< Oweruza 10 >
1 Atafa Abimeleki panabwera Tola mwana wa Puwa, mdzukulu wa Dodo kudzapulumutsa Aisraeli. Iyeyu anali wa fuko la Isakara ndipo ankakhala ku Samiri mʼdziko la mapiri la Efereimu.
Ngemva kwensuku zika-Abhimelekhi kwavela umuntu wako-Isakhari, uThola indodana kaPhuwa, indodana kaDodo ukuba ahlenge u-Israyeli. Wayehlala eShamiri, elizweni lezintaba elako-Efrayimi.
2 Iye anatsogolera Aisraeli kwa zaka 23, ndipo anamwalira ndi kuyikidwa ku Samiri.
Wakhokhela u-Israyeli iminyaka engamatshumi amabili lantathu; wasesifa, wangcwatshwa eShamiri.
3 Atafa Tola panabwera Yairi wa ku Giliyadi, amene anatsogolera Israeli kwa zaka 22.
Walandelwa nguJayiri owaseGiliyadi, owakhokhela u-Israyeli iminyaka engamatshumi amabili lambili.
4 Iyeyu anali ndi ana aamuna makumi atatu, amene ankakwera pa abulu makumi atatu. Iwo anali ndi mizinda makumi atatu mʼdziko la Giliyadi, imene mpaka lero ikutchedwa kuti Havoti Yairi.
Wayelamadodana angamatshumi amathathu, ayegada obabhemi abangamatshumi amathathu. Ayephethe amadolobho angamatshumi amathathu eGiliyadi, lalamhlanje abizwa ngokuthi Havothi Jayiri.
5 Atamwalira Yairi anayikidwa mʼmanda ku Kamoni.
Ekufeni kwakhe uJayiri wangcwatshwa eKhamoni.
6 Aisraeli anachitanso zoyipira Yehova. Iwo anatumikira Abaala ndi Asitoreti, milungu ya ku Aramu, Sidoni, Mowabu, Aamoni ndi Afilisti. Choncho analeka osatumikiranso Yehova.
Abako-Israyeli benza okubi futhi emehlweni kaThixo. Bakhonza oBhali labo-Ashithorethi, labonkulunkulu base-Aramu, labonkulunkulu baseSidoni, labonkulunkulu baseMowabi, labonkulunkulu bama-Amoni, kanye labonkulunkulu bamaFilistiya. Ngenxa yokuthi abako-Israyeli bamdela uThixo kabaze babe besamkhonza,
7 Tsono Yehova anapsera mtima Aisraeli ndipo anawapereka mʼmanja mwa Afilisti ndi Aamoni.
wabathukuthelela kakhulu. Wabanikela ezandleni zamaFilistiya lama-Amoni,
8 Iwowa anawagonjetseratu Aisraeli mʼchaka chimenechi, ndipo kwa zaka 18 anakhala akusautsa Aisraeli onse amene anali pa tsidya la Yorodani, mʼdziko la Aamori ku Giliyadi.
okwathi ngalowomnyaka abachitha abanqoba. Ancindizela abako-Israyeli bonke okweminyaka elitshumi lasificaminwembili ngasempumalanga kweJodani eGiliyadi, ilizwe lama-Amori.
9 Aamori anawoloka mtsinje wa Yorodani kukathira nkhondo mafuko a Yuda, Benjamini ndi Efereimu kotero kuti Israeli anavutika kwambiri.
Ama-Amoni futhi achapha iJodani ukuba alwe loJuda, loBhenjamini kanye lendlu ka-Efrayimi; u-Israyeli wayephakathi kohlupho olukhulu.
10 Kenaka Aisraeli analira kwa Yehova kuti, “Ife takuchimwirani popeza tasiya Inu Mulungu wathu ndi kutumikira Abaala.”
Lapho-ke abako-Israyeli bakhala kuThixo bathi, “Senze isono kuwe, sadela uNkulunkulu wethu sakhonza oBhali.”
11 Yehova anawafunsa kuti, “Suja ine ndinakupulumutsani kwa Aigupto, Aamori, Aamoni ndi Afilisti?
UThixo waphendula wathi, “Lapho amaGibhithe, lama-Amori, lama-Amoni, lamaFilistiya,
12 Ndiponso pamene Asidoni, Aamaleki ndi Amoni anakuzunzani, inu nʼkulirira kwa ine suja ndinakupulumutsani kwa anthu amenewa?
lamaSidoni, lama-Amaleki kanye lamaMawoni alincindezela lakhulekela usizo kimi, kangilihlenganga ezandleni zawo na?
13 Komabe inu mwandikana ndipo mukutumikira milungu ina. Choncho sindidzakupulumutsaninso.
Kodwa selingidelile lakhonza abanye onkulunkulu, ngakho angisayikulisindisa.
14 Pitani kalireni kwa milungu imene mwayisankha. Iyoyo ikupulumutseni ku mavuto anuwo.”
Hambani liyekhala kubonkulunkulu elibathembileyo. Kabalisindise nxa seliphakathi kokuhlupheka!”
15 Koma Aisraeli anayankha Yehova kuti, “Ife tachimwa. Tichitireni chimene mukuona kuti ndi chabwino, koma chonde tipulumutseni lero lokha.”
Kodwa abako-Israyeli bathi kuThixo, “Senze isono. Yenza kithi lokho okubona kulungile kuwe, kodwa ake usihlenge khathesi nje.”
16 Ndipo anachotsa milungu ya chilendo pakati pawo ndi kuyamba kutumikira Yehova. Ndipo Yehova anamva chisoni poona mmene Aisraeli ankazunzikira.
Ngakho basusa onkulunkulu bezizweni phakathi kwabo bakhonza uThixo. Wayengeke alumele futhi usizi luka-Israyeli.
17 Tsono Aamoni anasonkhana ndi kumanga zithando za nkhondo ku Giliyadi. Nawonso Aisraeli anasonkhana ndi kumanga zithando zawo za nkhondo ku Mizipa.
Kwathi ama-Amoni esebizelwe empini njalo emise eGiliyadi, abako-Israyeli abuthana amisa eMizipha.
18 Kenaka anthuwo ndi atsogoleri a Agiliyadi anayamba kufunsana kuti, “Kodi ndi munthu wotani amene atayambe kuthira nkhondo Aamoni? Iyeyu adzakhala mtsogoleri wolamulira anthu onse a ku Giliyadi.”
Abakhokheli babantu baseGiliyadi bathi omunye komunye, “Lowo ozaqalisa ukuhlasela ama-Amoni uzakuba yinduna yabo bonke abahlala eGiliyadi.”