< Oweruza 1 >
1 Atamwalira Yoswa Aisraeli anafunsa Yehova kuti, “Ndani mwa ife ayambe nkhondo yomenyana ndi Akanaani?”
MAHOPE iho o ka make ana o Iosua, ninau aku la ka poe mamo a Iseraela ia Iehova, i aku la, Owai ko makou mea e pii mua aku i ke alo o ko Kanaana, e kaua aku ia lakou?
2 Yehova anayankha kuti, “Fuko la Yuda ndilo liyambe kupita. Ndawapatsa dzikolo mʼmanja mwawo.”
I mai la o Iehova, E pii ae ka Iuda; aia hoi, ua haawi au i ka aina i kona lima.
3 Choncho Ayuda anawuza abale awo a fuko la Simeoni kuti, “Bwerani tipitire limodzi mʼdziko limene tapatsidwa kuti tikamenyane ndi Akanaani. Ifenso tidzapita nanu mʼdziko limene anakugawirani.” Ndipo Asimeoni anapita nawo.
I ae la ka Iuda i ka Simeona, i kona kaikuaana, E hele pu oe me au, ma ko'u hele ana, i kaua aku kakou i ko Kanaana, a e hele pu no hoi au me oe, ma kou hele ana. A hele pu aku la ka Simeona me ia.
4 Choncho Ayuda ananyamuka, ndipo Yehova anapereka Akanaani ndi Aperezi mʼmanja mwawo. Ndipo anapha anthu 10,000 ku Bezeki.
Pii aku la ka Iuda, a haawi mai la o Iehova i ko Kanaana, a me ka Pereza, i ko lakou lima. A luku aku la lakou i kela poe ma Bezeka, he umi tausani kanaka.
5 Ku Bezekiko anakumana ndi ankhondo a mfumu Adoni-Bezeki ndipo anamenyana nawo, ndipo Ayudawo anagonjetsa Akanaani ndi Aperezi.
A ma Bezeka, loaa ia lakou o Adonibezeka; a kaua aku la lakou ia ia, a luku aku la lakou i ko Kanaana, a me ka Pereza.
6 Adoni-Bezekiyo anathawa, koma anamuthamangira ndi kumupeza, namugwira. Atamugwira anamudula zala zake zazikulu za ku manja ndi miyendo.
Holo aku la o Adonibezeka, a hahai aku la lakou ia ia, a loaa oia, alaila ooki ae la lakou i na manamana nui o kona mau lima, a me na manamana nui o kona mau wawae.
7 Tsono Adoni-Bezeki anati, “Mafumu 70 omwe anadulidwa zala zazikulu za ku manja ndi miyendo yawo ankatola nyenyeswa pansi pa tebulo langa. Mulungu tsopano wandibwezera zomwe ndinawachita.” Kenaka anapita naye ku Yerusalemu ndipo anafera komweko.
I ae la o Adonibezeka, He kanahiku alii, ua okiia na manamana nui o ko lakou lima, a me ko lakou wawae, hoiliili lakou malalo iho o ko'u papaaina. E like me ka'u i hana aku ai, pela i hoopai mai ai ke Akua ia'u. Lawe ae la lakou ia ia i Ierusalema, a malaila ia i make ai
8 Pambuyo pake Ayuda anakathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu ndipo anawulanda. Anapha anthu ambiri ndi kutentha mzinda wonse.
Ua kaua aku ka poe mamo a Iuda, a ua hoopio, a ua luku aku ia Ierusalema, i ka maka o ka pahikaua, a ua puhi aku ia kulanakauhale i ke ahi.
9 Kenaka Ayuda anapita kukamenyana ndi Akanaani omwe amakhala ku dziko la ku mapiri, dziko la Negevi kummwera ndiponso mu zigwa.
A mahope iho hele ae la na mamo a Iuda e kaua aku i ko Kanaana, i ka poe i noho ma ka mauna, a ma ka aoao hema, a ma ka papu.
