< Oweruza 10 >

1 Atafa Abimeleki panabwera Tola mwana wa Puwa, mdzukulu wa Dodo kudzapulumutsa Aisraeli. Iyeyu anali wa fuko la Isakara ndipo ankakhala ku Samiri mʼdziko la mapiri la Efereimu.
Après Abimélec, Tola, fils de Puah, fils de Dodo, homme d'Issacar, se leva pour sauver Israël. Il habitait à Schamir, dans la montagne d'Éphraïm.
2 Iye anatsogolera Aisraeli kwa zaka 23, ndipo anamwalira ndi kuyikidwa ku Samiri.
Il jugea Israël pendant vingt-trois ans, puis il mourut et fut enterré à Schamir.
3 Atafa Tola panabwera Yairi wa ku Giliyadi, amene anatsogolera Israeli kwa zaka 22.
Après lui se leva Jaïr, le Galaadite. Il fut juge en Israël pendant vingt-deux ans.
4 Iyeyu anali ndi ana aamuna makumi atatu, amene ankakwera pa abulu makumi atatu. Iwo anali ndi mizinda makumi atatu mʼdziko la Giliyadi, imene mpaka lero ikutchedwa kuti Havoti Yairi.
Il avait trente fils qui montaient sur trente ânes. Ils avaient trente villes, qui sont appelées jusqu'à ce jour Havvoth Jaïr, et qui sont situées dans le pays de Galaad.
5 Atamwalira Yairi anayikidwa mʼmanda ku Kamoni.
Jaïr mourut, et il fut enterré à Kamon.
6 Aisraeli anachitanso zoyipira Yehova. Iwo anatumikira Abaala ndi Asitoreti, milungu ya ku Aramu, Sidoni, Mowabu, Aamoni ndi Afilisti. Choncho analeka osatumikiranso Yehova.
Les enfants d'Israël firent encore ce qui est mal aux yeux de Yahvé, et ils servirent les Baals, les Ashtaroths, les dieux de Syrie, les dieux de Sidon, les dieux de Moab, les dieux des enfants d'Ammon et les dieux des Philistins. Ils abandonnèrent Yahvé et ne le servirent pas.
7 Tsono Yehova anapsera mtima Aisraeli ndipo anawapereka mʼmanja mwa Afilisti ndi Aamoni.
La colère de Yahvé s'enflamma contre Israël, et il les vendit entre les mains des Philistins et entre les mains des enfants d'Ammon.
8 Iwowa anawagonjetseratu Aisraeli mʼchaka chimenechi, ndipo kwa zaka 18 anakhala akusautsa Aisraeli onse amene anali pa tsidya la Yorodani, mʼdziko la Aamori ku Giliyadi.
Ils troublèrent et opprimèrent les enfants d'Israël cette année-là. Ils opprimèrent pendant dix-huit ans tous les enfants d'Israël qui étaient au-delà du Jourdain, dans le pays des Amoréens, qui est en Galaad.
9 Aamori anawoloka mtsinje wa Yorodani kukathira nkhondo mafuko a Yuda, Benjamini ndi Efereimu kotero kuti Israeli anavutika kwambiri.
Les enfants d'Ammon passèrent le Jourdain pour combattre Juda, Benjamin et la maison d'Ephraïm, de sorte qu'Israël fut très éprouvé.
10 Kenaka Aisraeli analira kwa Yehova kuti, “Ife takuchimwirani popeza tasiya Inu Mulungu wathu ndi kutumikira Abaala.”
Les enfants d'Israël crièrent à Yahvé, en disant: « Nous avons péché contre toi, parce que nous avons abandonné notre Dieu et servi les Baals. »
11 Yehova anawafunsa kuti, “Suja ine ndinakupulumutsani kwa Aigupto, Aamori, Aamoni ndi Afilisti?
Yahvé dit aux enfants d'Israël: « Ne vous ai-je pas sauvés des Égyptiens, des Amoréens, des enfants d'Ammon et des Philistins?
12 Ndiponso pamene Asidoni, Aamaleki ndi Amoni anakuzunzani, inu nʼkulirira kwa ine suja ndinakupulumutsani kwa anthu amenewa?
Les Sidoniens, les Amalécites et les Maonites vous ont opprimés; vous avez crié vers moi, et je vous ai sauvés de leur main.
13 Komabe inu mwandikana ndipo mukutumikira milungu ina. Choncho sindidzakupulumutsaninso.
Mais vous m'avez abandonné et vous avez servi d'autres dieux. C'est pourquoi je ne vous sauverai plus.
14 Pitani kalireni kwa milungu imene mwayisankha. Iyoyo ikupulumutseni ku mavuto anuwo.”
Va et crie vers les dieux que tu as choisis. Qu'ils te sauvent au temps de ta détresse! »
15 Koma Aisraeli anayankha Yehova kuti, “Ife tachimwa. Tichitireni chimene mukuona kuti ndi chabwino, koma chonde tipulumutseni lero lokha.”
Les enfants d'Israël dirent à Yahvé: « Nous avons péché! Fais de nous ce qui te semble bon; mais délivre-nous, je t'en prie, aujourd'hui. »
16 Ndipo anachotsa milungu ya chilendo pakati pawo ndi kuyamba kutumikira Yehova. Ndipo Yehova anamva chisoni poona mmene Aisraeli ankazunzikira.
Ils chassèrent les dieux étrangers du milieu d'eux et servirent Yahvé; et son âme fut affligée de la misère d'Israël.
17 Tsono Aamoni anasonkhana ndi kumanga zithando za nkhondo ku Giliyadi. Nawonso Aisraeli anasonkhana ndi kumanga zithando zawo za nkhondo ku Mizipa.
Alors les enfants d'Ammon se rassemblèrent et campèrent à Galaad. Les enfants d'Israël se rassemblèrent et campèrent à Mitspa.
18 Kenaka anthuwo ndi atsogoleri a Agiliyadi anayamba kufunsana kuti, “Kodi ndi munthu wotani amene atayambe kuthira nkhondo Aamoni? Iyeyu adzakhala mtsogoleri wolamulira anthu onse a ku Giliyadi.”
Le peuple, les princes de Galaad, se dirent les uns aux autres: « Quel est l'homme qui commencera à combattre les enfants d'Ammon? Il sera le chef de tous les habitants de Galaad. »

< Oweruza 10 >