< Oweruza 11 >
1 Yefita wa ku Giliyadi anali wankhondo wa mphamvu. Iyeyu amayi ake anali mkazi wachiwerewere, ndipo abambo ake anali Giliyadi.
Now Yiphthach the Gil'adite was a mighty man of valor, but he was the son of a harlot; and Gil'ad had begotten Yiphthach.
2 Mkazi wake wa Giliyadi anabereka naye ana aamuna. Tsono ana amenewa atakula anapirikitsa Yefita ndi kumuwuza kuti, “Sudzalandirako cholowa mʼnyumba ya abambo athu chifukwa ndiwe mwana wa mkazi wina.”
And the wife of Gil'ad also bore him sons; and when the sons of the wife were grown up, they drove away Yiphthach, and said unto him, Thou shalt not inherit in the house of our father: for the son of another woman art thou.
3 Choncho Yefita anathawa kuchoka kwa abale ake ndi kukakhala mʼdziko la Tobu. Kumeneko anakakopa ndi kusonkhanitsa anthu achabechabe ndipo anatuluka pamodzi kukasakaza zinthu.
And Yiphthach fled away from his brothers, and dwelt in the land of Tob; and there gathered themselves to Yiphthach idle men, and they went out with him.
4 Patapita nthawi Aamoni anadzachita nkhondo ndi Israeli.
And it came to pass after some time, that the children of 'Ammon made war against Israel.
5 Tsono pamene Aamoni ankathira nkhondo Aisraeli, akuluakulu a ku Giliyadi anapita kukamutenga Yefita ku dziko la Tobu.
And it was so, when the children of 'Ammon made war against Israel, that the elders of Gil'ad went to fetch Yiphthach out of the land of Tob.
6 Iwo anati kwa iye, “Bwera ukhale mkulu wathu wankhondo kuti timenyane ndi Amoni.”
And they said unto Yiphthach, Come, and become a leader unto us, that we may fight with the children of 'Ammon.
7 Yefita anawawuza Agiliyadi kuti, “Kodi inu suja munkadana nane ndi kundithamangitsa ku nyumba ya abambo anga? Nʼchifukwa chiyani lero mwabwera kwa ine pamene muli pa mavuto?”
And Yiphthach said unto the elders of Gil'ad, Did ye not hate me, and drive me away out of my father's house? and why are ye come unto me now, when ye are in distress?
8 Akuluakulu a ku Giliyadi aja anamuyankha kuti, “Chimene tabwerera kwa iwe ndi chakuti upite nafe kukamenyana ndi Aamoni, ndipo udzakhala wolamulira wa onse okhala mu Giliyadi.”
And the elders of Gil'ad said unto Yiphthach, Therefore are we now come back to thee, that thou mayest go with us, and fight against the children of 'Ammon; and thou shalt become unto us a head, unto all the inhabitants of Gil'ad.
9 Yefita anawayankha akuluakulu a ku Giliyadi kuti, “Ngati mundibwezeranso kwathu kuti ndikachite nkhondo ndi Aamoni ndipo Yehova nʼkukandithandiza kuwagonjetsa, ndidzakhaladi wokulamulirani?”
And Yiphthach said unto the elders of Gil'ad, If ye bring me home again to fight against the children of 'Ammon, and the Lord give them up before me, shall I remain your head?
10 Akuluakulu a ku Giliyadi anamuyankha kuti, “Yehova akhale mboni pakati pa inu ndi ife, ngati sitidzachita monga mwa mawu anu.”
And the elders of Gil'ad said unto Yiphthach, The Lord shall be a hearer between us, if we do not so according to thy word.
11 Choncho Yefita anapita nawo akuluakulu a ku Giliyadi aja, ndipo anthu a kumeneko anamusandutsa kukhala wowalamulira ndi mkulu wankhondo. Tsono Yefita anabwerezanso mawu omwewa pamaso pa Yehova ku Mizipa.
Then went Yiphthach with the elders of Gil'ad, and the people appointed him over them as head and as leader; and Yiphthach spoke all his words before the Lord in Mitzpah.
12 Kenaka Yefita anatuma amithenga kwa mfumu ya Aamoni ndi funso lakuti, “Kodi ife takuchimwirani chiyani kuti muzichita nkhondo ndi dziko langa?”
And Yiphthach sent messengers unto the king of the children of 'Ammon, saying, What have I to do with thee, that thou art come unto me to fight against my land?
13 Ndipo mfumu ya Aamoni inayankha amithenga a Yefita aja kuti, “Pamene Israeli amatuluka kuchokera mu Igupto, analanda dziko langa kuyambira ku mtsinje wa Arinoni mpaka ku mtsinje wa Yaboki mpakanso ku mtsinje wa Yorodani. Tsopano mundibwezere dziko langa mwamtendere.”
And the king of the children of 'Ammon said unto the messengers of Yiphthach, Because Israel took away my land, when they came up out of Egypt, from the Arnon even unto the Yabbok, and unto the Jordan: and now restore these [lands] again in peace.
