< Yoswa 8 >
1 Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, “Usachite mantha kapena kutaya mtima. Tenga gulu lonse la nkhondo, ndipo upite ku Ai. Taona, ndapereka mfumu ya Ai pamodzi ndi anthu ake, mzinda wake ndi dziko lake lonse mʼmanja mwako.
UThixo wathi kuJoshuwa, “Ungesabi, ungalahli ithemba. Thatha ibutho lonke uhambe uyehlasela i-Ayi, ngoba senginikele inkosi yase-Ayi, abantu bayo, idolobho layo lelizwe layo ezandleni zakho.
2 Mzinda wa Ai ndi mfumu yake muchite monga munachita ndi mzinda wa Yeriko ndi mfumu yake, koma katundu wa mumzindamo ndi zoweta mukazitenge ndi kuzisunga kuti zikhale zanu. Mukalalire mzinda wa Ai ndi kuwuthira nkhondo kuchokera kumbuyo.”
Khonale uzakwenza owakwenza eJerikho lenkosini yakhona, kodwa lingazithathela impahla zonke eliyabe lizithumbile lezifuyo kube ngokwenu. Cathamani ngemva kwedolobho.”
3 Kotero Yoswa ndi gulu lonse la nkhondo anakonzeka kupita ku Ai. Iye anasankha amuna 30,000 odziwa kumenya nkhondo bwino ndipo anawatumiza usiku
Ngakho uJoshuwa lebutho lonke baphuma bayahlasela i-Ayi. Wakhetha amabutho azinkulungwane ezingamatshumi amathathu ayezingcitshi ukwedlula amanye ekulweni, wasewathuma ebusuku.
4 nawapatsa malamulo awa kuti, “Mvetsani bwino; mukabisale kuseri kwa mzindawo. Musakapite patali ndi mzindawo, koma nonsenu mukakhale okonzekera nkhondo.
Wawalaya wathi, “Lalelisisani, kumele licathame ngemva kwedolobho. Lingaze laya khatshana lalo. Lonke kumele lihlale liqaphele.
5 Ine ndi gulu langa lonse tikayamba kuwuputa mzindawu, ndipo akadzangotuluka kudzalimbana nafe, ife tidzawathawa monga tinachitira poyamba.
Mina lalabo engizabe ngilabo sizaqhubeka siqonde edolobheni, kuthi nxa amadoda ephuma ukusihlasela njengalokho akwenza kuqala, sizawabalekela.
6 Iwo adzatithamangitsa mpaka titawakokera kutali ndi mzindawo, pakuti iwo adzati, ‘Akutithawa monga anachitira poyamba.’ Pamene ife tizidzathawa,
Bazaxotshana lathi size sibahugele khatshana ledolobho, ngoba bazakuthi, ‘Bayasibalekela njengalokhu abakwenza kuqala.’ Ngakho nxa sesibabalekela,
7 inu mudzatuluke pamene mwabisalapo ndi kulanda mzindawo. Yehova Mulungu wanu adzakupatsani mzindawo.
lina lizavuka lapho eliyabe licathame khona beselithumba idolobho. UThixo uNkulunkulu wenu uzalinikela ezandleni zenu.
8 Mukakawulanda mzindawo mudzawuyatse moto. Mukachite monga mwa mawu a Yehova. Amenewa ndiwo malamulo amene ndakupatsani.”
Nxa selilithumbile idolobho, lithungeleni ngomlilo. Yenzani lokho okulaywe nguThixo. Wobani leqiniso lokuthi lilandela iziqondiso zami.”
9 Yoswa atawatumiza, anapita ku malo wokabisalakowo ndipo anadikirira kumeneko. Malowa anali pakati pa Beteli ndi Ai, kumadzulo kwa Ai. Koma Yoswa anagona usiku umenewu pakati pa gulu lake lankhondo.
UJoshuwa wasebalaya ukuthi bahambe, basebesiya endaweni okwakumele bacathame kuyo phakathi kweBhetheli le-Ayi, entshonalanga ye-Ayi kodwa uJoshuwa waqeda ubusuku lobo elabantu.
