< Yoswa 9 >

1 Mafumu onse okhala kumadzulo kwa Yorodani atamva zimenezi pamodzi ndi mafumu okhala ku mayiko a ku mapiri, mu zigwa, mʼmbali mwa Nyanja yayikulu mpaka ku Lebanoni (mafumu a Ahiti, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi, ndi Ayebusi),
And it came to pass, when all the kings who were on this side Jordan, in the hills, and in the valleys, and in all the coasts of the great sea opposite Lebanon, the Hittite, and the Amorite, the Canaanite, the Perizzite, the Hivite, and the Jebusite, heard these things;
2 anapangana kuti achite nkhondo ndi Yoswa ndi Israeli.
That they gathered themselves together, to fight with Joshua and with Israel, with one accord.
3 Koma Ahivi ena a ku Gibiyoni atamva zomwe Yoswa anachitira mizinda ya Yeriko ndi Ai,
And when the inhabitants of Gibeon heard what Joshua had done to Jericho and to Ai,
4 anaganiza zochita zachinyengo. Anapita nasenzetsa abulu awo chakudya mʼmatumba akalekale ndiponso matumba a vinyo achikopa ongʼambikangʼambika.
They also worked deceitfully, and went and made as if they had been ambassadors, and took old sacks upon their donkeys, and wine bottles, old, and torn, and bound up;
5 Anthuwa anavala nsapato zakutha ndi zazigamba ndiponso anavala sanza. Buledi wawo yense anali wowuma ndi wowola.
And old and patched shoes upon their feet, and old garments upon them; and all the bread of their provision was dry and mouldy.
6 Ndipo anapita kwa Yoswa ku msasa ku Giligala ndikumuwuza kuti, pamodzi ndi Aisraeli onse, “Ife tachokera ku dziko lakutali, ndipo tikufuna kuti muchite mgwirizano ndi ife.”
And they went to Joshua to the camp at Gilgal, and said to him, and to the men of Israel, We have come from a far country: now therefore make ye a league with us.
7 Koma Aisraeli anayankha Ahiviwo kuti, “Mwinatu inu mukukhala pafupi ndi ife. Tsono ife tingachite bwanji mgwirizano ndi inu?”
And the men of Israel said to the Hivites, Perhaps ye dwell among us; and how shall we make a league with you?
8 Iwo anati kwa Yoswa, “Ife ndife akapolo anu.” Tsono Yoswa anawafunsa kuti, “Inu ndinu yani ndipo mukuchokera kuti?”
And they said to Joshua, We are thy servants. And Joshua said to them, Who are ye? and where did you come from?
9 Iwo anayankha kuti, “Akapolo anufe tachokera ku dziko lakutali chifukwa tamva za Yehova Mulungu wanu. Tamva mbiri yonse ya zimene Iye anachita ku Igupto,
And they said to him, From a very far country thy servants have come because of the name of the LORD thy God: for we have heard the fame of him, and all that he did in Egypt,
10 ndi zonse zimene anachita kwa mafumu awiri a Aamori kummawa kwa Yorodani, mfumu Sihoni ya Hesiboni ndi Ogi mfumu ya Basani amene amalamulira ku Asiteroti.
And all that he did to the two kings of the Amorites, that were beyond Jordan, to Sihon king of Heshbon, and to Og king of Bashan, who was at Ashtaroth.
11 Tsono akuluakulu athu ndi onse amene akukhala mʼdziko lathu anati kwa ife. Tengani chakudya cha pa ulendo wanu. Pitani mukakumane nawo ndipo mukati kwa iwo, ‘Ife ndife akapolo anu, ndipo tikufuna kuti mugwirizane nafe za mtendere.’”
Therefore our elders and all the inhabitants of our country spoke to us, saying, Take provisions with you for the journey, and go to meet them, and say to them, We are your servants: therefore now make ye a league with us.
12 Buledi wathuyu anali wotentha pamene timanyamuka ku mudzi kubwera kwa inu. Koma tsopano taonani ali gwaa ndiponso wawola.
This our bread we took hot for our provision out of our houses on the day we came forth to go to you; but now, behold, it is dry, and it is mouldy:
13 Zikopa zimene tinathiramo vinyozi zinali zatsopano, koma taonani zathetheka. Zovala zathu ndi nsapato zathu zatha chifukwa cha kutalika kwa ulendo.
And these bottles of wine, which we filled, were new; and, behold, they are torn: and these our garments and our shoes are become old by reason of the very long journey.
