< Oweruza 10 >

1 Atafa Abimeleki panabwera Tola mwana wa Puwa, mdzukulu wa Dodo kudzapulumutsa Aisraeli. Iyeyu anali wa fuko la Isakara ndipo ankakhala ku Samiri mʼdziko la mapiri la Efereimu.
Después de Abimelec, Tola, hijo de Fúa, hijo de Dodo, de la tribu de Isacar, se convirtió en el salvador de Israel; vivía en Samir, en la región montañosa de Efraín.
2 Iye anatsogolera Aisraeli kwa zaka 23, ndipo anamwalira ndi kuyikidwa ku Samiri.
Fue juez sobre Israel por veintitrés años; y en su muerte su cuerpo fue enterrado en la tierra en Samir.
3 Atafa Tola panabwera Yairi wa ku Giliyadi, amene anatsogolera Israeli kwa zaka 22.
Y después de él, vino Jair el galaadita, que había sido juez de Israel durante veintidós años.
4 Iyeyu anali ndi ana aamuna makumi atatu, amene ankakwera pa abulu makumi atatu. Iwo anali ndi mizinda makumi atatu mʼdziko la Giliyadi, imene mpaka lero ikutchedwa kuti Havoti Yairi.
Y tuvo treinta hijos, que montaban treinta asnos; y tenían treinta ciudades en la tierra de Galaad, que hasta hoy se llaman ciudades de Jair.
5 Atamwalira Yairi anayikidwa mʼmanda ku Kamoni.
Y a la muerte de Jair su cuerpo fue enterrado en Camon.
6 Aisraeli anachitanso zoyipira Yehova. Iwo anatumikira Abaala ndi Asitoreti, milungu ya ku Aramu, Sidoni, Mowabu, Aamoni ndi Afilisti. Choncho analeka osatumikiranso Yehova.
Y nuevamente los hijos de Israel hicieron lo malo ante los ojos del Señor, adorando a los baales y Astarte, de Siria, de Sidón, de Moab, de Amón, de los filisteos; renunciaron al Señor y ya no le sirvieron más.
7 Tsono Yehova anapsera mtima Aisraeli ndipo anawapereka mʼmanja mwa Afilisti ndi Aamoni.
Y se encendió la ira del Señor contra Israel, y los entregó en manos de los filisteos y en manos de los amonitas.
8 Iwowa anawagonjetseratu Aisraeli mʼchaka chimenechi, ndipo kwa zaka 18 anakhala akusautsa Aisraeli onse amene anali pa tsidya la Yorodani, mʼdziko la Aamori ku Giliyadi.
Y ese año los hijos de Israel fueron oprimidos bajo su yugo; durante dieciocho años, todos los hijos de Israel al otro lado del Jordán, en la tierra de los amorreos que se encuentra en Galaad, fueron oprimidos cruelmente.
9 Aamori anawoloka mtsinje wa Yorodani kukathira nkhondo mafuko a Yuda, Benjamini ndi Efereimu kotero kuti Israeli anavutika kwambiri.
Y los hijos de Amón cruzaron por el Jordán, para hacer guerra contra Judá y Benjamín y la casa de Efraín; e Israel estaba en un gran problema.
10 Kenaka Aisraeli analira kwa Yehova kuti, “Ife takuchimwirani popeza tasiya Inu Mulungu wathu ndi kutumikira Abaala.”
Entonces los hijos de Israel, clamando al Señor, dijeron: Grande es nuestro pecado contra ti, porque hemos abandonado a nuestro Dios y hemos sido siervos de los baales.
11 Yehova anawafunsa kuti, “Suja ine ndinakupulumutsani kwa Aigupto, Aamori, Aamoni ndi Afilisti?
Y él Señor dijo a los hijos de Israel: ¿No eran los egipcios y los amorreos y los hijos de Amón y los filisteos?
12 Ndiponso pamene Asidoni, Aamaleki ndi Amoni anakuzunzani, inu nʼkulirira kwa ine suja ndinakupulumutsani kwa anthu amenewa?
Y los sidonios y Amalec y Madián que los oprimieron, y en respuesta a su clamor, ¿no fui yo quien los salvó de sus manos?
13 Komabe inu mwandikana ndipo mukutumikira milungu ina. Choncho sindidzakupulumutsaninso.
Pero, por todo esto, me han abandonado y han adorado otros dioses: así que, ya no seré su salvador.
14 Pitani kalireni kwa milungu imene mwayisankha. Iyoyo ikupulumutseni ku mavuto anuwo.”
Ve, envía tu clamor de ayuda a los dioses de tu elección; Que sean tus salvadores en el tiempo de tu problema.
15 Koma Aisraeli anayankha Yehova kuti, “Ife tachimwa. Tichitireni chimene mukuona kuti ndi chabwino, koma chonde tipulumutseni lero lokha.”
Y los hijos de Israel dijeron al Señor: Somos pecadores; Haznos lo que te parezca bien: danos la salvación este día.
16 Ndipo anachotsa milungu ya chilendo pakati pawo ndi kuyamba kutumikira Yehova. Ndipo Yehova anamva chisoni poona mmene Aisraeli ankazunzikira.
Entonces apartaron a los dioses extranjeros de entre ellos, para volver a adorar al Señor; y su alma ya no pudo soportar el sufrimiento de Israel.
17 Tsono Aamoni anasonkhana ndi kumanga zithando za nkhondo ku Giliyadi. Nawonso Aisraeli anasonkhana ndi kumanga zithando zawo za nkhondo ku Mizipa.
Entonces los hijos de Amón se reunieron y pusieron su ejército en posición en Galaad. Y los hijos de Israel se reunieron y pusieron su ejército en posición en Mizpa.
18 Kenaka anthuwo ndi atsogoleri a Agiliyadi anayamba kufunsana kuti, “Kodi ndi munthu wotani amene atayambe kuthira nkhondo Aamoni? Iyeyu adzakhala mtsogoleri wolamulira anthu onse a ku Giliyadi.”
Y el pueblo de Israel se dijeron unos a otros: Quién sea el primero en atacar a los hijos de Amón, Le haremos jefe de los habitantes de Galaad.

< Oweruza 10 >