< Yuda 1 >
1 Ndine Yuda, mtumiki wa Yesu Khristu, komanso mʼbale wake wa Yakobo. Kwa inu amene Mulungu Atate anakuyitanani, amene amakukondani ndikukusungani mwa Yesu Khristu.
Juda, služebník Ježíše Krista, bratr Jakubův, píše těm, které Bůh povolal, miluje a pro Ježíše Krista chrání.
2 Chifundo, mtendere ndi chikondi zikhale nanu mochuluka.
Přeji vám, abyste zakoušeli stále více milosti, pokoje a lásky!
3 Okondedwa, ngakhale ndinkafunitsitsa kukulemberani za chipulumutso cha tonsefe, ndakakamizidwa kuti ndikulembereni ndi kukupemphani kolimba kuti mumenye ndithu nkhondo yotchinjiriza chikhulupiriro chimene Mulungu anachipereka kamodzi kokha kwa anthu onse oyera mtima.
Moji drazí, tolik jsem si přál napsat vám o našem společném spasení, ale cítím, že je potřebnější, abych vás povzbudil v zápase o víru, která byla jednou provždy darována Božímu lidu.
4 Pakuti anthu ena amene za chilango chawo zinalembedwa kale, alowa mobisika pakati panu. Amenewa ndi anthu osapembedza Mulungu, amene amapotoza chisomo cha Mulungu wathu kuchisandutsa ufulu ochitira zonyansa ndiponso amakana Yesu Khristu amene Iye ndiye Mbuye ndi Mfumu yathu.
Mezi vás se totiž vloudili lidé, kteří nemají žádnou úctu před Bohem a jeho milost využívají jako příležitost k nevázanému životu. O takových lidech bylo už dávno psáno, že jsou odsouzeni, protože se obrátili proti našemu jedinému Vládci a Pánu – Ježíši Kristu.
5 Ngakhale munazidziwa kale zonsezi, ndafuna kuti ndikukumbutseni kuti Ambuye anapulumutsa anthu ake ndi kuwatulutsa mʼdziko la Igupto, koma pambuyo pake anawononga amene sanakhulupirire.
Připomínám vám to, co už znáte: ačkoliv Bůh zachránil Izraelce vyvedením z Egypta, přece potom zahubil ty z nich, kteří mu nedůvěřovali a neposlouchali ho.
6 Ndipo mukumbukire angelo amene sanakhutire ndi maudindo awo, koma anasiya malo awo. Angelo amenewa Mulungu anawamanga ndi maunyolo osatha, ndipo akuwasunga mʼmalo a mdima mpaka tsiku lalikulu lachiweruzo. (aïdios )
Také anděly, kteří zklamali ve svém vysokém postavení, Bůh navždy vyhostil ze své blízkosti a střeží je pro den soudu. (aïdios )
7 Musayiwale mizinda ya Sodomu ndi Gomora ija, ndi mizinda yoyandikana nayo. Anthu mʼmenemo anadziperekanso kuchita zadama ndi kuchita zonyansa zachilendo. Mizinda imeneyi yakhala ngati chitsanzo cha amene adzalangidwa ndi moto wosatha. (aiōnios )
Podobně obyvatelé Sodomy a Gomory i okolních měst, kteří šli cestou nemravnosti a sexuální zvrácenosti, jsou stále výstražným příkladem hrozného konce ve věčném ohni. (aiōnios )
8 Nʼchimodzimodzinso zimene akuchita anthu amenewa potsata maloto awo, amadetsa matupi awo, amakana ulamuliro wa Mulungu ndiponso amachitira chipongwe angelo akumwamba.
Přesto se tito falešní křesťané chovají podobně. Zapadli hluboko do hříchu, zneužívají svá těla, pohrdají jakoukoliv autoritou a rouhají se nadpozemským mocnostem.
9 Koma ngakhale mkulu wa angelo Mikayeli, pamene ankalimbana ndi Mdierekezi za mtembo wa Mose, sanamunene kuti wachipongwe, koma anati, “Ambuye akudzudzule iwe!”
A přece ani sám archanděl Michael se neodvážil odsoudit satana. Když se s ním přel o Mojžíšovo tělo, řekl pouze: „Pán tě potrestej!“
10 Koma anthu awa amachita chipongwe zinthu zimene sakuzidziwa. Ndipo zinthu zimene amazidziwa ndi nzeru zachibadwa, monga za nyama, ndizo zimene zimawawononga.
Tito zbloudilci si však klidně tropí žerty z toho, co nechápou. Co svými pudy jako nerozumná zvířata znají, tomu propadají, a to je vede ke zkáze.
11 Tsoka kwa iwo chifukwa anatsatira njira ya Kaini. Iwo athamangira phindu, nʼchifukwa chake anagwa mʼtchimo la Baalamu. Iwo anawonongedwa chifukwa chowukira monga anachitira Kora.
Běda jim! Dali se cestou Kainovou, který nedbal na Boží příkazy a stal se nakonec vrahem svého bratra. Stejně jako Bileám jsou schopni zradit Boží pravdu pro peníze. Odsoudili se k záhubě vzpourou proti Bohu, podobně jako Kórach, který toužil dosáhnout vysokého postavení.
