< Oweruza 11 >

1 Yefita wa ku Giliyadi anali wankhondo wa mphamvu. Iyeyu amayi ake anali mkazi wachiwerewere, ndipo abambo ake anali Giliyadi.
And so in that tyme Jepte, a man of Galaad, was a ful strong man, and fiytere, the sone of a womman hoore, which Jepte was borun of Galaad.
2 Mkazi wake wa Giliyadi anabereka naye ana aamuna. Tsono ana amenewa atakula anapirikitsa Yefita ndi kumuwuza kuti, “Sudzalandirako cholowa mʼnyumba ya abambo athu chifukwa ndiwe mwana wa mkazi wina.”
Forsothe Galaad hadde a wijf, of which he hadde sones, whiche aftir that thei encressiden, castiden out Jepte, and seiden, Thou maist not be eir in the hows of oure fadir, for thou art born of a modir auoutresse.
3 Choncho Yefita anathawa kuchoka kwa abale ake ndi kukakhala mʼdziko la Tobu. Kumeneko anakakopa ndi kusonkhanitsa anthu achabechabe ndipo anatuluka pamodzi kukasakaza zinthu.
`Whiche britheren he fledde, and eschewide, and dwellide in the lond of Tob; and pore men and `doynge thefte weren gaderid to hym, and sueden as a prince.
4 Patapita nthawi Aamoni anadzachita nkhondo ndi Israeli.
In tho daies the sones of Amon fouyten ayens Israel;
5 Tsono pamene Aamoni ankathira nkhondo Aisraeli, akuluakulu a ku Giliyadi anapita kukamutenga Yefita ku dziko la Tobu.
and whanne thei contynueden scharpli, the grettere men in birthe of Galaad, yeden to take in to `the help of hem silf Jepte fro the lond of Tob;
6 Iwo anati kwa iye, “Bwera ukhale mkulu wathu wankhondo kuti timenyane ndi Amoni.”
and thei seiden to hym, Come thou, and be oure prince, and fiyte ayens the sones of Amon.
7 Yefita anawawuza Agiliyadi kuti, “Kodi inu suja munkadana nane ndi kundithamangitsa ku nyumba ya abambo anga? Nʼchifukwa chiyani lero mwabwera kwa ine pamene muli pa mavuto?”
To whiche he answeride, Whethir not ye it ben, that haten me, and castiden me out of the hows of mi fadir, and now ye camen to me, and weren compellid bi nede?
8 Akuluakulu a ku Giliyadi aja anamuyankha kuti, “Chimene tabwerera kwa iwe ndi chakuti upite nafe kukamenyana ndi Aamoni, ndipo udzakhala wolamulira wa onse okhala mu Giliyadi.”
And the princes of Galaad seiden to Jepte, Therfor for this cause we camen now to thee, that thou go with vs, and fiyt ayens the sones of Amon; and that thou be the duyk of alle men that dwellen in Galaad.
9 Yefita anawayankha akuluakulu a ku Giliyadi kuti, “Ngati mundibwezeranso kwathu kuti ndikachite nkhondo ndi Aamoni ndipo Yehova nʼkukandithandiza kuwagonjetsa, ndidzakhaladi wokulamulirani?”
And Jepte seide to hem, Whether ye camen verili to me, that Y fiyte for you ayens the sones of Amon, and if the Lord schal bitake hem in to myn hondis, schal Y be youre prince?
10 Akuluakulu a ku Giliyadi anamuyankha kuti, “Yehova akhale mboni pakati pa inu ndi ife, ngati sitidzachita monga mwa mawu anu.”
Whiche answeriden to hym, The Lord hym silf, that herith these thingis, is mediatour and witnesse, that we schulen do oure biheestis.
11 Choncho Yefita anapita nawo akuluakulu a ku Giliyadi aja, ndipo anthu a kumeneko anamusandutsa kukhala wowalamulira ndi mkulu wankhondo. Tsono Yefita anabwerezanso mawu omwewa pamaso pa Yehova ku Mizipa.
