< Oweruza 12 >

1 Gulu la nkhondo la fuko la Efereimu linayitanidwa ndipo anawolokera ku Zafoni nakafunsa Yefita kuti, “Nʼchifukwa chiyani unawoloka kukachita nkhondo ndi Aamoni osatiyitana kuti tipite nawe? Ife tikutenthera mʼnyumba mwakomu.”
Mais voilà que dans Ephraïm s’éleva une sédition; car les hommes de cette tribu passant vers l’aquilon, dirent à Jephté: Pourquoi marchant au combat contre les enfants d’Ammon, n’as-tu pas voulu nous appeler, afin que nous allassions avec toi? Aussi incendierons-nous ta maison.
2 Yefita anayankha kuti, “Ine ndi anthu anga tinakangana kwambiri ndi Aamoni. Ndinakuyitanani koma inu simunandipulumutse mʼmanja mwawo.
Jephté leur répondit: Nous avions un grand débat moi et mon peuple Contre les enfants d’Ammon; je vous ai appelés, pour me donner du secours, et vous ne l’avez pas Voulu faire.
3 Nditaona kuti simundithandiza, ndinayika moyo wanga pa chiswe ndipo ndinawoloka kukachita nkhondo ndi a Aamoni. Yehova anandithandiza ndipo ndinawagonjetsa. Nanga nʼchifukwa chiyani mwabwera kwa ine lero kuti muchite nane nkhondo?”
Ce que voyant, j’ai mis mon âme en mes mains, j’ai passé chez les enfants d’Ammon, et le Seigneur les a livrés en mes mains. En quoi ai-je mérité que vous vous éleviez contre moi pour me faire la guerre?
4 Choncho Yefita anasonkhanitsa anthu a ku Giliyadi ndi kuchita nkhondo ndi Aefereimu. Ndipo Agiliyadi anagonjetsa Aefereimu chifukwa Aefereimuwo amati, “Inu a Giliyadi ndinu othawa kuchokera ku Efereimu ndi pakati pa Amanase.”
C’est pourquoi ayant appelé à lui tous les hommes de Galaad, il combattit contre Ephraïm: et les hommes de Galaad battirent Ephraïm, parce qu’il avait dit: Galaad est un fugitif d’Ephraïm, et il habite au milieu d’Ephraïm et de Manassé.
5 Choncho Agiliyadi analanda Aefereimu madooko a mtsinje wa Yorodani. Munthu aliyense wothawa ku Efereimu amati akanena kuti, “Ndiloleni ndiwoloke,” Agaliyadi ankafunsa kuti, “Kodi ndiwe mu Efurati?” Ngati iye ayankha kuti, “Ayi”
Et les Galaadites occupèrent les gués du Jourdain, par lesquels Ephraïm devait revenir; et lorsqu’il y venait quelqu’un de l’armée d’Ephraïm, fuyant, et qu’il disait: Je vous conjure de me permettre de passer, les Galaadites lui répondaient: Est-ce que tu es Ephrathéen? lequel disant: Je ne le suis pas,
6 Ndiye amamuwuza kuti, “Nena kuti ‘Shiboleti.’” Tsono munthuyo akanena kuti Siboleti popeza samatha kutchula bwino mawuwa, ankamugwira ndi kumupha pomwepo pa madooko a mtsinje wa Yorodani. Nthawi imeneyo anaphedwa Aefereimu 42,000.
Ils lui demandaient: Dis donc Schibboleth, ce qu’on interprète par Epi. Il répondait Sibboleth, ne pouvant pas exprimer épi avec la même lettre. Et aussitôt, après l’avoir saisi, on regorgeait au passage même du Jourdain. Or, il périt en ce temps quarante-deux mille hommes d’Ephraïm.
7 Yefita anatsogolera Israeli zaka zisanu ndi chimodzi. Kenaka Yefita wa ku Giliyadi anamwalira, ndipo anayikidwa mu mzinda wake ku Giliyadi.
Ainsi, Jephté Galaadite jugea Israël pendant six ans; et il mourut et fut enseveli dans sa ville de Galaad.
8 Atamwalira Yefita, Ibizani wa ku Betelehemu anatsogolera Israeli.
Après lui Abésan de Bethléhem jugea Israël.
9 Iye anali ndi ana aamuna makumi atatu ndi ana aakazi makumi atatu. Anakwatitsa ana ake akaziwo kwa anthu a fuko lina, ndipo ana ake aamuna aja anawabweretsera atsikana makumi atatu kuti awakwatire amenenso anali a fuko lina. Ibizani anatsogolera Israeli kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
Il eut trente fils et autant de filles, qu’il maria, les établissant hors de chez lui; et il reçut pour ses fils des femmes en même nombre, les admettant dans sa maison. Abésan jugea Israël pendant sept ans;
10 Kenaka Ibizani anamwalira, ndipo anayikidwa mu Betelehemu.
Et il mourut et fut enseveli à Bethléhem.
11 Iye atamwalira, Eloni wa fuko la Zebuloni anakhala mtsogoleri wa Aisraeli, ndipo anatsogolera Aisraeli kwa zaka khumi.
À Abésan succéda Ahialon Zabulonite; et il jugea Israël pendant dix ans;
12 Kenaka Eloni anamwalira ndipo anayikidwa ku Ayaloni mʼdziko la Zebuloni.
Et il mourut et fut enseveli dans Zabulon.
13 Iye atamwalira, Abidoni mwana wa Hilelo wochokera ku Piratoni, anatsogolera Israeli.
Après lui, Abdon, fils d’Illel, Pharathonite, jugea Israël;
14 Iye anali ndi ana aamuna makumi anayi ndi zidzukulu makumi atatu, amene ankakwera pa abulu 70. Iye anatsogolera Israeli kwa zaka zisanu ndi zitatu.
Il eut quarante fils, et d’eux trente petits-fils, qui montaient sur soixante-dix poulains d’ânesses; et il jugea Israël pendant huit ans;
15 Ndipo Abidoni mwana wa Hilelo Mpiratoni uja anamwalira, nayikidwa ku Piratoni, mʼdziko la Efereimu, dziko lamapiri la Aamaleki.
Et il mourut et fut enseveli à Pharathon de la terre d’Ephraïm, sur la montagne d’Amalec.

< Oweruza 12 >