< Oweruza 11 >
1 Yefita wa ku Giliyadi anali wankhondo wa mphamvu. Iyeyu amayi ake anali mkazi wachiwerewere, ndipo abambo ake anali Giliyadi.
И галаадецът Ефтай беше силен и храбър мъж; той беше син на една блудница; а Ефтаевият баща беше Галаад.
2 Mkazi wake wa Giliyadi anabereka naye ana aamuna. Tsono ana amenewa atakula anapirikitsa Yefita ndi kumuwuza kuti, “Sudzalandirako cholowa mʼnyumba ya abambo athu chifukwa ndiwe mwana wa mkazi wina.”
И жената на Галаад му роди синове; а когато пораснаха синовете на жена му, те изпъдиха Ефтая, като му казаха: Ти няма да наследиш в бащиния ни дом, защото си син на чужденка.
3 Choncho Yefita anathawa kuchoka kwa abale ake ndi kukakhala mʼdziko la Tobu. Kumeneko anakakopa ndi kusonkhanitsa anthu achabechabe ndipo anatuluka pamodzi kukasakaza zinthu.
Затова Ефтай побягна от братята си, та живееше в земята Тов; и при Ефтая се събраха безделници, които и излизаха с него.
4 Patapita nthawi Aamoni anadzachita nkhondo ndi Israeli.
А след известно време амонците воюваха против Израиля.
5 Tsono pamene Aamoni ankathira nkhondo Aisraeli, akuluakulu a ku Giliyadi anapita kukamutenga Yefita ku dziko la Tobu.
И когато се биеха амонците против Израиля, галаадските старейшини отидоха да доведат Ефтая от земята Тов,
6 Iwo anati kwa iye, “Bwera ukhale mkulu wathu wankhondo kuti timenyane ndi Amoni.”
като казаха на Ефтая: Дойди та ни стани началник, за да се бием против амонците.
7 Yefita anawawuza Agiliyadi kuti, “Kodi inu suja munkadana nane ndi kundithamangitsa ku nyumba ya abambo anga? Nʼchifukwa chiyani lero mwabwera kwa ine pamene muli pa mavuto?”
А Ефтай рече на галаадските старейшини: Не ме ли намразихте, и не ме ли изпъдихте им бащиния ми дом? А защо сте дошли при мене сега, когато сте на тясно?
8 Akuluakulu a ku Giliyadi aja anamuyankha kuti, “Chimene tabwerera kwa iwe ndi chakuti upite nafe kukamenyana ndi Aamoni, ndipo udzakhala wolamulira wa onse okhala mu Giliyadi.”
И галаадските старейшини казаха на Ефтая: За това сме се върнали сега при тебе, за да дойдеш с нас и да се биеш против амонците; и ти ще станеш за нас началник над всичките галаадски жители.
9 Yefita anawayankha akuluakulu a ku Giliyadi kuti, “Ngati mundibwezeranso kwathu kuti ndikachite nkhondo ndi Aamoni ndipo Yehova nʼkukandithandiza kuwagonjetsa, ndidzakhaladi wokulamulirani?”
И Ефтай каза на галаадските старейшини: Ако ме върнете у дома, за да воювам против амонците, и Господ ми ги предаде, наистина ли ще стана началник над вас?
10 Akuluakulu a ku Giliyadi anamuyankha kuti, “Yehova akhale mboni pakati pa inu ndi ife, ngati sitidzachita monga mwa mawu anu.”
И галаадските старейшини казаха на Ефтая: Господ нека бъде свидетел помежду ни! сигурно ще направим според както си казал.
11 Choncho Yefita anapita nawo akuluakulu a ku Giliyadi aja, ndipo anthu a kumeneko anamusandutsa kukhala wowalamulira ndi mkulu wankhondo. Tsono Yefita anabwerezanso mawu omwewa pamaso pa Yehova ku Mizipa.
Тогава Ефтай отиде с галаадските старейшини, и людете го поставиха глава и началник над себе си. И Ефтай изговори всичките си думи пред Господа в Масфа.
12 Kenaka Yefita anatuma amithenga kwa mfumu ya Aamoni ndi funso lakuti, “Kodi ife takuchimwirani chiyani kuti muzichita nkhondo ndi dziko langa?”
Тогава Ефтай прати посланици до царя на амонците да кажат: Каква работа имаш с мене, та си дошъл при мене да се биеш против земята ми?
13 Ndipo mfumu ya Aamoni inayankha amithenga a Yefita aja kuti, “Pamene Israeli amatuluka kuchokera mu Igupto, analanda dziko langa kuyambira ku mtsinje wa Arinoni mpaka ku mtsinje wa Yaboki mpakanso ku mtsinje wa Yorodani. Tsopano mundibwezere dziko langa mwamtendere.”
И царят на амонците отговори на Ефтаевите посланици: Защото Израил, когато идеше от Египет, отне земята ми от Арнон до Явок и до Иордан; сега, прочее, върни тия земи по мирен начин.
