< Yoswa 1 >

1 Atamwalira Mose mtumiki wa Mulungu, Yehova anati kwa Yoswa mwana wa Nuni mthandizi wa Mose:
And it came to pass, after the death of Moses the servant of Yahweh, —that Yahweh spake unto Joshua son of Nun, the attendant of Moses, saying:
2 “Mose mtumiki wanga wamwalira. Ndipo iwe ndi anthu onsewa, tsopano konzekani kuwoloka mtsinje wa Yorodani kupita ku dziko limene ndiwapatse Aisraeli onse.
Moses my servant, is dead, —Now, therefore, arise, pass over this Jordan, thou, and all this people, into the land which I am giving unto them—unto the sons of Israel.
3 Paliponse pamene phazi lanu liponde, ndikupatsani monga momwe ndinalonjezera Mose.
Every place whereon the sole of your foot shall tread, unto you, have I given it, —as I spake unto Moses.
4 Dziko lanu lidzayambira ku chipululu kummwera mpaka ku mapiri a Lebanoni kumpoto, kuchokeranso ku mtsinje waukulu wa Yufurate kummawa, mpaka dziko lonse la Ahiti, kukafika ku Nyanja Yayikulu ya kumadzulo.
From the desert and this Lebanon, even unto the great river—the river Euphrates, all the land of the Hittites, and unto the great sea, toward the going in of the sun, shall be your boundary.
5 Palibe munthu amene adzatha kukugonjetsa masiku onse a moyo wako. Monga Ine ndinakhalira ndi Mose, chomwechonso ndidzakhala nawe. Sindidzakusiya kapena kukataya.
No man shall stand before thee, all the days of thy life, —as I was with Moses, so I will be with thee, I will not fail thee, neither will I forsake thee.
6 “Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima, chifukwa iwe udzatsogolera anthu awa kukalandira dziko limene Ine ndinalonjeza makolo awo kuti ndidzawapatsa.
Be firm and bold, —for, thou, shalt cause this people to inherit the land which I sware unto their fathers, —to give unto them.
7 Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima kwambiri. Usamale ndithu kuti umvere malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anakupatsa. Usachoke pa malamulo anga ndipo kulikonse kumene udzapite udzapambana.
Only be very firm and bold, taking heed to do according to all the law which Moses my servant commanded thee, do not turn aside therefrom, to the right hand or to the left, —that thou mayest prosper, whithersoever thou goest.
8 Uziwerenga Buku la Malamuloli, uzilingalira zolembedwa mʼmenemo usana ndi usiku, kuti uchite zonse zimene zinalembedwamo. Ukamatero udzapeza bwino ndi kupambana.
This scroll of the law must not cease out of thy mouth, but thou must talk to thyself therein, day and night, that thou mayest take heed to do according to all that is written therein, —for, then, shalt thou make thy way prosperous, and, then, shalt thou have good success.
9 Paja ndinakulamula kuti ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima. Choncho usamachite mantha kapena kutaya mtima popeza Ine Yehova Mulungu wako ndidzakhala nawe kulikonse kumene udzapite.”
Have I not commanded thee, Be firm and bold, do not start nor be dismayed, —for, with thee, is Yahweh thy God, whithersoever thou goest?
10 Tsono Yoswa analamula atsogoleri a Aisraeli nawawuza kuti,
So then Joshua commanded the officers of the people, saying:
11 “Pitani ku misasa yonse ndipo muwuze anthu kuti, ‘Konzekani, mangani katundu wanu, popeza pakapita masiku atatu kuyambira lero mudzawoloka Yorodani kupita kukatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.’”
Pass ye through the midst of the camp, and command the people, saying: Make ready for yourselves, provisions, —for, in three days more, are ye to pass over this Jordan, to go in and possess the land which Yahweh your God is giving you, to possess.
12 Koma Yoswa anawuza fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti,
And, unto the Reubenites, and unto the Gadites, and unto the half tribe of Manasseh, spake Joshua, saying:
13 “Kumbukirani zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani kuti, ‘Yehova Mulungu wanu akukupatsani mpumulo, ndi dziko ili kuti likhale lanu.’
Remember the word which Moses the servant of Yahweh commanded you, saying, —Yahweh your God, is granting you rest, and doth give you this land.
14 Tsono akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu zitsale mʼdziko lino limene Mose anakupatsani kummawa kwa Yorodani. Koma ankhondo anu okha ndiwo awoloke atatenga zida zawo ndi kupita patsogolo pa abale anu kukawathandiza.
Your wives, your little ones, and your cattle, shall remain in the land which Moses hath given you over the Jordan, —but, ye, shall pass over, armed, before your brethren, —all ye mighty men of valour, and shall help them;
15 Abale anuwo akadzalandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa monga inu mwachitira, inu mudzabwerera kudzakhazikika mʼdziko lanu limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya la kummawa kwa Yorodani.”
until that Yahweh shall grant rest unto your brethren, as unto you, so shall, they also, possess the land which Yahweh your God giveth them, —then shall ye return unto the land of your possession, and possess it, which Moses the servant of Yahweh hath given you over the Jordan, towards the rising of the sun.
16 Kenaka iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife tidzachita chilichonse chimene mwatilamula, ndipo kulikonse kumene mudzatitume tidzapita.
Then responded they to Joshua, saying, —All that thou hast commanded us, will we do, and, whithersoever thou shalt send us, will we go:
17 Monga momwe tinamvera Mose kwathunthu, chomwechonso tidzakumvera iwe. Yehova Mulungu wanu akhale nanu monga momwe anachitira ndi Mose.
As in every thing we hearkened unto Moses, so, will we hearken unto thee, —only let Yahweh thy God be with thee, as he was with Moses.
18 Aliyense wotsutsana ndi inu kapena wosamvera zimene mutilamula adzaphedwa. Inu mukhale wamphamvu ndi wolimba mtima!”
Any man who shall rebel against thy bidding, and not hearken unto thy words in all that thou shalt command him, shall be put to death, —only be firm and bold.

< Yoswa 1 >