< Oweruza 1 >
1 Atamwalira Yoswa Aisraeli anafunsa Yehova kuti, “Ndani mwa ife ayambe nkhondo yomenyana ndi Akanaani?”
I stało się po śmierci Jozuego, iż pytali synowie Izraelscy Pana, mówiąc: Któż z nas wprzód pójdzie przeciw Chananejczykowi, aby walczył z nim?
2 Yehova anayankha kuti, “Fuko la Yuda ndilo liyambe kupita. Ndawapatsa dzikolo mʼmanja mwawo.”
I rzekł Pan: Juda pójdzie; otom podał ziemię w rękę jego.
3 Choncho Ayuda anawuza abale awo a fuko la Simeoni kuti, “Bwerani tipitire limodzi mʼdziko limene tapatsidwa kuti tikamenyane ndi Akanaani. Ifenso tidzapita nanu mʼdziko limene anakugawirani.” Ndipo Asimeoni anapita nawo.
I rzekł Juda do Symeona, brata swego: Pójdź ze mną do losu mego, a będziemy walczyli przeciw Chananejczykowi; wszak ja też pójdę z tobą do losu twego. I szedł z nim Symeon.
4 Choncho Ayuda ananyamuka, ndipo Yehova anapereka Akanaani ndi Aperezi mʼmanja mwawo. Ndipo anapha anthu 10,000 ku Bezeki.
Tedy poszedł Juda, i podał Pan Chananejczyka, i Ferezejczyka w ręce ich, a porazili z nich w Bezeku dziesięć tysięcy mężów.
5 Ku Bezekiko anakumana ndi ankhondo a mfumu Adoni-Bezeki ndipo anamenyana nawo, ndipo Ayudawo anagonjetsa Akanaani ndi Aperezi.
Bo naleźli Adonibezeka w Bezeku, i walczyli przeciwko niemu, a porazili Chananejczyka i Ferezejczyka.
6 Adoni-Bezekiyo anathawa, koma anamuthamangira ndi kumupeza, namugwira. Atamugwira anamudula zala zake zazikulu za ku manja ndi miyendo.
I uciekał Adonibezek, którego oni gonili; a pojmawszy go, poucinali palce wielkie u rąk jego, i u nóg jego.
7 Tsono Adoni-Bezeki anati, “Mafumu 70 omwe anadulidwa zala zazikulu za ku manja ndi miyendo yawo ankatola nyenyeswa pansi pa tebulo langa. Mulungu tsopano wandibwezera zomwe ndinawachita.” Kenaka anapita naye ku Yerusalemu ndipo anafera komweko.
Tedy rzekł Adonibezek: Siedmdziesiąt królów z palcami wielkiemi obciętemi u rąk swych i u nóg swych, zbierali odrobiny pod stołem moim; jakom czynił, tak mi oddał Bóg. I przywiedli go do Jeruzalemu, i tamże umarł.
8 Pambuyo pake Ayuda anakathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu ndipo anawulanda. Anapha anthu ambiri ndi kutentha mzinda wonse.
Bo walczyli przedtem synowie Judowi przeciwko Jeruzalemowi i wzięli je, i wysiekli je ostrzem miecza, i miasto spalili ogniem.
9 Kenaka Ayuda anapita kukamenyana ndi Akanaani omwe amakhala ku dziko la ku mapiri, dziko la Negevi kummwera ndiponso mu zigwa.
Potem ciągnęli synowie Juda, aby walczyli przeciw Chananejczykowi mieszkającemu na górach, i na południe, i w polach.
10 Anakalimbananso ndi Akanaani amene ankakhala ku Hebroni (mzinda womwe kale unkatchedwa Kiriyati-Araba). Kumeneko anagonjetsa Sesai, Ahimani ndi Talimai.
Ciągnął tedy Juda przeciwko Chananejczykowi, który mieszkał w Hebronie, (a imię Hebronu było przedtem Karyjatarbe) i poraził Sesai i Ahymana, i Talmaja.
11 Kuchokera kumeneko, iwo anakathira nkhondo anthu amene ankakhala ku Debri (mzindawu poyamba unkatchedwa Kiriati Seferi).
Stamtąd zasię ciągnęli do mieszkających w Dabir, (a imię Dabir było przedtem Karyjatsefer.)
12 Tsono Kalebe anati, “Munthu amene angathire nkhondo mzinda wa Kiriati Seferi ndi kuwulanda, ndidzamupatsa mwana wanga Akisa kuti akhale mkazi wake.”
I rzekł Kaleb: Kto by dobył Karyjatsefer, a wziąłby je, dam mu Achsę, córkę moję, za żonę.
