< Oweruza 10 >

1 Atafa Abimeleki panabwera Tola mwana wa Puwa, mdzukulu wa Dodo kudzapulumutsa Aisraeli. Iyeyu anali wa fuko la Isakara ndipo ankakhala ku Samiri mʼdziko la mapiri la Efereimu.
And there arose, after Abimelech, to save Israel—Tola son of Puah son of Dodo, a man of Issachar, —and, he, used to sit in Shamir, in the hill country of Ephraim;
2 Iye anatsogolera Aisraeli kwa zaka 23, ndipo anamwalira ndi kuyikidwa ku Samiri.
and he judged Israel, twenty-three years, —and died, and was buried in Shamir.
3 Atafa Tola panabwera Yairi wa ku Giliyadi, amene anatsogolera Israeli kwa zaka 22.
And there arose, after him, Jair the Gileadite, —and judged Israel twenty-two years.
4 Iyeyu anali ndi ana aamuna makumi atatu, amene ankakwera pa abulu makumi atatu. Iwo anali ndi mizinda makumi atatu mʼdziko la Giliyadi, imene mpaka lero ikutchedwa kuti Havoti Yairi.
Now he had thirty sons, that rode on thirty ass colts, and they had, thirty cities, —they are called Havvoth-jair, until this day, which are in the land of Gilead.
5 Atamwalira Yairi anayikidwa mʼmanda ku Kamoni.
And Jair died, and was buried in Kamon.
6 Aisraeli anachitanso zoyipira Yehova. Iwo anatumikira Abaala ndi Asitoreti, milungu ya ku Aramu, Sidoni, Mowabu, Aamoni ndi Afilisti. Choncho analeka osatumikiranso Yehova.
And the sons of Israel again did the thing that was wicked in the sight of Yahweh, and served the Baals and the Ashtoreths, and the gods of Syria, and the gods of Zidon, and the gods of Moab, and the gods of the sons of Ammon, and the gods of the Philistines, —and forsook Yahweh, and served him not.
7 Tsono Yehova anapsera mtima Aisraeli ndipo anawapereka mʼmanja mwa Afilisti ndi Aamoni.
So the anger of Yahweh kindled upon Israel, —and he sold them into the hand of the Philistines, and into the hand of the sons of Ammon;
8 Iwowa anawagonjetseratu Aisraeli mʼchaka chimenechi, ndipo kwa zaka 18 anakhala akusautsa Aisraeli onse amene anali pa tsidya la Yorodani, mʼdziko la Aamori ku Giliyadi.
and they enfeebled and oppressed the sons of Israel in that year, —eighteen years, did they this unto all the sons of Israel who were beyond the Jordan, in the land of the Amorites, that was in Gilead.
9 Aamori anawoloka mtsinje wa Yorodani kukathira nkhondo mafuko a Yuda, Benjamini ndi Efereimu kotero kuti Israeli anavutika kwambiri.
And the sons of Ammon crossed the Jordan, to fight, even against Judah and against Benjamin, and against the house of Ephraim, —so that Israel was sore distressed.
10 Kenaka Aisraeli analira kwa Yehova kuti, “Ife takuchimwirani popeza tasiya Inu Mulungu wathu ndi kutumikira Abaala.”
Then did the sons of Israel make outcry unto Yahweh, saying, —We have sinned against thee, because we have forsaken our God, and have served the Baals.
11 Yehova anawafunsa kuti, “Suja ine ndinakupulumutsani kwa Aigupto, Aamori, Aamoni ndi Afilisti?
Then said Yahweh unto the sons of Israel, —Was it not, from the Egyptians, and from the Amorites, and from the sons of Ammon, and from the Philistines, [that I saved you]?
12 Ndiponso pamene Asidoni, Aamaleki ndi Amoni anakuzunzani, inu nʼkulirira kwa ine suja ndinakupulumutsani kwa anthu amenewa?
The Zidonians also, and the Amalekites, and the Maonites, oppressed you, —and ye made outcry unto me, and I saved you out of their hand.
13 Komabe inu mwandikana ndipo mukutumikira milungu ina. Choncho sindidzakupulumutsaninso.
Yet have, ye, forsaken me, and served other gods, —therefore will I not again save you.
14 Pitani kalireni kwa milungu imene mwayisankha. Iyoyo ikupulumutseni ku mavuto anuwo.”
Go and make outcry unto the gods whom ye have chosen, —they, must save you, in the time of your tribulation.
15 Koma Aisraeli anayankha Yehova kuti, “Ife tachimwa. Tichitireni chimene mukuona kuti ndi chabwino, koma chonde tipulumutseni lero lokha.”
And the sons of Israel said unto Yahweh—We have sinned, do, thou, with us, according to all that is fitting in thine eyes, —only rescue us, we beseech thee this day.
16 Ndipo anachotsa milungu ya chilendo pakati pawo ndi kuyamba kutumikira Yehova. Ndipo Yehova anamva chisoni poona mmene Aisraeli ankazunzikira.
And they put away the gods of the stranger out of their midst, and served Yahweh, —and his soul was impatient of the misery of Israel.
17 Tsono Aamoni anasonkhana ndi kumanga zithando za nkhondo ku Giliyadi. Nawonso Aisraeli anasonkhana ndi kumanga zithando zawo za nkhondo ku Mizipa.
Now the sons of Ammon were called out, and they encamped in Gilead, —and the sons of Israel assembled themselves together, and encamped in Mizpah.
18 Kenaka anthuwo ndi atsogoleri a Agiliyadi anayamba kufunsana kuti, “Kodi ndi munthu wotani amene atayambe kuthira nkhondo Aamoni? Iyeyu adzakhala mtsogoleri wolamulira anthu onse a ku Giliyadi.”
Then said the people, the princes of Gilead, one to another, Who is the man that will begin to fight against the sons of Ammon? he shall become head to all the inhabitants of Gilead.

< Oweruza 10 >