< Yoswa 1 >

1 Atamwalira Mose mtumiki wa Mulungu, Yehova anati kwa Yoswa mwana wa Nuni mthandizi wa Mose:
Efter Moses', Herrens tjeners død sa Herren til Josva, Nuns sønn, Moses' tjener:
2 “Mose mtumiki wanga wamwalira. Ndipo iwe ndi anthu onsewa, tsopano konzekani kuwoloka mtsinje wa Yorodani kupita ku dziko limene ndiwapatse Aisraeli onse.
Moses, min tjener, er død; så gjør dig nu rede og dra over Jordan her med hele dette folk til det land som jeg vil gi Israels barn!
3 Paliponse pamene phazi lanu liponde, ndikupatsani monga momwe ndinalonjezera Mose.
Hvert sted I setter eders fot på, gir jeg eder, som jeg sa til Moses:
4 Dziko lanu lidzayambira ku chipululu kummwera mpaka ku mapiri a Lebanoni kumpoto, kuchokeranso ku mtsinje waukulu wa Yufurate kummawa, mpaka dziko lonse la Ahiti, kukafika ku Nyanja Yayikulu ya kumadzulo.
Fra ørkenen og Libanon der nord like til den store elv, elven Frat - over hele hetittenes land og helt til det store hav i vest skal eders land nå.
5 Palibe munthu amene adzatha kukugonjetsa masiku onse a moyo wako. Monga Ine ndinakhalira ndi Mose, chomwechonso ndidzakhala nawe. Sindidzakusiya kapena kukataya.
Ingen skal kunne stå sig mot dig alle ditt livs dager; likesom jeg var med Moses, vil jeg være med dig; jeg vil ikke slippe dig og ikke forlate dig.
6 “Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima, chifukwa iwe udzatsogolera anthu awa kukalandira dziko limene Ine ndinalonjeza makolo awo kuti ndidzawapatsa.
Vær frimodig og sterk! For du skal skifte ut til arv blandt dette folk det land som jeg tilsvor deres fedre å ville gi dem.
7 Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima kwambiri. Usamale ndithu kuti umvere malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anakupatsa. Usachoke pa malamulo anga ndipo kulikonse kumene udzapite udzapambana.
Vær du bare riktig frimodig og sterk, så du akter vel på å gjøre efter hele den lov som Moses, min tjener, lærte dig! Vik ikke av fra den, hverken til høire eller til venstre, så du kan gå viselig frem i alt det du tar dig fore!
8 Uziwerenga Buku la Malamuloli, uzilingalira zolembedwa mʼmenemo usana ndi usiku, kuti uchite zonse zimene zinalembedwamo. Ukamatero udzapeza bwino ndi kupambana.
Denne lovens bok skal ikke vike fra din munn, men du skal grunde på den dag og natt, så du akter vel på å gjøre efter alt det som står skrevet i den; da skal du ha lykke på dine veier, og da skal du gå viselig frem.
9 Paja ndinakulamula kuti ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima. Choncho usamachite mantha kapena kutaya mtima popeza Ine Yehova Mulungu wako ndidzakhala nawe kulikonse kumene udzapite.”
Har jeg ikke befalt dig: Vær frimodig og sterk, frykt ikke og reddes ikke? For Herren din Gud er med dig i alt det du tar dig fore.
10 Tsono Yoswa analamula atsogoleri a Aisraeli nawawuza kuti,
Da bød Josva folkets tilsynsmenn og sa:
11 “Pitani ku misasa yonse ndipo muwuze anthu kuti, ‘Konzekani, mangani katundu wanu, popeza pakapita masiku atatu kuyambira lero mudzawoloka Yorodani kupita kukatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.’”
Gå midt igjennem leiren og byd folket og si: Lag i stand reisekost for eder! For om tre dager skal I gå over Jordan her, så I kan komme og innta det land som Herren eders Gud gir eder til eie.
12 Koma Yoswa anawuza fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti,
Og til rubenittene og gadittene og den halve Manasse stamme sa Josva:
13 “Kumbukirani zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani kuti, ‘Yehova Mulungu wanu akukupatsani mpumulo, ndi dziko ili kuti likhale lanu.’
Kom i hu det som Moses, Herrens tjener, bød eder da han sa: Herren eders Gud lar eder nu komme til ro og gir eder dette land.
14 Tsono akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu zitsale mʼdziko lino limene Mose anakupatsani kummawa kwa Yorodani. Koma ankhondo anu okha ndiwo awoloke atatenga zida zawo ndi kupita patsogolo pa abale anu kukawathandiza.
Eders hustruer, eders barn og eders fe skal bli i det land Moses har gitt eder østenfor Jordan; men selv skal I, så mange av eder som er djerve stridsmenn, dra fullt rustet frem foran eders brødre og hjelpe dem,
15 Abale anuwo akadzalandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa monga inu mwachitira, inu mudzabwerera kudzakhazikika mʼdziko lanu limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya la kummawa kwa Yorodani.”
inntil Herren lar eders brødre komme til ro likesom eder, og også de har tatt det land i eie som Herren eders Gud gir dem; da skal I vende tilbake og bosette eder i eders eget land, det som Moses, Herrens tjener, gav eder på østsiden av Jordan.
16 Kenaka iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife tidzachita chilichonse chimene mwatilamula, ndipo kulikonse kumene mudzatitume tidzapita.
Da svarte de Josva og sa: Alt det du har befalt oss, vil vi gjøre, og hvor du sender oss, vil vi gå.
17 Monga momwe tinamvera Mose kwathunthu, chomwechonso tidzakumvera iwe. Yehova Mulungu wanu akhale nanu monga momwe anachitira ndi Mose.
Aldeles som vi lød Moses, vil vi lyde dig, bare Herren din Gud må være med dig, likesom han var med Moses.
18 Aliyense wotsutsana ndi inu kapena wosamvera zimene mutilamula adzaphedwa. Inu mukhale wamphamvu ndi wolimba mtima!”
Enhver som er gjenstridig mot din befaling og ikke lyder dine ord i alt det du byder ham, han skal dø. Vær bare frimodig og sterk!

< Yoswa 1 >