< Yoswa 9 >

1 Mafumu onse okhala kumadzulo kwa Yorodani atamva zimenezi pamodzi ndi mafumu okhala ku mayiko a ku mapiri, mu zigwa, mʼmbali mwa Nyanja yayikulu mpaka ku Lebanoni (mafumu a Ahiti, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi, ndi Ayebusi),
Ces événements appris, tous les rois d’au-delà du Jourdain, qui demeuraient dans les montagnes, dans les plaines, dans les lieux maritimes et sur le rivage de la grande mer; ceux aussi qui habitaient près du Liban, l’Héthéen, et l’Amorrhéen, le Chananéen, le Phérézéen, l’Hévéen et le Jébuséen,
2 anapangana kuti achite nkhondo ndi Yoswa ndi Israeli.
Se réunirent tous ensemble pour combattre contre Josué et Israël, d’un même cœur et d’un même esprit.
3 Koma Ahivi ena a ku Gibiyoni atamva zomwe Yoswa anachitira mizinda ya Yeriko ndi Ai,
Mais ceux qui habitaient à Gabaon, apprenant tout ce qu’avait fait Josué à Jéricho et à Haï,
4 anaganiza zochita zachinyengo. Anapita nasenzetsa abulu awo chakudya mʼmatumba akalekale ndiponso matumba a vinyo achikopa ongʼambikangʼambika.
Et imaginant une ruse, prirent avec eux des vivres, mettant de vieux sacs sur leurs ânes et des outres de vin rompues et recousues,
5 Anthuwa anavala nsapato zakutha ndi zazigamba ndiponso anavala sanza. Buledi wawo yense anali wowuma ndi wowola.
Et des chaussures très vieilles, et qui, pour preuve de leur vétusté, étaient couvertes de pièces; ils étaient eux-mêmes vêtus de vieux habits: les pains aussi qu’ils portaient pour provisions de voyage, étaient durs et brisés en morceaux.
6 Ndipo anapita kwa Yoswa ku msasa ku Giligala ndikumuwuza kuti, pamodzi ndi Aisraeli onse, “Ife tachokera ku dziko lakutali, ndipo tikufuna kuti muchite mgwirizano ndi ife.”
C’est ainsi qu’ils vinrent vers Josué, qui alors se trouvait au camp de Galgala, et qu’ils lui dirent et en même temps à tout Israël: Nous sommes venus d’une terre lointaine, désirant faire la paix avec vous. Et les hommes d’Israël leur répondirent et dirent:
7 Koma Aisraeli anayankha Ahiviwo kuti, “Mwinatu inu mukukhala pafupi ndi ife. Tsono ife tingachite bwanji mgwirizano ndi inu?”
Peut-être que vous habitez dans la terre qui nous est due par le sort, et que nous ne pouvons faire alliance avec vous.
8 Iwo anati kwa Yoswa, “Ife ndife akapolo anu.” Tsono Yoswa anawafunsa kuti, “Inu ndinu yani ndipo mukuchokera kuti?”
Mais eux à Josué: Nous sommes vos serviteurs, dirent-ils. Et Josué leur demanda: Qui êtes-vous? Et d’où venez-vous?
9 Iwo anayankha kuti, “Akapolo anufe tachokera ku dziko lakutali chifukwa tamva za Yehova Mulungu wanu. Tamva mbiri yonse ya zimene Iye anachita ku Igupto,
Ils répondirent: C’est d’une terre très lointaine que sont venus vos serviteurs, au nom du Seigneur ton Dieu; car nous avons appris la renommée de sa puissance, tout ce qu’il a fait en Egypte,
10 ndi zonse zimene anachita kwa mafumu awiri a Aamori kummawa kwa Yorodani, mfumu Sihoni ya Hesiboni ndi Ogi mfumu ya Basani amene amalamulira ku Asiteroti.
Et aux deux rois des Amorrhéens, qui étaient au-delà du Jourdain, Séhon, roi d’Hésébon, et Og, roi de Basan, qui était à Astaroth.
11 Tsono akuluakulu athu ndi onse amene akukhala mʼdziko lathu anati kwa ife. Tengani chakudya cha pa ulendo wanu. Pitani mukakumane nawo ndipo mukati kwa iwo, ‘Ife ndife akapolo anu, ndipo tikufuna kuti mugwirizane nafe za mtendere.’”
Et les anciens et tous les habitants de notre terre nous ont dit: Prenez en vos mains des provisions pour ce très long voyage, et allez au-devant d’eux, et dites: Nous sommes vos serviteurs, faites alliance avec nous.
12 Buledi wathuyu anali wotentha pamene timanyamuka ku mudzi kubwera kwa inu. Koma tsopano taonani ali gwaa ndiponso wawola.
Voyez ces pains, quand nous sommes sortis de nos maisons, pour venir vers vous, nous les avons pris chauds; maintenant ils sont devenus secs et réduits en poudre par une excessive vétusté.
13 Zikopa zimene tinathiramo vinyozi zinali zatsopano, koma taonani zathetheka. Zovala zathu ndi nsapato zathu zatha chifukwa cha kutalika kwa ulendo.
Et ces outres de vin, nous les avons remplies neuves, maintenant elles sont rompues et décousues; et les vêtements que nous portons, et les chaussures que nous avons aux pieds, sont usés à cause de la longueur d’un trop long chemin, et presque entièrement détruits.
