< Yoswa 8 >

1 Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, “Usachite mantha kapena kutaya mtima. Tenga gulu lonse la nkhondo, ndipo upite ku Ai. Taona, ndapereka mfumu ya Ai pamodzi ndi anthu ake, mzinda wake ndi dziko lake lonse mʼmanja mwako.
And YHWH says to Joshua, “Do not fear, nor be frightened, take with you all the people of war, and rise, go up to Ai; see, I have given into your hand the king of Ai, and his people, and his city, and his land,
2 Mzinda wa Ai ndi mfumu yake muchite monga munachita ndi mzinda wa Yeriko ndi mfumu yake, koma katundu wa mumzindamo ndi zoweta mukazitenge ndi kuzisunga kuti zikhale zanu. Mukalalire mzinda wa Ai ndi kuwuthira nkhondo kuchokera kumbuyo.”
and you have done to Ai and to her king as you have done to Jericho and to her king; only spoil its spoil and its livestock for yourselves; for you set an ambush for the city at its rear.”
3 Kotero Yoswa ndi gulu lonse la nkhondo anakonzeka kupita ku Ai. Iye anasankha amuna 30,000 odziwa kumenya nkhondo bwino ndipo anawatumiza usiku
And Joshua rises, and all the people of war, to go up to Ai, and Joshua chooses thirty thousand men, mighty men of valor, and sends them away by night,
4 nawapatsa malamulo awa kuti, “Mvetsani bwino; mukabisale kuseri kwa mzindawo. Musakapite patali ndi mzindawo, koma nonsenu mukakhale okonzekera nkhondo.
and commands them, saying, “See, you are ones lying in wait against the city, at the rear of the city, you do not go very far off from the city, and all of you have been prepared,
5 Ine ndi gulu langa lonse tikayamba kuwuputa mzindawu, ndipo akadzangotuluka kudzalimbana nafe, ife tidzawathawa monga tinachitira poyamba.
and I and all the people who [are] with me draw near to the city, and it has come to pass, when they come out to meet us as at the first, and we have fled before them,
6 Iwo adzatithamangitsa mpaka titawakokera kutali ndi mzindawo, pakuti iwo adzati, ‘Akutithawa monga anachitira poyamba.’ Pamene ife tizidzathawa,
and they have come out after us until we have drawn them out of the city, for they say, They are fleeing before us as at the first, and we have fled before them,
7 inu mudzatuluke pamene mwabisalapo ndi kulanda mzindawo. Yehova Mulungu wanu adzakupatsani mzindawo.
and you rise from the ambush, and have occupied the city, and your God YHWH has given it into your hand;
8 Mukakawulanda mzindawo mudzawuyatse moto. Mukachite monga mwa mawu a Yehova. Amenewa ndiwo malamulo amene ndakupatsani.”
and it has been, when you capture the city, you burn the city with fire, you do according to the word of YHWH, see, I have commanded you.”
9 Yoswa atawatumiza, anapita ku malo wokabisalakowo ndipo anadikirira kumeneko. Malowa anali pakati pa Beteli ndi Ai, kumadzulo kwa Ai. Koma Yoswa anagona usiku umenewu pakati pa gulu lake lankhondo.
And Joshua sends them away, and they go to the ambush, and abide between Bethel and Ai, on the west of Ai; and Joshua lodges on that night in the midst of the people.
10 Mmawa mwake, Yoswa anadzuka nayitana asilikali ake. Tsono iye pamodzi ndi akuluakulu a Aisraeli anatsogola kupita ku Ai.
And Joshua rises early in the morning, and inspects the people, and goes up, he and [the] elderly of Israel, before the people to Ai;
11 Gulu lonse la nkhondo limene linali ndi iye linatsogolako ndi kukamanga zithando pafupi ndi mzindawo chakumpoto mopenyana nawo. Pakati pa iwo ndi mzindawo panali chigwa.
and all the people of war who [are] with him have gone up, and draw near and come in before the city, and encamp on the north of Ai; and the valley [is] between him and Ai.
12 Yoswa anali atatenga asilikali 5,000 ndi kuwabisa pakati pa Ai ndi Beteli, kumadzulo kwa mzindawo.
And he takes about five thousand men, and sets them [for] an ambush between Bethel and Ai, on the west of the city;
13 Anakhazika anthuwo mokonzekera nkhondo. Gulu lalikulu la nkhondo linakamanga zithando zawo kumpoto kwa mzinda, ndipo gulu lina linakamanga zithando zawo kumadzulo kwa mzindawo. Usiku umenewo Yoswa anakagona ku chigwa.
and they set the people, all the camp which [is] on the north of the city, and its rear on the west of the city, and that night Joshua goes on into the midst of the valley.
