< Yuda 1 >

1 Ndine Yuda, mtumiki wa Yesu Khristu, komanso mʼbale wake wa Yakobo. Kwa inu amene Mulungu Atate anakuyitanani, amene amakukondani ndikukusungani mwa Yesu Khristu.
Surat ini ditulis oleh Yudas, pelayan dari Yesus Kristus, dan saudara Yakobus. Saya menuliskan ini untuk mereka yang dipanggil dan dikasihi oleh Allah Bapa, dan dilindungi oleh Yesus Kristus:
2 Chifundo, mtendere ndi chikondi zikhale nanu mochuluka.
Kiranya belas kasihan, damai, dan kasih Allah semakin bertambah dalam perjalanan hidupmu!
3 Okondedwa, ngakhale ndinkafunitsitsa kukulemberani za chipulumutso cha tonsefe, ndakakamizidwa kuti ndikulembereni ndi kukupemphani kolimba kuti mumenye ndithu nkhondo yotchinjiriza chikhulupiriro chimene Mulungu anachipereka kamodzi kokha kwa anthu onse oyera mtima.
Teman-teman, saya sudah menanti-nantikan untuk menuliskan tentang berita keselamatan yang kita bagikan. Tetapi saat ini saya perlu segera menulis kepada kalian dan menguatkan kalian untuk membela kebenaran tentang Allah dengan penuh semangat, yang diberikan sekali dan untuk selamanya kepada umat Allah yang kudus.
4 Pakuti anthu ena amene za chilango chawo zinalembedwa kale, alowa mobisika pakati panu. Amenewa ndi anthu osapembedza Mulungu, amene amapotoza chisomo cha Mulungu wathu kuchisandutsa ufulu ochitira zonyansa ndiponso amakana Yesu Khristu amene Iye ndiye Mbuye ndi Mfumu yathu.
Bagi sebagian orang telah diam-diam menyusup di antara kalian Mereka ditulis dan dikutuk sejak lama, karena mereka adalah orang-orang jahat yang memutarbalikkan kasih karunia Allah, mengubahnya menjadi izin untuk amoralitas, sementara juga menyangkal Tuhan dan tuan kita Yesus Kristus.
5 Ngakhale munazidziwa kale zonsezi, ndafuna kuti ndikukumbutseni kuti Ambuye anapulumutsa anthu ake ndi kuwatulutsa mʼdziko la Igupto, koma pambuyo pake anawononga amene sanakhulupirire.
Sekalipun kalian sudah tahu akan hal ini, saya ingin mengingatkan kalian bahwa sekalipun Tuhan menyelamatkan umat-Nya keluar dari negeri Mesir, dia masih membinasakan mereka yang tidak percaya kepada-Nya.
6 Ndipo mukumbukire angelo amene sanakhutire ndi maudindo awo, koma anasiya malo awo. Angelo amenewa Mulungu anawamanga ndi maunyolo osatha, ndipo akuwasunga mʼmalo a mdima mpaka tsiku lalikulu lachiweruzo. (aïdios g126)
Bahkan para malaikat yang tidak puas dengan posisi yang Allah berikan kepada mereka dan meninggalkan posisi mereka yang benar — ditempatkannya mereka di dalam kegelapan dengan rantai kekekalan sampai pada hari Penghakiman Besar. (aïdios g126)
7 Musayiwale mizinda ya Sodomu ndi Gomora ija, ndi mizinda yoyandikana nayo. Anthu mʼmenemo anadziperekanso kuchita zadama ndi kuchita zonyansa zachilendo. Mizinda imeneyi yakhala ngati chitsanzo cha amene adzalangidwa ndi moto wosatha. (aiōnios g166)
Dengan cara yang sama, Sodom dan Gomora dan kota-kota di sekitarnya yang mengejar amoralitas dan seks sesat diberikan sebagai contoh dari mereka yang mengalami hukuman api abadi. (aiōnios g166)
8 Nʼchimodzimodzinso zimene akuchita anthu amenewa potsata maloto awo, amadetsa matupi awo, amakana ulamuliro wa Mulungu ndiponso amachitira chipongwe angelo akumwamba.
