< Oweruza 11 >
1 Yefita wa ku Giliyadi anali wankhondo wa mphamvu. Iyeyu amayi ake anali mkazi wachiwerewere, ndipo abambo ake anali Giliyadi.
Og Gileaditeren Jeftha var vældig til Strid, men han var en Horekvindes Søn; og Gilead havde avlet Jeftha.
2 Mkazi wake wa Giliyadi anabereka naye ana aamuna. Tsono ana amenewa atakula anapirikitsa Yefita ndi kumuwuza kuti, “Sudzalandirako cholowa mʼnyumba ya abambo athu chifukwa ndiwe mwana wa mkazi wina.”
Og Gileads Hustru fødte ham Børn; da Hustruens Børn bleve store, udstødte de Jeftha og sagde til ham: Du skal ikke arve i vor Faders Hus, thi du er en anden Kvindes Søn.
3 Choncho Yefita anathawa kuchoka kwa abale ake ndi kukakhala mʼdziko la Tobu. Kumeneko anakakopa ndi kusonkhanitsa anthu achabechabe ndipo anatuluka pamodzi kukasakaza zinthu.
Da flyede Jeftha fra sine Brødres Ansigt og boede i Landet Tob; og der samlede sig til Jeftha løse Mænd, og de droge ud med ham.
4 Patapita nthawi Aamoni anadzachita nkhondo ndi Israeli.
Og det skete efter nogle Aar, da strede Ammons Børn imod Israel.
5 Tsono pamene Aamoni ankathira nkhondo Aisraeli, akuluakulu a ku Giliyadi anapita kukamutenga Yefita ku dziko la Tobu.
Og det skete, der Ammons Børn strede mod Israel, da gik de Ældste af Gilead hen at hente Jeftha fra Landet Tob.
6 Iwo anati kwa iye, “Bwera ukhale mkulu wathu wankhondo kuti timenyane ndi Amoni.”
Og de sagde til Jeftha: Kom, saa skal du være vor Øverste, og vi ville stride imod Ammons Børn.
7 Yefita anawawuza Agiliyadi kuti, “Kodi inu suja munkadana nane ndi kundithamangitsa ku nyumba ya abambo anga? Nʼchifukwa chiyani lero mwabwera kwa ine pamene muli pa mavuto?”
Og Jeftha sagde til de Ældste af Gilead: Have I ikke hadet mig og udstødt mig af min Faders Hus? hvorfor komme I nu til mig, efterdi I have Trængsel?
8 Akuluakulu a ku Giliyadi aja anamuyankha kuti, “Chimene tabwerera kwa iwe ndi chakuti upite nafe kukamenyana ndi Aamoni, ndipo udzakhala wolamulira wa onse okhala mu Giliyadi.”
Og de Ældste af Gilead sagde til Jeftha: Derfor vende vi nu tilbage til dig, at du skal gaa med os og stride imod Ammons Børn; og du skal være vort Hoved, ja alle deres, som bo i Gilead.
9 Yefita anawayankha akuluakulu a ku Giliyadi kuti, “Ngati mundibwezeranso kwathu kuti ndikachite nkhondo ndi Aamoni ndipo Yehova nʼkukandithandiza kuwagonjetsa, ndidzakhaladi wokulamulirani?”
Og Jeftha sagde til de Ældste af Gilead: Dersom I hente mig for at stride imod Ammons Børn, og Herren giver dem for mit Ansigt, skal jeg da være eders Hoved?
10 Akuluakulu a ku Giliyadi anamuyankha kuti, “Yehova akhale mboni pakati pa inu ndi ife, ngati sitidzachita monga mwa mawu anu.”
Da sagde de Ældste af Gilead til Jeftha: Herren skal være Vidne imellem os, dersom vi ikke gøre saaledes efter dine Ord.
11 Choncho Yefita anapita nawo akuluakulu a ku Giliyadi aja, ndipo anthu a kumeneko anamusandutsa kukhala wowalamulira ndi mkulu wankhondo. Tsono Yefita anabwerezanso mawu omwewa pamaso pa Yehova ku Mizipa.