14 Aisraeli anatengako chakudya chawo koma sanafunse kwa Yehova.
Ils prirent donc de leurs vivres et ils n’interrogèrent point l’oracle du Seigneur.
15 Choncho Yoswa anapangana nawo za mtendere kuti sadzawapha, ndipo atsogoleri a gulu anavomereza pochita lumbiro.
Et Josué fit la paix avec eux, et, l’alliance contractée, il promit qu’ils ne seraient pas tués: les princes de la multitude aussi le leur jurèrent.
16 Patatha masiku atatu atachita mgwirizano wa mtendere ndi Agibiyoni, Aisraeli anamva kuti anali anansi awo, anthu amene amakhala nawo pafupi.
Mais après trois jours de l’alliance faite, ils apprirent qu’ils habitaient dans le voisinage, et qu’ils allaient se trouver au milieu d’eux.
17 Tsono Aisraeli ananyamuka ulendo ndipo tsiku lachitatu anafika ku mizinda ya Gibiyoni, Kefira, Beeroti ndi Kiriati-Yearimu.
Et les enfants d’Israël levèrent le camp, et ils arrivèrent le troisième jour dans leurs villes, dont les noms sont, Gabaon, Caphira, Béroth et Cariathiarim.
18 Koma Aisraeli sanawaphe anthuwo chifukwa atsogoleri awo anali atalonjeza mʼdzina la Yehova Mulungu wa Israeli za Agibiyoniwo. Koma anthu onse anatsutsana ndi atsogoleriwo.
Cependant ils ne les tuèrent point, parce que les princes de la multitude le leur avait juré au nom du Seigneur Dieu d’Israël. C’est pourquoi tout le peuple murmura contre les princes,
19 Koma atsogoleriwo anayankha kuti, “Ife tinawalonjeza mʼdzina la Yehova, Mulungu wa Israeli, ndipo tsopano sitingawaphe.
Qui leur répondirent: Nous leur avons juré au nom du Seigneur Dieu d’Israël, et c’est pour cela que nous ne pouvons les toucher.
20 Chimene tidzachita nawo ndi ichi: Tidzawasiya akhale ndi moyo kuti mkwiyo wa Yehova usatigwere chifukwa chophwanya lonjezo limene tinawalonjeza.”
Seulement, voici ce que nous leur ferons: Qu’à la vérité ils soient conservés à la vie, de peur que la colère du Seigneur ne s’élève contre nous, si nous nous parjurons;
21 Anapitiriza kunena kuti “Asiyeni akhale ndi moyo, komabe akhale otidulira mitengo ndi kutitungira madzi ogwiritsa ntchito pa chipembedzo.” Lonjezo la atsogoleriwo linasungidwa.
Mais qu’ils vivent de telle sorte qu’ils coupent du bois et qu’ils portent de l’eau pour l’usage de toute la multitude. Pendant que les princes disaient ces choses,
22 Kenaka Yoswa anayitanitsa Agibiyoni aja nawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani inu munatinyenga ponena kuti mumachokera kutali pamene zoona zake nʼzoti mumakhala pafupi pomwe pano?
Josué appela les Gabaonites, et leur dit: Pourquoi avez-vous voulu nous surprendre par fraude, jusqu’à dire: Nous habitons fort loin de vous, tandis que vous êtes au milieu de nous?
23 Tsopano popeza mwachita izi, Mulungu wakutembererani ndipo palibe wina mwa inu amene akhale mfulu. Nthawi zonse inu muzidzatidulira nkhuni ndi kutitungira madzi ku Nyumba ya Yehova.”
C’est pourquoi vous serez sous la malédiction, et jamais il ne manquera quelqu’un de votre race pour couper du bois et porter de l’eau dans la maison de mon Dieu.
24 Iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife akapolo anufe tinachita zimenezi chifukwa tinamva bwino lomwe kuti Yehova Mulungu wanu analamula Mose mtumiki wake kuti adzakupatsani dziko lonseli ndi kuti anthu onse okhalamo adzaphedwe. Tsono ife tinachita mantha aakulu ndipo tinachita zimenezi pofuna kupulumutsa miyoyo yathu.
Ceux-ci répondirent: Il a été annoncé à vos serviteurs, que le Seigneur votre Dieu avait promis à Moïse, son serviteur, qu’il vous livrerait toute cette terre, et qu’il en détruirait tous les habitants. Nous avons donc beaucoup craint, et nous avons pourvu à notre vie, poussés par la terreur de votre nom, et nous avons formé ce dessein.
25 Tsopanotu ife tili mʼmanja mwanu, ndipo inu chitani nafe monga kukukomerani.”
Mais maintenant nous sommes en ta main, fais-nous ce qui te paraît bon et juste.
26 Tsono Yoswa anawapulumutsa mʼmanja mwa Aisraeli ndipo sanawaphe.
Josué fit donc comme il avait dit; et il les délivra de la main des enfants d’Israël, afin qu’ils ne fussent pas tués.
27 Kuyambira tsiku limenelo Agibiyoni aja anasanduka odula nkhuni zaguwa lansembe la Yehova ndiponso otunga madzi. Mpaka lero lino iwo akuchitabe zimenezi kulikonse kumene Yehova anasankha.
Et en ce jour-là il déclara qu’ils étaient au service de tout le peuple et de l’autel du Seigneur, pour couper du bois et porter de l’eau dans le lieu que le Seigneur aurait choisi; ce qu’ils ont fait jusqu’au présent temps.

< Yoswa 9 >