14 Yefita anatumizanso amithenga akewo kwa mfumu ya Aamoni
Тогава Ефтай пак прати посланици до царя на амонците да му рекат:
15 kukanena kuti, Yefita akuti, “Israeli sanalande dziko la Mowabu kapena dziko la Aamoni.
Така казва Ефтай: Израил не е отнел моавската земя, нито земята на амонците;
16 Koma pamene Aisraeli ankachoka ku Igupto anadzera njira ya ku chipululu mpaka ku Nyanja Yofiira nakafika ku Kadesi.
но когато Израил идеше от Египет и отиваше през пустинята към Червеното море, и беше дощъл в Кадис,
17 Kenaka Israeli anatumiza amithenga kwa mfumu ya ku Edomu kuti, ‘Chonde tiloleni kuti tidutse mʼdziko lanu,’ Koma mfumu ya ku Edomu sinamvere zimenezo. Aisraeli anatumizanso amithenga kwa mfumu ya ku Mowabu, ndipo iyo inakananso. Choncho Israeli anakhala ku Kadesi.
тогава Израил прати посланици до едомския цар да рекат: Нека премина, моля през земята ти. А едомският цар не послуша. Прати още и до моавския цар; но и той не склони. Затова Израил остана в Кадис.
18 “Pambuyo pake, Aisraeli ananyamuka ulendo kudzera ku chipululu nazungulira dziko la Edomu ndi dziko la Mowabu, ndipo anafika ku mmawa kwa dziko la Mowabu ndi kumanga zinthando zawo ku mbali ina ya mtsinje wa Arinoni. Iwo sanalowe mʼdziko la Mowabu, chifukwa mtsinje wa Arinoni ndiwo unali malire a dziko la Mowabu.
Тогава отиде през пустинята, та обиколи едомската земя и моавската земя, и, като мина по източната страна на моавската земя, разположи стан оттатък Арнон; но не възлезе вътре в моавските предели, защото Арнон беше моавската граница.
19 “Pambuyo pake Israeli anatumiza amithenga kwa Sihoni mfumu ya Aamori, amene amalamulira ku Hesiboni ndipo anati kwa iye, ‘Chonde tiloleni kuti tidutse mʼdziko lanu popita kwathu.’
След това Израил прати посланици до аморейския цар Сион есевонския цар, та Израил му каза: Нека преминем, молим те, през земята ти до нашето място.
20 Koma Sihoni sanalole Israeli kuti adzere mʼdziko mwake. Mʼmalo mwake Sihoni anasonkhanitsa ankhondo ake onse nakamanga msasa ku Yahazi ndipo anachita nkhondo ndi Israeli.
Но Сион не се довери на Израиля та да го пусне да мине през пределите му; а напротив Сион събра всичките си люде и, като разположи стан в Яса, воюва против Израиля.
21 “Koma Yehova Mulungu wa Israeli anamupereka Sihoni pamodzi ndi anthu ake onse mʼmanja mwa Israeli, ndipo anawagonjetsa. Choncho Aisraeli analanda dziko lonse la Aamori amene amakhala mʼdzikolo.
И Господ Израилевият Бог предаде Сиона и всичките му люде в ръката на Израиля, и те ги поразиха; и така Израил завладя цялата земя на аморейците, жителите на оная земя.
22 Analanda dziko lonse kuchokera ku Arinoni mpaka ku Yaboki ndiponso kuchokera ku chipululu mpaka ku mtsinje wa Yorodani.
Те завладяха всичките предели на аморейците, от Арнон до Явок, и от пустинята дори до Иордан.
23 “Ndiye kuti Yehova Mulungu wa Aisraeli ndiye analanda dziko la Aamori, kuwalandirira anthu ake. Kodi inu mukufuna kutilanda dzikolo?
И сега, когато Господ Израилевият Бог е изгонил аморейците отпред людете Си Израиля, ти ли ще притежаваш земята им?
24 Bwanji inu osakhazikika mʼdziko limene Kemosi mulungu wanu anakupatsani, ifenso tikhazikike mʼdziko limene Yehova Mulungu wathu anatipatsa?
Не ще ли притежаваш онова, което твоят бог Хамос ти дава да притежаваш? Също и ние ще притежаваме земите на всички, които Иеова нашият Бог е изгонил отпред нас.
25 Kodi ndinu abwino kuposa Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Mowabu? Kodi iye anakanganapo kapena kuchita nkhondo ndi Israeli?
И сега, ти в какво си по-добър от моавския цар Валак Сеяфоровия син? Борил ли се е той някога с Израиля, или воювал ли е някога против него?
26 Pamene Aisraeli ankakhala mʼdziko la Hesiboni ndi mʼmidzi yake, mʼdziko la Aroeri ndi midzi yake, komanso mʼmizinda yonse imene ili mʼmbali mwa mtsinje wa Arinoni kwa zaka 300, nʼchifukwa chiyani inu simunalande malowo nthawi imeneyo?
Триста години са откак се е заселил Израил в Есевон и в селата му, в Ароир и в селата му, и във всичките градове, които са разположени край Арнон; а защо през това време не сте ги превзели обратно?
