< Oweruza 12 >

1 Gulu la nkhondo la fuko la Efereimu linayitanidwa ndipo anawolokera ku Zafoni nakafunsa Yefita kuti, “Nʼchifukwa chiyani unawoloka kukachita nkhondo ndi Aamoni osatiyitana kuti tipite nawe? Ife tikutenthera mʼnyumba mwakomu.”
The men of the tribe of Ephraim summoned their soldiers, and they crossed [the Jordan River] to [the town of] Zaphon [to talk with] Jephthah. They said to him, “(Why did you not ask us for help?/You should have requested us) to help your army fight the Ammon people-group. So we will burn down your house while you are in it.”
2 Yefita anayankha kuti, “Ine ndi anthu anga tinakangana kwambiri ndi Aamoni. Ndinakuyitanani koma inu simunandipulumutse mʼmanja mwawo.
Jephthah replied, “The Ammon people-group were oppressing us greatly. When we were prepared to start to attack them, I requested you to come and help us, but you refused. My men and I defeated the Ammon people-group, but you did not help us.
3 Nditaona kuti simundithandiza, ndinayika moyo wanga pa chiswe ndipo ndinawoloka kukachita nkhondo ndi a Aamoni. Yehova anandithandiza ndipo ndinawagonjetsa. Nanga nʼchifukwa chiyani mwabwera kwa ine lero kuti muchite nane nkhondo?”
When I saw that you would not help us, I was willing to be killed in the battle against the Ammon people-group. But Yahweh helped us to defeat them. [You did not help us when we requested it before], so (why have you come here today to fight against me?/you should not have come here today to fight against me.)” [RHQ]
4 Choncho Yefita anasonkhanitsa anthu a ku Giliyadi ndi kuchita nkhondo ndi Aefereimu. Ndipo Agiliyadi anagonjetsa Aefereimu chifukwa Aefereimuwo amati, “Inu a Giliyadi ndinu othawa kuchokera ku Efereimu ndi pakati pa Amanase.”
Then Jephthah summoned the men of [the] Gilead [region] to fight [against the men of the tribe of] Ephraim. The men of the tribe of Ephraim said, “You men from [the] Gilead [region] are men who deserted us. Long ago you left us and moved to the area between our tribe and the tribe of Manasseh.” [Because of their saying that], the men of [the] Gilead [region] attacked the men of the tribe of Ephraim.
5 Choncho Agiliyadi analanda Aefereimu madooko a mtsinje wa Yorodani. Munthu aliyense wothawa ku Efereimu amati akanena kuti, “Ndiloleni ndiwoloke,” Agaliyadi ankafunsa kuti, “Kodi ndiwe mu Efurati?” Ngati iye ayankha kuti, “Ayi”
The men of Gilead captured that (ford/place where people can walk across) at the Jordan [River] to go to the land where the tribe of Ephraim live. Whenever one of the soldiers from the tribe of Ephraim came to the ford to try to escape, he would say, “Let me cross the river.” Then the men of Gilead would ask him, “Are you from the tribe of Ephraim?” If he said “No,”
6 Ndiye amamuwuza kuti, “Nena kuti ‘Shiboleti.’” Tsono munthuyo akanena kuti Siboleti popeza samatha kutchula bwino mawuwa, ankamugwira ndi kumupha pomwepo pa madooko a mtsinje wa Yorodani. Nthawi imeneyo anaphedwa Aefereimu 42,000.
they would say to him, “Say the word ‘Shibboleth’.” The men of Ephraim could not pronounce that word correctly. So if the person from the tribe of Ephraim said ‘Sibboleth’, [they would know that he was lying and that he was really from the tribe of Ephraim, and] they would kill him there at the ford. So the men of Gilead killed 42,000 people from the tribe of Ephraim at that time.
7 Yefita anatsogolera Israeli zaka zisanu ndi chimodzi. Kenaka Yefita wa ku Giliyadi anamwalira, ndipo anayikidwa mu mzinda wake ku Giliyadi.
Jephthah, the man from [the] Gilead [region], was a leader of the Israeli people for six years. Then he died and was buried in a town in [the] Gilead [region].
8 Atamwalira Yefita, Ibizani wa ku Betelehemu anatsogolera Israeli.
After Jephthah died, a man named Ibzan, from Bethlehem, became the leader of the Israeli people.
9 Iye anali ndi ana aamuna makumi atatu ndi ana aakazi makumi atatu. Anakwatitsa ana ake akaziwo kwa anthu a fuko lina, ndipo ana ake aamuna aja anawabweretsera atsikana makumi atatu kuti awakwatire amenenso anali a fuko lina. Ibizani anatsogolera Israeli kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
He had 30 sons and 30 daughters. He forced all his daughters to marry men who were not in his clan, and brought women from outside his clan to marry his sons. He was the leader of the Israeli people for seven years.
10 Kenaka Ibizani anamwalira, ndipo anayikidwa mu Betelehemu.
When he died, he was buried in Bethlehem.
11 Iye atamwalira, Eloni wa fuko la Zebuloni anakhala mtsogoleri wa Aisraeli, ndipo anatsogolera Aisraeli kwa zaka khumi.
After Ibzan died, a man named Elon, from the tribe of Zebulun, became the leader of the Israeli people. He was their leader for ten years.
12 Kenaka Eloni anamwalira ndipo anayikidwa ku Ayaloni mʼdziko la Zebuloni.
Then he died and was buried in Aijalon [city] in the area where the tribe of Zebulun lives.
13 Iye atamwalira, Abidoni mwana wa Hilelo wochokera ku Piratoni, anatsogolera Israeli.
After Elon died, a man named Abdon who was the son of Hillel, from Pirathon [city, in the area where the tribe of Ephraim live] became the leader of the Israeli people.
14 Iye anali ndi ana aamuna makumi anayi ndi zidzukulu makumi atatu, amene ankakwera pa abulu 70. Iye anatsogolera Israeli kwa zaka zisanu ndi zitatu.
He had 40 sons and 30 grandsons. Each of them had his own donkey on which to ride. Abdon was the leader of the Israeli people for eight years.
15 Ndipo Abidoni mwana wa Hilelo Mpiratoni uja anamwalira, nayikidwa ku Piratoni, mʼdziko la Efereimu, dziko lamapiri la Aamaleki.
When Abdon died, he was buried in Pirathon, in the hilly area where the descendants of Amalek lived previously, [but now it is the area where the tribe of Ephraim lives].

< Oweruza 12 >