< Yoswa 8 >

1 Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, “Usachite mantha kapena kutaya mtima. Tenga gulu lonse la nkhondo, ndipo upite ku Ai. Taona, ndapereka mfumu ya Ai pamodzi ndi anthu ake, mzinda wake ndi dziko lake lonse mʼmanja mwako.
Ll’Eternel dit alors à Josué: "Sois sans crainte ni faiblesse! Prends avec toi toute la partie guerrière du peuple, et marche droit sur Aï. Vois, je livre en ton pouvoir le roi d’Aï et son peuple, et sa ville et son territoire.
2 Mzinda wa Ai ndi mfumu yake muchite monga munachita ndi mzinda wa Yeriko ndi mfumu yake, koma katundu wa mumzindamo ndi zoweta mukazitenge ndi kuzisunga kuti zikhale zanu. Mukalalire mzinda wa Ai ndi kuwuthira nkhondo kuchokera kumbuyo.”
Tu traiteras Aï et son roi comme tu as traité Jéricho et le sien; toutefois, vous pouvez capturer à votre profit les dépouilles et le bétail. Etablis une embuscade en arrière de la ville."
3 Kotero Yoswa ndi gulu lonse la nkhondo anakonzeka kupita ku Ai. Iye anasankha amuna 30,000 odziwa kumenya nkhondo bwino ndipo anawatumiza usiku
Josué se disposa à marcher sur Aï avec tous les gens de guerre. Il choisit d’abord trente mille hommes, soldats d’élite, qu’il fit partir la nuit,
4 nawapatsa malamulo awa kuti, “Mvetsani bwino; mukabisale kuseri kwa mzindawo. Musakapite patali ndi mzindawo, koma nonsenu mukakhale okonzekera nkhondo.
en leur donnant cet ordre: "Ecoutez: vous allez vous mettre en embuscade derrière la ville, pas trop loin des murs, afin d’être à portée d’agir.
5 Ine ndi gulu langa lonse tikayamba kuwuputa mzindawu, ndipo akadzangotuluka kudzalimbana nafe, ife tidzawathawa monga tinachitira poyamba.
De mon côté, je m’approcherai de la ville avec tout le peuple qui est avec moi; les habitants sortiront pour nous repousser comme la première fois, et nous fuirons devant eux,
6 Iwo adzatithamangitsa mpaka titawakokera kutali ndi mzindawo, pakuti iwo adzati, ‘Akutithawa monga anachitira poyamba.’ Pamene ife tizidzathawa,
afin qu’ils nous poursuivent, jusqu’à ce que nous les ayons attirés hors de la ville; car ils se diront: "Ils fuient devant nous comme la première fois"; mais, tandis que nous fuirons devant eux,
7 inu mudzatuluke pamene mwabisalapo ndi kulanda mzindawo. Yehova Mulungu wanu adzakupatsani mzindawo.
vous, vous sortirez de votre embuscade et vous vous emparerez de la ville: l’Eternel, votre Dieu, la livrera en votre pouvoir.
8 Mukakawulanda mzindawo mudzawuyatse moto. Mukachite monga mwa mawu a Yehova. Amenewa ndiwo malamulo amene ndakupatsani.”
Quand vous serez maîtres de la ville, vous y mettrez le feu, vous conformant à l’ordre de l’Eternel. Faites attention à ce que je vous prescris."
9 Yoswa atawatumiza, anapita ku malo wokabisalakowo ndipo anadikirira kumeneko. Malowa anali pakati pa Beteli ndi Ai, kumadzulo kwa Ai. Koma Yoswa anagona usiku umenewu pakati pa gulu lake lankhondo.
Là-dessus, Josué les fit partir, et ils allèrent se poster en embuscade entre Aï et Béthel, à l’occident d’Aï, tandis que Josué passa cette nuit au milieu de l’armée.
10 Mmawa mwake, Yoswa anadzuka nayitana asilikali ake. Tsono iye pamodzi ndi akuluakulu a Aisraeli anatsogola kupita ku Ai.
Le lendemain de bonne heure, il passa le peuple en revue, puis avec les anciens d’Israël, il marcha sur Aï à la tête du peuple.
11 Gulu lonse la nkhondo limene linali ndi iye linatsogolako ndi kukamanga zithando pafupi ndi mzindawo chakumpoto mopenyana nawo. Pakati pa iwo ndi mzindawo panali chigwa.
Toute l’armée qu’il conduisait s’avança ainsi et arriva en face de la ville; ils firent halte au nord d’Aï, dont ils étaient séparés par la vallée.
12 Yoswa anali atatenga asilikali 5,000 ndi kuwabisa pakati pa Ai ndi Beteli, kumadzulo kwa mzindawo.
Josué prit encore environ cinq mille hommes, qu’il plaça en embuscade entre Béthel et Aï, à l’ouest de cette ville.