10 Anakalimbananso ndi Akanaani amene ankakhala ku Hebroni (mzinda womwe kale unkatchedwa Kiriyati-Araba). Kumeneko anagonjetsa Sesai, Ahimani ndi Talimai.
Hele ka e aku la ka Iuda i ko Kanaana, i ka poe i noho ma Heberona; o Kiriatareba ka inoa kahiko o Heberona; a pepehi aku la lakou ia Sesai, a me Ahimana, a me Talemai.
11 Kuchokera kumeneko, iwo anakathira nkhondo anthu amene ankakhala ku Debri (mzindawu poyamba unkatchedwa Kiriati Seferi).
A malaila aku lakou i hele ai e ku e ia Debira; o Kiriatesepera ka inoa kahiko o Debira.
12 Tsono Kalebe anati, “Munthu amene angathire nkhondo mzinda wa Kiriati Seferi ndi kuwulanda, ndidzamupatsa mwana wanga Akisa kuti akhale mkazi wake.”
I iho la o Kaleba, O ka mea nana e pepehi ia Kiriatesepera, a e hoopio iho, e haawi aku au ia Akesa, i ka'u kaikamahine, i wahine nana.
13 Otanieli mwana wa Kenazi, mngʼono wake wa Kalebe, ndiye anawulanda. Choncho Kalebe anamupatsa mwana wake Akisa kuti akhale mkazi wake.
Na Oteniela, ke keiki a Kenaza, ke kaikaina o Kaleba i hoopio aku ia wahi; a haawi iho la oia ia Akesa, i kana kaikamahine, i wahine nana.
14 Tsiku lina atafika Akisayo, Otanieli anamuwumiriza mkazi wakeyo kuti apemphe munda kwa Kalebe abambo ake. Pamene Akisa anatsika pa bulu wake, Kalebe anamufunsa kuti, “Kodi ukufuna ndikuchitire chiyani?”
Eia hoi kekahi, a hiki mai ka wahine io na la, koi ae la oia ia ia e noi aku i kona makuakane i aina. A iho iho la ia mai luna mai o ka hoki. Ninau ae la o Kaleba i ke kaikamahine, Heaha kau?
15 Iye anayankha kuti, “Mundikomere mtima. Popeza mwandipatsa ku Negevi, kumalo kumene kulibe madzi, mundipatsenso akasupe amadzi.” Choncho Kalebe anamupatsa akasupe a kumtunda ndi a kumunsi.
I mai la kela, E haawi mai oe ia'u i mea e pomaikai ai. No ka mea, ua haawi mai oe ia'u i aina ma ke kukuluhema; e haawi mai no hoi oe i na kumuwai. A haawi mai la o Kaleba i na kumuwai luna a me na kumuwai lalo.
16 Tsono zidzukulu za Hobabu, Mkeni uja, mpongozi wa Mose, zinachoka ku Yeriko mzinda wa migwalangwa pamodzi ndi anthu a fuko la Yuda mpaka ku chipululu chimene chili kummwera kwa Aradi ndi kukakhala ndi Aamaleki.
Pii aku la na mamo a ka mea no Keni, a ka makuahonowai kane o Mose, mai ke kulanakauhale o na laau pama aku, me na mamo a Iuda, a i ka waonahele o ka Iuda, aia no ia ma ka aoao hema o Arada; a hele ae la lakou a noho pu iho la me kanaka.
17 Kenaka anthu a fuko la Yuda anapita pamodzi ndi abale awo a fuko la Simeoni ndi kukagonjetsa Akanaani amene amakhala ku Zefati, ndipo mzindawo anawuwononga kwambiri. Choncho mzindawo anawutcha Horima.
Hele pu aku la ka Iuda, me ka Simeona, kona kaikuaana, a luku aku la lakou i ko Kanaana, ka poe i noho ma Zepata, a hooki loa iho la ia wahi. Ua kapaia ka inoa o ia kulanakauhale, o Horema.