27 Choncho ine sindinakuchimwireni. Koma inu mukundilakwira pomenyana nane. Yehova woweruza, ndiye aweruze lero mlandu wa pakati pa Aisraeli ndi Aamoni.”
Прочее, аз не съм ти съгрешил; но ти ме онеправдаваш като воюваш против мене. Господ Съдията нека съди днес между израилтяните и амонците.
28 Koma mfumu ya Aamori, sinasamale mawu amene Yefita anatumiza kwa iyo.
Но царят на амонците не послуша думите, които Ефтай му изпрати.
29 Tsono Mzimu wa Yehova unatsikira pa Yefita. Ndipo iye ananyamuka nadzera ku Giliyadi ndi ku Manase. Anafika ku Mizipa mʼdziko la Giliyadi, ndipo kuchokera kumeneko anapita kukalimbana ndi Aamoni.
Тогава дойде Господният Дух на Ефтая; и той мина през Галаад и Манасия, мина и през галаадската Масфа, и от галаадската Масфа мина против амонците.
30 Yefita analumbira kwa Yehova kuti, “Ngati mupereka Aamoni mʼmanja mwanga,
И Ефтай направи обрек Господу, като каза: Ако наистина предадеш амонците в ръката ми,
31 aliyense amene atuluke pa khomo la nyumba yanga kudzandichingamira pobwerera nditagonjetsa Aamoni adzakhala wake wa Yehova, ndipo ndidzamupereka kuti akhale nsembe yopsereza.”
тогава онова, което излезе из вратата на къщата ми да ме посрещне, когато се върна с мир от амонците, ще бъде Господу, и ще го принеса всеизгаряне.
32 Kenaka Yefita anawolokera kwa Aamoni kukamenya nawo nkhondo, ndipo Yehova anawaperekadi mʼmanja mwake.
И тъй, Ефтай замина към амонците, за да воюва против тях, и Господ ги предаде в ръката му;
33 Iye anawononga mizinda makumi awiri kuchokera ku Ariori mpaka pafupi ndi mzinda wa Miniti. Anapitirira mpaka ku Abeli-Keranimu. Choncho Aisraeli anagonjetsa Aamoni.
та ги порази от Ароир до Минит, двадесет града, и до Авел-Керамим, с твърде голямо поражение. Така се покориха амонците пред израилтяните.
34 Pambuyo pake Yefita anabwerera ku nyumba yake. Tsono anangoona mwana wake wamkazi akutuluka kudzamuchingamira akuyimba ngʼoma ndi kuvina. Uyu anali mwana yekhayo wa Yefita. Analibenso mwana wina wamwamuna kapena wamkazi.
Тогава, като дойде Ефтай у дома си в Месфа, ето, дъщеря му излизаше да го посрещне с тъпанчета и хора; и тя му беше едничка; освен нея нямаше ни син ни дъщеря.
35 Yefita ataona mwana wake uja, anangʼamba zovala zake ndi kulira, “Kalanga ine! Mwana wanga! Wandivulaza kwambiri ndipo iwe ndi gwero la mavuto anga. Ine ndinalumbira kwa Yehova ndi pakamwa pangapa ndipo sindingathe kubweza malumbiro angawo.”
И като я видя той, раздра дрехите си и каза: Горко ми, щерко моя! ти съвсем си ме унижила, и си от ония, които ме смущават; защото аз изговорих думи към Господа, и не мога да отстъпя.
36 Mwanayo anayankha kuti, “Abambo, ngati munalonjeza kwa Yehova ndi pakamwa panu, chitani zimene munalonjezera pakuti Yehova wakuthandizani kulipsira adani anu Amowabu.”
А тя му каза: Тате, понеже си изговорил думи към Господа, стори с мене според това, тъй като Господ извърши за тебе възмездие на неприятелите ти амонците.
37 Anatinso kwa abambo ake, “Ndikupempheni chinthu ichi: Mundilole ndikayendeyende ku mapiri miyezi iwiri ndizikalira pamodzi ndi anzanga chifukwa ndikufa ndikanali namwali wosadziwa mwamuna.”
Каза още на баща си: Нека ми се направи това: остави ме два месеца да ида да ходя по хълмовете, аз и другарките ми, и да оплача девството си.
38 Yefita anamuyankha kuti, “Pita.” Ndipo anamulola kuti apite miyezi iwiri. Tsono anapita kumapiri ndi atsikana anzake kukalira chifukwa cha unamwali wake.
И той рече: Иди, И пусна я за два месеца. И тя отиде с другарките си, та оплака девството си по хълмовете.
39 Miyezi iwiri itatha iye anabwerera kwa abambo ake, ndipo anachitadi zimene analonjeza. Motero unakhala mwambo wa Aisraeli,
И в края на двата месеца се върна при баща си; и той стори с нея според обрека, който бе направил. И тя не беше познала мъж. От това стана обичай в Израил,
40 kuti atsikana a Israeli ankapita chaka chilichonse kukalira maliro a mwana wa mkazi wa Yefita, Mgiliyadi uja masiku makumi anayi pa chaka.
да ходят Израилевите дъщери всяка година, четири дена в годината, за да оплакват дъщерята на галаадеца Ефтай.