14 Aisraeli anatengako chakudya chawo koma sanafunse kwa Yehova.
And the men took of their provisions, and asked not counsel at the mouth of the LORD.
15 Choncho Yoswa anapangana nawo za mtendere kuti sadzawapha, ndipo atsogoleri a gulu anavomereza pochita lumbiro.
And Joshua made peace with them, and made a league with them, to let them live: and the princes of the congregation swore to them.
16 Patatha masiku atatu atachita mgwirizano wa mtendere ndi Agibiyoni, Aisraeli anamva kuti anali anansi awo, anthu amene amakhala nawo pafupi.
And it came to pass at the end of three days after they had made a league with them, that they heard that they were their neighbours, and that they dwelt among them.
17 Tsono Aisraeli ananyamuka ulendo ndipo tsiku lachitatu anafika ku mizinda ya Gibiyoni, Kefira, Beeroti ndi Kiriati-Yearimu.
And the children of Israel journeyed, and came to their cities on the third day. Now their cities were Gibeon, and Chephirah, and Beeroth, and Kirjathjearim.
18 Koma Aisraeli sanawaphe anthuwo chifukwa atsogoleri awo anali atalonjeza mʼdzina la Yehova Mulungu wa Israeli za Agibiyoniwo. Koma anthu onse anatsutsana ndi atsogoleriwo.
And the children of Israel smote them not, because the princes of the congregation had sworn to them by the LORD God of Israel. And all the congregation murmured against the princes.
19 Koma atsogoleriwo anayankha kuti, “Ife tinawalonjeza mʼdzina la Yehova, Mulungu wa Israeli, ndipo tsopano sitingawaphe.
But all the princes said to all the congregation, We have sworn to them by the LORD God of Israel: now therefore we may not touch them.
20 Chimene tidzachita nawo ndi ichi: Tidzawasiya akhale ndi moyo kuti mkwiyo wa Yehova usatigwere chifukwa chophwanya lonjezo limene tinawalonjeza.”
This we will do to them; we will even let them live, lest wrath be upon us, because of the oath which we swore to them.
21 Anapitiriza kunena kuti “Asiyeni akhale ndi moyo, komabe akhale otidulira mitengo ndi kutitungira madzi ogwiritsa ntchito pa chipembedzo.” Lonjezo la atsogoleriwo linasungidwa.
And the princes said to them, Let them live; but let them be hewers of wood and drawers of water to all the congregation; as the princes had promised them.
22 Kenaka Yoswa anayitanitsa Agibiyoni aja nawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani inu munatinyenga ponena kuti mumachokera kutali pamene zoona zake nʼzoti mumakhala pafupi pomwe pano?
And Joshua called for them, and he spoke to them, saying, Why have ye deceived us, saying, We are very far from you; when ye dwell among us?
23 Tsopano popeza mwachita izi, Mulungu wakutembererani ndipo palibe wina mwa inu amene akhale mfulu. Nthawi zonse inu muzidzatidulira nkhuni ndi kutitungira madzi ku Nyumba ya Yehova.”
Now therefore ye are cursed, and there shall none of you be freed from being slaves, and hewers of wood and drawers of water for the house of my God.
24 Iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife akapolo anufe tinachita zimenezi chifukwa tinamva bwino lomwe kuti Yehova Mulungu wanu analamula Mose mtumiki wake kuti adzakupatsani dziko lonseli ndi kuti anthu onse okhalamo adzaphedwe. Tsono ife tinachita mantha aakulu ndipo tinachita zimenezi pofuna kupulumutsa miyoyo yathu.
And they answered Joshua, and said, Because it was certainly told thy servants, how the LORD thy God commanded his servant Moses to give you all the land, and to destroy all the inhabitants of the land from before you, therefore we were greatly afraid for our lives because of you, and have done this thing.
25 Tsopanotu ife tili mʼmanja mwanu, ndipo inu chitani nafe monga kukukomerani.”
And now, behold, we are in thy hand: do as it seemeth good and right to thee to do to us.
26 Tsono Yoswa anawapulumutsa mʼmanja mwa Aisraeli ndipo sanawaphe.
And so did he to them, and delivered them out of the hand of the children of Israel, that they slew them not.
27 Kuyambira tsiku limenelo Agibiyoni aja anasanduka odula nkhuni zaguwa lansembe la Yehova ndiponso otunga madzi. Mpaka lero lino iwo akuchitabe zimenezi kulikonse kumene Yehova anasankha.
And Joshua made them that day hewers of wood and drawers of water for the congregation, and for the altar of the LORD, even to this day, in the place which he should choose.

< Yoswa 9 >