< Oweruza 10 >
1 Atafa Abimeleki panabwera Tola mwana wa Puwa, mdzukulu wa Dodo kudzapulumutsa Aisraeli. Iyeyu anali wa fuko la Isakara ndipo ankakhala ku Samiri mʼdziko la mapiri la Efereimu.
And there rises after Abimelech, to save Israel, Tola son of Puah, son of Dodo, a man of Issachar, and he is dwelling in Shamir, in the hill-country of Ephraim,
2 Iye anatsogolera Aisraeli kwa zaka 23, ndipo anamwalira ndi kuyikidwa ku Samiri.
and he judges Israel [for] twenty-three years, and he dies, and is buried in Shamir.
3 Atafa Tola panabwera Yairi wa ku Giliyadi, amene anatsogolera Israeli kwa zaka 22.
And there rises Jair the Gileadite after him, and he judges Israel [for] twenty-two years,
4 Iyeyu anali ndi ana aamuna makumi atatu, amene ankakwera pa abulu makumi atatu. Iwo anali ndi mizinda makumi atatu mʼdziko la Giliyadi, imene mpaka lero ikutchedwa kuti Havoti Yairi.
and he has thirty sons riding on thirty donkey-colts, and they have thirty cities (they call them Havoth-Jair to this day), which [are] in the land of Gilead;
5 Atamwalira Yairi anayikidwa mʼmanda ku Kamoni.
and Jair dies, and is buried in Kamon.
6 Aisraeli anachitanso zoyipira Yehova. Iwo anatumikira Abaala ndi Asitoreti, milungu ya ku Aramu, Sidoni, Mowabu, Aamoni ndi Afilisti. Choncho analeka osatumikiranso Yehova.
And the sons of Israel add to do evil in the eyes of YHWH, and serve the Ba‘alim, and Ashtaroth, and the gods of Aram, and the gods of Sidon, and the gods of Moab, and the gods of the sons of Ammon, and the gods of the Philistines, and forsake YHWH, and have not served Him;
7 Tsono Yehova anapsera mtima Aisraeli ndipo anawapereka mʼmanja mwa Afilisti ndi Aamoni.
and the anger of YHWH burns against Israel, and He sells them into the hand of the Philistines, and into the hand of the sons of Ammon,
8 Iwowa anawagonjetseratu Aisraeli mʼchaka chimenechi, ndipo kwa zaka 18 anakhala akusautsa Aisraeli onse amene anali pa tsidya la Yorodani, mʼdziko la Aamori ku Giliyadi.
and they crush and oppress the sons of Israel in that year; [and for] eighteen years—all the sons of Israel [who] are beyond the Jordan, in the land of the Amorite, which [is] in Gilead.
9 Aamori anawoloka mtsinje wa Yorodani kukathira nkhondo mafuko a Yuda, Benjamini ndi Efereimu kotero kuti Israeli anavutika kwambiri.
And the sons of Ammon pass over the Jordan to also fight against Judah, and against Benjamin, and against the house of Ephraim, and Israel has great distress.
10 Kenaka Aisraeli analira kwa Yehova kuti, “Ife takuchimwirani popeza tasiya Inu Mulungu wathu ndi kutumikira Abaala.”
And the sons of Israel cry to YHWH, saying, “We have sinned against You, because we have even forsaken our God, and serve the Ba‘alim.”
11 Yehova anawafunsa kuti, “Suja ine ndinakupulumutsani kwa Aigupto, Aamori, Aamoni ndi Afilisti?
And YHWH says to the sons of Israel, “[Have I] not [saved you] from the Egyptians, and from the Amorite, from the sons of Ammon, and from the Philistines?
12 Ndiponso pamene Asidoni, Aamaleki ndi Amoni anakuzunzani, inu nʼkulirira kwa ine suja ndinakupulumutsani kwa anthu amenewa?
And the Zidonians, and Amalek, and Maon have oppressed you, and you cry to Me, and I save you out of their hand;
13 Komabe inu mwandikana ndipo mukutumikira milungu ina. Choncho sindidzakupulumutsaninso.
and you have forsaken Me, and serve other gods, therefore I do not add to save you.
14 Pitani kalireni kwa milungu imene mwayisankha. Iyoyo ikupulumutseni ku mavuto anuwo.”
Go and cry to the gods on which you have fixed; they save you in the time of your tribulation.”
15 Koma Aisraeli anayankha Yehova kuti, “Ife tachimwa. Tichitireni chimene mukuona kuti ndi chabwino, koma chonde tipulumutseni lero lokha.”
And the sons of Israel say to YHWH, “We have sinned, do to us according to all that is good in Your eyes; only please deliver us this day.”
16 Ndipo anachotsa milungu ya chilendo pakati pawo ndi kuyamba kutumikira Yehova. Ndipo Yehova anamva chisoni poona mmene Aisraeli ankazunzikira.
And they turn aside the gods of the stranger out of their midst, and serve YHWH, and His soul is grieved with the misery of Israel.
17 Tsono Aamoni anasonkhana ndi kumanga zithando za nkhondo ku Giliyadi. Nawonso Aisraeli anasonkhana ndi kumanga zithando zawo za nkhondo ku Mizipa.
And the sons of Ammon are called together, and encamp in Gilead, and the sons of Israel are gathered together, and encamp in Mizpah.
18 Kenaka anthuwo ndi atsogoleri a Agiliyadi anayamba kufunsana kuti, “Kodi ndi munthu wotani amene atayambe kuthira nkhondo Aamoni? Iyeyu adzakhala mtsogoleri wolamulira anthu onse a ku Giliyadi.”
And the people—heads of Gilead—say to one another, “Who [is] the man that begins to fight against the sons of Ammon? He is for head to all inhabitants of Gilead.”