< Oweruza 12 >

1 Gulu la nkhondo la fuko la Efereimu linayitanidwa ndipo anawolokera ku Zafoni nakafunsa Yefita kuti, “Nʼchifukwa chiyani unawoloka kukachita nkhondo ndi Aamoni osatiyitana kuti tipite nawe? Ife tikutenthera mʼnyumba mwakomu.”
Nifanontoñe o nte-Efraimeo naho nimb’e Tsafone mb’eo, nanao ty hoe amy Ieftake, Ino ty nitsaha’ areo mb’eo hialia’o amo nte-Amoneo f’ie tsy nitoka anay hindreza’ay? Ho forototoe’ay añ’ afo ama’o ty anjomba’o.
2 Yefita anayankha kuti, “Ine ndi anthu anga tinakangana kwambiri ndi Aamoni. Ndinakuyitanani koma inu simunandipulumutse mʼmanja mwawo.
Le hoe ty natoi’ Ieftake am’ iareo, Toe niampohek’ amo ana’ i Amoneo naho ondatiko iraho te nikanjy anahareo, f’ie tsy nañaro ahy am-pità’ iareo.
3 Nditaona kuti simundithandiza, ndinayika moyo wanga pa chiswe ndipo ndinawoloka kukachita nkhondo ndi a Aamoni. Yehova anandithandiza ndipo ndinawagonjetsa. Nanga nʼchifukwa chiyani mwabwera kwa ine lero kuti muchite nane nkhondo?”
Aa kanao tsy narova’ areo le namoeako fiay nitsake mb’ amo ana’ i Amoneo mb’eo, vaho natolo’ Iehovà an-tañako. Aa le ino ty nitroara’ areo amako androany hialia’ areo?
4 Choncho Yefita anasonkhanitsa anthu a ku Giliyadi ndi kuchita nkhondo ndi Aefereimu. Ndipo Agiliyadi anagonjetsa Aefereimu chifukwa Aefereimuwo amati, “Inu a Giliyadi ndinu othawa kuchokera ku Efereimu ndi pakati pa Amanase.”
Natonto’ Ieftake o lahilahi’ i Gilade iabio naho nialy amy Efraime; vaho linafa’ o nte-Giladeo t’i Efraime, ami’ty natao’ iareo ty hoe: Ondaty gike e Efraime nahareo nte Gilade añivo’ i Efraime naho i Menasè ao.
5 Choncho Agiliyadi analanda Aefereimu madooko a mtsinje wa Yorodani. Munthu aliyense wothawa ku Efereimu amati akanena kuti, “Ndiloleni ndiwoloke,” Agaliyadi ankafunsa kuti, “Kodi ndiwe mu Efurati?” Ngati iye ayankha kuti, “Ayi”
Rinambe’ o nte-Giladeo amy Efraime o fitsaha’ Iordaney boake Efraimeo, ie amy zao naho teo ty nipoliotse amo nte-Efraimeo nanao ty hoe: Ehe angao hi­tsake? Le nañontane aze o nte-Giladeo ty hoe: nte Efraime hao? Aa naho Tsie ty natao’e;
6 Ndiye amamuwuza kuti, “Nena kuti ‘Shiboleti.’” Tsono munthuyo akanena kuti Siboleti popeza samatha kutchula bwino mawuwa, ankamugwira ndi kumupha pomwepo pa madooko a mtsinje wa Yorodani. Nthawi imeneyo anaphedwa Aefereimu 42,000.
le nanoe’ iareo ama’e ty hoe: Ano ty hoe: Sibolete, te mone nanao ty hoe Tsibolete—ie toe tsy nahafanoñoñe’e—le nitsepaheñe vaho vinono’ iareo amo fitsaha’ Iordaneio; nte Efraime efats’ ale-tsi-ro’ arivo ty nikorovoke henane zay.
7 Yefita anatsogolera Israeli zaka zisanu ndi chimodzi. Kenaka Yefita wa ku Giliyadi anamwalira, ndipo anayikidwa mu mzinda wake ku Giliyadi.
Enen-taoñe ty nizakà’ Ieftake Israele, le nivilasy t’Ieftake nte-Gilade, vaho nalentek’ an-drova’ o nte-Giladeo.
8 Atamwalira Yefita, Ibizani wa ku Betelehemu anatsogolera Israeli.
Nanonjohy aze, t’Ibtsane nte-Betlekheme nizaka ­Israele.
9 Iye anali ndi ana aamuna makumi atatu ndi ana aakazi makumi atatu. Anakwatitsa ana ake akaziwo kwa anthu a fuko lina, ndipo ana ake aamuna aja anawabweretsera atsikana makumi atatu kuti awakwatire amenenso anali a fuko lina. Ibizani anatsogolera Israeli kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
Nanañ’ anadahy telo-polo re naho anak’ ampela telopolo naho naondra’e añe vaho nampimoahe’e boak’ añe ka ty anak’ ampela ho a o ana-dahi’eo. Nizaka Israele fito taoñe
10 Kenaka Ibizani anamwalira, ndipo anayikidwa mu Betelehemu.
le nivilasy t’Ib­tsane, vaho nalenteke e Betlekheme ao.
11 Iye atamwalira, Eloni wa fuko la Zebuloni anakhala mtsogoleri wa Aisraeli, ndipo anatsogolera Aisraeli kwa zaka khumi.
Ie añe le nizaka Israele folo taoñe t’i Elone nte-Zebolone.
12 Kenaka Eloni anamwalira ndipo anayikidwa ku Ayaloni mʼdziko la Zebuloni.
Ie nihomake t’i Elone nte-Zebolone, le nalenteke Aialone an-tane Zebolone ao.
13 Iye atamwalira, Abidoni mwana wa Hilelo wochokera ku Piratoni, anatsogolera Israeli.
Nanonjohy aze nizaka Israele t’i Abdone ana’ i Mpandrenge nte-Piratone.
14 Iye anali ndi ana aamuna makumi anayi ndi zidzukulu makumi atatu, amene ankakwera pa abulu 70. Iye anatsogolera Israeli kwa zaka zisanu ndi zitatu.
Nanañ’ana-dahy efa-polo re naho afe telo-polo mpiningitse ana-borìke fitom-polo, nizaka valo taoñe.
15 Ndipo Abidoni mwana wa Hilelo Mpiratoni uja anamwalira, nayikidwa ku Piratoni, mʼdziko la Efereimu, dziko lamapiri la Aamaleki.
Nivilasy t’i Abdone ana’ i Mpandrenge nte-Piratone vaho nalenteke e Piratone an-tane Efraime am-bohi’ i Amaleke ao.

< Oweruza 12 >