< Yoswa 9 >
1 Mafumu onse okhala kumadzulo kwa Yorodani atamva zimenezi pamodzi ndi mafumu okhala ku mayiko a ku mapiri, mu zigwa, mʼmbali mwa Nyanja yayikulu mpaka ku Lebanoni (mafumu a Ahiti, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi, ndi Ayebusi),
Kwasekusithi lapho wonke amakhosi ayenganeno kweJordani, entabeni, lesihotsheni, lekhunjini lolwandle olukhulu, maqondana leLebhanoni, amaHethi lamaAmori, amaKhanani, amaPerizi, amaHivi lamaJebusi ezwa,
2 anapangana kuti achite nkhondo ndi Yoswa ndi Israeli.
abuthana ndawonye ukulwa loJoshuwa loIsrayeli nganhliziyonye.
3 Koma Ahivi ena a ku Gibiyoni atamva zomwe Yoswa anachitira mizinda ya Yeriko ndi Ai,
Kwathi abahlali beGibeyoni sebezwile lokho uJoshuwa ayekwenzile eJeriko laseAyi,
4 anaganiza zochita zachinyengo. Anapita nasenzetsa abulu awo chakudya mʼmatumba akalekale ndiponso matumba a vinyo achikopa ongʼambikangʼambika.
labo basebesenza ngobuqili; bahamba bazenza izithunywa, bathwalisa obabhemi babo amasaka agugileyo lemigodla yewayini egugileyo ledabukileyo lebekelweyo,
5 Anthuwa anavala nsapato zakutha ndi zazigamba ndiponso anavala sanza. Buledi wawo yense anali wowuma ndi wowola.
lamanyathela agugileyo labekelweyo enyaweni zabo, lezigqoko ezigugileyo bezigqokile, lezinkwa zonke zomphako wabo sezomile zikhuntile.
6 Ndipo anapita kwa Yoswa ku msasa ku Giligala ndikumuwuza kuti, pamodzi ndi Aisraeli onse, “Ife tachokera ku dziko lakutali, ndipo tikufuna kuti muchite mgwirizano ndi ife.”
Basebesiya kuJoshuwa enkambeni eGiligali, bathi kuye lemadodeni akoIsrayeli: Sivela elizweni elikhatshana, ngakho-ke yenzani isivumelwano lathi.
7 Koma Aisraeli anayankha Ahiviwo kuti, “Mwinatu inu mukukhala pafupi ndi ife. Tsono ife tingachite bwanji mgwirizano ndi inu?”
Kodwa amadoda akoIsrayeli athi kumaHivi: Mhlawumbe lihlala phakathi kwethu; pho, singenza njani isivumelwano lenu?
8 Iwo anati kwa Yoswa, “Ife ndife akapolo anu.” Tsono Yoswa anawafunsa kuti, “Inu ndinu yani ndipo mukuchokera kuti?”
Asesithi kuJoshuwa: Sizinceku zakho. UJoshuwa wasesithi kiwo: Lingobani? Njalo livela ngaphi?
9 Iwo anayankha kuti, “Akapolo anufe tachokera ku dziko lakutali chifukwa tamva za Yehova Mulungu wanu. Tamva mbiri yonse ya zimene Iye anachita ku Igupto,
Asesithi kuye: Izinceku zakho zivela elizweni elikhatshana kakhulu, ngenxa yebizo leNkosi uNkulunkulu wakho, ngoba sizwile indumela yayo lakho konke eyakwenza eGibhithe,
10 ndi zonse zimene anachita kwa mafumu awiri a Aamori kummawa kwa Yorodani, mfumu Sihoni ya Hesiboni ndi Ogi mfumu ya Basani amene amalamulira ku Asiteroti.
lakho konke eyakwenza emakhosini amabili amaAmori ayengaphetsheya kweJordani, uSihoni inkosi yeHeshiboni, loOgi inkosi yeBashani, eyayiseAshitarothi.
11 Tsono akuluakulu athu ndi onse amene akukhala mʼdziko lathu anati kwa ife. Tengani chakudya cha pa ulendo wanu. Pitani mukakumane nawo ndipo mukati kwa iwo, ‘Ife ndife akapolo anu, ndipo tikufuna kuti mugwirizane nafe za mtendere.’”
Ngakho abadala bethu labo bonke abakhileyo elizweni lakithi bakhuluma kithi besithi: Thathani umphako wendlela esandleni senu, lihambe liyehlangana labo, lithi kibo: Sizinceku zenu; ngakho-ke yenzani isivumelwano lathi.
12 Buledi wathuyu anali wotentha pamene timanyamuka ku mudzi kubwera kwa inu. Koma tsopano taonani ali gwaa ndiponso wawola.
Lesisinkwa sethu sasithatha sitshisa singumphako wethu ezindlini zethu mhla siphumayo sisiza kini; kodwa khathesi, khangela, sesomile sakhunta.
13 Zikopa zimene tinathiramo vinyozi zinali zatsopano, koma taonani zathetheka. Zovala zathu ndi nsapato zathu zatha chifukwa cha kutalika kwa ulendo.
Lalimigodla yewayini esayigcwalisayo yayimitsha; kodwa khangela, isidabukile. Lalezizigqoko zethu lamanyathela ethu sekugugiswe luhambo olude kakhulu.
14 Aisraeli anatengako chakudya chawo koma sanafunse kwa Yehova.
Ngakho amadoda athatha kokomphako wabo, engabuzanga umlomo weNkosi.