12 Anthu amenewa ndiwo amayipitsa maphwando anu achikondi. Amadya nanu mopanda manyazi ndipo ali ngati abusa amene amangodzidyetsa okha. Anthuwa ali ngati mitambo yowuluzika ndi mphepo, yopanda mvula. Ali ngati mitengo ya nthawi ya masika, yopanda zipatso, yozuka mizu, mitengo yoferatu.
Při vašem bratrském stolování se tito lidé beze studu přecpávají, protože myslí jen na sebe, a tak se stávají poskvrnou vašeho společenství. Jsou jako mraky bez deště hnané větrem sem a tam, jako neplodné stromy na podzim, mrtvé a vykořeněné.
13 Iwowa ali ngati mafunde awukali apanyanja, amene amatulutsa thovu la zonyansa zawo. Amenewa ali ngati nyenyezi zosochera, ndipo Mulungu akuwasungira mdima wandiweyani mpaka muyaya. (aiōn )
Jsou jako divoké mořské vlny vyplavující vlastní špínu, jako zbloudilé hvězdy, které se ztratily v temnotě vesmíru. (aiōn )
14 Enoki, wachisanu ndi chiwiri kuyambira pa Adamu, ananeneratu za anthu amenewa kuti, “Onani, Ambuye akubwera ndi oyera ake osawerengeka
O takových lidech prorokoval Henoch, příslušník šesté generace od Adama: „Pán přijde s mnoha tisíci anděly,
15 kuti adzaweruze aliyense, ndi kudzagamula kuti onse osapembedza ndi olakwa, chifukwa cha ntchito zawo zosalungama zimene anachita mʼmoyo wawo osaopa Mulungu. Adzawatsutsa chifukwa cha mawu onse achipongwe amene osapembedzawa ananyoza nawo Ambuye.”
aby všechny soudil a bezbožné hříšníky trestal za jejich nevěru, špatné jednání a tvrdá slova proti Bohu.“Těmto lidem není nic vhod a dělají všechno zlé, co se jim zachce.
16 Anthu amenewa amangʼungʼudza ndi kudandaula. Amatsatira zilakolako zawo zoyipa. Amayankhula zodzitamandira ndipo amanamiza ena pofuna kupeza phindu.
Mluví nadutě a lichotí lidem, přináší-li jim to prospěch.
17 Koma okondedwa, kumbukirani zimene atumwi a Ambuye athu Yesu Khristu ananeneratu.
Ale vy, moji milovaní, pamatujte na slova Ježíšových apoštolů,
18 Iwo anakuwuzani kuti, “Mʼmasiku otsiriza kudzafika anthu onyoza, otsatira zofuna zawo zoyipa.”
kteří nám předpověděli, že se v posledním čase objeví lidé zlehčující Boží pravdu. Jejich jediným cílem je „užívat života“, jak se dá.
19 Anthu amenewa ndi amene akubweretsa mipatuko pakati panu, amatsatira nzeru zachibadwa ndipo alibe Mzimu Woyera.
Působí roztržky. Jsou to lidé ovládaní svými pudy, a ne Božím Duchem.
20 Koma inu okondedwa, muthandizane kuti mukule pa chikhulupiriro chanu choyera, ndipo muzipemphera ndi mphamvu ya Mzimu Woyera.
Ale vy, moji přátelé, budujte dále na základech dokonalé víry, modlete se v Duchu svatém a zůstávejte v Boží lásce.
21 Khalani mʼchikondi cha Mulungu pamene mukudikira chifundo cha Ambuye athu Yesu Khristu kuti akubweretsereni moyo wosatha. (aiōnios )
Trpělivě čekejte na věčný život daný z milosti našeho Pána Ježíše Krista. (aiōnios )
22 Muwachitire chifundo amene akukayika.
Soucitně pomáhejte těm, kteří kolísají ve víře.
23 Ena muwapulumutse powalanditsa ku moto. Enanso muwachitire chifundo, koma mwa mantha, ndipo muzidana ngakhale ndi mwinjiro yomwe yayipitsidwa ndi machimo.
Zachráníte je tak od záhuby. Mějte slitování i nad těmi, kteří hrubě zhřešili. Přistupujte k nim však s velkou opatrností, abyste sami zůstali čistí.
24 Kwa Iye amene angathe kukusungani kuti mungagwe mʼmachimo, ndiponso amene angathenso kukufikitsani pamaso pake pa ulemerero wopanda cholakwa muli okondwa,
Bůh má moc uchránit vás před pádem a přivést vás čisté a dokonalé do slávy ve věčně trvající radosti.
25 kwa Mulungu yekhayo, Mpulumutsi wathu, kwa Iye kukhale ulemerero, ukulu, mphamvu ndi ulamuliro, mwa Yesu Khristu Ambuye athu, kuyambira isanayambe nthawi, tsopano mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
Pouze jemu jedinému, který nás v Kristu zachránil, patří všechna sláva, velebnost, vláda a moc nyní a zůstane navěky! (aiōn )