi kuchita nkhondo ndi Aefereimu. Ndipo Agiliyadi anagonjetsa Aefereimu chifukwa Aefereimuwo amati, “Inu a Giliyadi ndinu othawa kuchokera ku Efereimu ndi pakati pa Amanase.”
پس یفتاح تمامی مردان جلعاد را جمع کرده، با افرایم جنگ نمود و مردان جلعاد افرایم را شکست دادند، چونکه گفته بودندای اهل جلعاد شما فراریان افرایم در میان افرایم و در میان منسی هستید.۴
5 Choncho Agiliyadi analanda Aefereimu madooko a mtsinje wa Yorodani. Munthu aliyense wothawa ku Efereimu amati akanena kuti, “Ndiloleni ndiwoloke,” Agaliyadi ankafunsa kuti, “Kodi ndiwe mu Efurati?” Ngati iye ayankha kuti, “Ayi”
و اهل جلعاد معبرهای اردن را پیش روی افرایم گرفتند و واقع شد که چون یکی از گریزندگان افرایم می‌گفت: «بگذارید عبور نمایم.» اهل جلعاد می‌گفتند: «آیاتو افرایمی هستی؟» و اگر می‌گفت نی،۵
6 Ndiye amamuwuza kuti, “Nena kuti ‘Shiboleti.’” Tsono munthuyo akanena kuti Siboleti popeza samatha kutchula bwino mawuwa, ankamugwira ndi kumupha pomwepo pa madooko a mtsinje wa Yorodani. Nthawi imeneyo anaphedwa Aefereimu 42,000.
پس او رامی گفتند: بگو شبولت، و او می‌گفت سبولت، چونکه نمی توانست به درستی تلفظ نماید، پس او را گرفته، نزد معبرهای اردن می‌کشتند، و در آن وقت چهل و دو هزار نفر از افرایم کشته شدند.۶
7 Yefita anatsogolera Israeli zaka zisanu ndi chimodzi. Kenaka Yefita wa ku Giliyadi anamwalira, ndipo anayikidwa mu mzinda wake ku Giliyadi.
و یفتاح بر اسرائیل شش سال داوری نمود. پس یفتاح جلعادی وفات یافته، در یکی ازشهرهای جلعاد دفن شد.۷
8 Atamwalira Yefita, Ibizani wa ku Betelehemu anatsogolera Israeli.
و بعد از او ابصان بیت لحمی بر اسرائیل داوری نمود.۸
9 Iye anali ndi ana aamuna makumi atatu ndi ana aakazi makumi atatu. Anakwatitsa ana ake akaziwo kwa anthu a fuko lina, ndipo ana ake aamuna aja anawabweretsera atsikana makumi atatu kuti awakwatire amenenso anali a fuko lina. Ibizani anatsogolera Israeli kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
و او را سی پسر بود و سی دختر که بیرون فرستاده بود و از بیرون سی دختر برای پسران خود آورد و هفت سال بر اسرائیل داوری نمود.۹
10 Kenaka Ibizani anamwalira, ndipo anayikidwa mu Betelehemu.
و ابصان مرد و در بیت لحم دفن شد.۱۰
11 Iye atamwalira, Eloni wa fuko la Zebuloni anakhala mtsogoleri wa Aisraeli, ndipo anatsogolera Aisraeli kwa zaka khumi.
وبعد از او ایلون زبولونی بر اسرائیل داوری نمود وداوری او بر اسرائیل ده سال بود.۱۱
12 Kenaka Eloni anamwalira ndipo anayikidwa ku Ayaloni mʼdziko la Zebuloni.
و ایلون زبولونی مرد و در ایلون در زمین زبولون دفن شد.۱۲
13 Iye atamwalira, Abidoni mwana wa Hilelo wochokera ku Piratoni, anatsogolera Israeli.
و بعد از او عبدون بن هلیل فرعتونی براسرائیل داوری نمود.۱۳
14 Iye anali ndi ana aamuna makumi anayi ndi zidzukulu makumi atatu, amene ankakwera pa abulu 70. Iye anatsogolera Israeli kwa zaka zisanu ndi zitatu.
و او را چهل پسر و سی نواده بود، که بر هفتاد کره الاغ سوار می‌شدند وهشت سال بر اسرائیل داوری نمود.۱۴
15 Ndipo Abidoni mwana wa Hilelo Mpiratoni uja anamwalira, nayikidwa ku Piratoni, mʼdziko la Efereimu, dziko lamapiri la Aamaleki.
و عبدون بن هلیل فرعتونی مرد و در فرعتون در زمین افرایم در کوهستان عمالیقیان دفن شد.۱۵

< Oweruza 12 >