And so Jepte wente with the princes of Galaad, and al the puple made hym her prince; and Jepte spak alle hise wordis bifor the Lord in Maspha.
12 Kenaka Yefita anatuma amithenga kwa mfumu ya Aamoni ndi funso lakuti, “Kodi ife takuchimwirani chiyani kuti muzichita nkhondo ndi dziko langa?”
And he sente messangeris to the kyng of the sones of Amon, whiche messangeris schulden seie `of his persoone, What is to me and to thee, for thou hast come `ayens me to waaste my lond?
13 Ndipo mfumu ya Aamoni inayankha amithenga a Yefita aja kuti, “Pamene Israeli amatuluka kuchokera mu Igupto, analanda dziko langa kuyambira ku mtsinje wa Arinoni mpaka ku mtsinje wa Yaboki mpakanso ku mtsinje wa Yorodani. Tsopano mundibwezere dziko langa mwamtendere.”
To whiche the kyng answeride, For Israel whanne he stiede fro Egipt took awei my lond, fro the coostis of Arnon `til to Jaboch and to Jordan, now therfor yeelde it to me with pees.
14 Yefita anatumizanso amithenga akewo kwa mfumu ya Aamoni
Bi whiche massangeris Jepte sente eft, and comaundide to hem, that thei schulden seie to the kyng of Amon,
15 kukanena kuti, Yefita akuti, “Israeli sanalande dziko la Mowabu kapena dziko la Aamoni.
Jepte seith these thingis, Israel took not the lond of Moab, nether the lond of the sones of Amon;
16 Koma pamene Aisraeli ankachoka ku Igupto anadzera njira ya ku chipululu mpaka ku Nyanja Yofiira nakafika ku Kadesi.
but whanne thei stieden fro Egipt, `he yede bi the wildirnesse `til to the Reed See, and cam in to Cades;
17 Kenaka Israeli anatumiza amithenga kwa mfumu ya ku Edomu kuti, ‘Chonde tiloleni kuti tidutse mʼdziko lanu,’ Koma mfumu ya ku Edomu sinamvere zimenezo. Aisraeli anatumizanso amithenga kwa mfumu ya ku Mowabu, ndipo iyo inakananso. Choncho Israeli anakhala ku Kadesi.
and he sente messangeris to the kyng of Edom, and seide, Suffre thou me, that Y go thoruy thi lond; which kyng nolde assente to his preyeres. Also Israel sente to the kyng of Moab, and he dispiside to yyue passage;
18 “Pambuyo pake, Aisraeli ananyamuka ulendo kudzera ku chipululu nazungulira dziko la Edomu ndi dziko la Mowabu, ndipo anafika ku mmawa kwa dziko la Mowabu ndi kumanga zinthando zawo ku mbali ina ya mtsinje wa Arinoni. Iwo sanalowe mʼdziko la Mowabu, chifukwa mtsinje wa Arinoni ndiwo unali malire a dziko la Mowabu.
and so Israel dwellyde in Cades, and cumpasside bi the side the lond of Edom, and the lond of Moab; and he cam to the eest coost of the lond of Moab, and settide tentis biyende Arnon, nether he wolde entre in to the termes of Moab; for Arnon is the ende of the lond of Moab.
19 “Pambuyo pake Israeli anatumiza amithenga kwa Sihoni mfumu ya Aamori, amene amalamulira ku Hesiboni ndipo anati kwa iye, ‘Chonde tiloleni kuti tidutse mʼdziko lanu popita kwathu.’
And so Israel sente messangeris to Seon, kyng of Ammorreis, that dwellide in Esebon; and thei seiden to hym, Suffre thou, that Y passe thorouy thi lond `til to the ryuer.
20 Koma Sihoni sanalole Israeli kuti adzere mʼdziko mwake. Mʼmalo mwake Sihoni anasonkhanitsa ankhondo ake onse nakamanga msasa ku Yahazi ndipo anachita nkhondo ndi Israeli.