13 Anakhazika anthuwo mokonzekera nkhondo. Gulu lalikulu la nkhondo linakamanga zithando zawo kumpoto kwa mzinda, ndipo gulu lina linakamanga zithando zawo kumadzulo kwa mzindawo. Usiku umenewo Yoswa anakagona ku chigwa.
Quand on eut ainsi posté le peuple, le gros de l’armée au nord de la ville et sa réserve à l’ouest, Josué opéra, cette nuit même, une reconnaissance dans la vallée.
14 Mfumu ya Ai itaona ankhondo a Yoswa, inachita zinthu mofulumira. Inadzuka mmamawa ndipo inapita pamodzi ndi anthu ake ku malo otsika oyangʼanana ndi Araba kuti akachite nkhondo ndi Aisraeli. Koma iyo sinadziwe kuti ayithira nkhondo kudzera kumbuyo kwa mzindawo.
Quand le roi d’Aï s’en aperçut, il fit lever en toute hâte les habitants de la ville, et ils s’avancèrent vers Israël pour livrer bataille lui et tout son peuple à l’endroit désigné, en avant de la plaine, le roi ne se doutant pas qu’une embuscade le menaçait derrière la ville.
15 Yoswa ndi Aisraeli onse anachita ngati agonja ndi kumathawira ku chipululu.
Josué et tout Israël se laissèrent mettre par eux en déroute, et s’enfuirent dans la direction du désert.
16 Anthu onse a ku Ai anawuzidwa kuti awapirikitse. Ndipo iwo anapirikitsadi Yoswa uja, ndi kupita kutali ndi mzinda wawo.
Toute la population, d’Aï se rassembla pour les poursuivre, et, en poursuivant ainsi Josué, elle s’éloigna de la ville.
17 Palibe munthu wamwamuna wa mzinda wa Ai kapena wa Beteli amene sanatuluke kukapirikitsa Aisraeli. Iwo anasiya mzinda wosatseka ndi kumapirikitsa Aisraeli.
II ne resta, dans Aï et dans Béthel, pas un homme qui ne fût sorti à la poursuite d’Israël; ils laissèrent la ville ouverte pour courir sus aux Israélites.
18 Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, “Loza mkondo uli mʼdzanja lako ku Ai pakuti ine ndipereka mʼdzanja lanu mzindawo.” Kotero Yoswa analoza mkondowo ku Ai.
Alors l’Eternel dit à Josué: "Incline vers Aï le javelot que tu as à la main, car je la livre en ton pouvoir." Et Josué inclina du côté de la ville le javelot qu’il avait à la main.
19 Atangotambalitsa dzanja lake, anthu amene anabisala aja ananyamuka msangamsanga pamalo pawo ndi kuthamangira kutsogolo. Iwo analowa mu mzindamo ndi kuwulanda ndipo anawutentha mofulumira.
Aussitôt, les hommes embusqués quittèrent leur poste, s’élancèrent au signal, entrèrent dans la ville et la prirent, puis se hâtèrent d’y mettre le feu.
20 Anthu a ku Ai aja atangochewukira mʼmbuyo anaona utsi uli tolotolo. Koma mpata woti athawireko panalibe pakuti Aisraeli amene amathawira ku chipululu anabwerera nayamba kuwathamangitsa.
Les gens d’Aï, en se retournant, virent la fumée de leur ville qui montait vers le ciel, et les bras leur tombèrent, ne pouvant fuir d’aucun côté; et le peuple qui fuyait devant eux vers le désert, fit volte-face pour arrêter leur poursuite.
21 Yoswa ndi Aisraeli onse ataona kuti obisalira aja alanda mzinda ndipo kuti utsi unali tolotolo, iwo anatembenuka ndi kuyamba kupha anthu a ku Ai.
Josué et tout Israël avaient jugé que la ville était prise, en voyant s’élever sa fumée, et ils reprenaient l’offensive contre les troupes d’Aï.
22 Nawonso Aisraeli amene anali mu mzindamo anatuluka kudzalimbana ndi anthu a ku Ai. Choncho iwo anazingidwa mbali zonse ndi Aisraeli ndipo onse anaphedwa. Palibe amene anatsala wamoyo kapena wothawa
Cependant, les autres s’élançaient contre elles, de la ville, de sorte qu’elles se trouvèrent enveloppées, devant et derrière, par les Israélites, qui les taillèrent en pièces sans en épargner un seul.
23 kupatula mfumu ya ku Ai yokha imene anayigwira nabwera nayo kwa Yoswa.
Pour le roi d’Aï, on le prit vivant et on l’amena à Josué.
24 Aisraeli aja atatha kupha anthu onse a ku Ai amene anali mʼthengo ndi mʼchipululu kumene anawapirikitsira, onse anabwerera ku Ai ndi kupha onse amene anali mu mzindamo.
Quand les Israélites eurent tué tous les habitants d’Aï dans la campagne dans le désert où ils les avaient poursuivis, et que tous, jusqu’au dernier, furent tombés sous leurs armes, tout Israël revint sur Aï et passa tout au fil de l’épée.
