< Yoswa 1 >

1 Atamwalira Mose mtumiki wa Mulungu, Yehova anati kwa Yoswa mwana wa Nuni mthandizi wa Mose:
و واقع شد بعد از وفات موسی، بنده خداوند، که خداوند یوشع بن نون، خادم موسی را خطاب کرده، گفت:۱
2 “Mose mtumiki wanga wamwalira. Ndipo iwe ndi anthu onsewa, tsopano konzekani kuwoloka mtsinje wa Yorodani kupita ku dziko limene ndiwapatse Aisraeli onse.
«موسی بنده من وفات یافته است، پس الان برخیز و از این اردن عبور کن، تو و تمامی این قوم، به زمینی که من به ایشان، یعنی به بنی‌اسرائیل می‌دهم.۲
3 Paliponse pamene phazi lanu liponde, ndikupatsani monga momwe ndinalonjezera Mose.
هر جایی که کف پای شما گذارده شود به شما داده‌ام، چنانکه به موسی گفتم.۳
4 Dziko lanu lidzayambira ku chipululu kummwera mpaka ku mapiri a Lebanoni kumpoto, kuchokeranso ku mtsinje waukulu wa Yufurate kummawa, mpaka dziko lonse la Ahiti, kukafika ku Nyanja Yayikulu ya kumadzulo.
از صحرا و این لبنان تانهر بزرگ یعنی نهر فرات، تمامی زمین حتیان و تادریای بزرگ به طرف مغرب آفتاب، حدود شماخواهد بود.۴
5 Palibe munthu amene adzatha kukugonjetsa masiku onse a moyo wako. Monga Ine ndinakhalira ndi Mose, chomwechonso ndidzakhala nawe. Sindidzakusiya kapena kukataya.
هیچکس را در تمامی ایام عمرت یارای مقاومت با تو نخواهد بود. چنانکه با موسی بودم با تو خواهم بود، تو را مهمل نخواهم گذاشت و ترک نخواهم نمود.۵
6 “Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima, chifukwa iwe udzatsogolera anthu awa kukalandira dziko limene Ine ndinalonjeza makolo awo kuti ndidzawapatsa.
قوی و دلیر باش، زیرا که تو این قوم را متصرف، زمینی که برای پدران ایشان قسم خوردم که به ایشان بدهم، خواهی ساخت.۶
7 Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima kwambiri. Usamale ndithu kuti umvere malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anakupatsa. Usachoke pa malamulo anga ndipo kulikonse kumene udzapite udzapambana.
فقط قوی و بسیار دلیر باش تابرحسب تمامی شریعتی که بنده من، موسی تو راامر کرده است متوجه شده، عمل نمایی. زنهار ازآن به طرف راست یا چپ تجاوز منما تا هر جایی که روی، کامیاب شوی.۷
8 Uziwerenga Buku la Malamuloli, uzilingalira zolembedwa mʼmenemo usana ndi usiku, kuti uchite zonse zimene zinalembedwamo. Ukamatero udzapeza bwino ndi kupambana.
این کتاب تورات ازدهان تو دور نشود، بلکه روز و شب در آن تفکرکن تا برحسب هر‌آنچه در آن مکتوب است متوجه شده، عمل نمایی زیرا همچنین راه خود را فیروز خواهی ساخت، و همچنین کامیاب خواهی شد.۸
9 Paja ndinakulamula kuti ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima. Choncho usamachite mantha kapena kutaya mtima popeza Ine Yehova Mulungu wako ndidzakhala nawe kulikonse kumene udzapite.”
آیا تو را امر نکردم؟ پس قوی ودلیر باش، مترس و هراسان مباش زیرا در هر جاکه بروی یهوه خدای تو، با توست.»۹
10 Tsono Yoswa analamula atsogoleri a Aisraeli nawawuza kuti,
پس یوشع روسای قوم را امر فرموده، گفت:۱۰
11 “Pitani ku misasa yonse ndipo muwuze anthu kuti, ‘Konzekani, mangani katundu wanu, popeza pakapita masiku atatu kuyambira lero mudzawoloka Yorodani kupita kukatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.’”
«در میان لشکرگاه بگذرید و قوم را امرفرموده، بگویید: برای خود توشه حاضر کنید، زیرا که بعد از سه روز، شما از این اردن عبورکرده، داخل خواهید شد تا تصرف کنید در زمینی که یهوه خدای شما، به شما برای ملکیت می‌دهد.»۱۱
12 Koma Yoswa anawuza fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti,
و یوشع روبینیان و جادیان و نصف سبطمنسی را خطاب کرده، گفت:۱۲
13 “Kumbukirani zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani kuti, ‘Yehova Mulungu wanu akukupatsani mpumulo, ndi dziko ili kuti likhale lanu.’
«بیاد آورید آن سخن را که موسی، بنده خداوند، به شما امرفرموده، گفت: یهوه، خدای شما به شما آرامی می‌دهد و این زمین را به شما می‌بخشد.۱۳
14 Tsono akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu zitsale mʼdziko lino limene Mose anakupatsani kummawa kwa Yorodani. Koma ankhondo anu okha ndiwo awoloke atatenga zida zawo ndi kupita patsogolo pa abale anu kukawathandiza.
زنان واطفال و مواشی شما در زمینی که موسی در آن طرف اردن به شما داد خواهند ماند، و اما شمامسلح شده، یعنی جمیع مردان جنگی پیش روی برادران خود عبور کنید، و ایشان را اعانت نمایید.۱۴
15 Abale anuwo akadzalandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa monga inu mwachitira, inu mudzabwerera kudzakhazikika mʼdziko lanu limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya la kummawa kwa Yorodani.”
تا خداوند برادران شما را مثل شما آرامی داده باشد، و ایشان نیز در زمینی که یهوه، خدای شمابه ایشان می‌دهد تصرف کرده باشند، آنگاه به زمین ملکیت خود خواهید برگشت و متصرف خواهید شد، در آن که موسی، بنده خداوند به آن طرف اردن به سوی مشرق آفتاب به شما داد.»۱۵
16 Kenaka iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife tidzachita chilichonse chimene mwatilamula, ndipo kulikonse kumene mudzatitume tidzapita.
ایشان در جواب یوشع گفتند: «هر‌آنچه به ما فرمودی خواهیم کرد، و هر جا ما را بفرستی، خواهیم رفت.۱۶
17 Monga momwe tinamvera Mose kwathunthu, chomwechonso tidzakumvera iwe. Yehova Mulungu wanu akhale nanu monga momwe anachitira ndi Mose.
چنانکه موسی را در هر چیزاطاعت نمودیم، تو را نیز اطاعت خواهیم نمود، فقط یهوه، خدای تو، با تو باشد چنانکه با موسی بود.۱۷
18 Aliyense wotsutsana ndi inu kapena wosamvera zimene mutilamula adzaphedwa. Inu mukhale wamphamvu ndi wolimba mtima!”
هر کسی‌که از حکم تو رو گرداند و کلام تو را در هر چیزی که او را امر فرمایی اطاعت نکند، کشته خواهد شد، فقط قوی و دلیر باش.»۱۸

< Yoswa 1 >