And he dispiside the wordis of Israel, and suffride not hym passe bi hise termes, but with a multitude with out noumbre gaderid to gidere he yede out ayens Israel, and ayenstood strongli.
21 “Koma Yehova Mulungu wa Israeli anamupereka Sihoni pamodzi ndi anthu ake onse mʼmanja mwa Israeli, ndipo anawagonjetsa. Choncho Aisraeli analanda dziko lonse la Aamori amene amakhala mʼdzikolo.
And the Lord bitook hym with al his oost in to the hondis of Israel; and Israel smoot hym, and hadde in possessioun al the lond of Ammorrey,
22 Analanda dziko lonse kuchokera ku Arinoni mpaka ku Yaboki ndiponso kuchokera ku chipululu mpaka ku mtsinje wa Yorodani.
dwellere of that cuntrey, and al the coostis therof fro Arnon `til to Jaboch, and fro the wildirnesse `til to Jordan.
23 “Ndiye kuti Yehova Mulungu wa Aisraeli ndiye analanda dziko la Aamori, kuwalandirira anthu ake. Kodi inu mukufuna kutilanda dzikolo?
Therfor the Lord God of Israel distriede Ammorrey, fiytynge ayens hym for his puple Israel. And wolt thou now haue in possessioun `his lond? Whether not tho thingis whiche Chamos, thi god, hadde in possessioun, ben due to thee bi riyt?
24 Bwanji inu osakhazikika mʼdziko limene Kemosi mulungu wanu anakupatsani, ifenso tikhazikike mʼdziko limene Yehova Mulungu wathu anatipatsa?
Forsothe tho thingis whiche `oure Lord God ouercomere gat, schulen falle in to oure possessioun;
25 Kodi ndinu abwino kuposa Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Mowabu? Kodi iye anakanganapo kapena kuchita nkhondo ndi Israeli?
no but in hap thou art betere than Balach, the sone of Sephor, kyng of Moab, ether thou maist preue, that he stryuede ayens Israel, and fauyt ayens hym,
26 Pamene Aisraeli ankakhala mʼdziko la Hesiboni ndi mʼmidzi yake, mʼdziko la Aroeri ndi midzi yake, komanso mʼmizinda yonse imene ili mʼmbali mwa mtsinje wa Arinoni kwa zaka 300, nʼchifukwa chiyani inu simunalande malowo nthawi imeneyo?
whanne he dwellide in Esebon, and in townes therof, and in Aroer, and in townes therof, and in alle citees biyende Jordan, bi thre hundrid yeer. Whi in so myche time assaieden ye no thing on this axyng ayen?
27 Choncho ine sindinakuchimwireni. Koma inu mukundilakwira pomenyana nane. Yehova woweruza, ndiye aweruze lero mlandu wa pakati pa Aisraeli ndi Aamoni.”
Therfor not Y do synne ayens thee, but thou doist yuel ayens me, and bryngist in batels not iust to me; the Lord, iuge of this dai, deme bitwixe the sones of Israel and bitwixe the sones of Amon.
28 Koma mfumu ya Aamori, sinasamale mawu amene Yefita anatumiza kwa iyo.
And the kyng of the sones of Amon nolde assente to the wordis of Jepte, whiche he sente bi messangeris.
29 Tsono Mzimu wa Yehova unatsikira pa Yefita. Ndipo iye ananyamuka nadzera ku Giliyadi ndi ku Manase. Anafika ku Mizipa mʼdziko la Giliyadi, ndipo kuchokera kumeneko anapita kukalimbana ndi Aamoni.
Therfor the spirit of the Lord was maad on Jepte, and he cumpasside Galaad and Manasses, Maspha and Galaad; and he passide fro thennus to the sones of Amon,
30 Yefita analumbira kwa Yehova kuti, “Ngati mupereka Aamoni mʼmanja mwanga,
and made a vow to the Lord, and seide, If thou schalt bitake the sones of Amon in to myn hondis,
31 aliyense amene atuluke pa khomo la nyumba yanga kudzandichingamira pobwerera nditagonjetsa Aamoni adzakhala wake wa Yehova, ndipo ndidzamupereka kuti akhale nsembe yopsereza.”
who euer goith out first of the dores of myn hows, and cometh ayens me turnynge ayen with pees fro the sones of Amon, Y schal offre hym brent sacrifice to the Lord.
