< Yoswa 9 >
1 Mafumu onse okhala kumadzulo kwa Yorodani atamva zimenezi pamodzi ndi mafumu okhala ku mayiko a ku mapiri, mu zigwa, mʼmbali mwa Nyanja yayikulu mpaka ku Lebanoni (mafumu a Ahiti, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi, ndi Ayebusi),
Yodane Hano eso dabe la: idi hina bagade dunu huluane da Isala: ili dunu ilia gasa bagade hasalasu hou nabi dagoi. Amo hou ilia da goumi soge ganodini, umi soge Medidela: inia Wayabo Bagade bega: amola soge gano asili Lebanone sogega doaga: i, amo esalebe dunu huluane da Isala: ili dunu ilia hou nabi. Amo hina bagade dunu ilia fi da Hidaide, A:moulaide, Ga: ina: naide, Belesaide, Haifaide amola Yebiusaide.
2 anapangana kuti achite nkhondo ndi Yoswa ndi Israeli.
Amo hina bagade dunu da gilisili, Yosiua amola Isala: ili dunu ilima gegemusa: gilisi.
3 Koma Ahivi ena a ku Gibiyoni atamva zomwe Yoswa anachitira mizinda ya Yeriko ndi Ai,
Be Gibionaide dunu (ilia da Haifaide fi dunu) ilia da Yosiua ea hou amo Yeligou amola A: iai amoma hamoi nababeba: le,
4 anaganiza zochita zachinyengo. Anapita nasenzetsa abulu awo chakudya mʼmatumba akalekale ndiponso matumba a vinyo achikopa ongʼambikangʼambika.
ilia da Yosiuama ogogomusa: dawa: i galu. Ilia da ha: i manu lale, ilia dougi da: iya esa wadela: lesi dagoi amola waini gadofo gadelale nodomei ligisi.
5 Anthuwa anavala nsapato zakutha ndi zazigamba ndiponso anavala sanza. Buledi wawo yense anali wowuma ndi wowola.
Ilia da abula wadela: i amola hea emo salasu wadela: iba: le nodomei gasisali.
6 Ndipo anapita kwa Yoswa ku msasa ku Giligala ndikumuwuza kuti, pamodzi ndi Aisraeli onse, “Ife tachokera ku dziko lakutali, ndipo tikufuna kuti muchite mgwirizano ndi ife.”
Amalalu, ilia da Isala: ili abula diasu gilisisu Giliga: le amoga gala amoga asili, Yosiua amola Isala: ili dunu ilima amane sia: i, “Ninia da soge sedagaga misi. Ninia da dilima gousa: su hamomu galebe.”
7 Koma Aisraeli anayankha Ahiviwo kuti, “Mwinatu inu mukukhala pafupi ndi ife. Tsono ife tingachite bwanji mgwirizano ndi inu?”
Be Isala: ili dunu da amane sia: i, “Ninia da dilima gousa: su abuliga hamoma: bela: ? Amabela: ? Dilia da gadenene esalabala?”
8 Iwo anati kwa Yoswa, “Ife ndife akapolo anu.” Tsono Yoswa anawafunsa kuti, “Inu ndinu yani ndipo mukuchokera kuti?”
Ilia da Yosiuama amane sia: i, “Ninia da dia hawa: hamosu dunu esala.” Yosiua da ilima amane adole ba: i, “Dilia da nowala: ? Dilia da habidili misibala: ?”
9 Iwo anayankha kuti, “Akapolo anufe tachokera ku dziko lakutali chifukwa tamva za Yehova Mulungu wanu. Tamva mbiri yonse ya zimene Iye anachita ku Igupto,
Amalalu, ilia da amo sia: ema olelei, “Ninia da dilia Hina Gode Ea hou nababeba: le, soge sedade amoga misi dagoi. Ninia da Ea hou Idibidi soge ganodini hamoi,
10 ndi zonse zimene anachita kwa mafumu awiri a Aamori kummawa kwa Yorodani, mfumu Sihoni ya Hesiboni ndi Ogi mfumu ya Basani amene amalamulira ku Asiteroti.
amola E da A: moulaide hina bagade aduna Yodane Hano eso mabadi la: idiga esalu (amo da Hesiabone hina bagade amo ea dio Saihone amola Ba: isia: ne hina bagade Asiadalode moilai bai bagadega esalu amo ea dio Oge) Hina Gode da elama hamoi, amo ninia nabi.