18 Anthu a fuko la Yuda analandanso mzinda wa Gaza ndi dziko lonse lozungulira, mzinda wa Asikeloni pamodzi ndi dziko lake lonse lozungulira, ndi mzinda wa Ekroni pamodzi ndi dziko lonse lozungulira.
Hoopio iho la ka Iuda ia Gaza a me ko laila mau mokuna, a ia Asekelona kekahi me ko laila mau mokuna, a ia Ekerona hoi me ko laila mau mokuna.
19 Yehova anathandiza anthu a fuko la Yuda. Iwo analanda dziko la kumapiri, koma sanathe kuwachotsa anthu ku zigwa, chifukwa anali ndi magaleta azitsulo.
O Iehova pu no kekahi me ka Iuda, a loaa ia lakou ka mauna; aole hiki ia lakou ke kipaku aku i ka poe i noho ma na aina haahaa, no ka mea, he hao ko lakou kaakaua.
20 Monga analonjezera Mose, Kalebe anapatsidwa Hebroni. Kalebe anapirikitsa mafuko atatu a Anaki mu mzindamo.
A haawi ae la lakou ia Heberona no Kaleba, e like me ka Mose i olelo mai ai. A kipaku aku la ia, malaila aku, i na keiki ekolu a Anaka.
21 Koma fuko la Benjamini linalephera kuwachotsa Ayebusi, amene amakhala mu Yerusalemu. Choncho Ayebusiwo akukhalabe ndi fuko la Benjamini mu Yerusalemu mpaka lero.
Aole i kipaku na mamo a Beniamina i ka Iebusi, i noho ma Ierusalema; aka, noho pu no ka Iebusi me na mamo a Beniamina ma Ierusalema, a hiki loa mai i keia la.
22 A banja la Yosefe nawonso anathira nkhondo mzinda wa Beteli, ndipo Yehova anali nawo.
O ka ohana a Iosepa kekahi i pii, e kaua aku ia Betela; a o Iehova pu no me lakou.
23 Anatumiza anthu kuti akazonde Beteli. Mzindawo kale unkatchedwa Luzi.
Kiu aku ka ohana a Iosepa ia Betela. o Luza ka inoa kahiko o ia kulanakauhale.
24 Anthu okazondawo anaona munthu akutuluka mu mzindamo ndipo anamuwuza kuti, “Tisonyeze njira yolowera mu mzindamu, ndipo ife tidzakuchitira chifundo.”
Ike aku la na kiu i kekahi kanaka, mai ke kulanakauhale ia i hele mai ai. I aku la lakou ia ia, E kuhikuhi mai oe ia makou, i kahi e komo aku ai iloko o ke kulanakauhale, a e hana lokomaikai aku makou ia oe.
25 Choncho iye anawaonetsa njirayo, ndipo iwo anapha anthu onse mu mzindamo ndi lupanga koma munthu uja pamodzi ndi banja lake sanawaphe.
Kuhikuhi mai la oia ia lakou i kahi o komo aku ai iloko o ke kulanakauhale, a luku aku la lakou ia kulanakauhale i ka maka o ka pahi kaua; a kuu aku la lakou i ua kanaka la, a me kona poe a pau.
26 Ndipo iye anapita ku dziko la Ahiti, kumene anamangako mzinda nawutcha dzina lake Luzi. Mpaka lero lino mzindawo dzina lake ndi lomwelo.
A hele aku la ua kanaka nei i ka aina o ka Heta, a kukulu iho la i kulanakauhale, a kapa aku la i ka inoa, o Luza, oia hoi kona inoa a hiki mai i neia la.
27 Koma a fuko la Manase sanachotse nzika za mzinda wa Beti-Seani pamodzi ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena nzika za mzinda wa Taanaki ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapenanso nzika za mzinda wa Dori ndi mʼmidzi yake yozungulira. Iwo sanapirikitse nzika za mzinda wa Ibuleamu ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena mzinda wa Megido ndi mʼmidzi yake yozungulira. Choncho Akanaani anapitirirabe kukhala mʼdzikomo.
