< Yoswa 1 >

1 Atamwalira Mose mtumiki wa Mulungu, Yehova anati kwa Yoswa mwana wa Nuni mthandizi wa Mose:
Stalo se pak po smrti Mojžíše, služebníka Hospodinova, že mluvil Hospodin k Jozue, synu Nun, služebníku Mojžíšovu, řka:
2 “Mose mtumiki wanga wamwalira. Ndipo iwe ndi anthu onsewa, tsopano konzekani kuwoloka mtsinje wa Yorodani kupita ku dziko limene ndiwapatse Aisraeli onse.
Mojžíš, služebník můj, umřel; protož nyní vstaň, přejdi Jordán tento, ty i všecken lid tento, a jdi do země, kterouž já dávám synům Izraelským.
3 Paliponse pamene phazi lanu liponde, ndikupatsani monga momwe ndinalonjezera Mose.
Každé místo, po kterémž šlapati budete nohama svýma, dal jsem vám, jakož jsem mluvil k Mojžíšovi.
4 Dziko lanu lidzayambira ku chipululu kummwera mpaka ku mapiri a Lebanoni kumpoto, kuchokeranso ku mtsinje waukulu wa Yufurate kummawa, mpaka dziko lonse la Ahiti, kukafika ku Nyanja Yayikulu ya kumadzulo.
Od pouště a Libánu toho až k řece veliké, řece Eufrates, všecka země Hetejská až do moře velikého na západ slunce bude pomezí vaše.
5 Palibe munthu amene adzatha kukugonjetsa masiku onse a moyo wako. Monga Ine ndinakhalira ndi Mose, chomwechonso ndidzakhala nawe. Sindidzakusiya kapena kukataya.
Neostojí žádný před tebou po všecky dny života tvého; jakož jsem byl s Mojžíšem, tak budu s tebou; nenechám tebe samého, aniž tě opustím.
6 “Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima, chifukwa iwe udzatsogolera anthu awa kukalandira dziko limene Ine ndinalonjeza makolo awo kuti ndidzawapatsa.
Posilniž se a zmužile se měj, nebo ty uvedeš v dědictví lidu tomuto zemi, kterouž jsem s přísahou zaslíbil otcům jejich, že ji dám jim.
7 Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima kwambiri. Usamale ndithu kuti umvere malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anakupatsa. Usachoke pa malamulo anga ndipo kulikonse kumene udzapite udzapambana.
Toliko posilň se a udatně sobě počínej, abys ostříhal a činil všecko podlé zákona, kterýž přikázal tobě Mojžíš, služebník můj; neuchyluj se od něho na pravo ani na levo, abys byl opatrný ve všem, k čemuž se obrátíš.
8 Uziwerenga Buku la Malamuloli, uzilingalira zolembedwa mʼmenemo usana ndi usiku, kuti uchite zonse zimene zinalembedwamo. Ukamatero udzapeza bwino ndi kupambana.
Neodejdeť kniha zákona tohoto od úst tvých, ale přemyšlovati budeš o něm dnem i nocí, abys ostříhal a činil všecko podlé toho, což psáno jest v něm; nebo tehdáž šťastný budeš na cestách svých, a tehdáž opatrný budeš.
9 Paja ndinakulamula kuti ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima. Choncho usamachite mantha kapena kutaya mtima popeza Ine Yehova Mulungu wako ndidzakhala nawe kulikonse kumene udzapite.”
Zdaliž jsem nepřikázal tobě, řka: Posilni se a zmužile se měj, neboj se, ani lekej, nebo s tebou jest Hospodin Bůh tvůj, kamž se koli obrátíš.
10 Tsono Yoswa analamula atsogoleri a Aisraeli nawawuza kuti,
Tedy přikázal Jozue správcům lidu, řka:
11 “Pitani ku misasa yonse ndipo muwuze anthu kuti, ‘Konzekani, mangani katundu wanu, popeza pakapita masiku atatu kuyambira lero mudzawoloka Yorodani kupita kukatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.’”
Projděte skrze tábor a přikažte lidu, řkouce: Nachystejte sobě potravy, nebo po třech dnech půjdete přes Jordán tento, abyste vejdouce, opanovali zemi, kterouž Hospodin Bůh váš dává vám k dědičnému vládařství.
12 Koma Yoswa anawuza fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti,
Rubenovu pak pokolení a Gádovu, a polovici pokolení Manassesova mluvil Jozue, řka:
13 “Kumbukirani zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani kuti, ‘Yehova Mulungu wanu akukupatsani mpumulo, ndi dziko ili kuti likhale lanu.’
Pomněte na to, co vám přikázal Mojžíš služebník Hospodinův, když řekl: Hospodin Bůh váš způsobil vám odpočinutí, že vám dal zemi tuto.
14 Tsono akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu zitsale mʼdziko lino limene Mose anakupatsani kummawa kwa Yorodani. Koma ankhondo anu okha ndiwo awoloke atatenga zida zawo ndi kupita patsogolo pa abale anu kukawathandiza.
Ženy vaše, dítky vaše i dobytek váš nechť zůstanou v zemi, kterouž dal vám Mojžíš s této strany Jordánu, vy pak jděte vojensky zpořádaní před bratřími svými, kteříkoli jste muži silní, a pomáhejte jim,
15 Abale anuwo akadzalandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa monga inu mwachitira, inu mudzabwerera kudzakhazikika mʼdziko lanu limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya la kummawa kwa Yorodani.”
Dokudž nedá odpočinutí Hospodin bratřím vašim jako i vám, a neobdrží dědičně také i oni země, kterouž Hospodin Bůh váš dává jim. Potom navrátíte se do země dědictví svého, kterouž dal vám Mojžíš, služebník Hospodinův, s této strany Jordánu, k východu slunce, a dědičně vlásti jí budete.
16 Kenaka iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife tidzachita chilichonse chimene mwatilamula, ndipo kulikonse kumene mudzatitume tidzapita.
I odpověděli k Jozue, řkouce: Všecko, což jsi nám rozkázal, učiníme, a kamžkoli pošleš nás, půjdeme.
17 Monga momwe tinamvera Mose kwathunthu, chomwechonso tidzakumvera iwe. Yehova Mulungu wanu akhale nanu monga momwe anachitira ndi Mose.
Rovně jakž jsme poslouchali Mojžíše, tak poslouchati budeme tebe; jediné nechť jest Hospodin Bůh tvůj s tebou, jako byl s Mojžíšem.
18 Aliyense wotsutsana ndi inu kapena wosamvera zimene mutilamula adzaphedwa. Inu mukhale wamphamvu ndi wolimba mtima!”
Kdo by koli odporný byl rozkázaní tvému, a neposlouchal by řečí tvých ve všech věcech, kteréž bys přikázal jemu, umřeť; toliko posilň se a zmužile se měj.

< Yoswa 1 >