32 Kenaka Yefita anawolokera kwa Aamoni kukamenya nawo nkhondo, ndipo Yehova anawaperekadi mʼmanja mwake.
And Jepte yede to the sones of Amon, to fiyte ayens hem, whiche the Lord bitook in to hise hondis;
33 Iye anawononga mizinda makumi awiri kuchokera ku Ariori mpaka pafupi ndi mzinda wa Miniti. Anapitirira mpaka ku Abeli-Keranimu. Choncho Aisraeli anagonjetsa Aamoni.
and he smoot fro Aroer `til to thou comest in to Mennyth, twenti citees, and `til to Abel, which is set aboute with vyneris, with ful greet veniaunce; and the sones of Amon weren maad low of the sones of Israel.
34 Pambuyo pake Yefita anabwerera ku nyumba yake. Tsono anangoona mwana wake wamkazi akutuluka kudzamuchingamira akuyimba ngʼoma ndi kuvina. Uyu anali mwana yekhayo wa Yefita. Analibenso mwana wina wamwamuna kapena wamkazi.
Forsothe whanne Jepte turnede ayen in to Maspha, his hows, his oon gendrid douyter cam to hym with tympanys and croudis; for he hadde not othere fre children.
35 Yefita ataona mwana wake uja, anangʼamba zovala zake ndi kulira, “Kalanga ine! Mwana wanga! Wandivulaza kwambiri ndipo iwe ndi gwero la mavuto anga. Ine ndinalumbira kwa Yehova ndi pakamwa pangapa ndipo sindingathe kubweza malumbiro angawo.”
And whanne `sche was seyn, he to-rente his clothis, and seide, Allas! my douytir, thou hast disseyued me, and thou art disseyued; for Y openyde my mouth to the Lord, and Y may do noon other thing.
36 Mwanayo anayankha kuti, “Abambo, ngati munalonjeza kwa Yehova ndi pakamwa panu, chitani zimene munalonjezera pakuti Yehova wakuthandizani kulipsira adani anu Amowabu.”
To whom sche answeride, My fadir, if thou openydist thi mouth to the Lord, do to me what euer thing thou bihiytist, while veniaunce and victorie of thin enemyes is grauntid to thee.
37 Anatinso kwa abambo ake, “Ndikupempheni chinthu ichi: Mundilole ndikayendeyende ku mapiri miyezi iwiri ndizikalira pamodzi ndi anzanga chifukwa ndikufa ndikanali namwali wosadziwa mwamuna.”
And sche seide to the fadir, Yyue thou to me oneli this thing, which Y biseche; suffre thou me that in two monethis Y cumpasse hillis, and biweile my maidynhed with my felowis.
38 Yefita anamuyankha kuti, “Pita.” Ndipo anamulola kuti apite miyezi iwiri. Tsono anapita kumapiri ndi atsikana anzake kukalira chifukwa cha unamwali wake.
To whom he answeride, Go thou. And he sufferide hir in two monethis. And whanne sche hadde go with hir felowis and pleiferis, sche biwepte hir maydynhed in the hillis.
39 Miyezi iwiri itatha iye anabwerera kwa abambo ake, ndipo anachitadi zimene analonjeza. Motero unakhala mwambo wa Aisraeli,
And whanne twey monethis weren fillid, sche turnede ayen to hir fadir, and he dide to hir as he avowide; and sche knew not fleischli a man. Fro thennus a custom cam in Israel,
40 kuti atsikana a Israeli ankapita chaka chilichonse kukalira maliro a mwana wa mkazi wa Yefita, Mgiliyadi uja masiku makumi anayi pa chaka.
and the custom is kept, that aftir the `ende of the yeer the douytris of Israel come togidere, and biweile `the douytir of Jepte of Galaad `foure daies.

< Oweruza 11 >