Dengan cara yang sama, para pemimpi ini mengotori tubuh jasmani mereka, meremehkan otoritas, dan menghina mahkluk-mahkluk surgawi.
9 Koma ngakhale mkulu wa angelo Mikayeli, pamene ankalimbana ndi Mdierekezi za mtembo wa Mose, sanamunene kuti wachipongwe, koma anati, “Ambuye akudzudzule iwe!”
Bahkan Mikael, pemimpin tertinggi malaikat, ketika dia berdebat dengan Iblis mengenai mayat Musa, tidak berani mendakwa Iblis dengan hinaan seperti itu, hanya berkata, “Semoga Tuhan menghardik kamu.”
10 Koma anthu awa amachita chipongwe zinthu zimene sakuzidziwa. Ndipo zinthu zimene amazidziwa ndi nzeru zachibadwa, monga za nyama, ndizo zimene zimawawononga.
Tetapi orang-orang ini mengejek apa pun yang tidak mereka pahami; dan apa yang mereka pahami secara naluriah mereka ikuti seperti binatang yang tidak berpikir — inilah yang menghancurkan mereka.
11 Tsoka kwa iwo chifukwa anatsatira njira ya Kaini. Iwo athamangira phindu, nʼchifukwa chake anagwa mʼtchimo la Baalamu. Iwo anawonongedwa chifukwa chowukira monga anachitira Kora.
Mereka dalam kesulitan besar! Karena mereka sudah mengikuti cara Kain. Seperti Bileam dan khayalannya, mereka tersesat karena gila uang. Seperti Korah dan pemberontakannya, mereka menghancurkan diri mereka sendiri.
12 Anthu amenewa ndiwo amayipitsa maphwando anu achikondi. Amadya nanu mopanda manyazi ndipo ali ngati abusa amene amangodzidyetsa okha. Anthuwa ali ngati mitambo yowuluzika ndi mphepo, yopanda mvula. Ali ngati mitengo ya nthawi ya masika, yopanda zipatso, yozuka mizu, mitengo yoferatu.
Orang-orang ini merusak makanan persekutuan kalian, karena mereka seperti para gembala yang egois yang tidak memiliki rasa malu sedikit pun — mereka hanya menjaga diri sendiri. Mereka seperti awan yang tertiup angin tetapi tidak membawa hujan. Mereka seperti pohon gundul tanpa buah — mati dua kali, dicabut dari akarnya.
13 Iwowa ali ngati mafunde awukali apanyanja, amene amatulutsa thovu la zonyansa zawo. Amenewa ali ngati nyenyezi zosochera, ndipo Mulungu akuwasungira mdima wandiweyani mpaka muyaya. (aiōn g165)
Mereka seperti gelombang laut yang ganas, berbuih dalam aib mereka sendiri. Mereka seperti bintang-bintang palsu, dikutuk selamanya ke dalam kegelapan total. (aiōn g165)
14 Enoki, wachisanu ndi chiwiri kuyambira pa Adamu, ananeneratu za anthu amenewa kuti, “Onani, Ambuye akubwera ndi oyera ake osawerengeka
Henokh, tujuh generasi sesudah Adam, sudah bernubuat tentang orang-orang ini: “Lihat! Tuhan akan datang, bersama dengan jutaan orang suci-Nya
15 kuti adzaweruze aliyense, ndi kudzagamula kuti onse osapembedza ndi olakwa, chifukwa cha ntchito zawo zosalungama zimene anachita mʼmoyo wawo osaopa Mulungu. Adzawatsutsa chifukwa cha mawu onse achipongwe amene osapembedzawa ananyoza nawo Ambuye.”
untuk menghakimi semua orang, untuk mengungkapkan semua perbuatan jahat yang sudah dilakukan orang-orang, dan semua hal mengerikan yang dikatakan orang-orang berdosa yang bermusuhan terhadap-Nya.”