10 Mmawa mwake, Yoswa anadzuka nayitana asilikali ake. Tsono iye pamodzi ndi akuluakulu a Aisraeli anatsogola kupita ku Ai.
Ekuseni ngelanga elilandelayo uJoshuwa waqoqa amabutho akhe, kwathi yena labadala bako-Israyeli bahamba phambi kwabo besiya e-Ayi.
11 Gulu lonse la nkhondo limene linali ndi iye linatsogolako ndi kukamanga zithando pafupi ndi mzindawo chakumpoto mopenyana nawo. Pakati pa iwo ndi mzindawo panali chigwa.
Iviyo lonke lalabo ayelabo lahamba laya edolobheni lafika lema phambi kwabo. Bamisa izihonqo enyakatho ye-Ayi, isigodi siphakathi kwabo ledolobho.
12 Yoswa anali atatenga asilikali 5,000 ndi kuwabisa pakati pa Ai ndi Beteli, kumadzulo kwa mzindawo.
UJoshuwa wayethethe amadoda aphosa afike kunkulungwane ezinhlanu wawacathamisa phakathi kweBhetheli le-Ayi entshonalanga yedolobho.
13 Anakhazika anthuwo mokonzekera nkhondo. Gulu lalikulu la nkhondo linakamanga zithando zawo kumpoto kwa mzinda, ndipo gulu lina linakamanga zithando zawo kumadzulo kwa mzindawo. Usiku umenewo Yoswa anakagona ku chigwa.
Benza ukuthi amabutho aye ezikhundleni zawo zonke ezaziphakathi kwezihonqo enyakatho yedolobho lendaweni yokucathamela eyayisentshonalanga yalo. Ngalobobusuku uJoshuwa waya esigodini.
14 Mfumu ya Ai itaona ankhondo a Yoswa, inachita zinthu mofulumira. Inadzuka mmamawa ndipo inapita pamodzi ndi anthu ake ku malo otsika oyangʼanana ndi Araba kuti akachite nkhondo ndi Aisraeli. Koma iyo sinadziwe kuti ayithira nkhondo kudzera kumbuyo kwa mzindawo.
Inkosi yase-Ayi yathi ibona lokhu yona lawo wonke amadoda akulelodolobho aphanga aphuma kusesele ekuseni ukuze ayehlangana lo-Israyeli empini kweyinye indawo ekhangelane le-Arabha. Kodwa yayingazi ukuthi kwakulamabutho ayeyicathamele ngemva kwedolobho.
15 Yoswa ndi Aisraeli onse anachita ngati agonja ndi kumathawira ku chipululu.
UJoshuwa labantu bonke bako-Israyeli bathambela ukubuyiselwa emuva, babalekela enkangala.
16 Anthu onse a ku Ai anawuzidwa kuti awapirikitse. Ndipo iwo anapirikitsadi Yoswa uja, ndi kupita kutali ndi mzinda wawo.
Wonke amadoda e-Ayi atshelwa ukuthi abaxotshe, basebexotshana loJoshuwa badonselwa khatshana ledolobho.
17 Palibe munthu wamwamuna wa mzinda wa Ai kapena wa Beteli amene sanatuluke kukapirikitsa Aisraeli. Iwo anasiya mzinda wosatseka ndi kumapirikitsa Aisraeli.
Kakukho lendoda eyodwa eyasala e-Ayi kumbe eBhetheli engazanga ixotshane labako-Israyeli.
18 Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, “Loza mkondo uli mʼdzanja lako ku Ai pakuti ine ndipereka mʼdzanja lanu mzindawo.” Kotero Yoswa analoza mkondowo ku Ai.
UThixo wasesithi kuJoshuwa, “Phakamisa umkhonto osesandleni ukhombe e-Ayi, ngenxa yokuthi idolobho leli ngizalinikela ezandleni zakho.” Ngakho uJoshuwa wakhombela e-Ayi ngomkhonto wakhe.