Saa gik Jeftha med de Ældste af Gilead, og Folket satte ham over sig til et Hoved og til en Øverste, og Jeftha talede alle sine Ord for Herrens Ansigt i Mizpa.
12 Kenaka Yefita anatuma amithenga kwa mfumu ya Aamoni ndi funso lakuti, “Kodi ife takuchimwirani chiyani kuti muzichita nkhondo ndi dziko langa?”
Da sendte Jeftha Bud til Ammons Børns Konge og lod sige: Hvad har jeg med dig at gøre, at du kommer til mig at stride imod mit Land?
13 Ndipo mfumu ya Aamoni inayankha amithenga a Yefita aja kuti, “Pamene Israeli amatuluka kuchokera mu Igupto, analanda dziko langa kuyambira ku mtsinje wa Arinoni mpaka ku mtsinje wa Yaboki mpakanso ku mtsinje wa Yorodani. Tsopano mundibwezere dziko langa mwamtendere.”
Ammons Børns Konge sagde til Jefthas Bud: Fordi Israel har taget mit Land, der han drog op af Ægypten, fra Arnon og indtil Jakob og indtil Jordanen; saa giv mig nu de Stæder tilbage med Fred!
14 Yefita anatumizanso amithenga akewo kwa mfumu ya Aamoni
Men Jeftha sendte atter Bud til Ammons Børns Konge.
15 kukanena kuti, Yefita akuti, “Israeli sanalande dziko la Mowabu kapena dziko la Aamoni.
Og han lod sige til ham: Saa siger Jeftha: Israel har ikke taget Moabs Land eller Ammons Børns Land;
16 Koma pamene Aisraeli ankachoka ku Igupto anadzera njira ya ku chipululu mpaka ku Nyanja Yofiira nakafika ku Kadesi.
thi der de droge op af Ægypten, da vandrede Israel i Ørken indtil det røde Hav, og kom til Kades.
17 Kenaka Israeli anatumiza amithenga kwa mfumu ya ku Edomu kuti, ‘Chonde tiloleni kuti tidutse mʼdziko lanu,’ Koma mfumu ya ku Edomu sinamvere zimenezo. Aisraeli anatumizanso amithenga kwa mfumu ya ku Mowabu, ndipo iyo inakananso. Choncho Israeli anakhala ku Kadesi.
Og Israel sendte Bud til Edomiternes Konge og lod sige: Kære, lad mig drage igennem dit Land, men Edomiternes Konge vilde ikke høre; han sendte ogsaa Bud til Moabiternes Konge, men denne vilde heller ikke; saa blev Israel i Kades.
18 “Pambuyo pake, Aisraeli ananyamuka ulendo kudzera ku chipululu nazungulira dziko la Edomu ndi dziko la Mowabu, ndipo anafika ku mmawa kwa dziko la Mowabu ndi kumanga zinthando zawo ku mbali ina ya mtsinje wa Arinoni. Iwo sanalowe mʼdziko la Mowabu, chifukwa mtsinje wa Arinoni ndiwo unali malire a dziko la Mowabu.
Derefter vandrede han i Ørken og drog omkring Edomiternes Land og Moabiternes Land og kom fra Solens Opgang til Moabiternes Land, og de lejrede sig paa hin Side Arnon; og de kom ikke i Moabiternes Landemærke; thi Arnon er Moabiternes Landemærke.
19 “Pambuyo pake Israeli anatumiza amithenga kwa Sihoni mfumu ya Aamori, amene amalamulira ku Hesiboni ndipo anati kwa iye, ‘Chonde tiloleni kuti tidutse mʼdziko lanu popita kwathu.’
Og Israel sendte Bud til Sihon, Amoriternes Konge, Kongen i Hesbon, og Israel lod ham sige: Kære, lad os drage igennem dit Land indtil mit Sted.
20 Koma Sihoni sanalole Israeli kuti adzere mʼdziko mwake. Mʼmalo mwake Sihoni anasonkhanitsa ankhondo ake onse nakamanga msasa ku Yahazi ndipo anachita nkhondo ndi Israeli.
Men Sihon troede ikke Israel, saa at han lod ham drage igennem sit Landemærke; men Sihon samlede alt sit Folk, og de lejrede sig i Jahza, og han stred imod Israel.