16 Anthu amenewa amangʼungʼudza ndi kudandaula. Amatsatira zilakolako zawo zoyipa. Amayankhula zodzitamandira ndipo amanamiza ena pofuna kupeza phindu.
Orang seperti itu penggerutu, selalu mengeluh. Mereka mengikuti keinginan jahat mereka sendiri, berbicara dengan sombong tentang diri mereka sendiri, dan menyanjung orang lain untuk mendapatkan apa yang mereka inginkan.
17 Koma okondedwa, kumbukirani zimene atumwi a Ambuye athu Yesu Khristu ananeneratu.
Tetapi kalian, teman-teman terkasih, mohon ingat apa yang para rasul Tuhan kita Yesus Kristus katakan kepada kalian.
18 Iwo anakuwuzani kuti, “Mʼmasiku otsiriza kudzafika anthu onyoza, otsatira zofuna zawo zoyipa.”
Mereka menjelaskan kepadamu bahwa pada saat-saat terakhir para pengejek akan datang, mengikuti keinginan jahat mereka sendiri.
19 Anthu amenewa ndi amene akubweretsa mipatuko pakati panu, amatsatira nzeru zachibadwa ndipo alibe Mzimu Woyera.
Mereka menyebabkan perpecahan; mereka adalah orang-orang duniawi yang tidak memiliki Roh.
20 Koma inu okondedwa, muthandizane kuti mukule pa chikhulupiriro chanu choyera, ndipo muzipemphera ndi mphamvu ya Mzimu Woyera.
Tetapi kalian, teman-teman saya, haruslah membangun diri kalian sendiri melalui keyakinan kalian kepada Allah. Berdoa dalam Roh Kudus,
21 Khalani mʼchikondi cha Mulungu pamene mukudikira chifundo cha Ambuye athu Yesu Khristu kuti akubweretsereni moyo wosatha. (aiōnios g166)
jaga dirimu aman dalam kasih Tuhan, dan nantikan pengampunan Allah kita Yesus Kristus yang membawa kita kepada hidup yang untuk selama-lamanya. (aiōnios g166)
22 Muwachitire chifundo amene akukayika.
Tunjukkan kebaikan hati kepada orang yang ragu.
23 Ena muwapulumutse powalanditsa ku moto. Enanso muwachitire chifundo, koma mwa mantha, ndipo muzidana ngakhale ndi mwinjiro yomwe yayipitsidwa ndi machimo.
Selamatkan mereka yang bisa kalian selamatkan dengan mengeluarkan mereka dari api. Tunjukkan pengampunan — tetapi dengan sangat hati-hati, bahkan membenci “tampilan luar” yang terkontaminasi oleh sifat manusia yang berdosa.
24 Kwa Iye amene angathe kukusungani kuti mungagwe mʼmachimo, ndiponso amene angathenso kukufikitsani pamaso pake pa ulemerero wopanda cholakwa muli okondwa,
Sekarang bagi Dia yang dapat mencegah kita agar tidak jatuh dalam dosa, dan yang dapat membawa kita ke dalam kehadiran-Nya yang mulia tanpa dosa, dan dengan sukacita yang besar,
25 kwa Mulungu yekhayo, Mpulumutsi wathu, kwa Iye kukhale ulemerero, ukulu, mphamvu ndi ulamuliro, mwa Yesu Khristu Ambuye athu, kuyambira isanayambe nthawi, tsopano mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)
kepada satu-satunya Allah Juruselamat kita, melalui Yesus Kristus Tuhan kita, biarlah kemuliaan, keagungan, kuasa, dan otoritas, dahulu, sekarang, dan selamanya. Amin. (aiōn g165)

< Yuda 1 >