11 Tsono akuluakulu athu ndi onse amene akukhala mʼdziko lathu anati kwa ife. Tengani chakudya cha pa ulendo wanu. Pitani mukakumane nawo ndipo mukati kwa iwo, ‘Ife ndife akapolo anu, ndipo tikufuna kuti mugwirizane nafe za mtendere.’”
Ninia ouligisu dunu amola fi dunu huluane ninia soge ganodini esala da nini ha: i manu momagele, dima gousa: musa: masa: ne sia: i. Ilia da nini da dima hawa: hamomusa: sia: ne, dilima gousa: su hamoma: ne sia: i.
12 Buledi wathuyu anali wotentha pamene timanyamuka ku mudzi kubwera kwa inu. Koma tsopano taonani ali gwaa ndiponso wawola.
Ninia agi ga: gi ba: ma! Ninia da dilima gousa: musa: nini soge fisili, amo agi ga: gi da gugumi ba: i. Ba: ma! Wali amo da hafoga: i amola moloba: fi dagoi.
13 Zikopa zimene tinathiramo vinyozi zinali zatsopano, koma taonani zathetheka. Zovala zathu ndi nsapato zathu zatha chifukwa cha kutalika kwa ulendo.
Ninia da waini amo waini gadofo ganodini sogasalaloba, waini gadofo da gaheabolo ba: i. Be wali ilia da gadelai. Ninia sedagaga misiba: le ninia abula amola emo salasu da hea hamoi dagoi.”
14 Aisraeli anatengako chakudya chawo koma sanafunse kwa Yehova.
Isala: ili dunu da ilima ha: i manu lai, be ilia hou dawa: ma: ne Hina Godema hame adole ba: i.
15 Choncho Yoswa anapangana nawo za mtendere kuti sadzawapha, ndipo atsogoleri a gulu anavomereza pochita lumbiro.
Yosiua da hahawane gousa: su ilima hamoi amola amo dunu hame medole legei. Isala: ili ouligisu dunu da dafawane amo gousa: su hame fisima: ne ilegele sia: i.
16 Patatha masiku atatu atachita mgwirizano wa mtendere ndi Agibiyoni, Aisraeli anamva kuti anali anansi awo, anthu amene amakhala nawo pafupi.
Be eso udiana asili, Isala: ili dunu da Gibionaide dunu da gadenene fi amo nabi dagoi.
17 Tsono Aisraeli ananyamuka ulendo ndipo tsiku lachitatu anafika ku mizinda ya Gibiyoni, Kefira, Beeroti ndi Kiriati-Yearimu.
Amaiba: le, Isala: ili dunu da asili, eso udiana asili ilia esalebe moilale bai bagadega doaga: i. Amo moilale gagai bai bagade ilia dio da Gibione, Gifaila, Bialode amola Gilia: de Yialimi.
18 Koma Aisraeli sanawaphe anthuwo chifukwa atsogoleri awo anali atalonjeza mʼdzina la Yehova Mulungu wa Israeli za Agibiyoniwo. Koma anthu onse anatsutsana ndi atsogoleriwo.
Be Isala: ili ouligisu dunu da Hina Gode Ea Dioba: le amo dunu hame medomu ilegele sia: i dagoiba: le, ilia da amo dunu medole legemu hamedei ba: i. Isala: ili dunu huluane da ilia ouligisu dunuma sia: ga gegei.
19 Koma atsogoleriwo anayankha kuti, “Ife tinawalonjeza mʼdzina la Yehova, Mulungu wa Israeli, ndipo tsopano sitingawaphe.