14 Mfumu ya Ai itaona ankhondo a Yoswa, inachita zinthu mofulumira. Inadzuka mmamawa ndipo inapita pamodzi ndi anthu ake ku malo otsika oyangʼanana ndi Araba kuti akachite nkhondo ndi Aisraeli. Koma iyo sinadziwe kuti ayithira nkhondo kudzera kumbuyo kwa mzindawo.
And it comes to pass, when the king of Ai sees [it], that he hurries, and rises early, and the men of the city go out to meet Israel for battle, he and all his people, at the appointed time, at the front of the plain, and he has not known that an ambush [is] against him, on the rear of the city.
15 Yoswa ndi Aisraeli onse anachita ngati agonja ndi kumathawira ku chipululu.
And Joshua and all Israel [seem] struck before them, and flee the way of the wilderness,
16 Anthu onse a ku Ai anawuzidwa kuti awapirikitse. Ndipo iwo anapirikitsadi Yoswa uja, ndi kupita kutali ndi mzinda wawo.
and all the people who [are] in the city are called to pursue after them, and they pursue after Joshua, and are drawn away out of the city,
17 Palibe munthu wamwamuna wa mzinda wa Ai kapena wa Beteli amene sanatuluke kukapirikitsa Aisraeli. Iwo anasiya mzinda wosatseka ndi kumapirikitsa Aisraeli.
and there has not been a man left in Ai and Bethel who has not gone out after Israel, and they leave the city open, and pursue after Israel.
18 Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, “Loza mkondo uli mʼdzanja lako ku Ai pakuti ine ndipereka mʼdzanja lanu mzindawo.” Kotero Yoswa analoza mkondowo ku Ai.
And YHWH says to Joshua, “Stretch out with the javelin which [is] in your hand toward Ai, for I give it into your hand”; and Joshua stretches out with the javelin which [is] in his hand toward the city,
19 Atangotambalitsa dzanja lake, anthu amene anabisala aja ananyamuka msangamsanga pamalo pawo ndi kuthamangira kutsogolo. Iwo analowa mu mzindamo ndi kuwulanda ndipo anawutentha mofulumira.
and the ambush has risen [with] haste, out of its place, and they run at the stretching out of his hand, and go into the city, and capture it, and hurry, and burn the city with fire.
20 Anthu a ku Ai aja atangochewukira mʼmbuyo anaona utsi uli tolotolo. Koma mpata woti athawireko panalibe pakuti Aisraeli amene amathawira ku chipululu anabwerera nayamba kuwathamangitsa.
And the men of Ai look behind them, and see, and behold, the smoke of the city has gone up to the heavens, and there has not been power in them to flee here and there—and the people who are fleeing to the wilderness have turned against the pursuer—
21 Yoswa ndi Aisraeli onse ataona kuti obisalira aja alanda mzinda ndipo kuti utsi unali tolotolo, iwo anatembenuka ndi kuyamba kupha anthu a ku Ai.
and Joshua and all Israel have seen that the ambush has captured the city, and that the smoke of the city has gone up, and they turn back and strike the men of Ai;
22 Nawonso Aisraeli amene anali mu mzindamo anatuluka kudzalimbana ndi anthu a ku Ai. Choncho iwo anazingidwa mbali zonse ndi Aisraeli ndipo onse anaphedwa. Palibe amene anatsala wamoyo kapena wothawa
and these have come out from the city to meet them, and they are in the midst of Israel, some on this [side], and some on that [side], and they strike them until he has not left a remnant and escaped one to them;
23 kupatula mfumu ya ku Ai yokha imene anayigwira nabwera nayo kwa Yoswa.
and they have caught the king of Ai alive, and bring him near to Joshua.
24 Aisraeli aja atatha kupha anthu onse a ku Ai amene anali mʼthengo ndi mʼchipululu kumene anawapirikitsira, onse anabwerera ku Ai ndi kupha onse amene anali mu mzindamo.
