< Yoswa 9 >
1 Mafumu onse okhala kumadzulo kwa Yorodani atamva zimenezi pamodzi ndi mafumu okhala ku mayiko a ku mapiri, mu zigwa, mʼmbali mwa Nyanja yayikulu mpaka ku Lebanoni (mafumu a Ahiti, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi, ndi Ayebusi),
A gdy usłyszeli o tym wszyscy królowie, którzy byli po tej stronie Jordanu w górach, na równinach i nad całym brzegiem Morza Wielkiego aż po Liban: Chetyci, Amoryci, Kananejczycy, Peryzzyci, Chiwwici i Jebusyci:
2 anapangana kuti achite nkhondo ndi Yoswa ndi Israeli.
Zebrali się razem, aby jednomyślnie walczyć przeciw Jozuemu i Izraelowi.
3 Koma Ahivi ena a ku Gibiyoni atamva zomwe Yoswa anachitira mizinda ya Yeriko ndi Ai,
Lecz mieszkańcy Gibeonu, gdy usłyszeli o tym, co Jozue uczynił z Jerychem i Aj;
4 anaganiza zochita zachinyengo. Anapita nasenzetsa abulu awo chakudya mʼmatumba akalekale ndiponso matumba a vinyo achikopa ongʼambikangʼambika.
Użyli podstępu i wyruszyli, udając posłów, i wzięli stare wory na swoje osły i stare, popękane i połatane bukłaki na wino;
5 Anthuwa anavala nsapato zakutha ndi zazigamba ndiponso anavala sanza. Buledi wawo yense anali wowuma ndi wowola.
I stare, i połatane obuwie na nogi, stare szaty na siebie, a cały chleb, który ze sobą zabrali w drogę, był suchy i spleśniały.
6 Ndipo anapita kwa Yoswa ku msasa ku Giligala ndikumuwuza kuti, pamodzi ndi Aisraeli onse, “Ife tachokera ku dziko lakutali, ndipo tikufuna kuti muchite mgwirizano ndi ife.”
Wtedy przybyli do Jozuego, do obozu w Gilgal, i powiedzieli do niego i do mężczyzn Izraela: Przyszliśmy z dalekiego kraju. Zawrzyjcie więc teraz przymierze z nami.
7 Koma Aisraeli anayankha Ahiviwo kuti, “Mwinatu inu mukukhala pafupi ndi ife. Tsono ife tingachite bwanji mgwirizano ndi inu?”
Lecz mężczyźni Izraela odpowiedzieli Chiwwitom: A może mieszkacie wśród nas, jakże więc możemy zawrzeć z wami przymierze?
8 Iwo anati kwa Yoswa, “Ife ndife akapolo anu.” Tsono Yoswa anawafunsa kuti, “Inu ndinu yani ndipo mukuchokera kuti?”
A oni powiedzieli Jozuemu: Jesteśmy twoimi sługami. I Jozue zapytał ich: Kim jesteście i skąd przybywacie?
9 Iwo anayankha kuti, “Akapolo anufe tachokera ku dziko lakutali chifukwa tamva za Yehova Mulungu wanu. Tamva mbiri yonse ya zimene Iye anachita ku Igupto,
Odpowiedzieli mu: Twoi słudzy przybyli z bardzo dalekiego kraju ze względu na imię PANA, twego Boga. Usłyszeliśmy bowiem o jego sławie oraz o wszystkim, co uczynił w Egipcie;
10 ndi zonse zimene anachita kwa mafumu awiri a Aamori kummawa kwa Yorodani, mfumu Sihoni ya Hesiboni ndi Ogi mfumu ya Basani amene amalamulira ku Asiteroti.
I o wszystkim, co uczynił dwom królom amoryckim, którzy byli za Jordanem, Sichonowi, królowi Cheszbonu, i Ogowi, królowi Baszanu, który [był] w Asztarot.
11 Tsono akuluakulu athu ndi onse amene akukhala mʼdziko lathu anati kwa ife. Tengani chakudya cha pa ulendo wanu. Pitani mukakumane nawo ndipo mukati kwa iwo, ‘Ife ndife akapolo anu, ndipo tikufuna kuti mugwirizane nafe za mtendere.’”
I nasi starsi i wszyscy mieszkańcy naszego kraju nakazali nam: Weźcie ze sobą żywność na drogę, wyjdźcie im naprzeciw i powiedzcie im: Jesteśmy waszymi sługami, zawrzyjcie więc teraz przymierze z nami.
12 Buledi wathuyu anali wotentha pamene timanyamuka ku mudzi kubwera kwa inu. Koma tsopano taonani ali gwaa ndiponso wawola.
Ten nasz chleb był jeszcze ciepły, gdy wzięliśmy go z naszych domów w dniu, kiedy wyruszyliśmy do was; a teraz jest suchy i spleśniały.
13 Zikopa zimene tinathiramo vinyozi zinali zatsopano, koma taonani zathetheka. Zovala zathu ndi nsapato zathu zatha chifukwa cha kutalika kwa ulendo.
I te bukłaki na wino, które napełniliśmy, były nowe, a oto popękały. Także nasze szaty i obuwie zniszczyły się z powodu bardzo długiej podróży.
14 Aisraeli anatengako chakudya chawo koma sanafunse kwa Yehova.
A mężczyźni [Izraela] wzięli z ich żywności, lecz nie radzili się PANA.