Be Isala: ili ouligisu dunu da bu adole i, “Ninia da Isala: ili Hina Gode Ea Dioba: le amo dunuma sia: i dagoiba: le, ninia da ilima se imunu hamedei.
20 Chimene tidzachita nawo ndi ichi: Tidzawasiya akhale ndi moyo kuti mkwiyo wa Yehova usatigwere chifukwa chophwanya lonjezo limene tinawalonjeza.”
Ninia sia: i dagoiba: le, amo dunu hame medole legemu. Amai hame galea, Gode da ninima se imunu.
21 Anapitiriza kunena kuti “Asiyeni akhale ndi moyo, komabe akhale otidulira mitengo ndi kutitungira madzi ogwiritsa ntchito pa chipembedzo.” Lonjezo la atsogoleriwo linasungidwa.
Ilia da esalumu da defea. Be ilia da ninia lalu habei amola hano nasu gaguli misunu.”
22 Kenaka Yoswa anayitanitsa Agibiyoni aja nawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani inu munatinyenga ponena kuti mumachokera kutali pamene zoona zake nʼzoti mumakhala pafupi pomwe pano?
Yosiua da Isala: ili dunuma ilia da Gibionaide dunu ema oule misa: ne sia: i. E da ilima amane adole ba: i, “Dilia da abuliba: le ninima ogogobela: ? Dilia gadenene esalebeba: le, abuliba: le sedagaga esala sia: bela: ?
23 Tsopano popeza mwachita izi, Mulungu wakutembererani ndipo palibe wina mwa inu amene akhale mfulu. Nthawi zonse inu muzidzatidulira nkhuni ndi kutitungira madzi ku Nyumba ya Yehova.”
Dilia da agoane hamoiba: le, Gode da dilima ougi, se imunu. Dilia fi da mae fisili, eso huluane udigili hawa: hamosu dunu esalumu. Dilia da na Gode Ea modale ligiagai diasuga lalu habele amola hano dili gaguli misunu.
24 Iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife akapolo anufe tinachita zimenezi chifukwa tinamva bwino lomwe kuti Yehova Mulungu wanu analamula Mose mtumiki wake kuti adzakupatsani dziko lonseli ndi kuti anthu onse okhalamo adzaphedwe. Tsono ife tinachita mantha aakulu ndipo tinachita zimenezi pofuna kupulumutsa miyoyo yathu.
Ilia da bu adole i, “Ninia da sia: amo dilia Hina Gode da Ea hawa: hamosu dunu Mousese ema soge huluane lama amola amo ganodini fi dunu huluane medole legema sia: i dagoi, amo nababeba: le ninia da agoane hamoi. Ninia da dilima bagade beda: iba: le amola nini da bogosa: besa: le amo ogogosu hamoi.
25 Tsopanotu ife tili mʼmanja mwanu, ndipo inu chitani nafe monga kukukomerani.”
Be wali ninia da dia lobo ganodini gagui gala. Dia asigi dawa: su defele ninima hamoma.”
26 Tsono Yoswa anawapulumutsa mʼmanja mwa Aisraeli ndipo sanawaphe.
Amaiba: le Yosiua da agoane hamoi. E da Gibionaide dunu gaga: i amola Isala: ili dunuma amo mae medoma: ne sia: i.
27 Kuyambira tsiku limenelo Agibiyoni aja anasanduka odula nkhuni zaguwa lansembe la Yehova ndiponso otunga madzi. Mpaka lero lino iwo akuchitabe zimenezi kulikonse kumene Yehova anasankha.
Be e da ili da udigili hawa: hamoma: ne sia: i. Ilia da Isala: ili dunuma amola Hina Gode Ea oloda amoga lalu habele, amola hano dili gaguli misi. Amola mae fisili hamonanu, ilia da wali eso amola Hina Godema nodomusa: sogebi E da ilegei, amoga ilia da amo udigili hawa: hamonana.