19 Atangotambalitsa dzanja lake, anthu amene anabisala aja ananyamuka msangamsanga pamalo pawo ndi kuthamangira kutsogolo. Iwo analowa mu mzindamo ndi kuwulanda ndipo anawutentha mofulumira.
Wathi esanda kwenza lokhu, amadoda ayecathamele ukuhlasela aphakama masinyane ezindaweni ayekuzo agijimela phambili. Angena edolobheni alithumba, aphanga alithungela ngomlilo.
20 Anthu a ku Ai aja atangochewukira mʼmbuyo anaona utsi uli tolotolo. Koma mpata woti athawireko panalibe pakuti Aisraeli amene amathawira ku chipululu anabwerera nayamba kuwathamangitsa.
Amadoda e-Ayi anyemukula abona intuthu eyayisuka edolobheni iqonga emayezini kodwa aswela ukuthi azabalekela ngaphi ngoba abako-Israyeli ababebalekele enkangala basebephendukele labo ababebaxotsha.
21 Yoswa ndi Aisraeli onse ataona kuti obisalira aja alanda mzinda ndipo kuti utsi unali tolotolo, iwo anatembenuka ndi kuyamba kupha anthu a ku Ai.
Kwathi uJoshuwa labako-Israyeli bonke bebona ukuthi labo ababecatheme basebethumbe idolobho lokuthi intuthu yayiqonga emayezini ivela edolobheni, batshibilika baqalisa ukuhlasela amadoda ase-Ayi.
22 Nawonso Aisraeli amene anali mu mzindamo anatuluka kudzalimbana ndi anthu a ku Ai. Choncho iwo anazingidwa mbali zonse ndi Aisraeli ndipo onse anaphedwa. Palibe amene anatsala wamoyo kapena wothawa
Amadoda ayecatheme lawo aphuma edolobheni abahlasela, okwenza ukuthi babe phakathi laphakathi, inxa zombili zilabako-Israyeli. Abako-Israyeli babatshaya bababhuqa akwaze kwasala muntu owaphunyukayo.
23 kupatula mfumu ya ku Ai yokha imene anayigwira nabwera nayo kwa Yoswa.
Kodwa bathatha inkosi yase-Ayi iphila basebeyiletha kuJoshuwa.
24 Aisraeli aja atatha kupha anthu onse a ku Ai amene anali mʼthengo ndi mʼchipululu kumene anawapirikitsira, onse anabwerera ku Ai ndi kupha onse amene anali mu mzindamo.
Kwathi abako-Israyeli sebeqedile ukubulala wonke amadoda ase-Ayi emagcekeni enkangala lapho ababewaxotshele khona, njalo wonke esegwazwe ngenkemba, bonke abako-Israyeli babuyela e-Ayi babulala abantu bonke abakulelo dolobho.
25 Chiwerengero cha anthu onse a ku Ai, amuna ndi akazi, amene anaphedwa pa tsiku limeneli chinali 12,000.
Amadoda labesifazane abazinkulungwane ezilitshumi lambili bafa ngalelolanga, bonke kungabantu be-Ayi,
26 Yoswa sanatsitse dzanja lake limene ananyamula mkondo mpaka ataona kuti onse amene amakhala mu mzinda wa Ai aphedwa.
ngoba uJoshuwa kazange ehlise isandla sakhe esiphethe umkhonto ngawo baze babhujiswa bonke abantu ababehlala e-Ayi.
27 Tsono Aisraeli anatenga zoweta ndi katundu yense wa anthu ophedwa aja, monga momwe Yehova analamulira Yoswa.
Kodwa abako-Israyeli bathatha zonke izifuyo lempango yonke eyayithunjwe kulelodolobho njengokulaywa kukaJoshuwa nguThixo.
28 Pambuyo pake Yoswa anawutentha mzinda wa Ai ndi kuwusiya bwinja monga ulili leromu.
UJoshuwa watshisa i-Ayi wayenza yaba lunxiwa oluyinqwaba, indawo engelakuhlalwa muntu kuze kube lamhlanje.
