< Oweruza 11 >

1 Yefita wa ku Giliyadi anali wankhondo wa mphamvu. Iyeyu amayi ake anali mkazi wachiwerewere, ndipo abambo ake anali Giliyadi.
А Јефтај од Галада беше храбар јунак, али син једне курве, с којом Галад роди Јефтаја.
2 Mkazi wake wa Giliyadi anabereka naye ana aamuna. Tsono ana amenewa atakula anapirikitsa Yefita ndi kumuwuza kuti, “Sudzalandirako cholowa mʼnyumba ya abambo athu chifukwa ndiwe mwana wa mkazi wina.”
Али Галаду и жена његова роди синове, па кад дорастоше синови те жене, отераше Јефтаја рекавши му: Нећеш имати наследство у дому оца нашег, јер си син друге жене.
3 Choncho Yefita anathawa kuchoka kwa abale ake ndi kukakhala mʼdziko la Tobu. Kumeneko anakakopa ndi kusonkhanitsa anthu achabechabe ndipo anatuluka pamodzi kukasakaza zinthu.
Зато побеже Јефтај од браће своје, и настани се у земљи Тову; и стекоше се к њему људи празнови, и иђаху с њим.
4 Patapita nthawi Aamoni anadzachita nkhondo ndi Israeli.
А после неког времена завојштише синови Амонови на Израиља;
5 Tsono pamene Aamoni ankathira nkhondo Aisraeli, akuluakulu a ku Giliyadi anapita kukamutenga Yefita ku dziko la Tobu.
И кад завојштише синови Амонови на Израиља, отидоше старешине галадске да доведу Јефтаја из земље Това.
6 Iwo anati kwa iye, “Bwera ukhale mkulu wathu wankhondo kuti timenyane ndi Amoni.”
И рекоше Јефтају: Ходи и буди нам војвода, да војујемо са синовима Амоновим.
7 Yefita anawawuza Agiliyadi kuti, “Kodi inu suja munkadana nane ndi kundithamangitsa ku nyumba ya abambo anga? Nʼchifukwa chiyani lero mwabwera kwa ine pamene muli pa mavuto?”
А Јефтај рече старешинама галадским: Не мрзите ли ви на ме, и не истерасте ли ме из дома оца мог? Што сте дакле дошли к мени сада кад сте у невољи?
8 Akuluakulu a ku Giliyadi aja anamuyankha kuti, “Chimene tabwerera kwa iwe ndi chakuti upite nafe kukamenyana ndi Aamoni, ndipo udzakhala wolamulira wa onse okhala mu Giliyadi.”
А старешине галадске рекоше Јефтају: Зато смо сада дошли опет к теби да пођеш с нама и да војујеш са синовима Амоновим и да нам будеш поглавар свима који живимо у Галаду.
9 Yefita anawayankha akuluakulu a ku Giliyadi kuti, “Ngati mundibwezeranso kwathu kuti ndikachite nkhondo ndi Aamoni ndipo Yehova nʼkukandithandiza kuwagonjetsa, ndidzakhaladi wokulamulirani?”
А Јефтај рече старешинама галадским: Кад хоћете да ме одведете натраг да војујем са синовима Амоновим, ако ми их да Господ, хоћу ли вам бити поглавар?
10 Akuluakulu a ku Giliyadi anamuyankha kuti, “Yehova akhale mboni pakati pa inu ndi ife, ngati sitidzachita monga mwa mawu anu.”
А старешине галадске рекоше Јефтају: Господ нека буде сведок међу нама, ако не учинимо како си казао.
11 Choncho Yefita anapita nawo akuluakulu a ku Giliyadi aja, ndipo anthu a kumeneko anamusandutsa kukhala wowalamulira ndi mkulu wankhondo. Tsono Yefita anabwerezanso mawu omwewa pamaso pa Yehova ku Mizipa.
Тада отиде Јефтај са старешинама галадским, и народ га постави поглаварем и војводом над собом: и Јефтај изговори пред Господом у Миспи све речи које беше рекао.
12 Kenaka Yefita anatuma amithenga kwa mfumu ya Aamoni ndi funso lakuti, “Kodi ife takuchimwirani chiyani kuti muzichita nkhondo ndi dziko langa?”
Потом посла Јефтај посланике к цару синова Амонових, и поручи: Шта имаш ти са мном, те си допао к мени да ратујеш по мојој земљи?
13 Ndipo mfumu ya Aamoni inayankha amithenga a Yefita aja kuti, “Pamene Israeli amatuluka kuchokera mu Igupto, analanda dziko langa kuyambira ku mtsinje wa Arinoni mpaka ku mtsinje wa Yaboki mpakanso ku mtsinje wa Yorodani. Tsopano mundibwezere dziko langa mwamtendere.”
А цар синова Амонових рече посланицима Јефтајевим: Што је узео Израиљ моју земљу кад дође из Мисира, од Ариона до Јавока и до Јордана; сада дакле врати ми је с миром.
14 Yefita anatumizanso amithenga akewo kwa mfumu ya Aamoni
Али Јефтај посла опет посланике к цару синова Амонових.