25 Chiwerengero cha anthu onse a ku Ai, amuna ndi akazi, amene anaphedwa pa tsiku limeneli chinali 12,000.
Le nombre de ceux qui périrent en ce jour fut de douze mille, tant hommes que femmes, toute la population d’Aï.
26 Yoswa sanatsitse dzanja lake limene ananyamula mkondo mpaka ataona kuti onse amene amakhala mu mzinda wa Ai aphedwa.
Josué n’avait pas cessé de tenir son javelot en arrêt, jusqu’à ce qu’on eût exterminé tous les habitants d’Aï.
27 Tsono Aisraeli anatenga zoweta ndi katundu yense wa anthu ophedwa aja, monga momwe Yehova analamulira Yoswa.
Toutefois, les Israélites capturèrent pour leur compte le bétail et le butin de cette ville, selon l’autorisation que l’Eternel avait donnée à Josué.
28 Pambuyo pake Yoswa anawutentha mzinda wa Ai ndi kuwusiya bwinja monga ulili leromu.
Josué livra Aï aux flammes et la condamna à une ruine et à une solitude perpétuelles, ce qu’elle est encore aujourd’hui.
29 Iye anapachika pa mtengo mfumu ya Ai ndipo anayisiya mpaka madzulo. Pomwe dzuwa linalowa Yoswa analamula kuti akachotse mtembowo ndi kukawutaya ku chipata cha mzindawo. Pamwamba pa mtembowo anawunjikapo mulu waukulu wa miyala. Muluwo ulipobe mpaka lero lino.
Et le roi d’Aï, il le fit pendre au gibet, où il resta jusqu’au soir. Au coucher du soleil, Josué donna ordre de descendre son cadavre du gibet; on le jeta aux portes de la ville et l’on posa dessus un grand amas de pierres, qui se voit encore aujourd’hui.
30 Ndipo Yoswa anamanga guwa lansembe la Yehova Mulungu wa Israeli pa phiri la Ebala.
Josué bâtit alors un autel au Seigneur, Dieu d’Israël, sur le mont Hébal,
31 Analimanga motsata zimene Mose mtumiki wa Yehova analamulira Aisraeli, ndiponso potsata zomwe zinalembedwa mʼbuku la malamulo a Mose kuti guwa lansembe likhale la miyala yosasemedwa ndi chitsulo. Pa guwalo anapereka kwa Yehova nsembe yopsereza ndi nsembe yachiyanjano.
selon ce que Moïse, serviteur de Dieu, avait prescrit aux enfants d’Israël, comme il est écrit dans la loi de Moïse: un autel de pierres brutes, que le fer n’avait jamais touchées. Et l’on y offrit des holocaustes à l’Eternel, et l’on y sacrifia des rémunératoires.
32 Kenaka anthu onse akupenya, Yoswa analemba pa miyala chitsanzo cha malamulo amene Mose analemba.
Là, on traça sur les pierres une copie de la Doctrine que Moïse avait écrite pour les enfants d’Israël.
33 Aisraeli onse, akuluakulu awo, atsogoleri awo ndi oweruza awo, alendo pamodzi ndi mbadwa, anayimirira mbali zonse ziwiri za Bokosi la Chipangano la Yehova, ena uku ena uku moyangʼanana ndi ansembe a Chilevi. Theka la anthu linayima patsogolo pa phiri la Gerizimu ndipo theka lina patsogolo pa phiri la Ebala, monga momwe Mose mtumiki wa Yehova anawalamulira mʼmbuyomo pamene anawapatsa malangizo podalitsa Aisraeli.
Puis, des deux côtés de l’arche d’alliance du Seigneur, en face des prêtres, enfants de Lévi qui la portaient, tout Israël, avec ses anciens, ses préposés et ses juges, tous, étrangers comme indigènes se rangèrent, moitié vers la montagne de Garizim, moitié vers celle d’Hébal, afin que, selon l’ordre de Moïse, serviteur de Dieu, ce fût d’abord la bénédiction qu’on prononçât sur le peuple israélite.
34 Pambuyo pake Yoswa anawerenga mawu onse a malamulo, madalitso ndi matemberero monga momwe zinalembedwera mʼbuku la malamulo a Mose.
Et ensuite, on lut toutes les paroles de la Doctrine, bénédictions et malédictions, entièrement selon la teneur du livre de la Loi.
35 Yoswa anawerenga mawu onse amene Mose analamula, gulu lonse la Israeli limene linasonkhana likumva. Amayi, ana ndi alendo omwe okhala pakati pawo anali pomwepo.
Il n’y eut pas un détail, de tout ce qu’avait ordonné Moïse, dont Josué ne fit lecture en présence de toute l’assemblée d’Israël, même des femmes et des enfants, ainsi que des étrangers qui vivaient parmi eux.

< Yoswa 8 >