29 Iye anapachika pa mtengo mfumu ya Ai ndipo anayisiya mpaka madzulo. Pomwe dzuwa linalowa Yoswa analamula kuti akachotse mtembowo ndi kukawutaya ku chipata cha mzindawo. Pamwamba pa mtembowo anawunjikapo mulu waukulu wa miyala. Muluwo ulipobe mpaka lero lino.
Walengisa inkosi yase-Ayi esigodweni wayitshiya kwaze kwaba ntambama. Ekutshoneni kwelanga uJoshuwa walaya ukuthi bethule isidumbu sayo basiphosele esangweni ledolobho. Babuthelela inqumbi yamatshe phezu kwaso, njalo lokhu kunjalo kuze kube lamhlanje.
30 Ndipo Yoswa anamanga guwa lansembe la Yehova Mulungu wa Israeli pa phiri la Ebala.
UJoshuwa wasesakhela uThixo, uNkulunkulu wako-Israyeli i-alithari e-Ebhali.
31 Analimanga motsata zimene Mose mtumiki wa Yehova analamulira Aisraeli, ndiponso potsata zomwe zinalembedwa mʼbuku la malamulo a Mose kuti guwa lansembe likhale la miyala yosasemedwa ndi chitsulo. Pa guwalo anapereka kwa Yehova nsembe yopsereza ndi nsembe yachiyanjano.
Njengokulaya okwenziwa nguMosi inceku kaThixo kwabako-Israyeli, walakha njengokulaywa okulotshwe eNcwadini yoMthetho kaMosi i-alithari lamatshe angabazwanga, okungazanga kusetshenziswe nsimbi phezu kwawo. Kulo banikela kuThixo iminikelo yokutshiswa leminikelo yokuthula.
32 Kenaka anthu onse akupenya, Yoswa analemba pa miyala chitsanzo cha malamulo amene Mose analemba.
Lapho, phambi kwabako-Israyeli uJoshuwa waloba ematsheni umthetho kaMosi ayewubhalile.
33 Aisraeli onse, akuluakulu awo, atsogoleri awo ndi oweruza awo, alendo pamodzi ndi mbadwa, anayimirira mbali zonse ziwiri za Bokosi la Chipangano la Yehova, ena uku ena uku moyangʼanana ndi ansembe a Chilevi. Theka la anthu linayima patsogolo pa phiri la Gerizimu ndipo theka lina patsogolo pa phiri la Ebala, monga momwe Mose mtumiki wa Yehova anawalamulira mʼmbuyomo pamene anawapatsa malangizo podalitsa Aisraeli.
Bonke abako-Israyeli, abezizweni labayinzalo yalelolizwe, labadala babo, iziphathamandla labahluleli babemi emaceleni womabili omtshokotsho wesivumelwano sikaThixo bekhangelane lalabo ababelithwele, abaphristi, ababengabaLevi. Ingxenye yabantu yema phambi kwentaba yeGerizimu kwathi eyinye ingxenye yema phambi kwentaba ye-Ebhali, njengokulaya kukaMosi inceku kaThixo owayelaye ukuthi kubusiswe abantu bako-Israyeli.
34 Pambuyo pake Yoswa anawerenga mawu onse a malamulo, madalitso ndi matemberero monga momwe zinalembedwera mʼbuku la malamulo a Mose.
Emva kwalokho uJoshuwa wafunda wonke amazwi omthetho, izibusiso leziqalekiso, njengokulotshwa okwenziwe eNcwadini yeMithetho.
35 Yoswa anawerenga mawu onse amene Mose analamula, gulu lonse la Israeli limene linasonkhana likumva. Amayi, ana ndi alendo omwe okhala pakati pawo anali pomwepo.
Kakulalizwi elalaywa nguMosi elingazanga lifundwe nguJoshuwa phambi kombuthano wonke wako-Israyeli kugoqela abesifazane labantwana labezizweni ababehlala phakathi kwabo.