21 “Koma Yehova Mulungu wa Israeli anamupereka Sihoni pamodzi ndi anthu ake onse mʼmanja mwa Israeli, ndipo anawagonjetsa. Choncho Aisraeli analanda dziko lonse la Aamori amene amakhala mʼdzikolo.
Da gav Herren, Israels Gud, Sihon og alt hans Folk i Israels Haand, og de sloge dem; saa indtog Israel til Ejendom hele Landet fra Amoriterne, som boede sammesteds.
22 Analanda dziko lonse kuchokera ku Arinoni mpaka ku Yaboki ndiponso kuchokera ku chipululu mpaka ku mtsinje wa Yorodani.
Og de indtoge alt Amoriternes Landemærke til Ejendom, fra Arnon og indtil Jabok og fra Ørken og indtil Jordanen.
23 “Ndiye kuti Yehova Mulungu wa Aisraeli ndiye analanda dziko la Aamori, kuwalandirira anthu ake. Kodi inu mukufuna kutilanda dzikolo?
Saa har nu Herren, Israels Gud, fordrevet Amoriterne fra sit Folks Israels Ansigt; og du vil tage det i Eje?
24 Bwanji inu osakhazikika mʼdziko limene Kemosi mulungu wanu anakupatsani, ifenso tikhazikike mʼdziko limene Yehova Mulungu wathu anatipatsa?
Mon du ikke tager til Eje det, som din Gud Kamos giver dig i Eje? og alt hvad Herren vor Gud har gjort ryddeligt for vort Ansigt, det tage vi i Eje.
25 Kodi ndinu abwino kuposa Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Mowabu? Kodi iye anakanganapo kapena kuchita nkhondo ndi Israeli?
Og nu, er du vel meget bedre end Balak, Zippors Søn, Moabiternes Konge? har han vel trættet med Israel, eller har han vel ført Krig imod dem?
26 Pamene Aisraeli ankakhala mʼdziko la Hesiboni ndi mʼmidzi yake, mʼdziko la Aroeri ndi midzi yake, komanso mʼmizinda yonse imene ili mʼmbali mwa mtsinje wa Arinoni kwa zaka 300, nʼchifukwa chiyani inu simunalande malowo nthawi imeneyo?
Da Israel har boet i Hesbon og i dens tilhørende Stæder og i Aroer og i dens tilhørende Stæder og i alle Stæderne, som ligge ved Arnons Bredder, tre Hundrede Aar, hvorfor friede I dem da ikke i den Tid?
27 Choncho ine sindinakuchimwireni. Koma inu mukundilakwira pomenyana nane. Yehova woweruza, ndiye aweruze lero mlandu wa pakati pa Aisraeli ndi Aamoni.”
Og jeg har intet syndet imod dig, og du gør dette onde imod mig, at du strider imod mig; Herren, som er Dommer, skal dømme i Dag imellem Israels Børn og imellem Ammons Børn.
28 Koma mfumu ya Aamori, sinasamale mawu amene Yefita anatumiza kwa iyo.
Men Ammons Børns Konge hørte ikke Jefthas Ord, hvilke han sendte til ham.
29 Tsono Mzimu wa Yehova unatsikira pa Yefita. Ndipo iye ananyamuka nadzera ku Giliyadi ndi ku Manase. Anafika ku Mizipa mʼdziko la Giliyadi, ndipo kuchokera kumeneko anapita kukalimbana ndi Aamoni.
Og Herrens Aand var over Jeftha, og han drog igennem Gilead og Manasse; og han drog over til Mizpa i Gilead, og fra Mizpa i Gilead drog han over til Ammons Børn,
30 Yefita analumbira kwa Yehova kuti, “Ngati mupereka Aamoni mʼmanja mwanga,
og Jeftha lovede Herren et Løfte og sagde: Dersom du giver Ammons Børn i min Haand,
31 aliyense amene atuluke pa khomo la nyumba yanga kudzandichingamira pobwerera nditagonjetsa Aamoni adzakhala wake wa Yehova, ndipo ndidzamupereka kuti akhale nsembe yopsereza.”
da skal det ske, at det, som gaar ud, ja det, som gaar ud af mit Huses Døre imod mig, naar jeg kommer tilbage med Fred fra Ammons Børn, det skal høre Herren til, og jeg vil ofre det til et Brændoffer.