13 Otanieli mwana wa Kenazi, mngʼono wake wa Kalebe, ndiye anawulanda. Choncho Kalebe anamupatsa mwana wake Akisa kuti akhale mkazi wake.
I wziął je Otonijel, syn Keneza, młodszego brata Kalebowego.; a dał mu Achsę, córkę swą, za żonę.
14 Tsiku lina atafika Akisayo, Otanieli anamuwumiriza mkazi wakeyo kuti apemphe munda kwa Kalebe abambo ake. Pamene Akisa anatsika pa bulu wake, Kalebe anamufunsa kuti, “Kodi ukufuna ndikuchitire chiyani?”
I stało się, gdy przyszła do niego, namawiała go, aby prosił ojca jej o pole; i zsiadła z osła, i rzekł do niej Kaleb: Cóż ci?
15 Iye anayankha kuti, “Mundikomere mtima. Popeza mwandipatsa ku Negevi, kumalo kumene kulibe madzi, mundipatsenso akasupe amadzi.” Choncho Kalebe anamupatsa akasupe a kumtunda ndi a kumunsi.
A ona rzekła: Daj mi błogosławieństwo; gdyżeś mi dał ziemię suchą, daj mi też źródła wód. I dał jej Kaleb źródła wyższe i źródła dolne.
16 Tsono zidzukulu za Hobabu, Mkeni uja, mpongozi wa Mose, zinachoka ku Yeriko mzinda wa migwalangwa pamodzi ndi anthu a fuko la Yuda mpaka ku chipululu chimene chili kummwera kwa Aradi ndi kukakhala ndi Aamaleki.
Synowie też Ceni, świekra Mojżeszowego, wyszli z miasta Palm z synami Judowymi na puszczą Judowę, która jest na południe od Arad, i przyszedłszy mieszkali z ludem.
17 Kenaka anthu a fuko la Yuda anapita pamodzi ndi abale awo a fuko la Simeoni ndi kukagonjetsa Akanaani amene amakhala ku Zefati, ndipo mzindawo anawuwononga kwambiri. Choncho mzindawo anawutcha Horima.
Potem ciągnął Juda z Symeonem, bratem swym, a porazili Chananejczyka, mieszkającego w Sefat, a zburzyli je, i nazwali imię miasta onego Horma.
18 Anthu a fuko la Yuda analandanso mzinda wa Gaza ndi dziko lonse lozungulira, mzinda wa Asikeloni pamodzi ndi dziko lake lonse lozungulira, ndi mzinda wa Ekroni pamodzi ndi dziko lonse lozungulira.
Wziął też Juda Gazę z granicami jego, i Akkaron z granicami jego.
19 Yehova anathandiza anthu a fuko la Yuda. Iwo analanda dziko la kumapiri, koma sanathe kuwachotsa anthu ku zigwa, chifukwa anali ndi magaleta azitsulo.
I był Pan z Judą, i posiadł onę górę; ale nie wypędził mieszkających w dolinie, bo mieli wozy żelazne.
20 Monga analonjezera Mose, Kalebe anapatsidwa Hebroni. Kalebe anapirikitsa mafuko atatu a Anaki mu mzindamo.
A tak oddano Kalebowi Hebron, jako był rozkazał Mojżesz, skąd on wygnał trzech synów Enakowych.
21 Koma fuko la Benjamini linalephera kuwachotsa Ayebusi, amene amakhala mu Yerusalemu. Choncho Ayebusiwo akukhalabe ndi fuko la Benjamini mu Yerusalemu mpaka lero.
Ale Jebuzejczyka, mieszkającego w Jeruzalemie, nie wygnali synowie Benjaminowi; przetoż mieszkał Jebuzejczyk z synami Benjaminowymi w Jeruzalemie aż do dnia tego.
22 A banja la Yosefe nawonso anathira nkhondo mzinda wa Beteli, ndipo Yehova anali nawo.
Udał się też dom Józefów do Betel, a Pan był z nimi.
23 Anatumiza anthu kuti akazonde Beteli. Mzindawo kale unkatchedwa Luzi.
I szpiegował dom Józefów Betel; (a imię miasta tego było przedtem Luz.)
24 Anthu okazondawo anaona munthu akutuluka mu mzindamo ndipo anamuwuza kuti, “Tisonyeze njira yolowera mu mzindamu, ndipo ife tidzakuchitira chifundo.”
A ujrzawszy oni szpiegowie człowieka wychodzącego z miasta, rzekli do niego: Ukaż nam prosimy wejście do miasta, a uczynimy z tobą miłosierdzie.
