< Yoswa 1 >

1 Atamwalira Mose mtumiki wa Mulungu, Yehova anati kwa Yoswa mwana wa Nuni mthandizi wa Mose:
And after the death of Moses, the servant of the Lord, it happened that the Lord spoke to Joshua, the son of Nun, the minister of Moses, and he said to him:
2 “Mose mtumiki wanga wamwalira. Ndipo iwe ndi anthu onsewa, tsopano konzekani kuwoloka mtsinje wa Yorodani kupita ku dziko limene ndiwapatse Aisraeli onse.
“Moses, my servant, has died. Rise up, and cross this Jordan, you and all the people with you, into the land which I will give to the sons of Israel.
3 Paliponse pamene phazi lanu liponde, ndikupatsani monga momwe ndinalonjezera Mose.
I will deliver to you every place that the step of your foot will tread upon, just as I said to Moses.
4 Dziko lanu lidzayambira ku chipululu kummwera mpaka ku mapiri a Lebanoni kumpoto, kuchokeranso ku mtsinje waukulu wa Yufurate kummawa, mpaka dziko lonse la Ahiti, kukafika ku Nyanja Yayikulu ya kumadzulo.
From the desert and from Lebanon, even to the great river Euphrates, all the land of the Hittites, as far as the great sea opposite the setting of the sun, shall be your border.
5 Palibe munthu amene adzatha kukugonjetsa masiku onse a moyo wako. Monga Ine ndinakhalira ndi Mose, chomwechonso ndidzakhala nawe. Sindidzakusiya kapena kukataya.
No one will be able to resist you during all the days of your life. Just as I was with Moses, so will I be with you. I will not leave you, nor will I forsake you.
6 “Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima, chifukwa iwe udzatsogolera anthu awa kukalandira dziko limene Ine ndinalonjeza makolo awo kuti ndidzawapatsa.
Be strengthened and be steadfast. For you shall divide by lot, to this people, the land about which I swore to their fathers that I would deliver it to them.
7 Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima kwambiri. Usamale ndithu kuti umvere malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anakupatsa. Usachoke pa malamulo anga ndipo kulikonse kumene udzapite udzapambana.
Therefore, be strengthened and be very steadfast, so that you may observe and accomplish the entire law, which Moses, my servant, instructed to you. You may not turn aside from it to the right, nor to the left. So may you understand all that you should do.
8 Uziwerenga Buku la Malamuloli, uzilingalira zolembedwa mʼmenemo usana ndi usiku, kuti uchite zonse zimene zinalembedwamo. Ukamatero udzapeza bwino ndi kupambana.
The book of this law shall not depart from your mouth. Instead, you shall meditate upon it, day and night, so that you may observe and do all the things that are written in it. Then you shall direct your way and understand it.
9 Paja ndinakulamula kuti ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima. Choncho usamachite mantha kapena kutaya mtima popeza Ine Yehova Mulungu wako ndidzakhala nawe kulikonse kumene udzapite.”
Behold, I am instructing you. Be strengthened, and be steadfast. Do not dread, and do not fear. For the Lord your God is with you in all things, wherever you may go.”
10 Tsono Yoswa analamula atsogoleri a Aisraeli nawawuza kuti,
And Joshua instructed the leaders of the people, saying: “Cross through the midst of the camp, and command the people, and say:
11 “Pitani ku misasa yonse ndipo muwuze anthu kuti, ‘Konzekani, mangani katundu wanu, popeza pakapita masiku atatu kuyambira lero mudzawoloka Yorodani kupita kukatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.’”
‘Prepare your food supplies. For after the third day, you shall cross the Jordan, and you shall enter so as to possess the land, which the Lord your God will give to you.’”
12 Koma Yoswa anawuza fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti,
Likewise, he said to the Reubenites and to the Gadites, and to the one half tribe of Manasseh:
13 “Kumbukirani zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani kuti, ‘Yehova Mulungu wanu akukupatsani mpumulo, ndi dziko ili kuti likhale lanu.’
“Remember the words, which Moses, the servant of the Lord, instructed to you, saying: ‘The Lord your God has given you rest, and has given you all the land.’
14 Tsono akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu zitsale mʼdziko lino limene Mose anakupatsani kummawa kwa Yorodani. Koma ankhondo anu okha ndiwo awoloke atatenga zida zawo ndi kupita patsogolo pa abale anu kukawathandiza.
Your wives and sons, as well as the cattle, shall remain in the land which Moses delivered to you beyond the Jordan. But as for you, pass over with weapons, before your brothers, all you who are strong of hand, and fight on their behalf,
15 Abale anuwo akadzalandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa monga inu mwachitira, inu mudzabwerera kudzakhazikika mʼdziko lanu limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya la kummawa kwa Yorodani.”
until the Lord gives rest to your brothers, just as he has given to you, and until they also possess the land, which the Lord your God will give to them. And so shall you be returned to the land of your possession. And you shall live in the land, which Moses, the servant of the Lord, gave to you beyond the Jordan, opposite the rising of the sun.”
16 Kenaka iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife tidzachita chilichonse chimene mwatilamula, ndipo kulikonse kumene mudzatitume tidzapita.
And they responded to Joshua, and they said: “All that you have instructed to us, we shall do. And wherever you will send us, we shall go.
17 Monga momwe tinamvera Mose kwathunthu, chomwechonso tidzakumvera iwe. Yehova Mulungu wanu akhale nanu monga momwe anachitira ndi Mose.
Just as we obeyed Moses in all things, so shall we obey you also. But may the Lord your God be with you, just as he was with Moses.
18 Aliyense wotsutsana ndi inu kapena wosamvera zimene mutilamula adzaphedwa. Inu mukhale wamphamvu ndi wolimba mtima!”
Whoever will contradict your mouth, and whoever will not obey all of your words, which you will instruct to him, let him die. But may you be strengthened, and may you act manfully.”

< Yoswa 1 >