32 Kenaka Yefita anawolokera kwa Aamoni kukamenya nawo nkhondo, ndipo Yehova anawaperekadi mʼmanja mwake.
Saa drog Jeftha over til Ammons Børn for at stride imod dem, og Herren gav dem i hans Haand.
33 Iye anawononga mizinda makumi awiri kuchokera ku Ariori mpaka pafupi ndi mzinda wa Miniti. Anapitirira mpaka ku Abeli-Keranimu. Choncho Aisraeli anagonjetsa Aamoni.
Og han slog dem fra Aroer, og indtil man kommer til Minnith, tyve Stæder, og indtil Abel-Keramim med et saare stort Slag; saa bleve Ammons Børn ydmygede for Israels Børns Ansigt.
34 Pambuyo pake Yefita anabwerera ku nyumba yake. Tsono anangoona mwana wake wamkazi akutuluka kudzamuchingamira akuyimba ngʼoma ndi kuvina. Uyu anali mwana yekhayo wa Yefita. Analibenso mwana wina wamwamuna kapena wamkazi.
Og Jeftha kom til Mizpa til sit Hus, og se, hans Datter gik ud mod ham med Trommer og med Dans, og hun var hans eneste; han havde ellers hverken Søn eller Datter.
35 Yefita ataona mwana wake uja, anangʼamba zovala zake ndi kulira, “Kalanga ine! Mwana wanga! Wandivulaza kwambiri ndipo iwe ndi gwero la mavuto anga. Ine ndinalumbira kwa Yehova ndi pakamwa pangapa ndipo sindingathe kubweza malumbiro angawo.”
Og det skete, der han saa hende, da sønderrev han sine Klæder og sagde: Ak, min Datter! du har nedbøjet mig saare, og du har bedrøvet mig inderligen; thi jeg oplod min Mund til Herren, og jeg kan ikke kalde det tilbage.
36 Mwanayo anayankha kuti, “Abambo, ngati munalonjeza kwa Yehova ndi pakamwa panu, chitani zimene munalonjezera pakuti Yehova wakuthandizani kulipsira adani anu Amowabu.”
Og hun sagde til ham: Min Fader! har du opladt din Mund til Herren, da gør med mig, som det er udgaaet af din Mund, efter at Herren har skaffet dig fuldkommen Hævn over dine Fjender, over Ammons Børn.
37 Anatinso kwa abambo ake, “Ndikupempheni chinthu ichi: Mundilole ndikayendeyende ku mapiri miyezi iwiri ndizikalira pamodzi ndi anzanga chifukwa ndikufa ndikanali namwali wosadziwa mwamuna.”
Og hun sagde til sin Fader: Denne Ting lad mig vederfares, giv mig Frist to Maaneder, at jeg maa gaa og fare ned paa Bjergene og begræde min Jomfrustand, jeg og mine Veninder.
38 Yefita anamuyankha kuti, “Pita.” Ndipo anamulola kuti apite miyezi iwiri. Tsono anapita kumapiri ndi atsikana anzake kukalira chifukwa cha unamwali wake.
Og han sagde: Gak hen, og han gav hende Frist to Maaneder; da gik hun med sine Veninder hen og begræd sin Jomfrustand, paa Bjergene.
39 Miyezi iwiri itatha iye anabwerera kwa abambo ake, ndipo anachitadi zimene analonjeza. Motero unakhala mwambo wa Aisraeli,
Og det skete, der to Maaneder vare til Ende, da kom hun tilbage til sin Fader, og han gjorde med hende efter sit Løfte, som han havde lovet; og hun kendte ikke Mand. Og det blev en Skik i Israel:
40 kuti atsikana a Israeli ankapita chaka chilichonse kukalira maliro a mwana wa mkazi wa Yefita, Mgiliyadi uja masiku makumi anayi pa chaka.
Israels Døtre gaa fra Aar til Aar for at prise Gileaditeren Jefthas Datter fire Dage om Aaret.