Aole i kipaku ka Manase i ko Beteseana, a me ko laila mau wahi; aole hoi i ko Taanaka, a me ko laila mau wahi, aole i ka poe i noho ma Dora, a me ko laila mau wahi; aole i ka poe i noho ma Ibeleama, a me ko laila mau wahi, aole i ka poe i noho ma Megido, a me ko laila mau wahi; aka, hoopaa no ko Kanaana i ko lakou noho ana ma ia aina.
28 Aisraeli atakhala amphamvu, anawagwiritsa Akanaaniwo ntchito yakalavulagaga, koma sanawapirikitse.
A hiki i ka manawa i ikaika ai ka Iseraela, auhau aku la lakou i ko Kanaana, aole i kipaku loa ia lakou.
29 Nawonso Aefereimu sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Gezeri, choncho Akanaaniwo ankakhalabe pakati pawo ku Gezeriko.
Aole hoi i kipaku ka Eperaima i ko Kanaana i noho ma Gezera. Noho pu no ko Kanaana me lakou ma Gezera.
30 Azebuloni sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Kitironi kapena a ku Nahaloli. Iwo ankakhala pakati pawo ndipo ankawagwiritsa ntchito yakalavulagaga.
Aole hoi i kipaku aku ka Zebuluna i ka poe i noho ma Kiterona, aole i ka poe i noho ma Nahalola. Noho pu no ko Kanaana mo lakou, a lilo lakou i poe i hookupu mai.
31 A fuko la Aseri nawo sanathamangitse amene amakhala mu Ako, Sidoni, Ahilabu, Akizibu, Heliba, Afiki, ndi Rehobu.
Aole hoi i kipaku aku o Asera i ka poe i noho ma Ako, aole i ka poe i noho ma Zidona, aole i ko Ahelaba, aole i ko Akeziba, aole i ko Helaba, aole i ko Apika, aole i ko Rehoba.
32 Choncho anthu a fuko la Aseri anakhala pakati pa Akanaani amene ankakhala mʼdzikomo popeza sanawapirikitse.
Noho pu no ka Asera me ko Kanaana, na kanaka o ka aina, no ka mea, aole lakou i kipaku aku ia poe.
33 Nalonso fuko la Nafutali silinathamangitse anthu amene ankakhala ku Beti Semesi kapena ku Beti Anati. Koma Anafutaliwo ankakhala pakati pa Akanaaniwo mʼdzikomo. Koma anthu amene ankakhala ku Beti Semesi ndi ku Beti Anati anawasandutsa kukhala ogwira ntchito yathangata.
Aole hoi i kipaku aku ka Napetali i ka poe i noho ma Betesemesa, aole hoi i ka poe i noho ma Beteanata; noho pu no lakou me ko Kanaana, na kanaka o ka aina; aka, lilo na kanaka o Betesemesa, a me Beteanata, i poe hookupu mai na lakou.
34 Aamori anapirikitsira anthu a fuko la Dani ku dziko la ku mapiri popeza sanawalole kuti atsikire ku chigwa.
Hooke aku la ka Amora i na mamo a Dana, a hiki iluna o ka puu. Aole lakou i ae aku ke iho mai ia poe i na aina papu.
35 Aamori anatsimikiza mtima zokhalabe ku phiri la Hara-Heresi, ku Ayaloni, ndiponso ku Saalibimu. Koma a fuko la Yosefe anakula mphamvu ndipo anagwiritsa Aamoriwo ntchito yakalavulagaga.
Hoopaa no ka Amora i ko lakou noho ana ma ka mauna o Heresa, a ma Aialona, a ma Saalebima: aka, ua kaumaha aku no ka lima o ko Iosepa poe, a lilo kela i poe hookupu mai.
36 Malire a Aamori anayambira ku chikweza cha Akirabimu nʼkulowera ku Sela napitirira kumapita chakumapiri ndithu.
O na mokuna o ka Amora, mai ka puu o Akerabima aku ia, a mai I Sela aku no.