< Oweruza 10 >

1 Atafa Abimeleki panabwera Tola mwana wa Puwa, mdzukulu wa Dodo kudzapulumutsa Aisraeli. Iyeyu anali wa fuko la Isakara ndipo ankakhala ku Samiri mʼdziko la mapiri la Efereimu.
After Abimelech there arose to save Israel Tola the son of Puah, the son of Dodo, a man of Issachar; and he lived in Shamir in the hill country of Ephraim.
2 Iye anatsogolera Aisraeli kwa zaka 23, ndipo anamwalira ndi kuyikidwa ku Samiri.
He judged Israel twenty-three years, and died, and was buried in Shamir.
3 Atafa Tola panabwera Yairi wa ku Giliyadi, amene anatsogolera Israeli kwa zaka 22.
After him arose Jair, the Gileadite; and he judged Israel twenty-two years.
4 Iyeyu anali ndi ana aamuna makumi atatu, amene ankakwera pa abulu makumi atatu. Iwo anali ndi mizinda makumi atatu mʼdziko la Giliyadi, imene mpaka lero ikutchedwa kuti Havoti Yairi.
He had thirty sons who rode on thirty donkeys, and they had thirty towns, which are called Havvoth Jair to this day, which are in the land of Gilead.
5 Atamwalira Yairi anayikidwa mʼmanda ku Kamoni.
Jair died, and was buried in Kamon.
6 Aisraeli anachitanso zoyipira Yehova. Iwo anatumikira Abaala ndi Asitoreti, milungu ya ku Aramu, Sidoni, Mowabu, Aamoni ndi Afilisti. Choncho analeka osatumikiranso Yehova.
The children of Israel again did that which was evil in the sight of the LORD, and served the Baals, and the Ashtaroth, and the gods of Aram, and the gods of Sidon, and the gods of Moab, and the gods of the people of Ammon, and the gods of the Philistines; and they forsook the LORD, and did not serve him.
7 Tsono Yehova anapsera mtima Aisraeli ndipo anawapereka mʼmanja mwa Afilisti ndi Aamoni.
The anger of the LORD was kindled against Israel, and he sold them into the hand of the Philistines, and into the hand of the people of Ammon.
8 Iwowa anawagonjetseratu Aisraeli mʼchaka chimenechi, ndipo kwa zaka 18 anakhala akusautsa Aisraeli onse amene anali pa tsidya la Yorodani, mʼdziko la Aamori ku Giliyadi.
And they shattered and oppressed the children of Israel that year. Eighteen years they oppressed all the children of Israel that were beyond the Jordan in the land of the Amorites, which is in Gilead.
9 Aamori anawoloka mtsinje wa Yorodani kukathira nkhondo mafuko a Yuda, Benjamini ndi Efereimu kotero kuti Israeli anavutika kwambiri.
The people of Ammon passed over the Jordan to fight also against Judah, and against Benjamin, and against the house of Ephraim; so that Israel was very distressed.
10 Kenaka Aisraeli analira kwa Yehova kuti, “Ife takuchimwirani popeza tasiya Inu Mulungu wathu ndi kutumikira Abaala.”
The children of Israel cried to the LORD, saying, "We have sinned against you, even because we have forsaken our God, and have served the Baals."
11 Yehova anawafunsa kuti, “Suja ine ndinakupulumutsani kwa Aigupto, Aamori, Aamoni ndi Afilisti?
The LORD said to the children of Israel, "Did I not save you from the Egyptians, and from the Amorites, from the people of Ammon, and from the Philistines?
12 Ndiponso pamene Asidoni, Aamaleki ndi Amoni anakuzunzani, inu nʼkulirira kwa ine suja ndinakupulumutsani kwa anthu amenewa?
Also the Sidonians, and Amalek, and Midian oppressed you; and you cried to me, and I saved you out of their hand.
13 Komabe inu mwandikana ndipo mukutumikira milungu ina. Choncho sindidzakupulumutsaninso.
Yet you have forsaken me, and served other gods. Therefore I will save you no more.
14 Pitani kalireni kwa milungu imene mwayisankha. Iyoyo ikupulumutseni ku mavuto anuwo.”
Go and cry to the gods which you have chosen; let them save you in the time of your distress."
15 Koma Aisraeli anayankha Yehova kuti, “Ife tachimwa. Tichitireni chimene mukuona kuti ndi chabwino, koma chonde tipulumutseni lero lokha.”
The children of Israel said to the LORD, "We have sinned. Do to us whatever seems good to you; only deliver us, please, this day."
16 Ndipo anachotsa milungu ya chilendo pakati pawo ndi kuyamba kutumikira Yehova. Ndipo Yehova anamva chisoni poona mmene Aisraeli ankazunzikira.
They put away the foreign gods from among them, and served the LORD; and his soul was grieved with the misery of Israel.
17 Tsono Aamoni anasonkhana ndi kumanga zithando za nkhondo ku Giliyadi. Nawonso Aisraeli anasonkhana ndi kumanga zithando zawo za nkhondo ku Mizipa.
Then the people of Ammon were gathered together, and camped in Gilead. The children of Israel assembled themselves together, and camped at Mizpah.
18 Kenaka anthuwo ndi atsogoleri a Agiliyadi anayamba kufunsana kuti, “Kodi ndi munthu wotani amene atayambe kuthira nkhondo Aamoni? Iyeyu adzakhala mtsogoleri wolamulira anthu onse a ku Giliyadi.”
And the people, the leaders of Gilead, said to each other, "What man is he who will begin to fight against the people of Ammon? He shall be head over all the inhabitants of Gilead."

< Oweruza 10 >