15 kukanena kuti, Yefita akuti, “Israeli sanalande dziko la Mowabu kapena dziko la Aamoni.
И поручи му: Овако вели Јефтај: Није узео Израиљ земље моавске ни земље синова Амонових.
16 Koma pamene Aisraeli ankachoka ku Igupto anadzera njira ya ku chipululu mpaka ku Nyanja Yofiira nakafika ku Kadesi.
Него изашавши из Мисира пређе Израиљ преко пустиње до Црвеног Мора и дође до Кадиса.
17 Kenaka Israeli anatumiza amithenga kwa mfumu ya ku Edomu kuti, ‘Chonde tiloleni kuti tidutse mʼdziko lanu,’ Koma mfumu ya ku Edomu sinamvere zimenezo. Aisraeli anatumizanso amithenga kwa mfumu ya ku Mowabu, ndipo iyo inakananso. Choncho Israeli anakhala ku Kadesi.
И посла Израиљ посланике к цару едомском и рече: Пусти да прођем кроз твоју земљу. Али не послуша цар едомски. Посла такође к цару моавском: , али ни он не хте. И тако стаја Израиљ у Кадису.
18 “Pambuyo pake, Aisraeli ananyamuka ulendo kudzera ku chipululu nazungulira dziko la Edomu ndi dziko la Mowabu, ndipo anafika ku mmawa kwa dziko la Mowabu ndi kumanga zinthando zawo ku mbali ina ya mtsinje wa Arinoni. Iwo sanalowe mʼdziko la Mowabu, chifukwa mtsinje wa Arinoni ndiwo unali malire a dziko la Mowabu.
Потом идући преко пустиње обиђе земљу едомску и земљу моавску, и дошавши с Истока земљи моавској стаде у логор с оне стране Ариона; али не пређоше преко међе моавске, јер Арион беше међа моавска.
19 “Pambuyo pake Israeli anatumiza amithenga kwa Sihoni mfumu ya Aamori, amene amalamulira ku Hesiboni ndipo anati kwa iye, ‘Chonde tiloleni kuti tidutse mʼdziko lanu popita kwathu.’
Него посла Израиљ посланике к Сиону цару аморејском, цару есевонском, и рече му Израиљ; допусти нам да прођемо кроз твоју земљу до свог места.
20 Koma Sihoni sanalole Israeli kuti adzere mʼdziko mwake. Mʼmalo mwake Sihoni anasonkhanitsa ankhondo ake onse nakamanga msasa ku Yahazi ndipo anachita nkhondo ndi Israeli.
Али Сион не верова Израиљу да га пусти да пређе преко међе његове, него Сион скупи сав свој народ и стадоше у логор у Јаси, и поби се са Израиљем.
21 “Koma Yehova Mulungu wa Israeli anamupereka Sihoni pamodzi ndi anthu ake onse mʼmanja mwa Israeli, ndipo anawagonjetsa. Choncho Aisraeli analanda dziko lonse la Aamori amene amakhala mʼdzikolo.
А Господ Бог Израиљев предаде Сиона и сав народ његов у руке синовима Израиљевим, те их побише; и зароби Израиљ сву земљу Амореја, који живљаху у оној земљи.
22 Analanda dziko lonse kuchokera ku Arinoni mpaka ku Yaboki ndiponso kuchokera ku chipululu mpaka ku mtsinje wa Yorodani.
Задобише сву земљу аморејску од Ариона до Јавока, и од пустиње до Јордана.
23 “Ndiye kuti Yehova Mulungu wa Aisraeli ndiye analanda dziko la Aamori, kuwalandirira anthu ake. Kodi inu mukufuna kutilanda dzikolo?
Тако је дакле Господ Бог Израиљев отерао Амореје испред народа свог Израиља, па ти ли хоћеш да је земља њихова твоја?
24 Bwanji inu osakhazikika mʼdziko limene Kemosi mulungu wanu anakupatsani, ifenso tikhazikike mʼdziko limene Yehova Mulungu wathu anatipatsa?
Није ли твоје оно што ти да да је твоје Хемос бог твој? Тако кога год Господ Бог наш отера испред нас, оног је земља наша.
25 Kodi ndinu abwino kuposa Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Mowabu? Kodi iye anakanganapo kapena kuchita nkhondo ndi Israeli?
Или си ти по чем бољи од Валака сина Сефоровог цара моавског? Је ли се он кад свађао с Израиљем? Је ли кад војевао с нама?
26 Pamene Aisraeli ankakhala mʼdziko la Hesiboni ndi mʼmidzi yake, mʼdziko la Aroeri ndi midzi yake, komanso mʼmizinda yonse imene ili mʼmbali mwa mtsinje wa Arinoni kwa zaka 300, nʼchifukwa chiyani inu simunalande malowo nthawi imeneyo?
Израиљ живи у Есевону и у селима његовим и у Ароиру и селима његовим и по свим градовима дуж Арнона три стотине година; зашто не отесте за толико времена.
27 Choncho ine sindinakuchimwireni. Koma inu mukundilakwira pomenyana nane. Yehova woweruza, ndiye aweruze lero mlandu wa pakati pa Aisraeli ndi Aamoni.”