14 Yefita anatumizanso amithenga akewo kwa mfumu ya Aamoni
And Yiphthach again sent messengers unto the king of the children of 'Ammon;
15 kukanena kuti, Yefita akuti, “Israeli sanalande dziko la Mowabu kapena dziko la Aamoni.
And he said unto him, Thus hath said Yiphthach, Israel did not take away the land of Moab, nor the land of the children of 'Ammon;
16 Koma pamene Aisraeli ankachoka ku Igupto anadzera njira ya ku chipululu mpaka ku Nyanja Yofiira nakafika ku Kadesi.
For when they came up out of Egypt, Israel walked through the wilderness unto the Red Sea, and came to Kadesh;
17 Kenaka Israeli anatumiza amithenga kwa mfumu ya ku Edomu kuti, ‘Chonde tiloleni kuti tidutse mʼdziko lanu,’ Koma mfumu ya ku Edomu sinamvere zimenezo. Aisraeli anatumizanso amithenga kwa mfumu ya ku Mowabu, ndipo iyo inakananso. Choncho Israeli anakhala ku Kadesi.
And Israel then sent messengers unto the king of Edom, saying, Let me pass, I pray thee, through thy land; but the king of Edom would not hearken; and also to the king of Moab they sent; but he would not consent: and Israel remained in Kadesh.
18 “Pambuyo pake, Aisraeli ananyamuka ulendo kudzera ku chipululu nazungulira dziko la Edomu ndi dziko la Mowabu, ndipo anafika ku mmawa kwa dziko la Mowabu ndi kumanga zinthando zawo ku mbali ina ya mtsinje wa Arinoni. Iwo sanalowe mʼdziko la Mowabu, chifukwa mtsinje wa Arinoni ndiwo unali malire a dziko la Mowabu.
Then they wandered through the wilderness, and traveled round the land of Edom, and the land of Moab, and came from the rising of the sun to the land of Moab, and encamped on the other side of the Arnon: but they came not within the border of Moab; for the Arnon is the boundary of Moab.
19 “Pambuyo pake Israeli anatumiza amithenga kwa Sihoni mfumu ya Aamori, amene amalamulira ku Hesiboni ndipo anati kwa iye, ‘Chonde tiloleni kuti tidutse mʼdziko lanu popita kwathu.’
And Israel sent messengers unto Sichon the king of the Emorites, the king of Cheshbon; and Israel said unto him, Let us pass, we pray thee, through thy land unto my place.
20 Koma Sihoni sanalole Israeli kuti adzere mʼdziko mwake. Mʼmalo mwake Sihoni anasonkhanitsa ankhondo ake onse nakamanga msasa ku Yahazi ndipo anachita nkhondo ndi Israeli.
But Sichon trusted not Israel to [let them] pass through his territory; and Sichon assembled all his people, and encamped in Yahaz, and fought against Israel.
21 “Koma Yehova Mulungu wa Israeli anamupereka Sihoni pamodzi ndi anthu ake onse mʼmanja mwa Israeli, ndipo anawagonjetsa. Choncho Aisraeli analanda dziko lonse la Aamori amene amakhala mʼdzikolo.
and the Lord the God of Israel delivered Sichon and all his people into the hand of Israel, and they smote them; and Israel took possession of all the land of the Emorites, the inhabitants of that country.
22 Analanda dziko lonse kuchokera ku Arinoni mpaka ku Yaboki ndiponso kuchokera ku chipululu mpaka ku mtsinje wa Yorodani.
And they took possession of all the territory of the Emorites, from the Arnon even unto the Yabbok, and from the wilderness even unto the Jordan.
23 “Ndiye kuti Yehova Mulungu wa Aisraeli ndiye analanda dziko la Aamori, kuwalandirira anthu ake. Kodi inu mukufuna kutilanda dzikolo?
So now the Lord the God of Israel hath dispossessed the Emorites from before his people Israel, and shouldst thou possess it?
24 Bwanji inu osakhazikika mʼdziko limene Kemosi mulungu wanu anakupatsani, ifenso tikhazikike mʼdziko limene Yehova Mulungu wathu anatipatsa?
Truly! that which Kemosh thy god may give thee to possess, even that canst thou possess; but whatsoever the Lord our God hath driven out from before us, even that will we possess.
25 Kodi ndinu abwino kuposa Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Mowabu? Kodi iye anakanganapo kapena kuchita nkhondo ndi Israeli?
And now art thou then any better than Balak the son of Zippor, the king of Moab? did he ever strive against Israel, or did he ever fight against them?
26 Pamene Aisraeli ankakhala mʼdziko la Hesiboni ndi mʼmidzi yake, mʼdziko la Aroeri ndi midzi yake, komanso mʼmizinda yonse imene ili mʼmbali mwa mtsinje wa Arinoni kwa zaka 300, nʼchifukwa chiyani inu simunalande malowo nthawi imeneyo?
[And] while Israel hath dwelt in Cheshbon and in its towns, and in 'Ar'or and in its towns, and in all the cities that are along the margins of the Arnon, three hundred years: why did ye not recover them within that time?
27 Choncho ine sindinakuchimwireni. Koma inu mukundilakwira pomenyana nane. Yehova woweruza, ndiye aweruze lero mlandu wa pakati pa Aisraeli ndi Aamoni.”