And it comes to pass, at Israel’s finishing to slay all the inhabitants of Ai in the field, in the wilderness in which they pursued them (and all of them fall by the mouth of the sword until their consumption), that all of Israel turns back to Ai, and strikes it by the mouth of the sword;
25 Chiwerengero cha anthu onse a ku Ai, amuna ndi akazi, amene anaphedwa pa tsiku limeneli chinali 12,000.
and all who fall during the day, of men and of women, are twelve thousand—all men of Ai.
26 Yoswa sanatsitse dzanja lake limene ananyamula mkondo mpaka ataona kuti onse amene amakhala mu mzinda wa Ai aphedwa.
And Joshua has not brought back his hand which he stretched out with the javelin until he has devoted all the inhabitants of Ai;
27 Tsono Aisraeli anatenga zoweta ndi katundu yense wa anthu ophedwa aja, monga momwe Yehova analamulira Yoswa.
only the livestock and the spoil of that city has Israel spoiled for themselves, according to the word of YHWH which He commanded Joshua.
28 Pambuyo pake Yoswa anawutentha mzinda wa Ai ndi kuwusiya bwinja monga ulili leromu.
And Joshua burns Ai, and makes it a continuous heap—a desolation to this day;
29 Iye anapachika pa mtengo mfumu ya Ai ndipo anayisiya mpaka madzulo. Pomwe dzuwa linalowa Yoswa analamula kuti akachotse mtembowo ndi kukawutaya ku chipata cha mzindawo. Pamwamba pa mtembowo anawunjikapo mulu waukulu wa miyala. Muluwo ulipobe mpaka lero lino.
and he has hanged the king of Ai on the tree until evening, and at the going in of the sun Joshua has commanded, and they take down his carcass from the tree, and cast it to the opening of the gate of the city, and raise a great heap of stones over it until this day.
30 Ndipo Yoswa anamanga guwa lansembe la Yehova Mulungu wa Israeli pa phiri la Ebala.
Then Joshua builds an altar to YHWH, God of Israel, in Mount Ebal,
31 Analimanga motsata zimene Mose mtumiki wa Yehova analamulira Aisraeli, ndiponso potsata zomwe zinalembedwa mʼbuku la malamulo a Mose kuti guwa lansembe likhale la miyala yosasemedwa ndi chitsulo. Pa guwalo anapereka kwa Yehova nsembe yopsereza ndi nsembe yachiyanjano.
as Moses, servant of YHWH, commanded the sons of Israel, as it is written in the Scroll of the Law of Moses—an altar of whole stones, over which he has not waved iron—and they cause burnt-offerings to go up on it to YHWH, and sacrifice peace-offerings;
32 Kenaka anthu onse akupenya, Yoswa analemba pa miyala chitsanzo cha malamulo amene Mose analemba.
and he writes there on the stones a copy of the Law of Moses, which he has written in the presence of the sons of Israel.
33 Aisraeli onse, akuluakulu awo, atsogoleri awo ndi oweruza awo, alendo pamodzi ndi mbadwa, anayimirira mbali zonse ziwiri za Bokosi la Chipangano la Yehova, ena uku ena uku moyangʼanana ndi ansembe a Chilevi. Theka la anthu linayima patsogolo pa phiri la Gerizimu ndipo theka lina patsogolo pa phiri la Ebala, monga momwe Mose mtumiki wa Yehova anawalamulira mʼmbuyomo pamene anawapatsa malangizo podalitsa Aisraeli.
And all Israel, and its elderly, and authorities, and his judges, are standing on this [side] and on that [side] of the Ark, before the priests, the Levites, carrying the Ark of the Covenant of YHWH, the sojourner as well as the native, half of them in front of Mount Gerizim, and the half of them in front of Mount Ebal, as Moses servant of YHWH had commanded to bless the people of Israel at the first.
34 Pambuyo pake Yoswa anawerenga mawu onse a malamulo, madalitso ndi matemberero monga momwe zinalembedwera mʼbuku la malamulo a Mose.
And afterward he has proclaimed all the words of the Law, the blessing and the reviling, according to all that is written in the Scroll of the Law;
35 Yoswa anawerenga mawu onse amene Mose analamula, gulu lonse la Israeli limene linasonkhana likumva. Amayi, ana ndi alendo omwe okhala pakati pawo anali pomwepo.
there has not been a thing of all that Moses commanded which Joshua has not proclaimed before all the assembly of Israel, and the women, and the infants, and the sojourner who is going in their midst.

< Yoswa 8 >