15 Choncho Yoswa anapangana nawo za mtendere kuti sadzawapha, ndipo atsogoleri a gulu anavomereza pochita lumbiro.
UJoshuwa wasesenza ukuthula labo, wenza isivumelwano labo sokubayekela baphile, lezinduna zenhlangano zafunga kibo.
16 Patatha masiku atatu atachita mgwirizano wa mtendere ndi Agibiyoni, Aisraeli anamva kuti anali anansi awo, anthu amene amakhala nawo pafupi.
Kwasekusithi ekupheleni kwensuku ezintathu emva kokuthi sebenzile isivumelwano labo, bezwa ukuthi bangomakhelwane babo, lokuthi babehlala phakathi kwabo.
17 Tsono Aisraeli ananyamuka ulendo ndipo tsiku lachitatu anafika ku mizinda ya Gibiyoni, Kefira, Beeroti ndi Kiriati-Yearimu.
Abantwana bakoIsrayeli basebesuka bafika emizini yabo ngosuku lwesithathu. Njalo imizi yabo yayiyiGibeyoni leKefira leBherothi leKiriyathi-Jeyarimi.
18 Koma Aisraeli sanawaphe anthuwo chifukwa atsogoleri awo anali atalonjeza mʼdzina la Yehova Mulungu wa Israeli za Agibiyoniwo. Koma anthu onse anatsutsana ndi atsogoleriwo.
Njalo abantwana bakoIsrayeli kababatshayanga ngoba izinduna zebandla zazibafungele ngeNkosi, uNkulunkulu kaIsrayeli; inhlangano yonke yasingungunela izinduna.
19 Koma atsogoleriwo anayankha kuti, “Ife tinawalonjeza mʼdzina la Yehova, Mulungu wa Israeli, ndipo tsopano sitingawaphe.
Kodwa zonke izinduna zathi enhlanganweni yonke: Thina sifungile kibo ngeNkosi, uNkulunkulu kaIsrayeli, ngakho-ke kasilakubathinta.
20 Chimene tidzachita nawo ndi ichi: Tidzawasiya akhale ndi moyo kuti mkwiyo wa Yehova usatigwere chifukwa chophwanya lonjezo limene tinawalonjeza.”
Sizakwenza lokhu kibo, sibayekele baphile, ukuze kungabi khona ulaka phezu kwethu ngenxa yesifungo esasifunga kibo.
21 Anapitiriza kunena kuti “Asiyeni akhale ndi moyo, komabe akhale otidulira mitengo ndi kutitungira madzi ogwiritsa ntchito pa chipembedzo.” Lonjezo la atsogoleriwo linasungidwa.
Lezinduna zathi kubo: Bayekeleni baphile, kodwa kababe ngabagamuli benkuni labakhi bamanzi enhlanganweni yonke, njengokutsho kwezinduna kubo.
22 Kenaka Yoswa anayitanitsa Agibiyoni aja nawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani inu munatinyenga ponena kuti mumachokera kutali pamene zoona zake nʼzoti mumakhala pafupi pomwe pano?
UJoshuwa wasebabiza, wakhuluma labo esithi: Lisikhohliseleni, lisithi: Sikhatshana kakhulu lani; kanti lina lihlala phakathi kwethu?
23 Tsopano popeza mwachita izi, Mulungu wakutembererani ndipo palibe wina mwa inu amene akhale mfulu. Nthawi zonse inu muzidzatidulira nkhuni ndi kutitungira madzi ku Nyumba ya Yehova.”
Ngakho-ke liqalekisiwe, njalo kakuyikuqunywa phakathi kwenu izigqili labagamuli benkuni labakhi bamanzi bendlu kaNkulunkulu wami.
24 Iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife akapolo anufe tinachita zimenezi chifukwa tinamva bwino lomwe kuti Yehova Mulungu wanu analamula Mose mtumiki wake kuti adzakupatsani dziko lonseli ndi kuti anthu onse okhalamo adzaphedwe. Tsono ife tinachita mantha aakulu ndipo tinachita zimenezi pofuna kupulumutsa miyoyo yathu.
Basebephendula uJoshuwa bathi: Ngoba kwatshelwa lokutshelwa ezincekwini zakho ukuthi iNkosi uNkulunkulu wakho yalaya uMozisi inceku yayo ukulinika ilizwe lonke lokuchitha bonke abakhileyo belizwe phambi kwenu. Ngakho sesaba kakhulu ngempilo yethu ngenxa yenu. Yikho senze le into.
25 Tsopanotu ife tili mʼmanja mwanu, ndipo inu chitani nafe monga kukukomerani.”
Khathesi-ke, khangela, sesisesandleni sakho; yenza njengokulungileyo lanjengokuqondileyo emehlweni akho ukukwenza kithi.
26 Tsono Yoswa anawapulumutsa mʼmanja mwa Aisraeli ndipo sanawaphe.
Ngakho wenza njalo kubo, wabophula esandleni sabantwana bakoIsrayeli, ukuze bangababulali.
27 Kuyambira tsiku limenelo Agibiyoni aja anasanduka odula nkhuni zaguwa lansembe la Yehova ndiponso otunga madzi. Mpaka lero lino iwo akuchitabe zimenezi kulikonse kumene Yehova anasankha.
UJoshuwa wasebenza ngalolosuku baba ngabagamuli benkuni labakhi bamanzi benhlangano, labelathi leNkosi, kuze kube lamuhla, endaweni ezayikhetha.