25 Choncho iye anawaonetsa njirayo, ndipo iwo anapha anthu onse mu mzindamo ndi lupanga koma munthu uja pamodzi ndi banja lake sanawaphe.
I ukazał im wejście do miasta; i wysiekli miasto ostrzem miecza, a człowieka onego ze wszystkim domem jego puścili wolno.
26 Ndipo iye anapita ku dziko la Ahiti, kumene anamangako mzinda nawutcha dzina lake Luzi. Mpaka lero lino mzindawo dzina lake ndi lomwelo.
A tak poszedł on człowiek do ziemi Hetejczyków, i zbudował miasto, a nazwał imię jego Luz; to jest imię jego aż do dnia tego.
27 Koma a fuko la Manase sanachotse nzika za mzinda wa Beti-Seani pamodzi ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena nzika za mzinda wa Taanaki ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapenanso nzika za mzinda wa Dori ndi mʼmidzi yake yozungulira. Iwo sanapirikitse nzika za mzinda wa Ibuleamu ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena mzinda wa Megido ndi mʼmidzi yake yozungulira. Choncho Akanaani anapitirirabe kukhala mʼdzikomo.
Nie wypędził też Manases obywateli z Betsean i z miasteczek jego, ani z Tanach i z miasteczek jego, ani obywateli z Dor i z miasteczek jego, ani obywateli z Jeblam i z miasteczek jego, ani obywateli z Megiddo i z miasteczek jego; i począł Chananejczyk mieszkać w onej ziemi.
28 Aisraeli atakhala amphamvu, anawagwiritsa Akanaaniwo ntchito yakalavulagaga, koma sanawapirikitse.
A gdy się zmocnił Izrael, uczynił Chananejczyka hołdownikiem, a nie wygnał go.
29 Nawonso Aefereimu sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Gezeri, choncho Akanaaniwo ankakhalabe pakati pawo ku Gezeriko.
Także i Efraim nie wypędził Chananejczyka mieszkającego w Gazer; przetoż mieszkał Chananejczyk między nimi w Gazer.
30 Azebuloni sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Kitironi kapena a ku Nahaloli. Iwo ankakhala pakati pawo ndipo ankawagwiritsa ntchito yakalavulagaga.
Zabulon też nie wypędził mieszkających w Cetron, i mieszkających w Nahalol; przetoż mieszkał Chananejczyk między nimi, będąc hołdownikiem ich.
31 A fuko la Aseri nawo sanathamangitse amene amakhala mu Ako, Sidoni, Ahilabu, Akizibu, Heliba, Afiki, ndi Rehobu.
Aser też nie wypędził mieszkających w Acho, i mieszkających w Sydonie, i w Ahalab, i w Achsyb, i w Helba, i w Afek, i w Rohob.
32 Choncho anthu a fuko la Aseri anakhala pakati pa Akanaani amene ankakhala mʼdzikomo popeza sanawapirikitse.
I mieszkał Aser w pośrodku Chananejczyka, mieszkającego w onej ziemi; bo go nie wypędził.
33 Nalonso fuko la Nafutali silinathamangitse anthu amene ankakhala ku Beti Semesi kapena ku Beti Anati. Koma Anafutaliwo ankakhala pakati pa Akanaaniwo mʼdzikomo. Koma anthu amene ankakhala ku Beti Semesi ndi ku Beti Anati anawasandutsa kukhala ogwira ntchito yathangata.
Neftalim też nie wypędził obywateli z Betsemes, ani obywateli z Betanat, i mieszkał między Chananejczykami mieszkającymi w onej ziemi; jednak obywatele Betsemes i Betanat byli hołdownikami ich.
34 Aamori anapirikitsira anthu a fuko la Dani ku dziko la ku mapiri popeza sanawalole kuti atsikire ku chigwa.
I ścisnęli Amorejczycy syny Danowe na górach, tak iż im nie dopuścili schodzić na dolinę.
35 Aamori anatsimikiza mtima zokhalabe ku phiri la Hara-Heresi, ku Ayaloni, ndiponso ku Saalibimu. Koma a fuko la Yosefe anakula mphamvu ndipo anagwiritsa Aamoriwo ntchito yakalavulagaga.
I począł mieszkać Amorejczyk na górze Hares, w Ajalon i w Salebim; i wzmocniła się ręka domu Józefowego, i byli hołdownikami ich.
36 Malire a Aamori anayambira ku chikweza cha Akirabimu nʼkulowera ku Sela napitirira kumapita chakumapiri ndithu.
A była granica Amorejczykowa od góry, gdzie wstępują do niedźwiadków, od skały ich i wyżej.