Whereas I myself have not sinned against thee, and thou doest me wrong to war against me: may the Lord, the Judge, decide this day between the children of Israel and the children of 'Ammon.
28 Koma mfumu ya Aamori, sinasamale mawu amene Yefita anatumiza kwa iyo.
Nevertheless the king of the children of 'Ammon hearkened not unto the words of Yiphthach which he had sent to him.
29 Tsono Mzimu wa Yehova unatsikira pa Yefita. Ndipo iye ananyamuka nadzera ku Giliyadi ndi ku Manase. Anafika ku Mizipa mʼdziko la Giliyadi, ndipo kuchokera kumeneko anapita kukalimbana ndi Aamoni.
Then came upon Yiphthach the spirit of the Lord, and he passed through Gil'ad and Menasseh, and passed through Mitzpeh of Gil'ad, and from Mitzpeh of Gil'ad he passed over unto the children of Ammon.
30 Yefita analumbira kwa Yehova kuti, “Ngati mupereka Aamoni mʼmanja mwanga,
And Yiphthach made a vow unto the Lord, and said, If thou wilt indeed deliver the children of 'Ammon into my hand,
31 aliyense amene atuluke pa khomo la nyumba yanga kudzandichingamira pobwerera nditagonjetsa Aamoni adzakhala wake wa Yehova, ndipo ndidzamupereka kuti akhale nsembe yopsereza.”
Then shall it be, that whatsoever cometh forth out of the doors of my house to meet me, when I return in peace from the children of 'Ammon, shall belong to the Lord, and I will offer it up for a burnt-offering.
32 Kenaka Yefita anawolokera kwa Aamoni kukamenya nawo nkhondo, ndipo Yehova anawaperekadi mʼmanja mwake.
So Yiphthach passed over unto the children of 'Ammon to fight against them: and the Lord delivered them into his hand.
33 Iye anawononga mizinda makumi awiri kuchokera ku Ariori mpaka pafupi ndi mzinda wa Miniti. Anapitirira mpaka ku Abeli-Keranimu. Choncho Aisraeli anagonjetsa Aamoni.
And he smote them from 'Aro'er, even till thou comest to Minnith, twenty cities, and unto Abel-keramin, with a very great defeat; and the children of 'Ammon were humbled before the children of Israel.
34 Pambuyo pake Yefita anabwerera ku nyumba yake. Tsono anangoona mwana wake wamkazi akutuluka kudzamuchingamira akuyimba ngʼoma ndi kuvina. Uyu anali mwana yekhayo wa Yefita. Analibenso mwana wina wamwamuna kapena wamkazi.
And Yiphthach came to Mizpah unto his house, and, behold, his daughter came out to meet him with timbrels and with dances: and she was his sole child; he had beside her neither son nor daughter.
35 Yefita ataona mwana wake uja, anangʼamba zovala zake ndi kulira, “Kalanga ine! Mwana wanga! Wandivulaza kwambiri ndipo iwe ndi gwero la mavuto anga. Ine ndinalumbira kwa Yehova ndi pakamwa pangapa ndipo sindingathe kubweza malumbiro angawo.”
And it came to pass, when he saw her, that he rent his garments, and said, Alas, my daughter! thou hast bent me down very low, and thou art one of those that trouble me; for I have opened my mouth unto the Lord, and I cannot go back.
36 Mwanayo anayankha kuti, “Abambo, ngati munalonjeza kwa Yehova ndi pakamwa panu, chitani zimene munalonjezera pakuti Yehova wakuthandizani kulipsira adani anu Amowabu.”
And she said unto him, My father, if thou hast opened thy mouth unto the Lord, do to me in accordance with what hath proceeded out of thy mouth; since the Lord hath taken vengeance for thee on thy enemies, on the children of 'Ammon.
37 Anatinso kwa abambo ake, “Ndikupempheni chinthu ichi: Mundilole ndikayendeyende ku mapiri miyezi iwiri ndizikalira pamodzi ndi anzanga chifukwa ndikufa ndikanali namwali wosadziwa mwamuna.”
And she said unto her father, Let this thing be done for me: Let me alone two months, that I may descend to the mountains, and bewail my virginity, I with my companions.
38 Yefita anamuyankha kuti, “Pita.” Ndipo anamulola kuti apite miyezi iwiri. Tsono anapita kumapiri ndi atsikana anzake kukalira chifukwa cha unamwali wake.
And he aid, Go. And he sent her away for two months: and she went with her companions, and bewailed her virginity on the mountains.
39 Miyezi iwiri itatha iye anabwerera kwa abambo ake, ndipo anachitadi zimene analonjeza. Motero unakhala mwambo wa Aisraeli,
And it came to pass at the end of two months, that she returned unto her father, and he fulfilled on her his vow which he had vowed; and she knew no man; and it became a custom in Israel,
40 kuti atsikana a Israeli ankapita chaka chilichonse kukalira maliro a mwana wa mkazi wa Yefita, Mgiliyadi uja masiku makumi anayi pa chaka.
That the daughters of Israel went from year to year to lament for the daughter of Yiphthach the Gil'adite four days in the year.