И тако нисам ја теби скривио, него ти мени чиниш зло ратујући на ме. Господ судија нек суди данас између синова Израиљевих и синова Амонових.
28 Koma mfumu ya Aamori, sinasamale mawu amene Yefita anatumiza kwa iyo.
Али цар синова Амонових не послуша речи које му поручи Јефтај.
29 Tsono Mzimu wa Yehova unatsikira pa Yefita. Ndipo iye ananyamuka nadzera ku Giliyadi ndi ku Manase. Anafika ku Mizipa mʼdziko la Giliyadi, ndipo kuchokera kumeneko anapita kukalimbana ndi Aamoni.
И сиђе на Јефтаја дух Господњи, те прође кроз Галад и кроз Манасију, прође и Миспу галадску, и од Миспе галадске дође о синова Амонових.
30 Yefita analumbira kwa Yehova kuti, “Ngati mupereka Aamoni mʼmanja mwanga,
И заветова Јефтај завет Господу и рече: Ако ми даш синове Амонове у руке,
31 aliyense amene atuluke pa khomo la nyumba yanga kudzandichingamira pobwerera nditagonjetsa Aamoni adzakhala wake wa Yehova, ndipo ndidzamupereka kuti akhale nsembe yopsereza.”
Шта год изиђе на врата из куће моје на сусрет мени, кад се вратим здрав од синова Амонових, биће Господње, и принећу на жртву паљеницу.
32 Kenaka Yefita anawolokera kwa Aamoni kukamenya nawo nkhondo, ndipo Yehova anawaperekadi mʼmanja mwake.
И тако дође Јефтај до синова Амонових да се бије с њима; и Господ му их даде у руке.
33 Iye anawononga mizinda makumi awiri kuchokera ku Ariori mpaka pafupi ndi mzinda wa Miniti. Anapitirira mpaka ku Abeli-Keranimu. Choncho Aisraeli anagonjetsa Aamoni.
И поби их од Ароира па до Минита у двадесет градова и до равнице виноградске у боју врло великом; и синови Амонови бише покорени пред синовима Израиљевим.
34 Pambuyo pake Yefita anabwerera ku nyumba yake. Tsono anangoona mwana wake wamkazi akutuluka kudzamuchingamira akuyimba ngʼoma ndi kuvina. Uyu anali mwana yekhayo wa Yefita. Analibenso mwana wina wamwamuna kapena wamkazi.
А кад се враћаше Јефтај кући својој у Миспу, гле, кћи његова изиђе му на сусрет с бубњевима и свиралама; она му беше јединица, и осим ње не имаше ни сина ни кћери.
35 Yefita ataona mwana wake uja, anangʼamba zovala zake ndi kulira, “Kalanga ine! Mwana wanga! Wandivulaza kwambiri ndipo iwe ndi gwero la mavuto anga. Ine ndinalumbira kwa Yehova ndi pakamwa pangapa ndipo sindingathe kubweza malumbiro angawo.”
Па кад је угледа, раздре хаљине своје и рече: Ах кћери моја! Веле ли ме обори! Ти си од оних што ме цвеле; јер сам отворио уста своја ка Господу и не могу порећи.
36 Mwanayo anayankha kuti, “Abambo, ngati munalonjeza kwa Yehova ndi pakamwa panu, chitani zimene munalonjezera pakuti Yehova wakuthandizani kulipsira adani anu Amowabu.”
А она му рече: Оче мој, кад си отворио уста своја ка Господу, учини ми, како је изашло из уста твојих, кад те је Господ осветио од непријатеља твојих, синова Амонових.
37 Anatinso kwa abambo ake, “Ndikupempheni chinthu ichi: Mundilole ndikayendeyende ku mapiri miyezi iwiri ndizikalira pamodzi ndi anzanga chifukwa ndikufa ndikanali namwali wosadziwa mwamuna.”
Још рече оцу свом: Учини ми ово: остави ме до два месеца да отидем да се попнем на горе да оплачем своје девојаштво с другама својим.
38 Yefita anamuyankha kuti, “Pita.” Ndipo anamulola kuti apite miyezi iwiri. Tsono anapita kumapiri ndi atsikana anzake kukalira chifukwa cha unamwali wake.
А он јој рече: Иди. И пусти је на два месеца, и она отиде с другама својим и оплакива девојаштво своје по горама.
39 Miyezi iwiri itatha iye anabwerera kwa abambo ake, ndipo anachitadi zimene analonjeza. Motero unakhala mwambo wa Aisraeli,
А кад прођоше два месеца, врати се к оцу свом; и он сврши на њој завет свој који беше заветовао. А она не позна човека. И поста обичај у Израиљу
40 kuti atsikana a Israeli ankapita chaka chilichonse kukalira maliro a mwana wa mkazi wa Yefita, Mgiliyadi uja masiku makumi anayi pa chaka.
Да од године до године иду кћери Израиљеве да плачу за кћерју Јефтаја од Галада, четири дана у години.

< Oweruza 11 >