15 Choncho Yoswa anapangana nawo za mtendere kuti sadzawapha, ndipo atsogoleri a gulu anavomereza pochita lumbiro.
Wtedy Jozue zawarł z nimi pokój i ustanowił z nimi przymierze, że zachowa ich przy życiu. Także naczelnicy zgromadzenia im przysięgli.
16 Patatha masiku atatu atachita mgwirizano wa mtendere ndi Agibiyoni, Aisraeli anamva kuti anali anansi awo, anthu amene amakhala nawo pafupi.
Lecz po trzech dniach, po zawarciu z nimi przymierza, usłyszeli, że są oni sąsiadami i że mieszkają wśród nich.
17 Tsono Aisraeli ananyamuka ulendo ndipo tsiku lachitatu anafika ku mizinda ya Gibiyoni, Kefira, Beeroti ndi Kiriati-Yearimu.
Wtedy synowie Izraela wyruszyli i po trzech dniach dotarli do ich miast. Miastami ich były: Gibeon, Kefira, Beerot i Kiriat-Jearim.
18 Koma Aisraeli sanawaphe anthuwo chifukwa atsogoleri awo anali atalonjeza mʼdzina la Yehova Mulungu wa Israeli za Agibiyoniwo. Koma anthu onse anatsutsana ndi atsogoleriwo.
I nie wytracili ich synowie Izraela, gdyż naczelnicy zgromadzenia przysięgli im na PANA, Boga Izraela. I całe zgromadzenie szemrało przeciw naczelnikom.
19 Koma atsogoleriwo anayankha kuti, “Ife tinawalonjeza mʼdzina la Yehova, Mulungu wa Israeli, ndipo tsopano sitingawaphe.
I wszyscy naczelnicy powiedzieli do całego zgromadzenia: Przysięgliśmy im na PANA, Boga Izraela, dlatego teraz nie możemy ich tknąć.
20 Chimene tidzachita nawo ndi ichi: Tidzawasiya akhale ndi moyo kuti mkwiyo wa Yehova usatigwere chifukwa chophwanya lonjezo limene tinawalonjeza.”
Tak więc postąpimy z nimi: zachowamy ich przy życiu, żeby nie spadł na nas gniew z powodu przysięgi, którą im złożyliśmy.
21 Anapitiriza kunena kuti “Asiyeni akhale ndi moyo, komabe akhale otidulira mitengo ndi kutitungira madzi ogwiritsa ntchito pa chipembedzo.” Lonjezo la atsogoleriwo linasungidwa.
Ponadto naczelnicy powiedzieli im: Niech pozostaną przy życiu, ale niech rąbią drewno i noszą wodę dla całego zgromadzenia – zgodnie z tym, co obiecali naczelnicy.
22 Kenaka Yoswa anayitanitsa Agibiyoni aja nawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani inu munatinyenga ponena kuti mumachokera kutali pamene zoona zake nʼzoti mumakhala pafupi pomwe pano?
Potem Jozue wezwał ich i zapytał: Dlaczego nas oszukaliście, mówiąc: Jesteśmy z bardzo daleka, skoro mieszkacie wśród nas?
23 Tsopano popeza mwachita izi, Mulungu wakutembererani ndipo palibe wina mwa inu amene akhale mfulu. Nthawi zonse inu muzidzatidulira nkhuni ndi kutitungira madzi ku Nyumba ya Yehova.”
Teraz więc jesteście przeklęci i nie przestaniecie być niewolnikami rąbiącymi drewno i noszącymi wodę dla domu mego Boga.
24 Iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife akapolo anufe tinachita zimenezi chifukwa tinamva bwino lomwe kuti Yehova Mulungu wanu analamula Mose mtumiki wake kuti adzakupatsani dziko lonseli ndi kuti anthu onse okhalamo adzaphedwe. Tsono ife tinachita mantha aakulu ndipo tinachita zimenezi pofuna kupulumutsa miyoyo yathu.
Oni odpowiedzieli Jozuemu: Oznajmiono dokładnie twoim sługom, że PAN, twój Bóg, rozkazał swemu słudze Mojżeszowi dać wam całą ziemię i zgładzić przed wami wszystkich mieszkańców tej ziemi. Dlatego bardzo się baliśmy o nasze życie z waszego powodu i dlatego tak postąpiliśmy.
25 Tsopanotu ife tili mʼmanja mwanu, ndipo inu chitani nafe monga kukukomerani.”
A teraz oto jesteśmy w twoich rękach. Uczyń z nami to, co uważasz za dobre i słuszne.
26 Tsono Yoswa anawapulumutsa mʼmanja mwa Aisraeli ndipo sanawaphe.
I postąpił tak z nimi, i wybawił ich z rąk synów Izraela, żeby ich nie zabili.
27 Kuyambira tsiku limenelo Agibiyoni aja anasanduka odula nkhuni zaguwa lansembe la Yehova ndiponso otunga madzi. Mpaka lero lino iwo akuchitabe zimenezi kulikonse kumene Yehova anasankha.
I w tym dniu Jozue nakazał im narąbać drewna i nosić wodę dla zgromadzenia oraz dla ołtarza PANA w miejscu, które miał wybrać. I jest tak aż do dziś.